Download as pdf or txt
Download as pdf or txt
You are on page 1of 153

NYIMBO

ZA MULUNGU

ZOLEMBEDWA M'CHICHEWA

Improved Edition 1974


MAWU OYAMBA PAKUSINDIKIZA KOYAMBA

Nyimbo iyi ndiyo ntchito ya Kabungwe kamene kasankhika ndi


msonkhano wa Federated Missions of Nyasaland umene unachitika
chaka cha 1910.

M’buku muno nyimbo zimene zichokera mwambiri, makamaka


m’mabuku osiyanasiyana a mamisyoni ogwira ntchito m’dziko muno.

M’menemo nyimbo zina zakale anazilongosolanso, ndiponso


zatsopano zinaonjezedwamo kuti pakhale buku lotere. Nyimbo zambiri
nzachizungu; zina pang’ono ndi za konkuno.

Kabungwe kafuna kuyamika onse, Akuda ndi Azungu omwe, amene


anathandiza kusonkhanitsa nyimbozi.

Kabungwe kayamikanso amene analemba mabuku a maliu pakutilola


kutenga maliu a nyimbo zawo.
January 1916.

MAWU OYAMBA PAKUSINDIKIZA KWACHIWIRI


Kalekale chaka cha 1934 The Consultative Board of Federated
Missions anasankha kabungwe kuti kalongosolenso buku la Nyimbo la
Chichewa. Kuyambira pachiyambi, kabungwe kanafunitsa kulonga
m’malo mwa nyimbo zachizungu nyimbo zina za mu Afrika: za
malingiriro ake a eni dziko lino ndi zimene azitchula, ndi nyimbo
zambiri zofanana ndi nyimbo zawozawo kumene sikutheka maliu a
nyimbo zachizungu. Panali zambiri zochedwetsa, koma lingiliro la
kabungwe silidatha. Koma zoona kuti nyimbo zina maliu ake aoneka
ngati osayenera mumpingo wa m’dziko muno. Koma kuti buku lenileni
la nyimbo za anthu a kuno lifunikadi.
Koma Mpingo sungathe kumalindira kuti nyimbo yake idzaoneke
ndipo panatsimikizika kuti pakali pano tibasindikizanso nyimbo imene
inasindikizidwa chaka cha 1916, ndi kumasintha nyimbo zina monga
adziwira Kabungwe kukometsa nyimbozi. M’malo mwa nyimbo zina
mwaikidwa maliu osiyana ndi nyimbo yoyambayo; maliu atsopanowo
ndiwo ena amene anaimba kumipingo kwina, a m’buku lomweli.
Anaonjezanso nyimbo zina pang’ono zosiyanasiyana. Tiyamika eni
nyimbo ya “Sumu za Ukhristu” pakutilola kusanduliza nyimbo zina za
Chitumbuka.
Kabungwe kalembanso chiyamiko chake kwa eni nyimbo amene
anatilola kuchita ndi maliu a nyimbo zawo amene maina awo
analembedwa m’nyimbo ya chaka cha 1916.
February, 1954.

MAWU OYAMBA PAKUSINDIKIZA KWACHITATU


M’chaka cha 1962, Bungwe la The Fellowship of Christian Churches
in Malawi linaika kabungwe kuti kalongosolenso buku la Nyimbo za
Mulungu. Kulongosolanso uku kunafunika chifukwa chakusakhutira
pakati pa Akristu ambiri ndi buku la Nyimbo za Mulungu limene
linasindikizidwa chaka cha 1954. Kunanenedwa momveka bwino kuti
mawu ndi nyimbo zimene zinali kuimbidwa m’buku loyamba lija zinali
kukondedwa koposa za buku latsopanoli. Kabungweka
kanabvomerezana pakuchita malongosoledwe atsopano, kutenga
nyimbo zambiri zochokera mu buku loyamba lija, katayamba
kuyang’anitsitsa mosamala bwino ndikulinganiza ndime ili yonse ndi
nyimbo yake. Chotsatira chake ndicho kuti nyimbo zambiri zoyamba
zija zidzaimbidwanso. Zambiri za izo zalongosoledwanso, ndipo
mwina ndime zina zalembedwanso. Nyimbo zatsopano
zaonjezedwamo, kotero kuti nyimbo zonse zakwanira 376. Poti nyimbo
zochuluka zinatidzera mwa Chizungu, muno talembanso mawu
oyamba a Chizungu chake cha nyimbozo. Maimbidwe (maliu) amene
alipowa sanasinthidwe. M’tsogolomo kabungwe kena ka Odziwa za
Maimbidwe (Musical Committee) kadzasankhidwa kuti aone za dera
limeneli.
Malongosoledwe amenewa a Nyimbo za Mulungu adzakhala omaliza.
Ngati m’tsogolomo kudzapezeka kuti buku latsopano lilikufunika ,
pamenepo buku latsopano kotheratu lidzalongosoledwa, makamaka
buku la nyimbo ndi maimbidwe za m’dziko muno.
Kabungwe kafuna kuyamikira kwa onse amene anathandiza
malongosoledwe a buku latsopanoli. Kuyamikanso President wa dziko
la Malawi amene anapereka chilolezo kuti Nyimbo ya Malawi (Malawi
National Anthem) ilowe m’buku muno.
Pemphero lathu ndilo kuti nyimbozi zidzaimbidwa kukometsera
mapembedzedwe athu a m’Mipingo ya m’Malawi, pamene ife tonse
pamodzi tikweza mawu athu kuimba nyimbo zoyenera zakutamanda
Iye amene ife tonse tiyenera kumtamanda ndi kumulemekeza.
May, 1967.

ENI AKE BUKU ILI


Pa 18th May 1967, Bungwe la The Fellowship of Christian Churches in
Malawi linapereka umwini wa buku ili la Nyimbo za Mulungu kwa
bungwe la mabuku la The Christian Counsil of Malawi koma
kuyambira 1968 bukuli lili m’manja mwa Christian Literature
Association in Malawi. Bungwe la The Fellowship of Christian
Churches in Malawi linatha ntchito yake nilinapasuka.
May, 1968.

MAWU OYAMBA POKONZA MAIMBIDWE (DODODO)


Pamene tinali pantchito yokonza maimbidwe (maliu), Kabungwe
kanakonzanso Chichewa pena ndi pena, koma osasintha kwenikweni.
Tiyamika kuti panapezeka maimbidwe ambiri achikhalidwe chathu
(achifirika). Mwa ichi pa nyimbo zina panaonjezedwa mang’ombe
amene panalibe m’buku lakale. Pano tipangiranso kuti kutcharitchi
mang’ombe aziimbidwa kamodzi kokha, koma m’midzi timaimba
mang’ombe kawiri (mobwereza).
Ambiri anali kudandaula chifukwa cha nyimbo zina zokoma zimene
zinaiwalika (zinachotsedwa) m’buku la 1967. Motero tinaziikanso pa
chionjezero m’buku ili (Nyimbo 377-384).

Maliu a m’dziko muno si oluluka kapena oipa, kapena achikunja


kapenanso oyenera kuimbidwa pamaliro pokha ndi pamisonkhano ya
kumidzi kapena ya amayi okha, iyayi. Koma ndithudi ayeneranso
kumaimbidwa m’misonkhano ya chipembedzo m’nyumba ya
Mulungu, kuti anthu aimbe mwamoyo ndi mwachimwemwe,
mochokera mumtima.

July, 1974.
MALONGOSOLEDWE A NYIMBO
MULUNGU NYIMBO

Mmodzi mwa Atatu ...................................................................................................................1-5, 245


Mlengi ............................................................................................................................................. 6-7
Mtetezi.................................................................................................................................... 8-17, 311
Mpulumutsi............................................................................................................................ 18-23, 331

AMBUYATHU YESU KHRISTU


Kubadwa kwake..................................................................................................................... 24-28, 325
Chitsanzo chake .............................................................................................................................29-31
Kufera kwake......................................................................................................... 32-39, 324, 330, 341
Kudzukanso kwake................................................................................................................ 40-42, 349
Ulemerero wake...................................................................................................................... 43-44,350
Kuthandiza kwake ..................................................................................................45-50, 321, 361, 368
Kubweranso kwake.................................................................................................................51-54, 333
Kumyamikira.................................................. 55-63, 315, 319, 328, 336, 359, 362-363, 366, 372, 381

MZIMU WOYERA................................................................................64-72, 155, 198, 203, 322, 364

MAWU A MULUNGU ................................................................................................................ 73-75

UTHENGA WABWINO ..............................................76-101, 337, 340, 356-358, 360, 366-367, 374

NJIRA YA CHIKHRISTU
Kutembenuka mtima...........................................102-115, 314, 316, 318, 338, 347, 354, 369-370, 380
Kukonda ndi kuthokoza..............................................................................116-127, 345, 355, 372, 382
Chimwemwe ndi mtendere .............................................................................. 128-137, 346, 373, 379
Chikhulupiriro ............................................................................................................138-149, 335, 384
Kuyera mtima ........................................................................................................... 150-163, 322, 339
Kutumikira .........................................................................................................164-171, 320, 326, 377
Nkhondo za mayesedwe.....................................................................................................172-180, 348
Ulendo wakumwamba........................................................................................181-188, 342, 365, 371
Za maliro ...................................................................................................................189-191, 332, 344
Ulemerero wakumwamba .................................................................................................192-194, 343
Pemphero....................................................................................................195-200, 317, 323, 327, 353

MPINGO WA MULUNGU................................................................................201-204, 313, 362, 383


Kupemphera kwa mamawa .......................................................................................................205-206
Kupemphera kwa madzulo.........................................................................................................207-215
Tsiku la Mulungu ...............................................................................................................216-218, 352
Nyumba ya Mulungu ................................................................................................................219-220
Kuyamikira ................................................................................................................................221-223
Ubatizo................................................................................................................224-226, 337, 351, 373
Mgonero wa Ambuye .............................................................................................75, 98, 314, 227-235
Zopereka.............................................................................................................................126, 236-238
Zolalikira .....................................................................................................................239-247,366, 374
Atumiki .........................................................................................................................................248

POMANGA NYUMBA ZA MULUNGU ................................................................................249-250

UKWATI ...................................................................................................................................251-252

CHAKA CHATSOPANO .........................................................................................................253-255

DZINJA NDI MASIKA ....................................................................................................256-259, 312

ULENDO...................................................................................................................................260-261

NYIMBO ZA ANA
Mulungu Mtetezi ......................................................................................................................262-263
Kubadwa kwa Khristu...............................................................................................................264-269
Kufera kwa Khristu ..................................................................................................................270-271
Kuyamikira Khristu ..................................................................................................................272-281
Kukhulupirira Khristu ..............................................................................................................282-286
Kutsata Khristu..........................................................................................................................287-297
Za Kumwamba..........................................................................................................................298-303
Mamawa............................................................................................................................................304
Madzulo............................................................................................................................................305

NYIMBO ZOMALIZIRA ................................................................................................306-308, 329

ZOYAMIKIRA MULUNGU.....................................................................................................309-310

NYIMBO ZINA ........................................................................................................................311-374

AMEN ..............................................................................................................................................334

BOMA NDI DZIKO..................................................................................................................375-376

CHIONJEZERO........................................................................................................................377-384

MAWU OYAMBA A NYIMBO.........................................................................................tsamba-116

MAWU OYAMBA A M'CHIZUNGU...............................................................................tsamba-124


MULUNGU MMODZI MWA ATATU 1
2
MULUNGU MMODZI MWA ATATU
1 Inu Mulungu, tikuyamikani;
1 Tibvomereza ndinu Ambuyathu;
Ponse, Atate, akugwadirani,
1 Ndinu wakuyera! Ndinu wamuyaya!
E, wamphamvu zonse.
Nthawi ya m’mamawayi 2 Nanu akukuzani amithenga,
Tiimba nyimboyi. Nanu zam’mwamba ndi
Mlengi wachifundo, zamphamvu zake,
Tikuyamikani, Nanu angelo a mitundu yonse
E! Mlungu Mmodzi Akuimbirani!
Mwa Atatuwo. 3 “Mbuye Woyera! E, Woyera
nokha!
2 Ndinu wakuyera!
Mbuye Woyera! Mbuye wa
Anthu ochuluka makamu!
Akuimbirani, Ponse ulemu wanu ndi wodzaza
Nakupempheranibe; Pansi ndi Kumwamba.”
Akumwamba omwe,
Nagwadira Inu, 4 Nanu Atumwi akumveka aja,
Wachikhalire Ndi Aneneri oyanjana omwe,
Ndi wosafa ‘yi. Ndi aunyinji anakuferani
Akuyamikani.
3 Ndinu wakuyera!
Ife akuchimwa 5 Mpingo woyera wa kwa anthu
Zaulemerero zanu onse
Sitiona ‘yi; Ukumverani, Mfumu ndi Atate,
Mwayeradi nokha, Mwana woona wa ulemu wonse,
Wina saoneka Mzimu Nkhoswe yemwe.
Wangwiro m’mphamvu 6 Kristu Mfumuyo yaulemerero!
Ndi m’kuyeramo. Mwana wosatha wa Atate ndinu!
Simunanyoza mimba ya
4 Ndinu wakuyera! Namwali
Zakumwamba zonse Potipulumutsa.
Ndi zapansi zitamabe
Dzina lanulo 7 Imfa mutagonjetsa ndi zowawa,
Mlengi wachifundo. Njira munatsegula tikalowe
Mphambi, Ambuyathu, Momwe mukhala Inu ndi Atate
E! Mlungu Mmodzi, Mwaulemerero.
Mwa Atatuwo.
2 MULUNGU MMODZI MWA ATATU
8 Kumva milandu yathu mudzabwera Ochimwa tikupemphani:
Mutithandize, atumiki anu; Mutikhululukire 'fe.
Mwatiwombola nawo mwazi wanu:
Mutipulumutse.
4
9 Mtiwerengere m'Mwamba ndi oyera; 1 Lemekeza Mlungu 'Tate,
Mutidalitse, ndife anthu anu; Lemekeza Mlungu Mwana,
Moyo wosatha mutipatse tonse, Lemekeza Mlungu Mzimu,
Mutilamulire. Mlungu Mmodzi ndi wamkulu.
Lemekeza, lemekeza,
10 Tsiku ndi tsiku timalemekeza; Mlungu wathu yemweyo.
Nanu tikukuzani osaleka;
Mbuye, mtisunge tingachimwe lero: 2 Mlemekeze, anakonda
Mtichitire nsisi. Natitsuka m'mtima mwathu;
Anatiombola ife
11 Mbuye, chifundo chanu chitigwere Tikakhale ndi chifumu.
Monga tikhulupira Inu nokha; Lemekeza, lemekeza,
Ndakhulupira zedi mwanu, Mbuye, Yesu Mbuye Nsembeyo.
Ndisagome konse!
3 Lemekeza Mfumu yathu,
Mfumu ya mipingo yonse,
Ipambana anthu onse
3 Akumwamba ndi apansi.
1 Atate wa Kumwambako, Lemekeza, lemekeza,
Munawombola ife ndi Mfumu ya mafumuyo.
Chikondi chanu chijacho;
Tiyamikira Inutu.
5
2 Ambuye Yesu, Inutu 1 Ndi Aleluya imbirani
Munabadwira anthu 'fe; 'Tate wathu, wakumwamba,
Munatifera tonsefe; Analenga zonse.
Tiyamikira Inutu. Chifundo chake chachikulu,
Nzeru, mphamvu ndi ufumu
3 Mzimu Woyera, m'mtimamo Tiyamike tonse.
Tiyeretsedwe ndinutu;
Munatisunga bwinoli; 2 Ndi Aleluya imbirani
Tiyamikira Inutu. Yesu Khristu Mpulumutsi,
Anachoka kwawo,
4 Atate, Mwana, Mzimunso, Nakhala munthu, pansi pano,
Ndinu Atatu Mmodzitu, Nasauka, natifera,
MULUNGU MLENGI 3
Natisiyira mawu. 5 Zam'madzi zonse zakuopsyazo,
Nyanja, matiti ndi mitsinjeyo,
3 Ndi Aleluya imbirani Chigumula chakulindimacho.
Mzimu wake Wakuyera, Aleluya.
Amakhala nafe.
Atilangiza za Mulungu, 6 Zamoyo zili m'thengo zonsezo,
Nayeretsanso mitima Zodzuma, zina zobangulazo,
Ya akhristu ife. Zinene ndi kulira konseko:
Aleluya.
4 Mulungu wathu tiyamika,
'Tate, Mwana, Mzimu yemwe 7 Inu mumvere anyamatawo,
Aleluya Inu. Okondwerera kusewerako,
Woyera Inu ndi wamphamvu, Mumtima mubvomere monsemo:
Muyenera anthu onse Aleluya.
Agwadire Inu.
8 Ndi anamwali obvekedwa mbuu!
MULUNGU MLENGI Ndi ana osakula msinkhu 'nu,
Ana a Mlungu mubvomeretu:
6 Aleluya.
1 Mitambo inu yakumwambako,
Yogunda mvula 'mlengalengamo 9 Akulu nonse ndi mafumu 'nu,
Mawu akulu muzinenadi: Magulu nonse apadzikopa,
Aleluya. Mulemekeze Mbuye yemweyo:
Aleluya.
2 Paphiri paja papakulupo,
Pamwala ponse pakuwala mbuu! 10 Ndi amithenga akumwambako,
Mubvomereze mawu omwewo: Ndi anthu ndi zamoyo zonsezo,
Aleluya. Bvomerezani mawu omwewo:
Aleluya.
3 Mphepo yay'kulu yakuombayo,
Chisanu chija chozizirachi, 7
Ndi kabvumbulu muzinenadi: 1 Tamani Ambuye,
Aleluya. Wamphamvu ndi Iye,
Akhala m'ulemu
4 Mitengo yaitalitali 'nu Kumwamba komweko;
Yachiimire mumaimabe, Chikopa cholimba
Mubvomereze ndi kunenabe: Ndi kothawiranso
Aleluya. Kwa anthu akewo,
Kotero ndi Mlungu.
4 MULUNGU MLENGI
2 Uzani zamphamvu, MULUNGU MTETEZI
Imbani chisomo,
Za Mwini ulemu,
8
Ambuye wathuyo; 1 Tsopano linoli
Powomba chimphepo Tiimbe nyimbo zathu;
Mvulanso ndi bingu Tiimbe nyimbozi,
Padziko, pathambo, Titame Mlungu wathu;
Akhala ponsepo. Masiku onsewo
Anatisungadi,
3 Zozizwa za m'dziko, Anatipatsanso
Za m'mwamba zonsezi. Zabwino zonsezi.
Mulungu wamphamvu,
Munalenga zonse; 2 Mulungu yemweyo
Muyendetsa mwezi Akhale m'fupi mwathu;
Nyenyezi ndi dzuwa; Mtendere wakewo
Zolengedwa zonse Ukhale m'mtima mwathu;
Zimvera Ambuye. Timtsate Iyedi
Ndi nsoni zakezo,
4 Sititha ifedi Panjira yakeyi
Kukamba zokoma Masiku onsewo
Za Inu Mulungu .
Wolera anthuwa; 3 Tilemekezetu
Zifika ndi mphepo Atate Wakumwamba,
Ndi mvula ndi dzuwa, Ndi Yesu Mbuyathu,
Zigwera ponsepo Ndi Mzimu Wakuyera;
Pa anthu onsewo. Mulungu Mmodziyu
Wanthawi zonsezo,
5 Wamphamvu yosatha, Timlemekezetu
Chikondi changwiro, Masiku onsewo.
Angelo akonda
Kutama Mulungu; 9
Ndiponso ifetu 1 Ndi mitima yokondwera
Ananu tonsefe Mbuye wathu tiyamika.
Tiimba nyimboyi
Yotama Ambuye. E, chifundo chake chonse
Ndichosatha nthawi zonse.

2 Dzina lake tibukitsa,


MULUNGU MTETEZI 5
Mlungu ndiye yekhayekha.
3 Mlungu kuona athiratu
3 Mphamvu yake inalenga Inde m'maso awo osapenyawo.
Dziko lonse ndikumwamba. Natuma akumvera mpumulo;
Amathandiza inde aulendo ofokatu,
4 Anatsogolera kale Akazi amasiye maka ndi anawo
M'chipululu anthu ake. …onsewo,
Olira atonthoza mtimadi.
5 Ndi chifundo atipenya
Ife anthu osauka. 4 Nditamatu Ambuyangayu,
Moyo wanga wonse ndidzamtamatu
6 Amaweta nyama zonse, Ndiponso m'dziko lakumwamba;
Zingasowe kanthu konse. Masiku anga onse ndidzamlemekeza
…Iye;
7 Tiimbire Mlungu wathu Sindidzaleka konsekonse m'mene
Waulemu ndi wamkulu ndili m'moyotu,
. Padziko pano pena
8 Tithawire kwa Mulungu, ...m'Mwambamo.
Ndiko tikapeze moyo.
11
10 1 Paphiri ndi padambo
1 Nditamatu Ambuyangayu, Ponsepo pali Mlungu,
Moyo wanga wonse ndidzamtamatu, Poyenda ife m'njira
Ndiponso m'dziko lakumwambako; Poima pali Mlungu;
Masiku anga onse ndidzamlemekeza
....Iye; Kokwera maganizo,
Sindidzaleka konsekonse m'mene Komweko kuli Mlungu,
...ndili m'moyotu, Kumwamba ndi pansipo
Padziko pano pena m'Mwambamo. Ponsepo pali Mlungu.

2 Ndiye wokondwa, E, munthuyo (Mulungu ali nane!)


Wokhulupirira Mlungu yekhadi, (Ali nane, aIi nane, ali nane,
Wolenga dziko, nyanja, zonsezi; ali nane, Aa!
Choona chake chonse Mulungu ali nane!)
...chingokhalatu chosatha;
Apulumutsa onse namadyetsa anthu... 2 Ndi maso Ambuyathu
. akewo, Apenyetsetsa ife;
Wokonda ndiye Mbuye wathuyo. Amadalitsa onse
6 MULUNGU MTETEZI
Okhulupirira Iye; Nthawi zonse sasanduka
Mlungu wathu yemweyo.
Amamva timbalame,
Namveka dziko lonse; 3 Nthawi zonse monga 'Tate
Sataya tizilombo, Atisamaliratu,
Asunga zina zonse. Atisunga m'manja mwake,
Atipulumutsatu.
3 Okwawa pansi inu,
Oyenda m'madzi inu, 4 Anthu a mitundu yonse,
Oyesa dziko nkwanu, Ndipo a Kumwambako,
Am'mlengalenga inu, Yamikani Mlungu wathu,
Ndiye wakukomatu.
Nonsenu ntchito zake
Muona tsiku n'tsiku, …… Anthu onse, anthu onse,
Saleka kusamala …… Yamikani Mlunguyo.
Ndi kudalitsa inu.

4 Nditama mphamvu yake


13
Ya Mlungu yondizinga; 1 Yehova ndiye Mbusa wanga,
N'kafoka an'limbitsa, sin'ngasowe konse;
N'kadwala andichiza. Andigonetsa pali busa
la misipu yonse.
Pakundisiya bwenzi
Mulungu ali paja; …… (Ndiye M'busa wanga,
N'kalowa imfa ine …… Ndiye M'busa wanga!
Alipo Mlungu wanga. Yehova ndiye Mbusa wanga,
Sin'ngasowe konse.)

12 2 Kumadzi kuli njiratu


1 Mtima wanga uyamike andiyendetsa bwino,
Mfumu Yakumwambako; Nalimbikitsa moyo wanga
Anandiwombola ine ndi chifundo chino.
Nanditsuka m'mtimamo.
3 Pabande lolunjika
…… Ife tonse, ife tonse, Andilondolera njira;
…… Tiyamike Mlunguyo. Chifukwacho cha dzina lake
Anandisungira.
2 Tiyamike Mlungu wathu
Kaamba ka chifundocho; 4 Chigwa choopsacho cha imfa
ndikachilowera,
MULUNGU MTETEZI 7
Ndilibe mantha, muli ndine, Mlungu wathu yamikani!
ndodo ndiigwira.

5 Pamaso pa adaniwo
15
mwayala gome langa; 1 Mulungu ndiye Mbusa wanga,
E, mutu mwaudzoza, sindisowa konse;
chisefuka chikho changa. Amandiweta nandidyetsa;
nandipatsa zonse.
6 Zabwino ndi zokoma …… (Ndiye M'busa wanga,
zinditsata chitsatire; …… Ndiye M'busa wanga!
E, m'nyumba ya Yehova …… Mulungu ndiye M'busa wanga,
ndidzakhala chikhalire. …… Sindisowa konse.)
14
1 Mtima wanga lemekeza 2 M'mitsinje yamtendere mtima
Mlungu wako ndi chimwemwe. wanga aumwetsa;
Nthawi zonse ndimtamanda; Mapazi omwe m'njira
Ndimwimbira nyimbo zanga. yolungama nandiyendetsa
Moyo, mphamvu, nzeru zonse,
Zidzamlemekeza konse. 3 Za m'mdima, imfa, nkhondo ndi
zoipa sindiopa;
2 Ndi wamwayi munthu uja Ndikakhumudwa ndikutopa,
Amthandiza Mbuye wake. Andipulumutsa.
Akachita mantha iye
Amchotsera nkhawa yake, 4 Podwala ine pobvutidwa
Ndipo likamgwera tsoka Andisamalira;
Amakhulupira kokha. Pondisautsa adani anga
nandithangatira.
3 Mbuye ndiye wachifundo,
Achiritsa akudwala; 5 Chisomo ndi zokoma zake
Anyamula akufoka sizileka konse;
Nawadyetsatu anjala. Ndi m'nyumba ya Mulungu
Wakusunga mlendo ndiye, ndidzakhala nsiku zonse.
Nathandiza amasiye.
16
4 Ndiye Mbuye wa ambuye; 1 Zobvuta zoopsa ndi zosaukazi
Mphamvu yake ndi yokwana, Sitingathe ife kuzithawa tokha.
Adzakhala chikhalire, Koma Ambuyathu timtamande Iye,
Mfumu yathu yopambana, Uthenga Wabwino timveretu tokha.
Aleluya! Kondwerani!
8 MULUNGU MTETEZI
2 Amadyetsa Iye mbalame Kuopa kanthu kena;
...zam'mwamba, Mumtumikire mokondwera,
Timtamande ndithu potisunga ife; Akusungani 'nu.
Timvere malembo a m'kalata mwake,
Ambuye yemweyo atisungirabe. 6 Mulungu wathu Mmodzi yekha
Atate, Mwana, Mzimu,
3 Abramu kalelo anamvera bwino; Akhale ndi ulemerero
Timverenso ngatitu yemwe wakale. Wachikhalirewo!
Pokhala alendo atsogoza iwo,
Timkhulupirire Ambuye tonsefe. MULUNGU MPULUMUTSI

4 Timtamande Iye ndi moyo wathunso


18
Pakutsatatsata malembedwe awo. 1 Kuzani Mlungu m'Mwambamo,
Tipezemo malo okwanira ife Mtamande m'kuyanso;
Ambuye wathuyo atipatsa kwawo. Nzozizwa nkhani zakezo.
Njolimba ntchito njo!

2 Pochimwa anthu onsewo


17 Nja Mlungu nzeruyi;
1 Pokondwa ndi poona bvuto Adamu wachiwiriyo
Ndi tsoka pena mwayi, Wathetsa tchimoli.
Ndikumbukira, ndiimbira
Mulungu wangayo. 3 Thupi lamwazi wathu'li
Lochimwa kalelo,
2 Kwezani nane Ambuyathu, Labweranso ku nkhondoyi,
Timlemekeze yekha; Laposa monsemo.
Popsinja mtima ndinamtchula,
Nandithangata 'ne. 4 Choposa nalo thupilo,
Chikhale momwemu,
3 Angelo amazinga nyumba Chiyeretsetsa m'katimo,
Za anthu olungama; Ndi Mulungu Iyeyu.
Mulungu ateteza omwe
Amkhulupirira. 5 Anatikondakonda 'Ye,
Ndi Mlungu Iyeyo,
4 Lawani chikondano chake; Anatifera anthu 'fe,
Mudzadziwitsa msanga Ndi Munthu Iyenso.
Kudala kwawo kwa anake
Omkonda Mbuyeyo. 6 Ndi m'munda muja chete, phee!
Pamtanda pati njo!
5 Opani Iye, nimuleke
MULUNGU MPULUMUTSI 9
Anaphunzitsa 'bale 'fe Yatsika pamadzipo,
Titero ifenso. Yathyolatu mayani,
Yampatsa Nowa yemwe,
7 Kuzani Mlungu m'Mwambamo, Yampatsa Nowa yemwe.
Mtamande m'kuyanso;
Nzozizwa nkhani zakezo, 6 Kalelo Mbuye Yesu
Njolimba ntchito njo! Nafera anthu onse,
Ndiyeyo chombo chathu,
Tikabisala mommo,
19 Tipulumuka mommo,
1 Kalelo anthu onse Tipulumuka mommo.
Nachimwa kwa Mulungu,
Mulungu anaona,
Naona tchimo lawo, 20
…… Nafuna kwaononga 1 Mulungu awakonda anthu
Nafuna kwaononga Ali pansi pano;
Afuna kuwapulumutsa
2 Mulungu anatuma, Kumilandu yawo
Natuma Nowa uja,
Wamanga chombo chake, A! chikondi chachikulu
Ndi chachitalitali, Mulungu ali nacho,
…… Nowayo nayendamo, Chinan'tengera Mpulumutsi,
…… Nowayo nayendamo. Andifere pano.

3 Mulungu anatuma, 2 Ndikhulupira mwa Ambuye


Natuma mvula ija, Mlungu namukitsa,
Yadzaza dziko lonse, Imfayo indipulumutsa,
Anafa anthu onse, Mwazi undiyeretsa.
… Anafa m'mvula muja
Anafa m'mvula muja. 3 Chikondi chake chindidzera
M'mtima mwanga muno,
4 Nowayo anatuma, Chipulumutsa nditalema
Natuma chikwangwala, Ndi machimo anga.
Chatsika pansi pansi,
Chosabwerera konse, 4 Mukondwe anthu a Mulungu,
Chithawa m'talitali Tere mulandira.
Chithawa m'talitali. Chimwemwe chija chakumwamba
Chidzalowa m'mtima.
5 Kutuma wabwereza,
5 Mulungu atipatsa mphamvu
Natuma nkhunda ija,
Yoletsetsa tchimo;
10 MULUNGU MPULUMUTSI
Pofika tsikulo la imfa. Andithandiza, nandipulumutsa.
Tidzakhala bwino.
2 Mulungu wanga ndiye wachifundo
Ndiwolungama mtima ndi wabwino;
21 Apulumutsa anthu akufoka,
1 Tiimbe nyimbo zotamanda Akathandiza nkhawa imachoka.
Mulungu wathu wabwino,
Pakuti akondana nawo 3 Mtimanga, bwera kuti upumule,
Anthu okhala padziko; Wakuchitiranso zokoma Mbuye,
Tero natuma Mwana wake, Wakuchotsera imfa ndi misozi,
Wakukondedwa kalelo, Ndingakhumudwe asungira phazi.
Kutiphunzitsa ife tonse
Za chikondano chakecho. 4 Nditani ine kubwezera Mbuye
Zokoma zonse anandichitira?
2 Mulungu ndiye wachifundo, Chipulumutso chake ndidzatama,
Nadzalandira onsewa Ndinalumbira zija ndidzapatsa.
Akuulula mphulupulu
Ndi kukondana ndi Yesu, 5 Imfa ya anthu ake imkomera,
Tilondelonde njira yake, Awalandira m'nyumba zokonzeka,
Yopapatiza yaing'ono; Mbuye, kapolo wanu ndipereka
Adzatilondolera ndiye Nsembeyi yonga yanu, ndine
Kutifikitsa m'Mwambamo. ...ndekha.
3 Pakuwoloka mtsinje wa imfa
Dzanja Mbuyathu agwira; 23
Tikadagwira ntchito zake 1 Titame Mlungu Wakumwamba,
Atipatsatu korona; Timwimbire nyimbo,
Kukoma kwake kwatipatsa
Komwe kulibe masauko, Zonse tili nazo.
Pena misozi maliro;
Mulungu tidzamtamandira, (Timwimbire nyimbo,
Inde kosalekezanso. Timwimbire nyimbo!
Kukoma kwake kwatipatsa
Zonse tili nazo.)
22
1 Ndikonda Mlungu pomva Mbuye 2 Poyamba paja analenga
…wanga Zonse m'dziko muno,
Amva pemphero ndi kulira kwanga, Tsopano lomwe azisunga
Namatchereza khutu nditapfuula, Zonse zili moyo.
MULUNGU MPULUMUTSI 11
3 Tinasokera ngati nkhosa, 4 M'dzikomo Ambuye
Moyo tinataya, Mnabadwira ife,
Tinakondwera ndi zoipa Ulemu wosatha muyeneradi,
Zonse tinatsata. Mawu a 'Tate
Munalowa m'thupi.
4 Komweko titasaukira,
Titafuna kufa,
Atate anatilondola
25
Naitana ife. 1 Ndilikulemekeza
Ambuye Mpulumutsi wanga;
5 Tiyeni tizipita kwathu, Moyo ndi mtima wanga
Tisasokerenso, ndilikukondwa mwa Mulungu.
Tilape m'mtima kuti tikakhale ndi
…Mulungu. 2 Ndiye anayang'ana
umphawi wa mdzakazi wake;
AMBUYATHU YESU KRISTU- Onse adzandiyesa
KUBADWA KWAKE ine wodala nsiku zonse.

24 3 Ndiye wamphamvu zonse


1 Oonadi mtima, andichitira zazikulu;
'Dzani mokondwera, Dzina la Ambuyanga
Tiyeni, tiyeni ku Betelehemu; lili loyera kopambana.
Modyera ng'ombe
Muli Mfumu yathu. 4 Ndiye amachitira
chifundo anthu a mibadwo,
Tiyeni timgwadire E! a mibadwo yonse
Kristuyo. yakumuopa ndi kumvera.

2 Mulungu wamkulu 5 Iye amazichita


Wakuyerayera zamphamvu nawo mkono wake;
Kubadwa mwa mkazi sanakana 'yi; Iye nabalalitsa
Mwana wa 'Tate, omwe anyada nadzitama.
Sanalengedwadi.
6 Iye natsitsa kunsi
3 Angelo kwezani mafumu ku mipando yawo,
Nyimbo zanu zonse, Iye nakweza konko
M'mwambamo mumveke zoyamikazo; omwe afatsa nasauka.
Lemekezani
Mlungu Wakumwamba. 7 Iye amakhutitsa
12 AMBUYATHU YESU KRISTU- KUBADWA KWAKE
anjala ndi zabwino zake, Munakhala mwana kuno;
Ndi olemera onse Mnatifera mwaufulu.
nawaingitsa opanda kanthu. Inu nonse amithenga,
Inu mumtamande Iye;
8 Monga anapangana Anthu onse ali pansi
ponena kwa makolo athu, Adze akondane naye.
Ali kithandizadi Zoonazi amithenga
lero anake a Yakobo. Anaimba m'mlengalenga.

9 Poti akumbukira
27
atate wathu Abrahamu; 1 Mbuye ngwodalitsika,
Inde chifundo chokha Mulungu wa Israyeli ndiye,
akuchitira ana ake. Poti anayang'ana
Nawawombola anthu ake,

26 2 Napulumutsa tonse
1 Amithenga a Mulungu mwapfuko la Davide mwana wake;
Anaimba nyimbo yomwe, Monga analankhula
Posonkhana m'mlengalenga, mwa aneneri ake, kuti
Natitu usiku womwe;
“Onse azilemekeza 3 Adzatipulumutsa
Mlungu Wakumwambamwamba; kudzanja la onse akutida,
Akhalebe ndi mtendere Ndipo adzachitira
Anthu ali ponseponse" akulu chifundo ndi chisoni.
Amithenga anaimba
Ndi usiku m'mlengalenga. 4 Ndiye akumbukira
pangano loyera lake lija,
2 Anamva abusa omwe Ndi chilumbiro chake
Anaweta nkhosa zawo, cha kwa atate Abrahamu.
Mthenga nati: "Musaope;
Mumve ndikufotokoza: 5 Choti timtumikire
Wabadwa usiku uno osawaopa 'dani athu,
Yesu Kristu Ambuyathu Ndi kuyeranso mtima
Ndiye Mpulumutsi wathu; mwa chilungamo nsiku zonse.
Anabadwa m'Betlehemu"
Amithenga anaimba 6 Mwana, adzakuyesa
Ndi usiku m'mlengalenga. mnneneritu wa Wamkulukulu;
Ndiwe udzakonzera
3 Yesu ndinu Mbuye wathu, njira ya Mbuye Wakumwamba.
Munasiya za Kumwamba!
AMBUYATHU YESU KRISTU- CHITSANZO CHAKE 13
7 Udzadziwitsa anthu "Tsata Ine mkristu iwe."
za Mpulumutsi wawo yemwe
Awakhululukira 2 Kale ophunzira ake
nafafaniza tchimo lawo. Namvanso kunyanja kwawo,
Zinthu zonse anasiya
8 Poti Mulungu wathu Kukatsata Mbuye wawo.
ali ndi mtima wachifundo,
Ndiye kumwamba komwe 3 Yesu aitana ife:
ationetsa mbandakucha. Tikakonda chuma chokha,
Ati yesu: "Mwana wanga,
9 Powalitsira omwe undikondetu koposa."
ali mumdima ndi muimfa
Ndi potilunjikitsa 4 Mwachimwemwe, mwachisoni,
tonse munjira yamtendere. Pogwiritsa ntchito zonse,
Aitana Mpulumutsi
Kuti tizimkonda tonse.
28
1 Ambuye tsopano lino, 5 Yesu aitana ife;
monga mwa mawu anu aja, Mbuye, mutimvetse ndithu,
Lolani kapolo wanu Tipereke mtima wathu,
ndikachokere mumtendere; Tikondane lero ndithu.

2 Chifukwa chipulumutso 30
chanu mwandionetsa zedi, 1 Ife timakufunani
Chimene munachikonza Inu wotonthoza mtima.
akachione anthu onse. Yesu nyimbo zathu zonse
Ziyamika Inu nokha.
3 Ndi nyali yakuwalitsa Munasiya zonse m'Mwamba,
omwe sadziwa mawu anu; Kudzakhala pansi pano
Ndiwo ulemerero Kuwombola akapolo,
wa Israyeli mpingo wanu. Kumasula anthu anu.
AMBUYATHU YESU KRISTU- 2 Yesu, ndi chifundo chanu
CHITSANZO CHAKE Chachikulu munadzera
Ife anthu osauka,
29 Tsoka lathu mnachotsera.
1 M'kati mwa zobvuta zathu Mwazi ndi misozi yanu
Yesu aitana ife, Munakhetsa m'munda muja,
Tsiku lonse amanena: Kukonzera ife njira
14 AMBUYATHU YESU KRISTU- CHITSANZO CHAKE
Yonkako Kumwamba kuja. Mutsogoledwe nawonso
Kwanu Kumwamba komweko.
3 Yesu munalaswa m'mtima,
Ndi zonyoza munafoka, 5 "Senzani mtanda wanuwo."
Mnasenzera anthu mkwiyo Tsatani Yesu m'njiramu;
Wa Atate, Inu nokha. Iye wakusalemayo
Chikho chija ndi choopsa Ndiye alandiridwadi.
Munamwacho m'phiri lija
M'mene munalola mtanda, AMBUYATHU YESU KRISTU-
E! chifundo chanu chija. KUFERA KWAKE

4 Yesu ndinu moyo wathu,


Chuma chathu choposetsa.
32
E! tikondwerera mtanda, 1 Munthu Wazisoniyo
Apo moyo munapatsa. Timtcha dzina lakelo,
Mbuye tikondana nanu, Mpulumutsi linanso;
Yesu Mbuye Mwini zonse; Aleluya, ndiye Yesu.
Ndi mitima ndi milomo,
Tikuyamikani tonse. 2 Anapeputsidwako,
Nandifera m'mtandamo,
Anandiwombolayo;
31 Aleluya, ndiye Yesu.
1 "Senzani mtanda wanuwu."
Atero Yesu Mbuyathu; 3 Ife tinachimwadi,
"Mukanditsata Inetu, Iye sanachimwa 'yi,
Mudzikanize nokhanu." Anachotsa tchimoli,
Aleluya, ndiye Yesu.
2 "Sezani mtanda wanuwu."
Musaopsedwe nawotu; 4 Anapachikidwatu,
Mphamvu za Yesu nzanunso; Natha ntchito yake myu!
Limbani mtima wanuwo. Anakwera m'Mwamba duu!
Aleluya, ndiye Yesu.
3 Senzani mtanda wanuwu."
Bwanji manyazi mumva 'nu? 5 Adzabwera Iyenso
Yesu anapiriratu, Kudzatenga akewo;
Kuti mupulumuketu. Nyimbo tidzaimbanso,
Aleluya, ndiye Yesu.
4 "Senzani mtanda wanuwu."
Nawo muyende chetetu,
AMBUYATHU YESU KRISTU- KUFERA KWAKE 15
33 Lachiza nalo nthendazo,
1 Unakhetsedwa mwazi do! Papyola msomaliwo.
Wa Yesu Mfumuyo,
Poweramira mutuwo 3 Mapazi ake namvatu
Pamtanda pakepo. Zowawa zopambanazo,
Napachikidwa kaamba ka
Ambuye mthandize inetu Zoipa zathu zonsezi.
Kukonda Inudi,
Ndi kuli mpando wanuwo 4 Ambuye tikondweratu
Ndifuna kudzako. Kupulumutsa kwanuko;
Satana tisammvere 'yi,
2 Zochimwa zanga zonsezo Komabe Mpulumutsiyo.
Anaziferadi,
Chikondi chake chonsecho 35
Sindingadziwe 'yi. 1 Tiyeni, dzalireni nane,
Tidze ku mtanda wa Ambuye,
3 Linadetsedwa dzuwa bii! Tonse tichitetu maliro;
Pakufa Iyeyo, Wapachikidwa Ambuyathu.
Pakumwalira indedi
Wakundilengayo. 2 Kodi misozi itisowa,
Poona anthu amanyoza?
4 Pokumbukira mtandawo Onani umo apirira;
Wa Mpulumutsiyu, Wapachikidwa Ambuyathu.
Ndiphimba nkhope yangayi,
Ndi nsoni n'chitatu. 3 Anena mawu m'mtanda momwe,
Mawu ochepa achifundo,
5 Zofuna zanga zonsezo Apempherera 'dani ake;
Za mtima wangawu Wapachikidwa Ambuyathu.
Ndizipereka kwa Inu,
Mundiweruzetu. 4 Mtima wangawe, uyenera
Kuduka ndi manyazi lero,
34 Zamlasa ndi zoipa zako;
1 Ku Mzinda wakuyerawo Wapachikidwa Ambuyathu.
Wapachikidwa Mbuyeyo,
Nasautsidwa Mbuyeyo, 5 Ona chikondi cha Mulungu,
Akatipulumutse 'fe. Ona zoipazo za anthu,
Koma chakula ndi chikondi;
2 Padzanja lachifundolo Wapachikidwa Ambuyathu.
Linapenyetsa 'khunguwo,
16 AMBUYATHU YESU KRISTU- KUFERA KWAKE
Chisoni m'mtimamo,
36 Mpweteko wonse wathuwo
1 Pamtandapo Ambuyeyo Wa dziko lonseli.
anafera ifetu,
Nakhetsa mwazi wakewo 4 Pamutu minga kwe!
Kutiwombola tonsefe. Pamoyo wakewo
Zoipa zathu zonsezo
Pamtandapo, pamtandapo Zinaikidwapo.
Ambuye wanga 'nafatu;
Pamtandapo, pamtandapo 5 Andiferatu 'Ye,
Anandiwombolerapo. Afera inedi;
Athetsa nsembe zonsezi
2 Kwa munthu wasokerayo Ambuye Nsembeyi.
Kudziko lakutaliko,
Atero Yesu: "Bweratu 6 Pakugomedwapo
Ukhale nawo moyowo." Pa mlandu wangawo,
Ndidzaitana Mbuyeyo
3 E! Yesu Mbuye wangadi, Andilanditsepo.
Ndipatsa Inu mtimawu;
Ndithandizeni inedi
Ndisalekane nanu 'yi. 38
1 A! Mutu wakuyera,
4 Zochimwa zanga zonsezo Wolaswa wachisoni,
Wandichotsera mwaziwo; Abveka Inu anthu
Mumtima mwanga muli mbee! Ndi minga ya udani;
Mwayeretsedwa indetu. Ambuye mwafokatu
Ndi masauko aja,
37 Mwatuwa m'maso mwanu,
Mumayerera kale.
1 Zathedwa zonsetu
Za moyo wakewo,
2 Ambuye Mwini moyo,
Ambuye anatsikayo
Kokoma mnafumako;
Nafika pansipa.
Ndizizwa pomva mawu
Umo mwachitiramo.
2 Zintchito zakezi
Chisoni chija chanu
Zofunika 'Tatewo
Mcha pamachimo anga,
Anatsiriza zonsedi,
Mwasaukira Inu
Sanazisiya 'yi.
Kupalamula kwanga.
3 Pa Iye padzapo
3 Nditani Bwenzi langa
AMBUYATHU YESU KRISTU- KUDZUKANSO KWAKE 17
Kulemekeza Inu AMBUYATHU YESU KRISTU-
Chifukwa cha chifundo KUDZUKANSO KWAKE
Ndi imfa ija yanu?
Mundikhalitse wanu,
40
Wokhulupira Inu; 1 Lero Kristu anauka, Aleluya,
Musandilole konse Ndilo tsiku lokondwera, Aleluya,
Kufulatira Inu. Iye kale anafera, Aleluya
Nawombola otaika. Aleluya.
4 Pakufa ine Mbuye
Mukhaletu pafupi, 2 Timwimbire zomtamanda, Aleluya
Mundithandize ine, Ndiye Kristu wa Kumwamba, Aleluya
E, mudzandimasula; 'Natsikirako kumanda Aleluya
Ndipenyetsetsa Yesu, Nalanditsa akuipa, Aleluya.
Ambuye Mfumu yanga,
Ndikafa ndine wanu, 3 Koma masauko ake Aleluya
Ndikhale nanu m'Mwamba. Anatiwombola ife, Aleluya
Ndiye Mfumu ya mafumu, Aleluya
Mwana ndithu wa Mulungu, Aleluya
39
1 Pokumbukira mtandawo 4 Timwimbire Mlungu wathu, Aleluya
Ambuye 'nandiferapo, Kuti atikonda ndithu; Aleluya
Ndiyesa zingochepazo Mtamenso angelo inu, Aleluya
Ndinazitama kalelo. Ndiye 'Tate, Mwana, Mzimu. Aleluya.

2 Mndiletse, ndisateme 'yi


Zachabe, koma imfayo;
41
Zijazo ndinakondazo 1 Nla Mlungu dzuwali;
Ndazilekera mwaziwo. Pa m'banda kuchapo
Angelo 'nadzatu
3 Onani m'mutu, m'manjanso Nachotsa mwalawo.
Mudzera nsoni m'mwazimo.
A! panalibe kalelo Ndi mtima wonse mwimbedi
Wondibvalira mingayo. Wauka Mbuye leroli.

4 Chinkana dziko lonselo 2 Alonda onsewo


Lichepa ndithu mtulowo, 'Nagwidwa manthadi
Chikondicho chagwirabe Poona zo'psyazo
Mtimanga, moyo, ndense 'ne. Zoonekerazi.

3 Mulibe m'mandamu,
18 AMBUYATHU YESU KRISTU- KUDZUKANSO KWAKE
Wadzuka Mbuyetu; Tsono ndi mtima wonse tiimba;
Woposa imfayo Aleluya!
Ndi Mwini moyowu.
AMBUYATHU YESU KRISTU-
4 Dzukani nayetu, ULEMERERO WAKE
Oyera inunso,
Lekani m'mandamo 43
Zakufa zanuzo. 1 Kondwerani dzuwa lino Aleluya,
Yesu wanka m'Mwamba momwe;
5 Titama Yesuyo, ……… Aleluya,
Ambuye m'Mwambamo Wachokera mdzik'o lino, Aleluya.
Wofera anthu 'Ye, Wabwerera kwawo komwe.Aleluya.
Timkondakondako.
2 Zomkweza zili m'Mwamba,Aleluya,
42 Zodikira Mbuye wathu; Aleluya,
1 Aleluya, Aleluya, Aleluya! Mlowetseni n'kumlambira, Aleluya,
Nkhondoyo yatha, imfa yagonja, Mfumu yathu yaulemu. Aleluya.
Yesu wamoyo anaiposa,
3 Yesu nkana saoneka, Aleluya,
Msampha woipa wonse nawonja,
Atipempherera komwe; Aleluya,
Aleluya!
M'nyumba yake yokonzeka Aleluya,
Atilinda ife tomwe, Aleluya.
2 Mphamvu za imfa ndi za Satana
Naye Ambuye zinalimbana, 4 Tiyamike Dzina lake, Aleluya,
Komatu Yesu anapambana. Mfumu ya ulemu wonse, Aleluya,
Aleluya! Tibukitse mbiri yake Aleluya,
Pansipa padziko lonse. Aleluya.
3 Atha masiku aja ansoni,
Mbuye wauka, ali ndi mboni;
Lero chimwemwe chatha chisoni, 44
Aleluya! 1 Lambira Mfumuyo,
Ndi Yesu Mbuyathu,
4 Nsinga za imfa Iye 'nadula, Tamvani nyimbo za 'mithenga a
Khomo la m'Mwamba nalitsegula; ...Kumwambako;
Yesu timtama tonse tipfuula, Nafenso pansipa
Aleluya! Timyamike 'Yo,
Ndi Mpulumutsi wathu wotifera
5 Mbuye mabala anu olimba ...kalelo.
Atichotsera mantha a imfa;
2 Lambira Yesuyo
AMBUYATHU YESU KRISTU- ULEMERELO WAKE 19
Wokonda tonsefe; Akhumbira mtima wako
Mabala ake achikondi aonekabe; Akondadi!
Tisaiwale 'yi Mwazi wake ngwowombola,
Zowawa zakezo, M'chipululu wakufuna,
Tileke kumchimwira, kumsautsa M'khola mwake akusunga,
...Yesuyo. Akondadi!

3 Lambira Yesuyo, 3 Ukafuna kumdziwitsa,


Uthenga wakewu Akondadi!
Uyanjanitsa anthu onse m'dziko Uzimpatsa moyo wako,
...munomu; Akondadi!
Amaiwala za Kodi umachita mantha?
Kudana kwawoko, Pena umadera nkhawa?
Nayamikira Mfumu yamtendere Yesu amasangalatsa
...monsemo. Akondadi!

4 Lambira Mfumuyo 4 Bwenzi ndiye wakufera,


Wolenga zonsezi: Akondadi!
Nyenyezi, dziko, dzuwa, mwezi ndi Nthawi zonse sakusiya,
...mitamboyi; Akondadi!
Tikweze dzinalo Anthu ena akunyenga,
La Mbuye Yesuyo, Yesu sadzanyenga iwe,
Timyamikire pansi pano ndi Zakubvuta adzachotsa,
...Kumwambako. Akondadi!

AMBUYATHU YESU KRISTU- 5 Akhululukira iwe,


KUTHANDIZA KWAKE Akondadi!
Nadzainga mdani wako,
45 Akondadi!
1 Yesu wakukoma mtima, Adzakudalitsa iwe,
Akondadi! Nadzaletsa tsoka lonse,
Wakuposa m'bale ndiye, Nadzakutsogoza kwawo,
Akondadi! Akondadi!
Wina asautsa iwe,
Pena adzasiya iwe,
Yesu sadzanyenga iwe, 46
Akondadi! 1 Msandipitire, Yesu,
Mundimvere ine;
2 Kumdziwitsa ndiko moyo, Mulikudalitsa ena,
Akondadi! Msandipitirire.
20 AMBUYATHU YESU KRISTU- KUTHANDIZA KWAKE
Yesu Mbuye, 3 Ndikakhumudwa
Khutu munditchere Andilimbitsa;
M'mene muitana ena Ndikadzitama
Msandipitirire. Andichepetsa;
Ndikasokera;
2 Ndigwadira Inu, Yesu, Andilondola;
Musandikanize; E! Wokondedwa
Ndikalapatu machimo Yesu Ambuye.
Mbuye, mndithandize.
4 Ndimachitira
3 Nkhope yanu ndifunitsa, Inu umboni;
Sind'yenera konse; Ndikukuzani
M'mtima mwanga muchiritse Moyamikira;
Nthenda zanga zonse. Mphamvu ndi nzeru,
Moyo, zonsezi,
4 Yesu, ndinutu chitsime Si zanga, nzanu,
Cha chimwemwe chokha; Yesu Ambuye.
Sindifuna wina konse,
Koma Inu nokha.
48
1 Mbuye, mutsaganetu
47 Nane ndingachimwenso;
1 Idza wolema, Nanu ndisungidwedi,
Akupumitsa; Mwa chikondi chanucho.
Womva chisoni,
Akutonthoza; Mbuye Yesu,
Mlendo, limbika, Mundiperekeze inetu!
Mphamvu apatsa Ndine mlendo, Mbuye 'Nu,
Amatisunga, Mutsagane nanetu.
Yesu Ambuye.
2 Inu mundibisadi
2 Ndiye mtsamiro Mmene ndabvutidwamo,
Pogona ine; Ngati muli ndinedi
Pofika kufa Bwino ndidzakhalamo.
Andidzutsanso;
Podzichepetsa 3 Mbuye, mutsaganebe
Andikwezanso; Mpaka moyo watha zi!
Moyo wa moyo, Kwanu mindifitseko,
Yesu Ambuye. Komwe nsoni zathadi.
AMBUYATHU YESU KRISTU- KUTHANDIZA KWAKE 21
2 Popachikidwa pa Golgotapo
49 Yesu anandiwombola ine,
1 E, moyo wanga'we Etu, ndizizwa! Nakondetsadi
Utsitsimuketu; Nafera inetu.
Ambuye Yesuyo Nafera inetu, nafera inetu,
Akhala m'Mwambamo, Etu, ndizizwa! Nakondetsadi
Pampandopo Nafera inetu.
Akhalabe, natchula dzina langali.
3 M'busa wokoma ndi Mbuyangayo,
2 Kwa Mulungu m'Mwambamo Nandiitana posokerapo,
Amapempherako; Konse koipa nalondolako
Chikondi chakenso Kubweza inetu.
Chikhala chosatha; Kubweza inetu, kubweza inetu,
Ndi mwaziwo Konse koipa nalondolako
Akhalatu Wansembe wanga Yesuyo. Kubweza inetu.
3 Mabala ajawo 4 Uko Kumwambako Mbuyangayo
A m'thupi mwakemo Andikonzera mokhaliramo;
Amukumbutsanso Tsiku linalo adzabweranso
Za ine pansipa; Kutenga inetu.
Zoipazo
Achotsadi kotero sindingafe 'yi Kutenga inetu, kutenga inetu,
. Tsiku linalo adzabweranso
4 Mulungu ali wokhulula mtimatu, Kutenga inetu.
Ndilibe mantha 'yi,
Andisungiradi; AMBUYATHU YESU KRISTU-
Ndibwera kwa KUBWERANSO KWAKE
Atatewo, titayanjana leroli. 51
1 Alinkudza wansoni Munthu
50 Wakukhala Kumwamba,
Alinkudza m'ulemerero
1 M'khola mwa ng'ombe ku
Ndi Mwamuna wa mtanda.
....Betelehemu
Anabadwamo Ambuyangayo;
Aleluya, aleluya,
Etu, ndizizwa! Natsikirako,
Alinkudza kwa ife;
Kufuna inetu. Ndi chimwemwe tidzamkomana
Kufuna inetu, kufuna inetu, Pakufika Ambuye.
Etu ndizizwa! Natsikirako
Kufuna inetu. 2 Alinkudza Ambuye Yesu
Wakuphedwa padziko,
22 AMBUYATHU YESU KRISTU- KUBWERANSO KWAKE
Alinkudza kukhala Mfumu Mawu awa achimwemwe
Yoweruza maiko. Azimveka m'dziko lonse.
Adzabwera, adzabwera;
3 Pakufika asonkhanitsa E! bwerani Mbuye wathu.
Anthu ake oyera;
Adzafuna m'mitundu yonse 2 Dziko lino linaona
Omwe Iye 'nafera. Masauko a Mbuyathu,
Lidzaonanso ulemu,
M'mene adzabwera Iye.
52 Adzabwera, adzabwera;
1 Pakwitana Mbuye wanga Tibvomera, E! mubwere.
Potsiriza dzikoli,
Pakufika tsiku lakuwalalo 3 Anthu anu amafoka,
Posonkhana akumvera, Pa ulendo nasokera;
Pakuona Yesuyo, Ha! Adzaonana nanu
Ndidzakondwerera naye komweko. Atabvalanso zoyera.
Mudzabwera, mudzabwera;
Pakwitana Mbuye wanga, Inde, Mbuyetu mubwere.
Pakwitana Mbuye wanga,
Pakwitana Mbuye wanga, 4 Ndi chiyembekezo ichi
Ndidzakondwerera naye komweko. Sitikhala chete ife;
Tiimbitsa nyimbo zathu
2 Potuluka m'manda mwawo Zakulemekeza Mlungu.
Anthu ake onsewo, Adzabwera, adzabwera;
Tidzasanganatu nawo nthawiyo, E! mubwere msanga Yesu.
Pakuuka osankhidwa,
Kunka naye Yesuyo,
Ndidzakondwerera naye komweko. 54
1 Yang'anani anthu onse,
3 Tisaleke kugwirabe Yesu Mbuye wathuyo;
Ntchito ya Mulunguyo, Alinkudza ndi ulemu,
Tibukitse mbiri yake m'dzikoli, Kuoneka m'Mwambamo.
Ndi podzatha moyo wathu
Ndi zintchito zathuzo, Anthu onse amlambire
Tidzakondwerera naye komweko. Yesu Mwana wa Mulungu;
Alinkudza ndi ulemu
Wopambana, indetu.'
53
1 Mbuye Yesu adzabwera, 2 Adzatenga anthu ake
Asekere anthu onse; Akummvera pansipo,
AMBUYATHU YESU KRISTU- KUBWERANSO KWAKE 23
Iwo adzakhala naye Kwa Mulungu 'Tatewo.
M'dziko la Kumwambako.
7 Adzabwera,
3 Koma anthu onse omwe Adzabwera Iyeyo
Anamnyoza pansipo, Tsiku lomalizalo.
Nthawi Yesu alinkudza
Adzaopa m'mtimamo. 8 Aleluya,
Aleluya Yesuyo,
4 Ife tonse tikumbuke Tizitama dzinalo.
Mawu ake onsewo;
Timuyang'anire Iye,
Yesu Mbuye wathuyo.
56
1 Idzani nose 'nu
Okonda Yesuyo;
AMBUYATHU YESU KRISTU- Libuke Dzinalo,
KUMYAMIKIRA Timtame konseko.
Uzani onse m'Mwambamo,
55 Uzani onse pansipa,
1 A Mulungu Wafera Iye anthuwo.
Munatuma Yesuyo,
Mwana wanu yekhayo. 2 Waleka koronayo,
Nasiya 'Tatewo,
2 Anabadwa, Natsika m'Mwambamo,
Anabadwa motere, Nalira, nafatu.
Monga mphawi m'kholamo Zowawa zake zonsezi
Nazimva, zinaposatu
3 Anakonda, Kuti tipulumukedi.
Anakonda anthuwo
Nawapulumutsanso. 3 Nadzuka m'mandamo
Moopsya m'mdimamo,
4 Anafera Nigonja imfayo
Anafera m'mtandamo, Ndi mdani waketu;
Anafera ifenso. Nakweradi Kumwambako,
Nakhala Mfumu monsemo,
5 Anadzuka, Ambuye wathu Mlunguyo.
Anadzuka m'mandamo,
Anatenga moyowo. 4 Adzadza indetu
Kudziko linoli;
6 Anakwera, Tidzanka nayeyu
Anakwera m'Mwambamo M'ufumu wakedi.
24 AMBUYATHU YESU KRISTU- KUMYAMIKIRA
Momwemo tidzampenya 'Ye, Inde, ndilira m'mtimamo
Momwemo tidzakhala 'fe, Chipulumutso chakecho.
Nkuwala kwake koti mbee!
2 Zina za Yesu ndimvetu,
Kuti ndichite zakezo;
57 Mzimu Woyera, mudzetu,
1 Yesu, dzina lakukonda, Ndiphunzitseni zonsezo.
Lopambana onse ena,
Tonse tidzaligwadira 3 M'mawu a Yesu Mbuyeyo,
Ndi mitima yochepetsa. Inde, acheza nanemo;
Liu ndimamva m'Bukumo
2 Yesu, dzina lokondwetsa Ndilo la Yesu Mbuyeyo.
Akuipa a padziko,
Kale linatidziwitsa 4 Zina za Yesu m;Mwambamo,
Mpulumutsi ndiye Yesu. Ali pampando pakepo;
Udze Ufumu wakewo,
3 Yesu, dzina lakufatsa, Ndiyetu Mfumu ponsepo.
Anamutcha 'kali Mwana,
M'mene analowa kale
M'dziko lino lakudana. 59
1 Wina atikonda ife,
4 Yesu, dzina ndi lomweli Bwenzi lathu ndiyeyu;
La pa dziko lino lonse, Atifunafuna ife,
Ndi la mphamvu yolanditsa Inde, nthawi zonsetu.
Anthu mu masoka onse.
Chikondano chakechi
5 Yesu, dzina lakukonda Nchachikulukuludi.
La Mwanayo wa Mulungu,
Ife anthu osauka 2 Ndani mwa abale athu
Tithawira nalo kwanu. Akanatifera 'fe?
Koma Yesu m'malo mwathu
Anapachikidwatu.
58
1 Inde, ndifuna kumvatu 3 Anamnyoza pansi pano,
Za chikondano chakecho Bwenzi la ochimwawo;
Cha Yesu Mbuye wangayo, Muulemerero wake
Zomwe anamva kalelo. Alikonda Dzinali.
E! dzina la Yesu, 4 Timchimwira kopambana,
E! dzina la Yesu, Ndi kumusautsa 'Ye,
AMBUYATHU YESU KRISTU- KUMYAMIKIRA 25
Koma Bwenzi lathu Yesu
Atikondakondabe
61
. 1.Konda dzinalo la Yesu
5 Mtiphunzitse, Mbuye Yesu, ... Mwana wosauka 'we;
Tikondane nanutu; ... Ndilo lothandiza anthu;
Tisaiwalire konse ... Khala nalo ponse phee!
Bwenzi lathu ndinutu.
Dzina la Yesuyo
Nlokondwetsa onsewo,
60 M'mwambamo ponsepo
1 Nditama Mlungu m'mtimamo, Litonthoza m'mtimamo.
Wakundifera pansipo,
Nafafaniza tchimolo, 2. .Konda dzinalo la Yesu
Nanditengera dipolo. ...M'moyo mwako monsemo;
...M'mene ulikuyesedwa,
Wandiwombola inetu ..Tchula Dzina lakelo.
Pokhetsa mwazi wakewo;
Timlemekeza Iyetu 3. ..Dzina ili ndi lokoma
Wotilipirira dipolo. ... La Mtetezi wathuyo;
... M'mene adzatilandira
2 Ndinasokera
. kalelo, ... M'mwamba, tidzakondwadi.
..Ndamkana
. Iye Yesuyo,
Koma ndiimba leroli: 4 ... Mbuye Yesu timtamanda
... Wandiwombola inedi ...Ndi zinyimbo zathuzo;
... Mfumu ya mafumu onse
3. Mtima ndimakondweramo, ...Yesu timayesadi.
... Popenyetsetsa Yesuyo
... Pamtanda pake pomwepo,
.. . Pakundifera inenso
62
1 Khamulo liliko
4.Sizitha ntchito zangazo, Kumwambako mbuu!
... Kundiyeretsa mtimamo, Pakukhala ndi Yesu
... Anandiyesa inetu Aimbirako:
... Wakulungama Yesuyo
"Kwa Iye atikonda
5. .Tsono mubwere inunso, Natsuka 'fe mbuu!
... Mtetetezi wanu ndiyedi E! kukhale ulemu
... Apulumutsa onsewo Kwa Mbuyathuyu.”
... Akumkhulupiriradi
26 MZIMU WOYERA
2 Onsewa 'nachimwa MZIMU WOYERA
Nadetsedwa bii, 64
Nthawi yino ayera
Naimbiradi: 1 Mubwere Mzimu Wakuyera,
Kuyatsa moto m'mtima mwathu;
3 Akhala mafumu Ntchito ndi yanu kudzozera
Kwa Mbuyathuyo, Ndi kutininkha mphatsozo.
Anawombola onse
Ndi mwaziwo pyu! 2 Kudzoza kwanu kutipatsa
Chimwemwe, moyo ndi mtendere;
4 Akadakhalabe Kuwala kwanu kupenyetsa
Osaukako A m'mdima ndi a m'ndendemo.
Ngati Yesu sakana-
wombolatuwo. 3 Mtima wodetsa mukonzere,
Chisomo chanu chakwanira;
5 Ndi nyimbo yabwino Adani athu muthawitse
Tidzamtamako, Ndi mphamvu yaikulu.
Kuti ena pakumva
Amwimbirenso: 4 Mutidziwitse 'Tate wathu,
Ndi Mwana wake ndinu Mmodzi;
Mnafuma kwa awiri onse,
63 Koma Mulungu Mmodziyo.
1 Tamani mphamvu ya Yesu,
Angelo agwade; 65
Tulutsanitu korona,
1 Mzimu Woyera, mudze mumitima
Mumbveke, mbveke, mbveke, ...mwathumo,
Mbveke, Mbuyeyo! Mufike nazo mphamvu zanu
...zazikuluzo.
2 Inu osankhidwa ake,
Owomboledwa 'nu, 2 Mufike monga nyali younika
Tamani Mpulumutsiyo, ...m'mtimamo,
Mutidziwitse zakuipa zakukhalamo.
3 Anthu ose ndi mitundu
Pa dziko linotu, 3 Mufike monga moto wakuotcha
Amlemekeze Mfumuyo, ...zomwezo.
Mutiyeretse ifetu m'mitima
4 Tifuna kuti komweko ...mwathumo.
Tikamgwadire 'Ye; 4 Mufike monga ngati njiwa
Tidzaimba kosaleka; ...yamtenderewo,
... MZIMU WOYERA 27
Kutitu anthu anu onse akondanetu. 67
1 Mpume pa inetu, Mpweya wa
5 Mufike monga ngati mphepo …Mulungu,
...yokokomayo, Ndi kundidzaza moyo wanuwo,
Tikhale tonse nazo mphamvu zanu Kuti ndikonde zomwe mukondanso,
...zonsezo. Ndichite chomwe mumachitanso.

66 2 Mpume pa inetu, Mpweya wa


1 Mzimu Woyera, mudzetu kwa ine, …Mulungu,
E, ngati mvula m'dziko lakuuma; Mpaka mtimanga ukayeretu,
Ndikhale munda wanu wakupatsa Ndipo zokhumba zanga zilingane
Zipatso zoyenera Mbuyeyo. Nazo zanuzo zakuyera mbuu!

2 M'phunzitsi, ndinu mudziwitse ine 3 Mpume pa inetu, Mpweya wa


Chikondi chanu chija chachikulu; …Mulungu,
Lembani mawu anu pamtimanga, Mpaka ndikhale wanu nokhatu;
Kuti ndikumbukire zanuzo. Ayeretsedwe makhalidwe anga
Ndi mphamvu yanu yondisunga nji!
3 Wosangalatsa, ine ndikalira
Muchotse nsoni, m'mtimamo 4 Mpume pa inetu, Mpweya wa
…mudikhe; …Mulungu,
Mundigoneke pachifuwa chake Kuti inedi ndisafe 'yitu,
Cha Yesu kuti ndikakondwepo. Koma ndikhale nanu m'moyo .
. womwe
4 Wotsogolera, munditsogolere Wangwiro ndi wa nthawi zonsetu.
Kuti n'kafike kwawo kwa Atate,
Nditsate Yesu ndikuyendayenda 68
M'njira yomweyo anapondamo. 1 Mubwere Mzimu Inu
Woyera wakufatsa,
5 Mthandizi ndinu, mndithangate ine Muchotse mdima m'mtima mwathu
Kupempha bwino izo zindisowa, Tikapenye m'maso.
Kupempha monga Mlungu amafuna,
Kulingalira zake zokhazo. 2 Mtisangalatse m'zonse,
Ndi wachifundo Inu,
6 Mzimu Woyera, n'dzipereka ndense, Tiyembekeze kumapazi
Mundichitire ntchito yaikulu; A Mbuyathu Yesu.
Mtima woyera ndi womvera mpatse,
Wodzala ndi chikondi chanucho. 3 Mtitsitsimutse ife
Kuchotsa nkhawa zathu,
28 MZIMU WOYERA
Muyatse moto wachikondi Ndikapumula pena
Mu mitima yathu. Mukhale ndithu ndine;
Zolingirira zanga
4 Mtitsutse titachimwa Ziyere zonse m'mtima;
Kutilapitsa m'mtima, Zoipa muzichotse,
Mwonetsenso chikondi Sindidzazichitanso.
.........chokhululukira tchimo.

5 Kutiyeretsa m'mtima 70
Ndi ntchito yanu yokha, 1 Mzimu Woyera, mudzetu
Kupatsa moyo watsopano Tiyeretsedwe m'mtimamu;
M'mene timafoka. Mupatse anthu anuwa
Mitulo yanu yonseyo.
6 Mukhale m'kati mwathu,
Mutichotsere mantha, 2 Kudzoza kwa Kumwambako
Tidzayamika 'Tate wathu, Kutitonthoza m'mtimamo,
Mwana wawo ndi 'Nu. Ndi kutidzutsa m'moyomu,
Tikhale okondanatu.

69 3 Pankhope pathu mthirepo


1 Idzani, Mzimu Inu, Chisomo chanu chijacho;
Mundidalitse kuno; Mtendere mutininkhebe,
Ndafoka mtima ine Mutiyendetse ponse phee!
Polendo wanga uno;
Kwambiri ndakhumudwa 4 Tionetseni tonsetu
Panjirayo ya moyo; Umodzi wanu monsemo,
Mkaleka kutsogola Atate, Mwana, Mzimu 'Nu
Ndiwonongeka pompo. Tiimbe nthawi zonsezo:

2 Wakunga mwana ine, … Titamire nthawi zonse


Sindidziwitsa konse; … 'Tate, Mwana, Mzimu, Nonse.
Mundilandize Mzimu; Amen.
Panjira yanga yonse;
Mundiyendetse bwino 71
Ndifike ine ndemwe 1 Mubwere kuno Mzimu 'Nu,
Panjira yolungama, Chitsime cha chikondicho;
Kudziko lachimwemwe. Mudziwa ndimaliratu,
Mukhale m'mtima mwangamo,
3 Mundilimbitse m'mtima Ndipatsa inu mtimawu,
Pogwira ntchito izi; Masiku onse mkhalemu.
MZIMU WOYERA 29
2 Mukonze mtima wangawu, 5 Kudzirala ndi kufatsa,
Muyere ndithu m'katimo; Inde, zonse muzikonda,
Ndilinda tere, Mzimu 'Nu, Mndiphunzitse pondipatsa
Mupatsetu chikondicho; Mzimu wanu Woyerawo.
Lichepa dontho lokhali,
Ndipempha mundidzazedi. MAWU A MULUNGU

3 Ndilira Mzimu leroli, 73


Mutsimikize Mawuwo; 1 Mbuye, Mawu anu
Ya Mbuye Yesu mphamvuyi, Atikondweretsa,
Ikhale yathu, yanganso; Atitsogolera,
Mulowe m'mtima, mdzazetu Salephera konse.
Ndi mphamvu nzeru, moyowu.
2 Poyensedwa ife
Atipambanitsa,
Natonthoza mtima
72 Natipulumutsa.
1 Mbuye wondipulumutsa
Mulandire mtima wanga, 3 Tikaona bvuto,
Mwandipatsa Mzimu wanu Tikalowa m'mdima,
Womeretsa zopatsomo. Kuunika kwake
Kusonyeza njira.
……Ndiye Mzimu Wakuyera
……Atipatsa ife makhalidwe 4 Atisangalatsa,
……Wofanana naye Yesu, Atilemeretsa
……Anatsika Kumwambako. Powerenga mommo
Nawo mtima wonse.
2 Naye Mzimu mndiphunzitse
Kukondwera nsiku zonse 5 Ndiwo alimbitsa
Ndi kukhala ndi mtendere Omwe akufooka,
Osaderatu nkhawa 'yi. Nawapatsa moyo
3 Mndithandize kukondana Akafuna kufa.
Ndikuthangatira onse, 6 Mbuye, mtiphunzitse
Ndi kukhululukirabe Nzeru zake zonse,
Akundichimwirawo. Tikayenderane
N'tiyanjane nanu.
4 Mndilimbitse ndipirire
Osadandaula konse,
Ndi kulamulira thupi
Ndi zofuna zakezo.
30 MAWU A MULUNGU
74 75
1 Cholimbitsa mtima ndi 1 Mundinyemere 'ne
Chonditsogolera Mkate wamoyo
M'njira ya Mulunguyo; Monga kunyanja kuja kalelo;
Ine ndili nacho. Ndipyola Mawuwo,
Ndifuna Inu,
M'Bukuli ine ndi Ndikhumba Inu mwini moyowo.
Onse owerenga
Mawu a Mulunguwo, 2 Mkate wamoyowo
Timapeza moyo. Ndinu Ambuye;
Mawu oyera anu n'khumbanso
2 Dzinthu zakumundazo Mun'dyetse omwewo
Zilimbitsa thupi; Ndikhale moyo,
Zolembedwa m'Bukumo Ndikonde zakuona zanuzo.
Zimadyetsa mtima.
3 Mtume tsopanoli
3 Ndikachimwa, Bukuli Mzimu Woyera,
Lindiyambotsutsa; Kuti andikonzere m'masomo;
Limanditonthoza ndi Abvumbulutse zinsinsi za m'Mawu,
Mawu a mtendere. Kuti ndionemo Ambuyeyo.
4 Pakudera nkhawa 'ne, 4 Mndidalitsere 'ne
Pakuchita mantha, Mawu amoyo,
N'kawerenga m'Bukuli Monga munadalitsa mkatewo;
Lindipatsa mphamvu. Ndikhale mfuludi,
Wosamangika,
5 Lindionetsera 'ne, Mukhale moyo wanga wonsewo.
Chifuniro chake
Cha Mbuyanga Yesuyo,
Ndikamvere bwino. UTHENGA WABWINO
76
6 Zonse mwazilembamo,
1 Mbiri yakalelomwe
Mzimu Wakuyera,
Mundisimbiretu
Kuzimvera zonsezo
Ya Yesu Mbuye yemwe
Mundithangatire.
Anandiferatu.
7 M'Buku lakuyerali
2 Simbani bwinobwino-
Powerenga ife,
Ndilibe nzeru 'yi-
Mbuye mutipatsemo
Ndimve tsopano lino
Moyo, moyo, moyo.
Mbiri ya moyowo.
UTHENGA WABWINO 31
2 Simbani bwinobwino- 77
Ndilibe nzeru 'yi-
1 Kodi ulikulemedwa
Ndimve tsopano lino
Ndi zoipazo?
Mbiri ya moyowo.
Idza kuno, ati Yesu,
Pumako.
Mbiri yakalelomwe,
Mbiri yakalelomwe,
2 Ndikamzindikira ninji
Mbiri yakalelomwe,
Mbuye wangayo?
Mundisimbiretu.
Ali ndi mabala m'manja
Mwakemo.
3 Mawu amveke bwino,
Alowe m'mtimamo,
3 Kodi ali ndi chilemba
Ndizindikire tsono
M'mphumi mwakemo?
Chipulumutsocho.
E, chilembacho chaminga
Chilimo.
4 Simbani mobwereza,
Ndisaiwale 'yi,
4 Ndikampeza, ndikamtsata
Koma ndisunge bwino
Ninji pansipa?
Mumtima Mbiriyi.
Masauko ndi misozi
Zilipo.
5 Simbani Mbiri yonse
Ya Mbuye wangayo;
5 Ndikamfunafuna Iye,
Zochimwa zanga ndizo
Ndipezenjiko?
Zinapha Yesuyo.
Kumaliza kwa chisoni
Chonsecho.
6 Simbanitu mwachete
Mbiri ya Yesuyi,
6 Ndikampempha anditenge,
Pakubvitidwa ine
Akataniko?
Inditonthozepo.
Ati Yesu, "Idza msanga,
Idzatu."
7 Simbani Mbiri yomwe,
Ndikhulupiredi,
Kuti pakuyesedwa 78
Ndipulumukepo.
1 Musawalole mawuwo
Apite ngati mphepozi,
8 Inde, pakufa panga
Musaumitse mtimatu,
M'maso mukhale mbee!
Polira Yesu Mbuyedi.
Mbiri ya Mbuye wanga
Mundisimbiredi.
32 UTHENGA WABWINO
Idzanitu, idzanitu, Bweratu kwa Mbuyeyo.
Idzani kwa Ambuye,
Idzanitu, idzanitu 4 Bvumbulutsa zonse zako
Apulumutse inunso. Zobisika m'mtimamo;
Ayeretse moyo wako
2 Musachitenso nthantha 'yi, Nawo mwazi wakewo.
Mufulumire inutu;
Tsiku labwino nleroli, 80
Mulandirenso moyowu. 1 Mipingo iyo idzatu,
Yoyenda mangu pajapo,
3 Zokandweretsa m'dzikomu Afuma kuti anthuwo?
Nzosakhutitsa m'mtimamo; Afika bwanji komweko?
Koma za Yesu zonsezo
Zikwaniritsa inudi. Anena anthu onsewo,
"Yesu Sing'anga apitapo."
4 Sakukanani Yesudi, Anena anthu onsewo,
E, mukalapa m'mtimamo; "Yesu Sing'anga apitapo."
Lolani kuti Mzimuyo
Agwire ntchito zakezo. 2 Azizwa anthu ajawo,
Nafunsa, "Ndani mlendoyo?
79 Wanzeru monga Iyeyo
1 Pakupempha ife pano, Kulibe wina konseko."
Pakwitana 'Tatewo,
Pakudziwa tsoka lako, 3 Ndi Yesu yemwe kalelo
Bweratu kwa Mbuyeyo. 'Nakhala munthu pansipa;
Anthenda onse nthawiyo
Idzatu, idzatu Nachira yake mphamvuyo.
Kwa Mbuyathu Yesudi,
Idzatu, idzatu, 4. Afika Yesu leroli,
Iwe bwera leroli. ...Chifundo m'mtima mwakemo,
...Timfitse msanga kwathuko,
2 Unachimwachimwa ndithu, ``Akhale nafe ponsepo.
Wasokera m'talimo;
Unachedweranji kudza 5 Timsankhe Yesu Mbuyeyo,
pakulinda Yesuyo? Timyese Mfumu yathuyo,
Chifukwa tikamkanatu
3 M'dziko lino pansi pano Tikhala otayikawo.
Sungapeze kanthumo
Kokwanitsa mtima wako;
UTHENGA WABWINO 33
Tsopano inu 'dzanitu, Zoipa zazikulu
Asanapitirirepo. Azigonjetsa 'Ye;
Tsopano inu 'dzanitu, Anena mawu ake
Asanapitirirepo. Ochotsa zonsezo,
Kalelo nalamula;
81 Pakhale bata duu!
1 Ukapenya kwa Yesu uliko moyoko,
Inde, moyo tsopanopanutu; 2 M'ulemerero mwake
Wolakwira upenye kwa Yesu .. .. Anenanenabe;
.. .Mbuyeyo, Munkhondo apambana
Kuwombola naferatu 'we. Ndi mawu akewo.
Akristu akondwera
... ...Ona! Ona! Onatu! Poona mphamvuyo
... ...Kuli moyo kwa yense apenya.. Ya Mbuye wathu Yesu
..... .Yesuyo Wotiwombolayo.
Wakuferatu pamtandapo.
3 Zobvala zake zonse
2 Anasenza pa bwanji uchimo .. Nza mwazi woti pyu!
...wonsewo, Pamphumi pake pomwe
Ngati wanu pa Yesu sulipo? Korona waketu.
Bwanji mwazi wakhetsa kutsuka.. Unyolo wa Satana
...ifetu, Umasulidwako;
Ngati uwu sitikwanako? Kumwamba amithenga
Atama Mbuyeyo.
3 Zilepheradi zonse kugula moyowo,
Koma mwazi wa Yesu Mbuyeyo. 4 M'kufatsa kwake komwe
Khulupira mwa mphamvu ya .. Anena nafenso,
...Mlungu wathuyi Tonsefe omangidwa
Kuyeretsa 'we m'mtimakomo! Ndi zakuipazi;
Ambuye amanena
4 Anathera pamtanda zintchito zonsezi Zotichenjezazi:
Zowombola mizimu yathuyi; Ananu, msiye zonse,
Ndipo yense akadza Mupulumuketu.
...mokondwakondwadi
Moyo apeza kwa Yesuko. 5 Chikondi cha Mbuyathu
Chiposa zonsetu;
Chisomo chake chomwe
82 Chikondweretsabe;
1 Ambuye wathu Yesu Ulemu wake wonse
Akhala Mfumunso;
34 UTHENGA WABWINO
Umapambanadi; 2 Ndidziwa kuti Yesu
Tiyeni, tikondwere Anafa kalelo,
Popita m'Mwambamo. Nafafaniza zonse
Tinazichimwazo.
83 3 Satana ndi unyolo
1 Sing'anga 'mkulu ndiye Yesu, Anandimanga nji!
Mwana wa Mulungu; Ambuye Yesu yekha
Asangalatsa achisoni, Nandimasuladi.
Ali wachifundo.
4 Ambuye mulowetse
Dzina la Yesu ndi lokoma, Mtendere m'mtimamo
Dzina la Yesu lipambana, Ndimvetse mawu anu
Dzina lake lakukonda, Masiku onsewo.
Yesu, inde Yesu.
Akuti anthu akumvera
2 Zoipa zakhululukidwa, Yesu awapulumutsa,
Yesu amatero; Inde, awapulumutsa, indetu.
Tiyende bwino m'njira yake,
Tilowemo lero.
85
3 Nditama Nsembe ya Mulungu, 1 Okoma ndiwo mawu
Ndilandira Yesu; A Yesu Mbuyeyo,
Ndikonda dzinalo labwino, Wopatsa ife anthu
Dzina lanu, Yesu. Mtendere wakowo.
Kwa ife akumvera
4 Akulu inu m'bwere nonse, Kulibe mantha 'yi;
Ana inu nomwe, Timamva liu lake
Ambuye akuitanani, Lingoti, "Mudza 'nu.”
Bvomerani nonse.
Inu akutopawo,
Yesu aitana 'nu;
84 Mudze kwa Ambuyeyo,
1 Uthenga wa Mulungu Mudze msangatu.
Walowa m'mtimamu,
Wochotsa zakuipa 2 Mukana Iye bwanji,
Zakundidetsazo. Wokoma Bwenzilo?
Pakuti anthu akumvera Mutsate Yesu yekha,
Yesu awapulumutsa, E, mpaka imfayo.
Inde, awapulumutsa, indetu. Mwafoka osokera,
UTHENGA WABWINO 35
Mwafoka osokera, 87
...Mwadetswa nazozi 1 Wochimwa iwe, bweratu
Zoipa mwazichita; Kwa Yesu Mbuyeyo;
...Mumvere Mbuyedi. Atero Iye; pumatu,
umvere mawuwo.
3 Ambuye, musendeze
Pafupi nafedi, Khulupira mawu onse
Timvetse Inu msanga, A Mbuyathuyo;
Poyenda m'dzikoli. Uli nawo pakumvera,
M'ulendo m'moyo uno Inde, moyowo.
Titsate Inutu;
Kumwamba mutifitse, 2 Ambuye Yesu anatsira
Tidzamve: "Idzani." Mwazi wake pyu!
Ubire m'mwazi womwewo,
86 Uyereyere mbuu!
1 Inu nonse obvutidwa,
Mbuye ali panopa; 3 Wamoyo ndiye Yesudi,
M'maso mwanu muli msozi; Nzoona zakezo;
'Dzani kwa Mbuyathuyo. Akhala Iye njiratu
Yofika m'Mwambamo.
Yesu ngwachifundodi,
E! wafera inutu, 4 Tiyeni tonse, tinkeko
E! wafera inutu. Ulendo wakewo
Kudziko lake m'Mwambamo,
2 Yesu ndiye Bwenzi lanu, Tikhale nayeko.
Ali wa chikondicho;
Kodi inu mumkanabe? 88
Mlape msanga m'mtimamo. 1 Yesu ndi wokonda;
Ati "Idzatu,
3 Pena imfa idza mawa, Yense wakufuna,
Manda ali m'fupimo; Bwera msangatu."
Nthawi yino ndi yabwino, Ali wachifundo
Mlole Yesu m'mtimamo. Ndi wamphamvunso
Nthawi zonse Yesuyo
4 Ndi angelo akumwamba Alindatu.
Anke ndi uthengawo Yesu akukonda,
Kuti wina wadza lero Idza msanga 'we,
Kwa Mbuyathu Yesuyo. Adikira iwenso;
Wachedwatu.
36 UTHENGA WABWINO
2 Iwetu afuna, 5 Ndiwe mlendo lero lino,
Inde, kalelo; Mvera ndikupempha iwe;
Leronso adika Yesu Mwana wa Mulungu
Mbuye wathuyo. Akufuna ndithu iwe.
Uza Iye zonse
Za uchimowo; 6 Inde, lero lino Yesu
Yesu ati leroli; Aitana inu nonse.
"Wachedwa 'we." Landirani Mpulumutsi,
Musazengereze konse.
3 Yesu alindira,
Inde, iwetu;
Idza ndi kukhala 90
Ndi chimwemwenso 1 Penyetsetsa Yesu,
Ku mikono yake Mtima wosauka;
Yachikondiyo; Anafera iwe,
Sankha Iye msangatu; Idza, nupulumule,
Wachedwatu. Iye anachotsa
Nsoni ndi zoipa;
Penyetsetsa Yesu,
89 Ndi kukhulupira.
1 Lero lino m'bale wanga,
2 Penyetsetsa Yesu
Ndilo dzuwa lakukoma;
Likatentha dzuwa;
Talandira Mpulumutsi
Yachuluka ntchito,
M'mene ali kuitana.
Mphamvu idzakula.
2 Lero lino m'bale wanga,
Usazengereza ayi; Akonzera kwawo
Ngati ulandira Yesu Nyumba zokhalamo;
Lero, udzachita mwayi. Penyetsetsa Yesu,
Mtsatetu tsopano.
3 Lero lino ndi labwino;
Moyo wako uli nawo; 3 Penyetsetsa Yesu
Pena m'mawa umwalira, Pogwirana nawo;
Udzatani mlandu wako? Nkhondo ikabvuta
Tamva Mbuye wako.
4 Lero lino m'bale wanga, Achuluka 'dani,
Lapa mtima, lapa tchimo, Iwe ungofoka;
Yesu adzakulandira, Penyetsetsa Yesu,
Ukapempha lero lino. Mantha adzachoka.
UTHENGA WABWINO 37
4 Ndipo pakulowa . ..... ...Khulupirani kuti mukalowe
M'dziko la Kumwamba, ..... ... m'Mwambamo.
Udzapeza komwe
Onse adzatama. 2 Amayi 'nu, amayi 'nu,
Mwa zowala zija Tsatani Ambuye.
Za Kumwamba kwawo;
Udzapenya maso 3 Abale 'nu, abale 'nu,
Yesu Mbuye wako. Kondani Ambuye.

4 Alongo 'nu, alongo 'nu,


91 Kondani Ambuye.
1 Malo anachepa,
Nyumba anammana, 5 Abwenzi 'nu, abwenzi 'nu,
Agona m'modyera, Tamani Ambuye.
Mutu paudzuwo.
Anthu sanamtama, 6 Oipa inu nonsetu,
Nyimbo panalibe, Mverani Ambuye.
M'nyumba ya alendo
Malo munalibe.
93
Apempha malo Ambuye; 1 Ndichitenji kukapeza
E, mlandiretu m'mtimamo, Moyo? Thandizeni!
Ungomvetu Kumwambako, Ndili wakutopa; Mzimu,
"Akusowanso malo." Muthandize ine.
2 Wina panalibe .. ... Zonse zinathedwadi;
Kumlandira Iye, .. ... Yesu watha zonsezo;
Wakumsangalatsa, .. ... Sutha ntchito, ungomvera
Womkonda nasowa, .. ... Mawu ake omwewo.
Anthu sanafuna
Chumacho chosatha, 2 Iye anatsika m'Mwamba,
Sanamkondweretsa, Anachoka kwawo,
Malo munalibe. Anafera anthu, nati:
"Ndatha zonse zawo."
92 3 Mbuye wanga ndilikumva,
1 Atate 'nu, atate 'nu, Ndikondana nanu;
Mverani Ambuye. Umapuma mzimu wanga;
Khulupirani kuti mukalowe Kwathu ndiko kwanu.
.. ... m'Mwambamo,
..
38 UTHENGA WABWINO
94 Ine ndidzachotsa
1 Kodi mwalandira Yesu? Zonse zomwezo."
Iye anakuferani.
3 Kodi ukafuna
Afunitsa inu nonse;
Kupumulatu?
Kodi mumufunanso?
Yesu aitana:
"Udze kunoku."
.. ..... ...Kodi mufunatu Yesu?
.. ..... ...Bvomerani msangatu:
4 Tula mtolo wako
.. ..... ..."Inde, Yesu ndifunadi,
Pali mtandapo,
. . ...Ndinu Mbuye wangatu."
Akanyamula
Mpulumutsiyo.
2 Nthawi zonse mufunabe
Zinthuzo za pansi pano;
Koma munyozabe Yesu 96
Wopachikwa kalelo. 1 Yesu ponong'oneza, .. .idzanitu;
...Mupempherera ife, ... ... idzanitu;
3 Yesu akuitanani Njabwino nthawi yino, idzanitu,
Kwanja kwake kwakukulu; ...Yomdziwa Mpulumutsi, idzanitu.
'Mvani mawu ake lero,
Musachite nthantha 'yi. 2 Tulani zoipazi, ... ... .. idzanitu,
...Yesu adzatha zonse, ... idzanitu,
4 Imfa idzafika msanga; Olema ndi ochimwa, idzanitu,
Ndipo mdzaikidwa m'manda; ...Sakumbukira izo, ... . .. idzanitu.
Nthawi yomwe simudzamva
Kuitana kwakeko. 3 Imvani mawu ake, idzanitu,
...Mudzalandira dalo, idzanitu,
95 ...Nacho chisomo chake, idzanitu,
...Yesu alainda inu, idzanitu.
1 'Mvani liwu lomwe
M'Khutu mwakomo,
4 Mverani Iye ati: idzanitu;
Alikuitana
...Tiyeni mudzamwone, idzanitu,
Mpulumutsiyo:
...E! Akuitanani, ... ... idzanitu,
.. ..... ..."Undipatsetu ...Ife tibvomereza, ... Tibweratu.
.. ..... ...Mtima wakowo;
.. ..... ...Ndinakuferatu
.. ..... ...Kalekalelo." 97
1 Iwe tiye, iwe tiye,
2 Ati: "Undiuze . .Tiye tsopanoli;
Nsoni zakozo; ... Pano tiye kuli Yesu,Tiye
. tsopanoli.
UTHENGA WABWINO 39
....(Ndaima pano, ndaima pakhomo: 2 Tadza kumtsinjeku
....Lowa, lowa, lowa, lowa! Wa moyo weni,
....Ndaima pano, ndaima pakhomo!) Chiza zowawazo
Za m;mtimamo;
2 Akukonda, akukonda, Mtsinje wodzalawo,
Tiye tsopanoli; Wokwaniratuwo
Pano akukonda iwe, Yesu sakana 'yi;
Tiye tsopanoli. Idzatu 'we.

3 Akupeza, akupeza, 3 M'dzina la Yesuyo


Tiye tsopanoli; Pemphatu iwe,
Pano akupeza iwe, Iye adzamvatu,
Tiye tsopanoli. Dikirapo.
Wamphamvu Mlunguyo
4 Salephera, salephera, Ndiye apatsatu,
Tiye tsopanoli; Dalo labwinolo;
Pano salephera Iye, Idzatu 'we.
Tiye tsopanoli.
4 Yamba ulendowo
5 Mvera Yesu, mvera Yesu, Wonka Kumwamba;
Tiye tsopanoli; Pano mpoipatu
Pano mvera Yesu iwe, Padzikoli;
Tiye tsopanoli. Komwe tikondwako,
...Tidzasekeranso;
6 Aleluya, Aleluya, tinke Kumwambako;
Aleluya, Amen; Idzatu 'we.
Aleluya, Aleluya,
Aleluya, Amen.
99
1 Mwamva mawu a Mulungu;
98 Mukabvomeranjiko?
1 Tadza kukudyaku, Kodi musandula mtima
Kwakonzedwatu; Ndi kumvera Yesuyo?
Mkate wamoyodi,
Idyatu 'we; Bvomerani, Bvomerani,
Bwera wochimwanso, Bvomerani msangatu
Yesu adikatu, Musazengereze ayi,
Akuitanaku; Landirani Yesuyo.
Mvetsatu 'we.
40 UTHENGA WABWINO
2 Munachita nthantha kale, 101
Musazengereze 'yi; 1 A! Mbusa wathu amvatu
Yesu akulindirani, Uko kuchipululuko
Sadzakana inu 'yi. Zilira nkhosa zakezo,
Zili kuthengo kunjako.
3 Musaope pokumbuka
Zakuipa zanuzo; .. ..... ...Bwezatu, bwezatu,
Khulupirirani Yesu, .. ..... ...Bweza zonse m'moopsyamo;
Adzachotsa zonsezo. .. ..... ...Bwezatu, bwezatu,
.. ..... ...Bweza zakezo kwa Yesu.
4 Perekani mtima wanu
Kwa Mulungu wathuyo; 2 Ndani afuna kunkako
Khulupirirani Yesu, Kukazipeza nkhosazo?
Wotifera kalelo. Ndani adzathandizako
Kuti zifunde m'kholamo?
100
1 Yesu wathu Mbuyeyo 3 M'tali mutali m'phirimo
Alandira onsewo Mvetsa, zilira nkhosazo;
Akuipa omwewo, A! Mbusa wathu atitu:
Osokera m'talimo. "Bweza zothodwa m'khkolamo."

Imba kawiri ndi kawirinso, 4 Etu, zilira konseko


Yesu Ambuye sakanatu, Zili m'phiri moopsyamo.
Mvetsa Uthenga Wabwinowo, Imva, anena Mwiniyo:
Wakuchimwa adzetu. "Kweye, upeze nkhosazo"
2 Idzatu kwa Yesuyo, NJIRA YACHIKRISTU
Apumitsa inunso, KUTEMBENUKA MTIMA
Inde m'mtima mwanumo
Ndi mtendere wakewo. 102
1 Thanthwe long'ambikatu,
3 Walandira inetu Ndibisale momwemu!
Tsiku lija kalelo, Madzi ndipo mwaziwo
Wanditsuka ine mbuu Zotuluka m'nthitimo
M'mtima mwanga momwemo. Zonditsuke m'mtima mbuu!
Zindilimbikitsetu.
4 Wandifera Yesuyo
Pansi pano kalelo, 2 Ntchito zanga zonsezo
Sindiopa mlanduwo Sizikondweretsa 'Nu;
Pakubwera Iyeyo. Ndikazigwiritsadi,
UTHENGA WABWINO 41
Ndikalira nsonizi, Laleka ndithu ludzulo,
Zonse sizikwanazi, Tsopano moyo wadza.
Koma Yesu yekhayo.
5 Ambuye naitana 'ne:
3 M'manja mopanda kanthu, "La dziko ndine Dzuwa,
Mtanda ndingogwiradi; Yang'ana Ine, kwacha 'we,
'Maliseche mbveke 'ne; Wachoka mdima uja."
Ndili ndekha, msunge 'ne;
Ndithawire m'mtsinjewo. 6 Ndayang'anira Mbuyeyo,
Munditsuke m'mtimamo. Ndapeza Dzuwa langa
Londiyendetsa bwinolo
4 M'moyo uno kunsiku Pa njira yonse yanga.
Pena ndimwaliratu,
M'mene ndidzakwerako
Tionane masowo;
104
Thanthwe long'ambikatu, 1 Yesu wondikondadi,
Ndibisale momwemu. Ndithawire mwanumo
Pakugunda mvulazi.
(Maiwe! Thanthwe long'ambikatu,
... ...Ndibisale momwemu!) Pakubvuta madziwo,
Yesu mundibise 'ne!
Ikaleka mphepoyo
103 Tsidya ilo chete phee!
1 Ambuye 'naitana 'ne: Mndilandire momwemo.
'Dzapumulire kuno,
Tsamira mutu, mwana 'we, 2 Pothawira pena 'yi,
M'chifuwa mwanga muno." Ndikhulupirira 'Nu;
Musasiye inedi,
2 Ndabwera kwa Ambuyeyo: Mundigwiriziretu.
Wolema, wachisoni; ...Ndinu wothandiza 'ne,
Anandipulumutsako, Wolimbitsa mtimawu;
Nakondweretsa ine. Pansi pamapiko phee!
Mundifungatiretu.
3 Ambuye naitana 'ne:
"Ndipatsa anthu madzi.
Wotopa ndi waludzu 'we, 3 Wina sindifuna 'yi,
Dzamwere moyo kuno." Zokhutitsa nzanuzo;
M'utsetu akugwawo,
4 Ndibwera kwa Ambuyeyo, Mchizetu odwalawo.
Ndamwera madzi awa; Ndine wakuipa bii!
Ndinu wakuyera mbuu!
42 NJIRA YACHIKRISTU KUTEMBENUKA MTIMA
Ndimadzala tchimoli, Zabwino m'mtima zonsezi
Wolungama ndinutu. Mwa Inu ndingapezezi;
Ndagonjatu Mbuyanga 'Nu.
4 Zindichulukirazi
Nsoni zanu m'mtimamu; 5 Ndi ine simufuna 'yi
Zindichiza nthendazo, Ndingatayike m'mdima bii,
Zindiyeretsa mbuu! Ndimvere mwandiuzazi;
Pachitsime panupo Ndagonjatu Mbuyanga 'Nu.
Moyo ndimwe ndimwebe;
Mubukatu m'mtimamo, 6 Ndi ine, m'mtima Mwanu mbee!
Mundidalitsetu 'ne. Mokoma ndingakhalebe,
Ndikhale wanu wanudi;
... ... (Mulungu ali nane! Ndagonjatu Mbuyanga 'Nu.
... ... Ali nane, ali nane , ali nane, ali
... ... . .nane, Aa! 7 Ndi inetu ndidziwedi
Mulungu ali nane!) Chikondi chodabwitsachi
Pansipa ndi Kumwambako;
105 Ndagonjatu Mbuyanga 'Nu.
1 Ndi inetu sinditha 'yi
Kunenako milanduyi, 106
Kupempha zachisonizi; 1 Ndikhulupira 'Nu,
Ndagonjatu Mbuyanga 'Nu. Mwana wa Mulungutu,
Mbuyangayo;
... ... (Aa! Mulungu wanga, Mumve popempha 'ne,
- Mundilembe pamphumipo! Tchimo muchotsebe,
... ... Chidzakhala chizindikiro Lero ndikhale 'ne
... ... Cha mpumulo ulinkudza ndi Yesu.) Wa Mlunguyo.

2 Ndi ine sizitheka 'yi 2 Mzimu mndipatseko,


Kuchoka zakuipazi; Wondilimbitsayo
Ndisambe m'mwazi wanuwo; Mumtimamu.
Ndagonjatu Mbuyamba 'Nu. Munandiferadi;
Ndiyambe leroli
3 Ndi ine pondibvutapo Kukonda Inu ndi
Kugwira nazo m'mtimamo, Mtimangawu.
Mundithandize monsemo;
Ndagonjatu Mbuyanga 'Nu. 3 Poyenda m'mdima bii,
M'mtimamo nsonizi
4 Ndi ine ndasaukadi,
NJIRA YACHIKRISTU KUTEMBENUKA MTIMA 43
Mndigwirepo; 108
Mdima uchoke zi, 1 Yesu mundimve, ndikuliratu,
Msozi ulekedi, 'Dzani kwa inetu;
Ndisasokere 'yi Mtimangawu ufuna Inudi,
Kwa Inuko. Bwerani, Yesudi.
4 Moyo ukatha zi,
... ... Ndinasokeratu kutaliko,
Pofika imfadi,
... ... Ndalekana naye Mulungudi;
Mndisungepo;
... ... Tsopano koma mndilandirenso,
Yesu Mbuyanga 'Nu.
... ... Bwerani Yesudi.
Mantha mthawitsetu,
Ndifike m'Mwambamo,
2 Ndilibe malo mokhaliramo,
E, wanuyu.
'Dzani kwa inetu;
Khalani nane m'mtima mwangamo,
107 Bwerani Yesudi.
1 Chitsimecho cha mwaziwo
Udzera mwa Mbuyanga; 3 Njobvuta njira ndimayendamo,
Wochimwa ndikasambamo, 'Dzani kwa inetu;
Nditaya tchimo langa. Adetswa m'maso ndimapunthwamo,
Bwerani Yesudi.
2 Wakuba uja nachiona,
Nangokhulupira, 4 Wolapa mtima simunyozadi,
Ambuye namva pempholo, 'Dzani kwa inetu;
M'Mwambamo namlambira. Pemphero mumve langa lonseli,
Bwerani Yesudi.
3 Ambuye, mwazi wanuwo
Siitha mphamvu yake, 109
E, mpaka Mpingo wonsewo 1 Ndilinkudza kwa Ambuye,
Wayera m;kati mwake. Ndisauka, ndinachimwa;
Zonse zanga ndizisiya,
4 Chionerere mwaziwo Kudzapeza moyo wina.
Wofuma m'bala lanu,
Sindinaleke ineyo Yesu ndikhulupirira
Kutama mtima wanu. Munafera ine ndemwe;
Mwa umphamwi ndipemphera,
5 Kumwamba komwe n'dzaimbira Mundipulumutse tere.
Mpulumutsi wanga,
Chifukwa ayeneratu, 2 Kale ndinalira Inu,
Wakonza m'mtima mwanga.
44 NJIRA YACHIKRISTU KUTEMBENUKA MTIMA
Kale lomwe ndangochimwa; 5 Kuti mundipatsa mphamvu
Mund'tana, "Idza bwino, Yopambanayo;
Kuti nkuchotsere tchimo." Mawu mndilonga m'kamwa
Mwangamo.
3 Yesu, n'kupatsani zonse,
Zili zanu zokhazokha, 6 Ndikhulupirira, Yesu,
Thupi lonse, mtima womwe, Mndibvomereko;
Mwini wake ndinu nokha. Ndine wanu lero, mawa,
Konseko.
4 E, ndikukhulupirani,
Ndauona mwazi wanu;
Tere ndikugwadirani, 111
Tere ndapachikwa nanu. 1 Ndasiya zonse ndi Yesu kalelo,
Inde, zakuipa zangazo;
5 Wadza Yesu wandidzoza, Anafera ine m'phirimo;
Ndakonzeka mwa Iyeyu; Pomva Mawu ake m'kondwako;
Ndine wake, tikondana, Mumachoka m'mtima
Ndiyamika Mbuye Yesu. mwangamo nsonizo,
Mumachoka m'mtima
110 mwangamo nsonizo.
1 Ndikhulupirira, Yesu,
Inu nokhadi 2 Chisoni andichotsera Mbuyeyu,
Mundipulumutsa konse An'thandiza ine teretu;
Leroli. Ndikhulupirira Iyeyu,
Andisunga m'manja mwakemu;
2 Kuti mukhululukira Alimbitsa mtima
Tchimo langalo wangawu teretu,
Ndi chifundo chachikulu Alimbitsa mtima
Chanucho. wanga teretu.

3 Kuti muyeretsa mtima 3 Mtima 'we siya ndi Yesu nsonizi,


Ndibvomeratu; Usabisa tchimo lakoli;
Mwazi wanu unditsuka Zichuluka mphamvu zakezi,
M'mtimamu. Likusunga dzanja lakeli;
Bwera kwa Mbuyathu
4 Kuti munditsogolera leroli mwana 'we,
Paulendopo; Bwera kwa Mbuyathu
Mukwanitsadi zosowa leroli mwana 'we.
Zangazo.
NJIRA YACHIKRISTU KUTEMBENUKA MTIMA 45
112 Ndinazengereza, ndati:
1 Kwa Inu Yesu ndilira, "Mawatu."
Wopanda Inu ndidzafa;
Mupulumutse inedi, 3 Lero mtima ungolema,
Mundilandiretu. Usaukadi;
Wina wakundimasula
Mundilandiretu, Ndilibe.
Ndiipa m'mtimamo;
Kotero mnandiferatu, 4 Mbuye, ndingogonja tere,
Mundilandiretu. Ndibvomerapo;
Mundithyole, mundikonze
2 Ndifoka ndi zoipazo, M'mtimamo.
Ndidzalatu ndi machimo,
Sinditha kuzitayazo; 5 Chifuniro change, Mbuye,
Mundilandiretu. Ndiperekachi;
Mutsogole, ndidzatsata
3 Ndayesa kudzikonzadi, Inudi.
Ndapeza mphamvu ndilibe,
Zoipa zakanikadi; 6 Tere moyo wanga wonse,
Mundilandiretu. Mawu, ntchitonso
Zidzakondweretsa Inu
4 Onani Mbuye ndigonja, Zonsezo.
Kuyesa kwanga ndaleka;
Chitani Inu mumtima; 7 E, chimwemwe chachikulu,
Mundilandiretu. N'taperekadi
Mtima wanga, ndimapeza
5 Muyambe ntchito yanuyi, Mtendere.
Musalekenso, chitani;
Ndidzipereka leroli; 114
Mundilandiretu. 1 Chitha nchiani kund'yeretsa?
Mwazi wa Ambuye Yesu;
113 Nchiani chindipulumutsa?
1 Yesu, mulikundipempha, Mwazi wa Ambuye Yesu.
Munaterodi:
"Mwana, gonja, ndikupatsa Chitsime ndi chokoma
Chimwemwe." Chindiyeretsa bwino;
Chinanso sindifuna,
2 Kale ndinakana Inu, Mwazi wa Ambuye ndiwo.
Ndinathawatu;
46 NJIRA YACHIKRISTU KUTEMBENUKA MTIMA
2 Mtanda m'mtima ndiyang'na, Ndi chikondi chomwechi.
Mwazi wa Ambuye Yesu;
Ndikhululukidwa nawo NJIRA YACHIKRISTU-
Mwazi wa Ambuye Yesu. KUKONDA NDI KUTHOKOZA
116
3 Zonse zina sizikwana,
1 A Chikondi chopambana,
Mwazi wa Ambuye ndiwo;
E, chinadza ndi Mbuye;
Ntchito zanga sinditama,
Chinasangalatsa m'Mwamba,
Mwazi wa Ambuye ndiwo.
Chinalowanso mwa 'fe.
Yesu ndinu wachifundo,
4 Ndikhulupirira bwino
Wa chikondi changwiro.
Mwazi wa Ambuye Yesu;
Ee, mulowetu m'mtimanga,
Chilungamo change ndicho
Mumuyese mwanutu.
Mwazi wa Ambuye Yesu.
2 'Dzanitu Wamphamvu yonse,
115 Mtilanditse konseko;
1 Mndilandire ine Mbuye Musachoke, thandizeni,
Yesu wondifera 'ne; Muchotse mwangamu:
M'mtima mwanga muzikhala Inu nokha timakuza
Mawu anu okhawa.; Ndititumikirabe;
Tinyadira chikondicho,
2 Ndasokera m'tali ndithu Tichitame konseko.
M'njira zopwetekazo;
Wolemedwa ndingopempha, 3 Tsirizani ntchito yanu
Mndilandire inetu. Yakulenganso ife;
Idzakhalatu yangwiro,
3 Pakukumbukira zanga Ndiyo yoyenera 'Nu;
Ndili ndi manyazitu; Usinthika 'lemu wathu,
Ndingogwera pansi, 'Tate, Udzakula momwemo,
Mlapo wandigwiratu. Mpakatu Kumwamba komwe
Tidzalemekeza 'Nu.
4 Ndingopatsa Inu Mbuye
M'manja mwanu mtimawu,
Moyo, mzimu, zonse zanga, 117
Mzilandire Mbuyetu. 1 Ndilikuva m'mtima mwanga
Mawu ake a Mbuyanga,
5 Mukhululukire ine, Ati, "Ndakukonda iwe,
'Tate mundikondadi; Kodi undikonda Ine?"
Mundisunge nthawi zonse
NJIRA YACHIKRISTU- KUKONDA NDI KUTHOKOZA 47
2 Ati: "Mwana, kumbukira 2 Mbuye ndimva leroli
Zonse ndinakuchitira; Za mphamvu zanuzi
Ndakukonda, ndakuferea, Zomwe zisandutsadi
Ndakufuna posokera. Mtima wanga woti bii!

3 "Ku zoipa zonse zako, 3 Ine kanthu ndilibe


Goli la pakhosi pako, Kogula moyowu;
Ndi kunthenda zosautsa Ndingotsuka m'mtimamo
Ndine ndakupulumutsa. M'mwazi wa Ambuye 'Nu.

4 "Kodi mayi wobereka 4 M'mene ndifa inedi,


Mwana wake adzamleka? Kumwamba mzimuwu
Pena adzamwalira, Udzakwera komweko
Koma ndikukumbukira. Kuonana Mbuyeyo.

5 "Nthawi ilikudza yonse 5 Ndipo pakuima phe!


Sindisinthanika konse; Pokhala Yesuyo,
Imfa sindiletsa Ine Ndidzamtama Mlunguyo
Ndisakondekonde iwe. Kosaleka konseko.

6 "Ine ndidzakuonetsa 119


Zonse zakukondweretsa 1 Lindikomera dzina la Ambuye Yesu
Za Kumwamba zanga izo, ..wanga,
Mwana, sundikonda ine?" Lisangalatsa, lichiritsa, lin'chotsera
... mantha.
7 Ambuyanga, ndalephera,
Mwachisoni ndipemphera ... ... ...Dzinalo la Yesu,
Mundipatse ine ndithu ... ... ...Dzinalo la Yesu!
Mtima wakukonda Inu. ... ... ...Lindikomera dzina la Ambuye
... ... ...Yesu wanga.
118
1 Ati Yesu Mbuyeyo: 2 Lichiza mzimu wophwetekwa
"Ofoka ndinutu, ... ukakhale bata,
Mudikire, mpemphedi, Lidyetsa mtima wonse, lipumitsa
Ndidzapatsa mphamvutu.” . .. thupi langa.
Yesu wathadi
3 Nlokoma dzinalo la Yesu, ndilo
Za mangawatu,
... thanthwe langa,
Inde ndinaipa bii!
Chikopa changa, linga langa
Watsuka ine mbuu!
48
NJIRA YACHIKRISTU- KUKONDA NDI KUTHOKOZA
... m'mene ndibisala. 121
1 Bwenzi ndinamkomanayo
4 Ambuye ndinu Mbusa, Bwenzi, ndi Anandikonda kale;
Wansembe wanga, Kukonda kwandigwirako,
Ndi Mfumu, Moyo, Njira yomwe, M'kukondamo nditsale.
Inu ndimatama. Kumtima kundimangako
Kosamasuka konse;
5 Tsopano ndibukitsabe chikondi Ambuye ndine wanutu
chanu chija, Kunthawi nthawi zonse.
Pakufa ine Dzina lanu
lindilimbikitsa. 2 Bwenzi ndinamkomanayo
Anandifera yekha,
120 Anandipatsa moyowo,
1 Ndidzaimba za Mulungu, Ndatenga ine ndekha.
Za kukonda kwakeko; Zimene ndili nazozi
Anatuma Mwana wake Nza Yesu mwini zonse,
Kundifera kalelo. Ndi moyo wanga wonse ndi
Wakenso nthawi zonse.
Inde ndidzaimba nyimbo
Za kukonda kwakeko, 3 Bwenzi ndinamkomanayo,
Ndidzaimba ndi angelo Ndapeza mphamvu zanga,
Akukhala m'Mwambamo. Zakundisunga inemo,
Ndiyende m'njira mwanga.
2 Ndinachita mphulupulu, Zolemerera zoti mbee!
Waiwala zonsezo! Zindilimbitsa monse;
Ndinakhala ndi zoipa, Ndalema kuno, komweko
Wazichotsa zonsezo! N'kupuma nthawi zonse.

3 Wandipatsa moyo wake, 4 Bwenzi ndimamkomanayo


Moyo wakuyera mbuu! Wokoma mtima wake,
Ine ndili mwana wake, Wotsogolera nzeruzo
Wandilera inetu. Zisunga m'njira mwake.
Palibe wondichotsa 'ne
4 Ndiyamika Mbuye wanga Kwa Iye wondikonda;
Ndidzamlemekezabe; Pamoyo, imfa, nayeyo
Ndipititsa mbiri yake Ndilipo nthawi zonse.
Ya kukonda kwakeko.
NJIRA YACHIKRISTU- KUKONDA NDI KUTHOKOZA 49
122 Yesu Ambuyathu;
1 Ndimkonde Kristuyo, Muli nazo zakezo,
Ndimkondebe; Zidzatu zinanso.
Pemphero langali Mlungu wachisomocho
Mlandiretu; Mbuye wathu ndiye,
Ndipempha Inutu, Ati zinthu zonsezo
Ndimkonde Kristuyo, Nzatha mwa Iyeyo.
Ndimkondebe,
(Zina ndi zinanso
Ndimkondebe.
Zidza kwa ifedi,
2 Ndatsatatsatabe Inde mtima wakewo
Za pansipa; Uli wokomadi.)
Ndisiye zonsezi,
Nditsate 'Nu. 2 Mwamva Yesu m'mtimamo,
M'mtimanga wonsewu Adzanso kawiri,
Ndimkonde Kristuyo, M'mene ali nanutu
Ndimkondebe, Muli ndi chimwemwe.
Ndimkondebe. Ntchito zachifundozi
Iye watha izi,
3 Chisoni chonsecho Kuti mwawo m'Mwambamo
Chidzatha phe! Naye tikhalebe.
Angelo anuwo
Afiketu; 3 Mwamva Mzimu wakewo,
Nawo ndiimbetu, Zake zimvekanso
Ndimkonde Kristuyo, Kugwa ngati mvulayo
Ndimkondebe, Yachisomo chake.
Ndimkondebe. Mzimu ndiye mphamvudi
M'moyo mwathu muno,
4 Pakufa pangapo Mpaka tidzafikako
Ndinenebe; Komwe kuli Yesu.
Myamiko wangawu
Ndikwezebe, 124
Ndidzapempheradi, 1 Poyambapo ndakondwadi,
Ndimkonde Kristuyo, N'tapeza Inu Mbuyetu,
Ndimkondebe, Ndiimba nyimbo yomweyi,
Ndimkondebe. Kukondwa sindikhala duu!
Kalelo! Kalelo!
123 Wandisambitsa m'mtimamo,
1 Mwakhulupiriradi Wandiweruza lomwelo,
50
NJIRA YACHIKRISTU- KUKONDA NDI KUTHOKOZA
Kupempha ndi kukondwako. "Ndikonda tsopano
Kalelo! Kalelo! Koposa kale lonse."
Wandisambitsa m'mtimamo.

2 Mnyamata wake ndinetu,


126
Ndimvera Mawu akewo; 1 Ambuye, m'imfamo
Ndampatsa mtima wonsewu, Munakonda ine;
Sindikaniza 'Nu
Ndimtumikire pansipa.
3 Kumwamba ndidzanenadi Kanthu konse 'yi.
Za chipangano chathucho. Ndimagwadira 'Nu,
Wamoyo sindimsiya 'yi, ndikonda m'mtimamu,
Nditafa ndinka kwawoko. Ndidzaperekatu
Nsembe yangayi.
125 2 Kumwamba kwanuko
1 Ambuyanga Yesu, Mundipempherere;
N'kukondani Inu; Ndikhulupirako,
Ndisiya zoipa N'dzalandiradi;
Chifukwa cha Inu. Ndisenze mtandawo,
Ambuye wabwino Ndikhale mboniyo,
Mndipulumutse konse; Ndikaperekeko
Ndikonda tsopano Mitoloyi.
Koposa kale lonse.
3 Ndikhumba mtimawo
2 Ndikonda chifukwa Wofatsa ndithu,
Mnayamba kukonda; Kuti ndiyamba 'ne
Mnafera pamtengo, Ntchito zanuzi;
Munandiwombola. Akusokerawo,
Mukhululukira Ofuna zawowo
Zoipa zanga zonse; Abwere kwawoko,
Ndikonda tsopano Inde, kwanutu.
Koposa kale lonse.
4 Zambiri zangazo
3 Ndidzakukondani Mnandipatsa kale,
Mwa moyo ndi m'imfa; Ndibweza zonsezi
Ndidzakutamani; Kwa Mbuyanga 'Nu;
Chikondi n'dzaimba. Ndikadzaona 'Nu,
Mpakatu ndidzafa, Mbuye wabwinotu,
N'dzanena nthawi zonse;
NJIRA YACHIKRISTU- KUKONDA NDI KUTHOKOZA 51
Nsembe yokomatu NJIRA YACHIKRISTU-
Ndidzakhalabe. CHIMWEMWE NDI MTENDERE

127 128
1 Ambuye Mulungu,
1 Wafunafuna ine
Ndikondwera maka,
Ambuye Yesuyo;
Ndapeza chimwemwe
Wapeza ine ndithu
Ndi moyo wosatha.
Wodwala m'mtimamo;
Zochimwa zanga zonsezo Aleluya, mlemekeze,
Wachotsa izo zomwezo.
Aleluya, ndiye Mfumu;
Aleluya, mumpembedze
E! chikondi ndithu,
Ambuye Mulungu.
E! chikondi ndithu,
Ndi chisomo chake chonsecho,
2 Ambuyanga Yesu
Ndi zozizwa zake zonsezo.
Nandikhetsera mwazi,
Nakonzera ine
2 Ndafoka ine kale,
Milandu yangayi.
Ndafuna kufaku;
Anadza kundichiza 3 Pamtanda woopsa
Zinthenda zangazo; Adakandifera,
Ndi mwazi wake woti pyu! Natsuka m'mtimanga
Ndayera nawo m'mtimamu. Mukhale moyera.

3 Mabala ake m'manja 4 Tsopano Mulungu


Ndaona indetu, Alandira ine,
Ndi minga ya pamutu Popeza Mbuyanga
Yolasa Mbuyeyu; Nawombola ine.
Etu, wakonda inedi,
Pamtandapo kufera 'ne. 5 Padziko lapansi
Ndikumva chisoni,
4 Ndikhumba ine ndithu Komatu Kumwamba
Madalo akewo; Ndikhala ndi Mboni.
Ndifuna kumyamika
Masiku onsewo;
Ndikafa ine pansipa,
129
Kumwamba ndidzamtamanso. 1 Imfa ndi mfumu ya mdimawo,
Anthu oipa imangawo,
Akristu amapulumuka.
Omwe aimbira moyo,
52
NJIRA YACHIKRISTU CHIMWEMWE NDI MTENDERE
Moyo ndi moyo ndi moyo, 3 Adalitsika, indetu,
Wosalekana ndi moyo Wodziwa wadza Yesuyu
Wosamaliza Mulunguyo. Nafera iye kalelo
Ampatse moyo wosatha.
2 Yesu anafa pamtandapo,
Mzimu woipa nugomapo, 4 Akondwerera nthawiyi
Ndi ife titame Mulungu, Pomvera mwini Mlungudi;
Ndife tamasudwa m'moyo, Mtendere ngwake panotu,
Imfa ithedwa ndi moyo, Nakhala nawo m'Mwambanso.
Tsiku lomaliza moyo
Wosamaliza Kumwambako.
131
3 M'mitima mwathu mwakhala mbee! 1 Ndidziwitsitsa Yesu ndi wanga,
Mtanda wamdima wang'ambwa ke! Tsiku ndi tsiku ndimakondwera.
Panyanjapo pagawanika. Anandigula ndi mwazi wake,
Ndife tipita ku moyo, Anandipatsa Mzimu woyera.
Mtima wabwino ndi moyo;
Kumbanda kucha kwa moyo Mawu omwewo, nyimbo yomweyi,
Kumatiuza za dzuwalo. Yesu ndimtama tsiku lonseli;
Mawu omwewo, nyimbo yomweyi,
4 Akumangidwa ndi mzimuwo, Yesu ndimtama tsiku lonseli.
Mudze ndi ife kwa Yesuko,
Akuchotserani magoli, 2 N'kamvera Yesu ndikakondwera,
Nadzakupatsani moyo, Ndiyang'anitsa nkhopeyo yake;
Mlandu walipa ndi moyo, Ndipo angelo anditengera
Moyo ndi moyo ndi moyo Ine chisomo ndi chuma chake.
Tiimbirana za moyowo.
3 Ndine kapolo wa Mbuye wanga;
130 Andigwirtsa zintchito zake.
1 Adalitsika munthuyo Ndimyembekeza adzabweranso,
Wopeza dalo lomwelo Adzanditenga kwawo ndikhale.
Chisomocho cha Mlunguyo
Chogwera m'Mpingo wakewo. 132
1 Sindinanyengedwa konse
2 Chikhulupiro chomwenso Pakutsata Yesuyo;
Chogweratu m'chikondicho;
Yesu apambana zonse
Akhala nazo nzeruzi
Ndinalingalirazo.
Zofumatu mwa Mbuyedi.
Pakuyenderana naye
NJIRA YACHIKRISTU CHIMWEMWE NDI MTENDERE 53
Ndimamdziwa ndi woona; 133
Ndifunitsa anthu onse 1 Mulungu wanga,
Adziwenso Yesuyo! Ndapeza moyo;
Ndifunitsa anthu onse Ndili wokondwera
Adziwenso Yesuyo! Masiku onse.

2 Sindinanyengedwa konse; Aleluya, muyenera!


Yesu wachotsera phe! Aleluya, Amen.
Zakuchimwa zanga zonse Aleluya, ndidzamtama
Zakupsinja mtimazo. Mulungu wanga.
Yesu potsagana nane 2 Mwazi wa Yesu
Wandidzaza ndi mtendere;
Unditsukatu,
Kundisunga, kundikonda
Ndiye Mbuye wanga
Sadzaleka konse 'yi!
Ndi Mpulumutsi.
Kundisunga, kundikonda,
Sadzaleka konse 'yi!
3 Pamtanda wake
'Nafera ine,
3 Sindinanyengedwa konse,
Ndi zoipa zanga
Yesu adzabwerabe;
'Nazichotsadi.
Mtima wanga udiuza
Akuyandikiradi.
4 Mulungu wanga
Omwe sangamzindikire
Andilandira,
Andinyoza nandijeda,
Chifukwa cha Yesu
Koma Yesu ati zedi:
Mwana wakeyo.
"Ine ndidzabweradi."
Koma Yesu ati zedi:
5 Adzabweranso
"Ine ndidzabweradi."
Kundilandira
Ndikhale ndi Iye
4 Sandinyenga, salephera;
Masiku onse.
Yesu wadalitsa 'ne,
Mpulumutsi ndi Myeretsi
Ndi Mchiritsi yemweyo. 134
Wandiyanjanitsa naye, 1 Tili ndi mtendere
Mtima wanga nakhutitsa; Wopambanatu,
Sindinanyengedwa konse, Monga ngati mtsinje
Yesu akwaniradi! Mumitimamo;
Sindinanyengedwa konse, Koma mtsinje uno
Yesu akwaniradi! Umayenda phee,
Nthawi zonse mtima
54
NJIRA YACHIKRISTU CHIMWEMWE NDI MTENDERE
Nutonthozabe. 3 Wapumitsa mtima wanga,
Kaamba ndaphunziratu
Tikakhulupira Mawu ake olembedwa
Mlungu wathuyo, Mukalata mwakemo.
Tidzaona mwayi
Ndi mtenderewo. 4 Mumvetu abwenzi athu,
Musakanirire 'yi;
2 Dzanja la Mulungu Yesu aitana inu,
Litisunga nji! Zalembedwa zomwezi.
Nkhondo ya Satana
Sitiopa 'yi.
Zaphokoso zonse 136
Ndi zoopsyazo 1 Mtendere uli m'mtima mwathumu,
Sizibvuta mtima, Chifukwa mwazi watitsuka mbuu!
Sizilowamo.
2 Zakutsogolo sitidziwa 'yi;
3 Masauko athu Adziwa Yesu wathu zonsezi.
Ndi zokondwazo,
Azilola zonse 3 Abale angakhale m'talimo
Ndi Atatewo. Mbuyathu asungira onsewo.
Ponkhulupirira
Tidzapezabe 4 Imfa ndi manda sitiopa 'yi,
Kuti mtima wake Chifukwa Yesu wazithetsadi.
Utikonda 'fe.
5 Mtendere wapambana
m'Mwambamo
135 Pakufa ife tidzaonanso.
1 Yesu ndiye Mbuye wanga,
Ndamva Mawu akewo;
Anandilandira ine,
137
Nandipulumutsatu. 1 Ndiimba mumtima mokondwa
Ndi nyimbo yokoma yoyera;
Mwalembedwa mukalata Ndiimba za Yesu Mbuyanga,
Mawu ake omwewo, Anditonthoza 'ne phee!
Kuti iwo akumvera
Akalandiridwatu. Chete! Chete!
M'mtima mtenderemu phee!
2 Ndinakhala wakuipa, Udzera kwa Yesu wokonda
Ndinamkana kalelo; Mtendere mumtimamu.
Koma Yesu waiwala
Mphulupulu zangazo.
NJIRA YACHIKRISTU CHIMWEMWE NDI MTENDERE 55
2 Pamtanda Mbuyanga 'nafera, 4 Khalani duu! Pakufa ifetu,
Akandichotsera zochimwa; Ndi Yesu tidzakhala indetu
Anandigulira mtendere, Popanda mantha ndi zowawazi,
Anditonthoza 'ne phee! Chikondi chokha koma m'mtimamo.
Khalani duu! Pakutha zonse phe
3 Pomulambira Yesu Mbuyanga, Tidzasonkhana tonse kuli 'Ye.
Mumtima mtendere walowa;
Mdalitso woposa ndapeza, 139
Anditonthoza 'ne phee! 1 Namondwe akawombabe,
Mafunde akakulanso,
4 Pokonda Yesuyo, mtendere! Palipo pobisala 'fe,
Kunthawi zosatha, mtendere! Ndi popemphera Yesuyo.
Potsata Mbuyanga apatsa
Mtendere mumtimamu. 2 Paja athira Yesutu
Chimwemwe muli m'manthamo,
NJIRA YACHIKRISTU- Paja pokometsatu
CHIKHULUPIRIRO Mwazi wa Yesu nukhapo.
138
3 Pakulekana ifetu
1 Khalani duu! Ambuye adzatu;
Mitima ikomanapo;
Senzani chete mtanda wanuwo;
Tikumbukana 'bwezi 'fe,
Mulungu adzakonza zanuzo,
Popemphererana komweko.
Sangasinthike mtima Iyeyu.
Khalani duu! Bwenzilo Yesuyo
4 Tidzathawira kuti 'fe
Atsogolera m'njira mwathumu.
Pochita mantha nkhawanso?
Pakuyesedwa, tinke ku?
2 Khalani duu! Mulungu wanuyu
Tipemphe Yesu mphamvuyo.
Akonzeratu nthawi zonsedi;
Musakayike mtima; zo'psyazo
5 Tikhale ndithu pomwepo;
Zimasulidwa pomalizapo.
Zapansi zisalowe 'yi.
Khalani duu! A Yesu mawuwo
Sitidzapempha m'Mwambamo;
Ngamphamvu lero monga kalelo.
Tidzayamika Mlungudi.
3 Khalani duu! Pakufa mnzathuyo,
Pakumlira ndi misoziyo; 140
Panthawizo abwera Yesutu, 1 Mulungu anditsogolera,
Mitima yathu natonthazadi. Ndapumula m`mtimamo;
Khalani duu! Ambuye athadi Ayang`anira njira zanga zonsezo.
Kutibwezera zochotsedwazi.
56
NJIRA YACHIKRISTU CHIKHULUPIRIRO
Mulungu anditsogolera Kuyenda ndekha sindikwana 'yi;
Nsiku zanga zonsezo; Mukandigwira dzanja langa, Mbuye,
Ndidzatsatira Mbuye wanga Sindikaopa kanthu kena 'yi.
M`njira mwake momwemo.
2 Mbuyanga Yesu, mundisunge ine
2 Masiku ena pali mdima, Pafupi ndi 'Nu nthawi yonseyo;
Ndibvutidwa m'mtimamo; Ndikasowatu Inu, Mpulumutsi,
Masiku ena ndikondwera Ndingosokera m'talimo.
Ndi zabwino zangazo.
3 Mbuyanga Yesu, ndikapanda Inu
3 Masiku onse m'mtima mwanga Ukadza mdima m'mtima mwangamu;
Ndili ndi mtenderewo, Koma ndinutu dzuwa langa ndithu
Chifukwa ndimakhulupira Lakuwalitsa m'mtima momwemu.
Mtsogoleri wangayo.
4 Mbuyanga Yesu, mundigwire dzanja
Pamene ine ndimwalirapo.
141 Mkhaletu m'fupi nthawi yomwe Mbuye,
1 M'mene ine ndisauka Mundilowetse ine m'Mwambamo.
Ndi zoipa zangazo,
Ndidzapita lwa Mulungu,
Adzandilandiratu. 143
1 Ndifuna Inu, Yesu,
Mlungu adzandilandila, Ndadzala ndi machimo,
Iye ndiye 'Tate wanga; Mumzimu muli mdima,
Watumiza Mwana wake Ndikufatu m'katimo.
Andifere kalelo. Ndifuna kutsukika
M'chitsimecho cha mwazi
2 Ngatitu abwenzi anga Wa Inu wokondedwa,
Sandikonda ine 'yi, Munandifera kale.
Ndikhulupirire Mlungu,
Iye sandikana 'yi. 2 Ndifuna Inu, Yesu,
Lisowa bwenzi lina
3 Pansi pano ndili mlendo, Losungiritsa ine,
Kwathu ndi Kumwambako; Londithandiza mwina.
M'mene ndimwalira ine Ndifuna mtima wanu
Ndidzapita komweko. Wodziwa nkhawa zanga,
Wondisenzera mtolo
142 Wa tchimo lonse langa.
1 Mbuyanga Yesu, mundigwire dzanja;
NJIRA YACHIKRISTU CHIKHULUPIRIRO 57
3 Ndifuna Inu, Yesu, 4 Ndifuna Yesuyo,
Ndimasauka ndithu, Ndichite 'ne
M'ulendo andisowa Zofuna zakezo,
Kambayo wa padziko. Ndidzazebe.
Ndifunanso chikondi
Cha Inu chondisunga, 5 Ndifuna Yesuyo
Chakundisangalatsa Woyeratu,
Panjira ponse panga. Ndikhale wakeyo
Wa Iyeyu.
4 Ndifuna Inu, Yesu,
Ndidzaonana nanu,
Mudzadza pamitambo
145
Ikhale mpando wanu; 1 Mtima wa Mbuyako
...Pamodzi ndi ananu Ukukonda 'we;
Ndidzakondwera kuti; Ndiye wakuona
Ndilemekeze Inu, Wopirirabe;
Ambuye, Mpulumutsi. Ukasowa bwenzi,
Usaope 'yi;
Chikondano chake
Chikwaniradi.
144
1 Ndifuna Yesuyo 2 Akukumbukira
Ambuyanga, Yesu yemweyo;
M'mtendere ndinkemo M'kuyanjana naye
Mwa Iyeyu. Muli moyomo.
Uderanji nkhawa?
Ndifuna Inu Yesu, Mpulumutsiyo
Nthawiyi ndifuna; Atisamalira,
Kwa Yesu Ambuyathu Atisungatu.
Ndifunako.
3 M'munda wa Mbuyako
2 Ndifuna Yesuyo Muli ntchitomo;
Mobvutamo, Amithenga ake
Ndipulumukemo Aigwirayo.
Mwa Iyeyo. Usaime chabe,
3 Ndifuna Yesuyo Usakhale duu!
Mokondwa ndi Yesu akufuna
Mowawa, adzemo Umthandizetu.
Ndi moyodi.
58
NJIRA YACHIKRISTU CHIKHULUPIRIRO
4 Kwawo kwa Mbuyako 2 Anthu onse pansi pano
Udzafikako; Sakhutitsa mtima wawo;
Mwa ulemerero Amadera zinthu zawo,
Udzapuma phee! Namakhumba zakutali.
Usalowerere,
Mvera Yesuyo, 3 Khala chete mtima wanga,
Ati: "Mwana wanga, Zikwanire zinthu zako;
Bwera kwathuko." Usakhumbe zapansipa,
Koma Mlungu wako yekha.
146
1 Pamene ndisauka, 148
Pamene ndibvutidwa, 1 Ngati mtima sumakonda
Mizimu yakuipa Yesu, supumula bwino;
Ikadza nindiyesa,
Mbuye, suwu mtima wanga,
Mulungu wanga, Ndiwo wanu, mulandire.
Mwini mphamvu,
Mkandikumbukire 'ne. 2 Dziko lonse ndilitaya;
Ndikondetsa Yesu Mbuye;
2 Pamene ndilemedwa An'komera kopambana
Ndi zakuipa zanga, Andikondweretsa ndiye.
Polowa mdima m'mtima,
Pochita ine mantha, 3 Ndakudani, mnandikonda
Ndi kukhetsa mwazi wanu.
3 Masiku anga onse Simuleka kundikonda;
Mulungu mundisunge; Ine sindidzalekanso.
Pamene ndimwalira,
Ndi tsiku lomaliza, 4 Mndisungire mtima wanga,
Uzikhalupira Inu,
147 Kuti moyo wanga wonse
1 Khala chete mtima wanga Ubisaletu mwa Yesu.
Mlungu wako ndiye Mfumu;
Zinthu zonse zisinthika, 149
Mlungu ndi wachikhalire. 1 Njira yanga sindidziwa,
(Khala chete, 'Tate muikonza;
Chidzakupinga ninji? ... Komatu ndizindikira
Usaope, ... Kuti mundikonda.
Mulungu ali nawe.)
NJIRA YACHIKRISTU CHIKHULUPIRIRO 59
2 M'mene mantha andigwira, 151
Andidetsa m'mtima, 1 Mndiyandikitse nanu, Yesu,
Mbuye, ndithawire kwanu Ndiyenderane nanu;
Poti mundikonda. E, nditsamire panu, Yesu,
Panjira yonseyi.
3 Sindidziwatu zamawa,
2 Ndionetsere kuunika
Koma sindiopa;
Kokoma kwanu, Yesu!
Ndidzakhulupira Inu
Yabwino mbiri ndibukitse
Kuti mundikonda. Yokondweretsayo.
4 Inde wakukonda ndinu;
Mawuwo oona 3 Chitsime chakuyera ine
Andidzaza ndi chimwemwe: Ndifanefane nacho;
Mlungu andikonda. Mundigwiritse ntchito zanu
E! zanu zokhazo.
NJIRA YACHIKRISTU-
KUYERA MTIMA 4 Mulamulire mtima, Yesu,
Ndi chifuniro changa;
150 ...Mulowe mwanga ngati Mfumu;
1 Odala ndi onsewo Mundimveretsedi.
Oyera m'mtima mwawo;
Adzaonana ndi Mulungu, 5 Ndimamva njala kuno, Yesu,
Yesu ndiye wawo. Yakufunitsa Inu;
Kumwamba kwanu ndikukhumba
2 Ambuye anachoka Kukondwa nanuko.
Kumwamba, Mwini moyo,
Wofatsa anakhala nafe,
Mfumu yachisomo. 152
1 "Khala mwa Ine," Yesu anatero;
3 Mumtima wakufatsa Mawu abwino, koma Mbuye wanga
Akonda kukhalabe; Sin'ngathe ndekha, mukhalitse ine
Asankha mtima wakuyera, Mwa 'Nu ndikhale nawo moyotu.
Ndiwo nuymba yake.
2 "Khala mwa Ine," munachotsa tsoka,
4 Tifuna Inu, Mbuye, Mletse Satana anganyenge ine;
Mtininkhe mtima uwu Mibvi yamoto yake muizime
Wodzichepetsa, wakuyera, M'mtimamo, ndikhulupirire 'Nu.
Woyenera Inu.
3 "Khala mwa Ine," ndinu mwini
...
60
NJIRA YACHIKRISTU KUYERA MTIMA
mphamvu, Kumwamba n'dzaimbira
Mundithandize ine ndikafoka; Kukoma kwanuku;
Mzimu Woyera andiululire N'dzatama nthawi zonse
Zoona zanu m'mtima mwangamu. Chikondi chanucho.

4 "Khala mwa Ine," ndinu mwini moyo,


Nthambi zouma zidulidwa m'mtengo; 154
Ine wopanda Inu ndifokanso, 1 Khalatu woyera,
Zipatso zikasowa msadze 'ne. Pempheratu m'tseri;
Werengani Mawu
5 "Khala mwa Ine," Mbuye, ndifunitsa; Masiku onsewo.
Mzimu Woyera mlonge m'mtima Uthangate omwe
... mwanga, Ali akufoka,
Akagonjetsetu machimo anga Madalitso ake
Mtima woyera andipatsenso. Ufunefunebe.

2 Khalatu woyera,
153 Dziko laipadi;
1 Ambuye mundisunge Pemphera kolimba
Pafupi ndinutu; Kwa Yesu Mbuyathu.
Palibe malo pena Yang'anitsa Yesu
Popuma pansipa. Ndi kumutsatira,
Adani andizinga, Kuti anthu ena
Zoipa m'katimo; Aonenso Iye.
Chifundo chanu Yesu
Chikonze m'mtimamo. 3 Khalatu woyera
Akutsogozetu;
2 Ndikabisala mwanu Usamtsogolere
Ndilibe mantha 'yi; Munjira zakozo.
Ndikasungidwa kwanu Pokondwa ndi m'nsoni
Mumtima muti phee! Tsata Ambuyako.
Ndi mphamvu yanu yokha Khulupira Yesu
Ndiposa 'daniwo; Ndi Mawu akewo.
Chifundo chanu Mbuye
Chitchinjirize 'ne. 4 Khalatu woyera,
Khalatu wofatsa;
3 Ndidzaonana nanu Alilamulire
Mokondwadi. Ganizo lakolo
Oyera mtima onse Utatsogozedwa
Apenya Mbuyeyo. Ndi Mzimu wakeyo,
NJIRA YACHIKRISTU KUYERA MTIMA 61
Msanga udzagwira Kuti ndinu ndikondane;
M'Mwamba ntchito yake. Ndinalira Inu Mbuye,
Msandileke poitana.
155 4 Mzimu, msandipitirire,
1 Mudzaze Yesu mtima wanga ndi Mupenyetsatu akhungu;
.......chikondicho,
Mboniyo ya Mbuye Yesu,
Ukhazikike pa Mulungu Mundipatse ine mphamvu.
.......wosachokapo.
5 Ndinagona mwa zoipa,
2 Mwa ine myatse moto wanu Ndinakunyozani ine,
.......wakuyera mbuu, Dziko lino ndinakonda,
Utenthemo zoipa zonse Mbuye, mukhululukire.
.......zidakhalamo.
6 Ha! Chikondi cha Mulungu,
3 Mubweretu nomwe 'Nu munatsika Mwazi wa Mbuyathu Yesu,
.......kalelo; Chiyanjano cha Mzimuyo,
Ndilira Ine mundidzaze mphamvu Zonse ndidzalemekeza.
.......yanuyo.

4 Ndikhazikike inetu, mumtima muli 157


.......mwai, 1 Ambuye, thandizenitu
Ndi Yesu ndikondanetu, si kanthu Ndi mphamvu zanuzo;
.......kena ai. Pantchito zathu zonsezi
Mthandize Mbuyathu.
156 2 Zochimwa zathu m'mtimamo
1 Mbuye ndamva mwawazira Tilira nazotu;
Anthu ena madalitso; Mumtima mwathu muti zii;
Mvula yanu yawagwera; Mthandize Mbuyathu.
Mbuye, ine mudalitse.
Etu ine, etu ine, 3 Mthandize Mbuye, timvetu,
Mbuye, ine mudalitse. Tikalandiredi
Zimene muperekazo
2 'Tate msandipitirire, Zakudalitsa 'fe.
Ndimaipa mtima ine
Ndiyenera munditaye, 4 Kumwamba Yesu mthandize,
Koma mukhululukire. Tilibe wina 'yi;
M'moyo muimfa mthandize,
3 Yesu, msandipitirire Tikhale kwanuko.
62
NJIRA YACHIKRISTU KUYERA MTIMA
158 4 Mubwere, Mzimu wa mpumulo
1 Pokhala mtendere mu mtimangamu, Mundileze m'kati;
Pamene ndisaukanso, Ndidana nazo zoipazo
Pamene mavuto ndi akuludi, Zinakuchotsani.
Moyo wangawu ngwabwinotu.
5 Mundichotsere tchimo lonse
Moyowo
Ndinakonda kale,
Ngwabwino,
E, muligwetse kuti ndinu
Moyo wanga ulitu bwino.
Mfumu mukakhale.
2 Ngakhale Satana andizunza 'ne,
Chilipo chitonthozacho; 6 Mkatero ndidzayenda m'njira
Chifundo cha Kristu anafera 'ne, Ndi Mulungu wanga,
Kundipatsa 'ne moyo wake. Idzandiunikira nyali
Njira ya Kumwamba.
3 Uchimo unapachikidwa pomwe
Pamtanda wa Yesu Mbuye;
Machimo angawo anatherapo;
160
Mbuye wanga, ndiyamika 'Nu. 1 Ndilira mtima wotamanda
Mlungu, ndi woyera,
4 Ambuyathu, ndikhumba tsiku lija E, mtima woyamika mwazi
Limene ndidzaona 'Nu; Munandikhetsera.
Lipenga limveke, ndidzakondwatu
Pakukomana ndi Yesuyo. 2 Mtimatu wopirira ndi
Wofatsa m'kati mwake,
Mumveke Mbuye Yesu yekha,
159 Ndiye Mfumu yake.
1 Ndilira ine kukayenda
M'njira ndi Mulungu; 3 Ndilira mtima wakulapa
Ndilira nyali ndikaone Ndi womvera Yesu,
Njira ya kwa Yesu. Wosasiyana ndi Ambuye
Wakukhala m'mwemo.
2 Chimwemwe chija chamumtima
Ndinalawa kale 4 E, mtima watsopano ndi
Poyambutsata ine Yesu, Wodzala ndi chikondi,
Chili kuti tere? Wangwiro ndi wokoma, Mbuye
Wakukhala wanu wonse.
3 Kalelo m'mtima ndinakondwa,
Tere ndingolira, 5 Mkhalidwe wanu mundipatse,
Zokoma zonse zapadziko Ndifane nanu,
Sizindikwanira. Mulembe m'mtima mwanga Dzina
NJIRA YACHIKRISTU KUYERA MTIMA 63
La chikondi chanu. 4 Chifukwa cha ichi ndipempheratu,
Ndidikira Inu Ambuyangayu;
Ndikhulupirira pa mwaziwo pyu!
161 Musambitse ine, ndiyeretu mbuu!
1 Zoipa zangazi
Zidetsa m'mtimamu;
Mnditsuke, Yesutu, 163
Kutsuka koti mbuu! 1 Usafune chuma chokha,
Pena masewera okha,
2 Ndafoka inetu, Koma za Mulungu zokha
Ndalema m'mtimamu; Zipambana zinazo.
Andilimbitsa 'Ye,
Kulimba koti njo! 2 Ukafuna kulemera,
Pempha chuma chosathera,
3 Zin'sowa indedi Ndiwo mtima wakuyera
Zabwino m'mtimamu; Ndi wokonda Yesuyo.
Ambuye, mdzazebe,
Kudzaza koti tho! 3 Zosauka unvomere,
Ndipo Yesu chaulere
Chikondano ndi mtendere
162 Alowetsa m'mtimamo.
1 Ambuye, ndifuna nditsukenitu;
Mukhale ndine mumtimamangamu; 4 Zonse umazinyadira
Muthyole zonsezo zodetsa 'netu; Udzaleka kusirira;
Musambitse ine, ndiyeretu mbuu! Uli nazo zokwanira
Pakupeza Yesuyo.
... ...Ndiyere mbuu! E, ndiyere mbuu!
... ...Mundisambitse ine, ndiyeretu mbuu! 5 Mbiri yake ubukitse,
Anthu onse nuphunzitse,
2 Ambuye, chotsani zonse zomwezo Kwa Mulungu nufikitse
Zakundisautsa mumtimangamu; Osokera onsewo.
Ndileke zangazo zoipa 'netu;
Mundisambitse ine, ndiyeretu mbuu! 6 Yesu sakusiya konse;
Mphamvu, nzeru, chuma chonse
3 Kumwamba ndiona Ambuyangayo, Akupatsa nsiku zonse;
Mudzandithandiza, nditsate 'nemo; Tsata Yesu yekhayo.
Mudzandichotsera zoletsa 'netu;
Musambitse ine, ndiyera mbuu!
64
NJIRA YACHIKRISTU KUYERA MTIMA
NJIRA YACHIKRISTU- 2 Ntchito za Yesu gwira
KUTUMIKIRA Pomva usiku udza;
Lero lonseli gwira,
164 Bwino udzapuma.
1 Mkristu, ulimbike Gwiratu tsiku lonse
M'ntchito yakeyo; Ntchito tsopano ntchito,
Yesu anafera Tere udzaleka.
Anthu akewo.
3 Mkristu gwiratu ntchito
2 Mphamvu zathu zonse Pomva usiku udza;
Tionetsenso, Dzuwalo lopendeka
Kuti kudziwike Tere lidzalowa.
Tili akewo. Gwiranso 'dzulodzulo
Kutada mdima bii!
3 Mtima wakufatsa Tsono zintchito zonse
Amakondako; Zatha zonsezi.
Ndipo anthu onse
Angatengewo.

4 Mapemphero athu
166
Tikakwezebe, 1 Tithawiranji ifetu?
Dzina lake lomwe Mphamvu za Yesu nzathunzo.
Tiyamike 'fe. Kristu atithangatatu
M'nkhondo ya moyo wathuyo.
5 Limbikani nonse
Mpaka imfayo, 2 Yendani bwino m'njiramo
Ndipo Mfumu yathu Ya kwa Mulungu wathuyo;
Idzakondwako. Kwezani maso kuli 'Ye;
Kristu ndi njira yomweyo.
3 Nkhawa tilibe; Yesuyo
165 Atsogolera m'njiramo;
1 Gwira zintchito zako, Tikhulupire Iyeyo,
Pomva usiku udza; Kristu ndi moyo wathuwo.
Yamba mamawa ndithu
Potuluka dzuwa. 4 Tioperanji ifetu?
Gwiranso m'nsana monse Ali pafupi Mbuyeyu;
Dzuwalo likatentha; Sangasinthike mtima 'yi;
Gwira tsopano ntchito; Kristu akonda ifetu.
Msanga udzaleka.
NJIRA YACHIKRISTU KUYERA MTIMA 65
167 Udzakhaliranso kuli Mbuye
1 Mbuye, nditsate bwanjiko? wakoyo;
Ine ndikonde bwanjinso? Adzapulumutsa thupi, mzimu
Bwanji kuyenda m'njiramo ......wakonso,
Yonka Kumwamba kwawoko. M'mphamvu ndi chilango cha
......zoipazo.
2 Kodi m'njiramo ndimvadi
Nsoni zowawa, nkhawazi 3 Kunsi kudambo, pena m'mwamba
Ndi masauko, mingayi? ......m'phirimo,
E, nkana izi n'tsatabe. Pomwe pali Yesu
......ndidzayendayendapo;
3 Anasauka Mbuyeyo, Andiperekeza bwino m'njira yakeyo,
Mwini nalola zonsezo; Kuli Mzinda wa Mulungu wangayo.
Anatsiriza ntchitozo,
Osabwerera imfayo. 169
1 Mbuye, mwatiuza 'fe
4 Ndikamayenda m'mdimamo,
Tizikhala mchere
Mletse zodandaulazo;
Wokometsa onsewo
Mundikumbutse mtandawo;
Akumanga kwathu.
Zanga zichepa zonsezo.
Mcherewu ndi ifetu;
Mtifanize nanu,
5 Inde nditaya chumacho,
Tikakope ndi chitsanzo
Ndikondweretse Mbuyeyo,
Onse akuchimwa.
Thupi liopa mingayo
Koma mlimbitse mtimawo.
2 Mbuye, mwatiuza 'fe
Tizikhala nyali
168 Yoonetsa onsewo
1 Yesu afuna iwe unnke kwawoko, Njira yonka kwanu.
Lowa m'njira yake yakuyerayeratu; Njaliyi ndi ifetu;
Anadzera m'Mwamba Kuunika kwanu
......kutiperekezako; Mutipatse tiwalire
Yamba msanga iwe kunka kwanuko. Osokera onse.

... ... ...Tsata, tsata, nditsatadi Yesu; 3 Tisasungaluke 'yi,


... . .....Iwetu, iwetu, ukatsatanso. Tisasiye Yesu.
... . .....Tsata, tsata, nditsatadi Yesu; Tisabise nyaliyi
......
.. .... ...Inu nonse mukatsate Mbuyeyo. Pakuchita mantha.
Mcheretu ndi nyaliyi
2 Ngati umtsata Mpulumutsi wakoyo, Tizikhala tonse;
66
NJIRA YACHIKRISTU KUYERA MTIMA
Mbuye, mtiyeretse m'mtima Sunayambe kukayenda,
Tikatero ndithu. Ugwadire Mlunguyo.
Pena ulikusekera,
170 Pena nkhawa m'mtimamo,
Wachimwemwe, wachisoni,
1 M'mawa tizifesa
Uza yesu zonsezo.
Mbewu zakukoma,
Msana ndi usiku
2 Wakuchezacheza naye
Tizifesa momwe.
Ukagwira ntchitozo;
Nyengo yamasika
Pakukumbukira Yesu,
Tidzatema m'munda
Nkhawa zidzachokanso.
Tidzabwera tonse
Ndi zapansi zikafuna
Ndi zipatsozo.
Kukudzaza m'mtimamo
Utsogole kopemphera,
Ndi zipatsozo,
Uza Yesu zonsezo.
Ndi zipatsozo,
Tidzabwera tonse
3 Ndi m'kutero udzadziwa
Ndizipatsozo.
Chifuniro chakecho;
Iye adzakuthandiza
2 Tizifesa m'dzuwa,
Uthangate enanso;
Tizifesa m'mthunzi,
Ndi ofoka ulimbitse,
Sitiopa ife
Akulapa bwezatu;
Mtambo ndi chisanu.
Ndi za ntchito zake izi
Athatu masika
Uza Yesu zonsezo.
Ntchitozi zidatha;
Tidzabwera tonse
4 Ndipo ngati ungolema,
Ndi zipatsozo.
Ulefuka m'dzulomo,
Ndi Satana akayesa
3 Tingolira kaya,
Kukukola m'mtimamo;
Koma tidzafesa
Wakufola, wakuopa,
Mbewu za Ambuye;
Penyetsetsa Iyeyo;
Ntchitoyo nja Yesu.
Udzakhazikika m'mtima
Adzachotsa msozi,
Pakumuza zonsezo.
Adzatilandira,
Tidzabwera tonse
NJIRA YACHIKRISTU-
Ndi zipatsozo.
NKHONDO ZA MAYESERO

171 172
1 M'mene umauka m'mawa, 1 Haya! 'Nzanga taonani
Sunagwire ntchitozo, Yoonekayo
NJIRA YACHIKRISTU KUYERA MTIMA 67
Yakumwamba iti: "Yesu 3 Amatininkha zida zoteteza mtima,
Alinkudzako.” ...ndizo:
Kupempherabe, kukhulupirira ndi
Kanganani nkhondo yanu .......kufatsa;
Ndi mbendera mbuu! Mtheradi, ndi lupanga ndilo Mawau a
Tibvomere: "Inde Mbuye ... Mulungu;
Mtithangatetu." Pogwira zida zakezi sitilephera
....konse.
2 A! mizimu yakuipa
Isautsabe, 4 Mafumu atiuza tikaletse ukapolo,
Tikanize zakuipa Ndi kumasula goli la anzathu akuopa.
Zotizinga 'fe. Tiyeni, tiwauze za Mbuyathu
...Mpulumutsi,
3 Mdani adza nazo mphamvu, Nitiwanditse mlathu.
Koma ifetu
Tidzamthetsa nkhondo yake
...Timwingitsetu. 174
1 Limba mtima mbale wanga,
4 Yesu ati, "Ndidza msanga!" Usapunthwe m'njirayi;
Thangateni phee! Onatu nyenyezi ija
Mbweze mawu akulimba: Ikutsogoleradi.
Tikanganabe. Tamveratu Mlungu yekha,
Chita zolungama 'we,
Yenda bwino, khulupirira
173 Mbuyeyo, Mbuyeyo,
1 Anatilemba Yesu tikagwire nkhondo Ndi kuchita zakezi.
...yake,
Natilimbitsa tipirire osaopa kanthu. 2 Taya zako zochenjera,
Kwa Satana n'ziwembu zake sitigonja Taya zamumdimanso;
........konse; Nthawi zonse khulupira,
Tiyenderana naye Mfumu yathu Chita zolungamazo.
...yopambana. Usayang'anire wina
M'khondo yako yomweyi,
2 Amaliwongo ochuluka amalowa Koma m'zonse khulupirira
...m'mtima Mbuyeyo, Mbuyeyo,
Nafuna kuipitsamo usana ndi usiku; Ndi kuchita zakezi.
Tikatsatabe Mfumu yathu sitidzagwa
.......konse, 3 Leka zakuipa zako,
Pakuti atipatsa mphamvu tipambane Myambi yonse yoti bii,
nazo. Usakhulupire mommo;
68 NJIRA YACHIKRISTU NKHONDO ZA MAYESERO
Tamveratu Mbuyedi. Landirani 'yo.
Adzadana nawe ena, ...Ndikachita mantha
Ena adzakonda 'we; Sindithawa 'yi;
Kweza maso, khulupirira Mtima udzalimba,
Mbuyeyo, Mbuyeyo, Ndidzaima nji!
Ndi kuchita zakezi.
4 Pakumalizidwa
4 Mawu ake atipatsa Moyo wangawu,
Mphamvu ndi mtenderenso, Pomwalira ine,
Bwino atitsogolera, Mudze Mbuyetu.
Tikhulupirira 'wo. Ndidzadzipereka
Limba mtima, usapunthwe M'manja mwanumo;
M'njira yamumdimayi; Mpulumutsi Yesu
Yenda bwino khulupirira Mndilandireko.
Mbuyeyo, Mbuyeyo,
Ndi kuchita zakezi. 176
1 Ambuye wa Kumwamba,
175 Mundithangatetu
1 Poyesedwa ine Kuyenda bwino lomwe
Yesu mudzetu, M'elendo unowu.
Mundipempherere Kawiri ndi kawiri
Ndisachimwetu. Ndipunthwa m'njiramo;
Mukaona kuti Mlimbitse mtima wanga,
Ndilefukatu, Ndingatayikeko.
Mbuye mndilimbitse
Nazo mphamvutu. 2 Ndikhumba Mzimu wanu
Kundiyeretsa mbuu!
2 Ndi zapansi pano Pang'ono ndi pang'ono
Mundiphunzitsetu;
Ndikokedwadi,
Ndifuna nzeru zanu
Koma ndi chisoni Zakundifitsako
Mndiphunzitsedi; Kumwamba kuli Inu,
Ndisaiwalire Ambuye wangayo.
Za Getsemane,
Pena mtanda wanu 3 Yochita ndi yodikha
Yesu Mbuye 'Nu. Mupatse mphamvuyo,
Ndikhale wochenjera,
3 Mukandipweteka, Wogwira ntchitozo.
Ndipirirapo; Zoipa zanga zonse
Nsembe yanga ndiyo,
NJIRA YACHIKRISTU NKHONDO ZA MAYESERO 69
Mufafanizezo, Koma Mpingo wake
Ndi yende nanu nokha Uli chikhalire;
Masiku onsewo. Udzalaka ndithu
Mphamvu za Satana,
Yesu analonjezetsa,
177 Mawuwo sakana.
1 Tiyeni Akristu,
Nkhondo tiigwire; 5 Tiyeni anzathu
yesu Mbuye wathu Tizithandizana;
Atitsogolera. Imbirani nafe
Mfumu yathu mwini Nyimbo zopambana.
Atipatsa moyo; Kristu ayenera
Taonanitu mbendera, Mphamvu ndi ulemu;
Yailowa nkhondo! Tidzamlemekeza kwawo
Komwe kuli Yesu.
Tiyeni Akristu,
Nkhondo tiigwire;
Yesu Mbuye wathu 178
Atitsogolera. 1 Tiyeni, Akristu inu,
Mumenyane nkhondo iyi,
2 Nkhondo ya Satana Mukafoka nonse, koma
Idzakuthawani; Yesu akulimbitsani.
Tiyeni Akristu,
Kaipambaneni. 2 Muyendenso kunka komwe,
Idzanjenjemera Mugonjetse mdani wanu;
Mukapfu'litsatu; Musafoke, musaleme,
Imbitsanitu anzathu, Musagone konse inu.
Mawu mukwezetse.
3 Musagonje, anthu inu,
3 Mpingo wa Mulungu Mtamiretu Yekha Mbuye;
Uli ngati nkhondo; Ipambana mphamvu yake,
Titsagane nawo Ya Mtsogoli wanu yemwe.
Ana a Mulungu.
Sitipatukana, 4 Mtima wanu wonse ndithu
Ndifetu amodzi; Udzakhala ndi chimwemwe.
Ch'yembekezo, chikondano, Zida zanu mbvale bwino
Chonse ndi chimodzi. Zakudzera m'Mwamba momwe.

4 Zonse zapadziko 5 Limbikani inu nonse,


Zidzamalizika, Msangalalo ngwanu nokha;
70 NJIRA YACHIKRISTU NKHONDO ZA MAYESERO
Musaope kanthu kena, M'njira yanuyi,
Mumtamire Mbuye Yekha. Kuti ndidzayenda
Osaleka 'yi.
6 Tiyeni ku nkhondo iyi, Mundipatse mtima
Mugonjetse zonse konko; Wopiriramo,
Muingitse mdani uja, Wakukana zonse
Muyendetse m'njira momwe. Zondipingazo.

179 2 Mzimu wakuipa


Undiyesa 'ne;
1 Akristu limbikani, Mundithangatire
Imani mtima nji! Ku'thawitsabe.
Mbendera nyamulani, Akandisautsa
Msatenthemere 'yi. Kum'dzi kunoku,
Wotsogolera wathu Mulowetse mphamvu
Ndi Mwana wa Mulungu; M'mtima mwangamu.
Adzagonjetsa onse
Adani athuwo. 3 Akathira nsembe
Ku mizimuyo,
2 Tigwire nkhondo yomwe Ndipenyera kwanu,
Ya Mbuye wathuyo; E, Kumwambako.
Tileke zakuipa Tsoka ndi zonyenga
Zokhala m'mtimamo. Za ufitizo,
Sitikwanira tokha Yesu, mndilimbitse
Kuleka zathu zomwe, Ndisaopezo.
Koma Mbuyathu Yesu
Atithangatatu. 4 Pena kumwa nawo,
Ndisateroko,
3 Tsopano timenyana Pena kukaona
Ndi zakuipazi; Gule woipa,
Pamene nkhondo yatha Pena kuwombeza
Tidzanka kwathuko. Sindifuna 'yi;
Yesu adzalandira Yesu mndithandize
Ankhondo ake onse; Kuzikanazi.
Adzakhalira naye
Kumwamba komweko. 5 Ndinu Mbusa wanga;
Mndithandizetu;
Ndisaipse nazo
180 Mtima wangawu.
1 Mbuye, ndapangana Osaoopa konse,
NJIRA YACHIKRISTU NKHONDO ZA MAYESERO 77
Osachimwa 'yi. 4 Kodi inu, aulendo,
Mndiyendetse Yesu Ife titsagane nanu?
M'njira yanuyi. Inde, mudze inu nonse,
Mudze nafe paulendo.
NJIRA YACHIKRISTU- Inde, mutiperekeze,
ULENDO WA KUMWAMBA Yesu atilinda ife.
Yesu atilinda ife
181 Kuli dzikolo labwino,
1 Aulendo, munka kuti Yesu atilinda ife
Ndi zindodo m'manja mwanu? Kuli dzikolo labwino.
Paulendo tizipita;
Aitana Mbuye wathu;
Pamapiri, pamadambo, 182
Tizipita komwe kwawo 1 Ana akumwamba ndife,
Kuli dzikolo labwino, Paulendo timaimba;
Tizipita komwe kwawo Timatama Mbuye wathu
Kuli dzikolo labwino. Wa ulemerero wonse.

2 Kodi simuona njira, Tilikupita kwathu kuja


Inu anthu akufoka? Munjira ya atate athu,
Ayi, atiperekeza Amakondwera lero lomwe;
Mbuye wathu wotikonda Tinka kuonana nawo.
Iye amakhala nafe,
Natitsogolera ife, 2 Mbuye anatiitana
Atitsogolera ife Kukagwira ntchito yake,
Kuli dzikolo labwino. Kuitana anthu onse
Atitsogolera ife Atsatenso njira yino.
Kuli dzikolo labwino.
3 Inde Mbuye, tibweradi,
3 Mundiuze, aulendo, Zathu zonse tizisiya,
Muli chiani m'Mwamba muja? Mtsogoleri wathu ndinu,
Atibvekako zoyera, Titsatabe Inu nokha.
Akorona natininkha:
Moyo, moyo atipatsa,
Kwa Mulungu tidzakhala. 183
Kuli dzikolo labwino, 1 Mbuye munditsogolere,
Kwa Mulungu tidzakhala Ndine mlendo m'dziko muno;
Kuli dzikolo labwino. Ndikafoka mundikweze,
Mundisunge m'manja mwanu;
Mundidyetse, mundidyetse,
72 NJIRA YACHIKRISTU ULENDO WA KUMWAMBA
Sindingamve njalayo. E, ulendo wanga utha,
Tsono ine ndimwalira;
2 Mundimwetse madzi anu, M'mene ndidzafika kwawo
Andichize nthenda zanga; And'landirako.
Utsogole mtambo wanu,
Ndikadziwe njira yanga; 4 Komwe ndi chimwemwe ine
Mpulumutsi, Mpulumutsi, N'dzaonana ndi Atate,
Munditchinjirizetu. N'dzamgwadira ndi kumtama
Amandikondabe.
3 Ndikalowa m'mtsinje muja, Sakandisautsa kanthu
Mndichotsere mantha onse; M'dziko lija lakukoma;
Mndilowetse tsidya lija, Adzandidalitsa Yesu,
Ndikondwere nthawi zonse; Ndidzakondwako.
Nyimbo zanga, nyimbo zanga
Zidzalemekeza 'Nu.
185
1 Mundiwalire m'njira mwangamo,
184 Mbuyanga 'Nu,
1 Ndimayenda paulendo, Kwada usiku, ndasokerako,
Ndi yaminga njira yake; Mtsogoletu.
Tsoka ndikapeza, koma Phazi langali mndisungirenso,
Ndinka kwa Atate; Ndilonde Inu m'njira monsemo.
Pena m'mtima mwanga mwada,
Pena andibvuta 'dani, 2 Sindidapempha kale Mbuye 'yi,
Ndikatenga nkhawa, mantha, Mtsogole 'Nu;
Amadziwako. Ndasankha ndine, koma leroli
Nditsatatu.
2 Ichi chindisangalatsa Ndidadzikuza osaopa 'yi;
M'mene nkhondo indigwira, Ambuye, msakumbuke zomwezi.
M'mene nsoni zazikulu
Zimanditsatira; 3 Ndi kale lonse mnandisunga 'ne;
Mtima ukhazikika m'mene Tsopanonso.
Kwathu kuja ndikumbuka, M'khwawa, paphiri, mundisungebe
Kuti Mlungu ali ndine, M'tsogolomo.
Andisungako. Ndipo mamawa n'dzaonana ndi
Abale anga adafikadi.
3 Mbuye andipeza lero,
Andikonda, andisunga;
Adzapitikitsa mdani 186
Akamandibvuta. 1 Tiyeni nonsenu okonda Yesuyo,
NJIRA YACHIKRISTU ULENDO WA KUMWAMBA 73
Tiimbe nyimbo yabwino, 2 Kaamba chisomo cha Mbuyathu
Tiimbe nyimbo yabwino, ...uyu,
Ku mpando wakewo, Malo koma tipeza m'Mwambamo;
Ku mpando wakewo. Kumva Mtetezi amene ndi Yesu,
Ndicho chimwemwe ndi
Tiyeni pamodzi, ...chachikulutu.
Tilikupita Kumwamba;
Akristu tilikupita 3 Onse aliko takonda kalelo,
Ku Mzinda wa Mlungu. Kale napita kwa Yesu Mbuyawo;
Koma kumwona Mtetezi wathuyo
2 Ngakhale enawo aleke kwimbako, Ndicho chimwemwe choposa,
Akristu 'fe tidzaimba, ...nchathucho.
Akristu 'fe tidzaimba,
Kulemekeza 'Ye,
Kulemekeza 'Ye. 188
1 Ukatha moyo wanga
3 Akristu tonsefe, tikondwe m'Dzikoli Kumwamba kundichera;
Koposa anthu enawo, Dzuwalo ndimalira
Koposa anthu enawo, Lafika lokomera.
Tisanafikeko, Usiku m'nali mdima,
Tisanafikeko. Tsopano mbanda kucha;
Kudzawalitsa ndithu
4 Tiimbe mokondwa, misozi iume; Ku Dziko la Mulungu.
Poyenda kunka kwathuko,
Poyenda kunka kwathuko, 2 Chitsime chachikondi
Kwa Mlungu wathuyo, Ndi Yesu Mbuye wanga;
Kwa Mlungu wathuyo. Ndalawa mtsinje pano
Ndzamwetsa ine m'Mwamba.
187 Komweko zidzakula
Chisomo ndi chifundo,
1 Ndamvatu kuti tifika komweko
Pondiwalira kuja
Kuli Ambuye, Mtetezi wathuyo
Ku Dziko la Mulungu.
Inde, pakutha zobvuta zathuzo
Iye tidzamuona maso ndi maso. 3 A! Yesu Bwenzi langa
Inenso bwenzi lake,
... ... ..Ndi Mbuyeyo tikhalamo, Woipa 'ne alola
... ... Kupenyanso wokondatu; Ndilowe m'Nyumba mwake;
... .. Tidzakondwera E Ndikhulupira Iye
... ... ..nthawi zonse, Achotsa mphulupulu;
... ... Ndicho chimwemwe ndi Kudzandiwalitsira
... ... ..ulemutu.
74 NJIRA YACHIKRISTU ULENDO WA KUMWAMBA
Ku Dziko la Mulungu.
190
4 Ambuye andisunga 1 Kodi uli ndi chisoni
M'chifundo chachikulu; Choliritsa mtima wako?
Zisoni zisanduka Kweza maso ndi Atate
Chimwemwe cha Mulungu. Akumvetsa zonsezi.
Dzanjalo ndilitama
Ndi mtima wachifundo, 2 Kodi umadandaula:
Mpakatu kwawalitsa "Mbale wanga waferanji?"
Ku Dziko la Mulungu. Kumbukira Wakumtenga
Saphophonya konse 'yi.
NJIRA YACHIKRISTU-
ZA MALIRO 3 Mbale wako unamkonda,
189 Koma Yesu amkondetsetsa;
1 Tikagwidwa ndi chisoni, Anamfuna nangomtenga;
Ikayendanso misozi, Usammane Yesu 'yi.
Poliriratu abale,
Yesu mutimveretu. 4 Pakutsazikana nanu
Ndi potseka maso ake,
2 Munabvala thupi lathu, Imfa, bii! Anangogona
Munadziwa masauko, Koma adzadzukanso.
Mnalirira bwenzi lanu;
Yesu mmutimveretu. 5 Usalire; Mpulumutsi
Analawa imfa Yekha;
3 M'mene imfa yathu idza, Imfa yomwe nagonjetsa
Mweya wathu ukaleka, Potuluka m'mandamo.
M'mene ife timwalira,
Yesu mutimveretu. 6 Chikondano sichifera;
Mbale wako udzamwona
4 Mnamwalira Inu paja, Kwathu komwe; zipirira
Mwazi wanu munakhetsa, Mpaka ukafikako.
Koma Inu munadzuka;
Yesu mutimveretu. 7 Leroli chisoni chokha,
Tsiku lija kungokondwa;
Kweza maso osalira,
5 Mtima ukachita nkhawa
Yesu akukondadi.
Ndi zoipa zotimanga,
M'mene tikachita mantha,
Yesu mutimveretu.
NJIRA YACHIKRISTU ULENDO WA KUMWAMBA 75
191 Nikhala nawo Mzinda
1 Ntchito yonse yakeyo Wakukongolawu.
Yatha m'dziko linoli;
2 Akondwerera anthu
Mlendo wafikatuko
Zokoma zonsezi
Pokocheza leroli.
Za midzi ya padziko
... ... 'Tate, mwa kusunga kwanu Lapansi lonseli;
... . ..Timusiya mwana wanu. Mtendere wake koma
... ... 'Tate, mwa kusunga kwanu Wa Mzinda wathuwo
... ... Timusiya mwana wanu. Upambanitsa zonse
Zapansi pomwepo.
2 Yatha misoziyo,
Zobisika zonse mbee! 3 Ndi nkhondo ikaleka
Aweruza bwinoko Kwa Mulungu komweko,
Ndiye Wolungamayo. Ndi ukapolo watha,
Udani wathanso;
3 Komwe Mbusa kwawoko Ndi zakuopsa zonse
Atengera nkhosa zonse, Ndi zosauka zii!
Zake asungiramo Ndi mwayi wa kwa Mlungu
Zosaopa kanthu konse. Udzaza mutu tho!

4 Onse akulapawo 193


Ayang'ana mtanda wake;
1 Nlokoma Dziko langa!
Aphunzira komweko
Ndiyang'anirapo,
Zonse za kukonda kwake.
Ndilira ndi chikondi
Poona dzinalo;
5 Dothili kudothilo,
Pakumva mbiri yanu
Pfumbili kupfumbi tere;
Mumtima muti duu!
Mpaka adzadzukanso Ndi moyo ndi mtendere
Timusiya mumtendere.
Imalowetsamo.
NJIRA YACHIKRISTU-
ULEMERERO WA KUMWAMBA 2 Mokhala mokhamokha
Mokondwa momwemo;
192 Misozi yatha yonse,
1 Mumzinda wa Mulungu Angosekeramo;
Moyera mulimo, Panyezimira ponse,
Ndiye amathu omwe Panyumba pati mbee!
Olera ifewo; Pamyala pakongola
Mitima yathu yomwe Yoyala ponsepo.
Ikondwereratu,
76 NJIRA YACHIKRISTU ULENDO WA KUMWAMBA
3 Makomo afanana ... ... ..Iwo asekera, iwo asekera,
Ndi myala yoti mbuu! ... ... Inde asekera kumwona Yesuyo.
Ndi Kristu wopambana
Aonekeramo; 3 Mulibe zoipa m'Dzikolo,
Ndi mtanda woyeretsa Nzokomazo zabwino;
Wopachikidwapo, Ndi nthenda, imfa, misoziyi
Amamlambira Mfumu Kumwamba kulibenso.
Namlemekezanso. ... ...Dziko labwinotu, dziko labwinotu,
... ...Nawo mtenderewo, tikhumba ilotu.
4 Kulibe gombe, nyanja,
Kulibe nthawi 'yi 4 Ndikonda kuganizirabe
Alendo alandira Za Dziko la Mulungu,
Zoziziritsazi; Za zonse zotikondweretsamo,
Pa Mwala Wamuyaya Nzosathanso chikondi.
Amanga Nyumbayo, Ife tikondwera, ife tikondwera,
Ndi omwe opambana ... ...M'mene tidzampenya Ambuye wathuyo.
Adzakondweramo.
NJIRA YACHIKRISTU-
5 Nlokoma Dziko langa! PEMPHERO
Kopita onsewo
Mulungu awasankha, 195
Tifuna kunkako. 1 'Tate wa Kumwambako,
Ambuye, mutsogole Likayere Dzinalo,
Ku Dziko komweko; Udzetu Ufumu wanu;
Tidzakuimbirani Chifuniro chanucho
M'ulemereromo. Chichitike pansipa
Monga chachitika kwanu.

194 2 Mutipatse leroli


1 Ndikondwa kuganizabe E, chakudya chathuchi
Za Dziko la Mulungu; Tsiku n'tsiku tichilira.
Momwemo muli abwenzitu Mukhululukiredi
Okhala mumtendere. Tchimo lathu, monga 'fe
... ... ...Iwo salekana, iwo salekana, Iwo adatichimwira.
... ... Ayi salekana abwenzi omwewo.
3 Musatifikitsemo
2 Komweko akhala Yesuyo Muli mayeserowo,
Mtetezi wa inedi Koma mutipulumutse.
Pakati pa 'womboledwawo; Wanu ndi ufumuwo,
Sadzamva kuwawanso. Mphamvu ndi ulemunso
NJIRA YACHIKRISTU ULEMERERO WA KUMWAMBA 77
Kufikira nthawi zonse.
Tulutsanso zachabe;
196 M'nyumbamo ugwadire
1 Mtima wanga ndikonzera, Ndi kukapempherabe.
Mbuye Yesu aitana;
2 Kumbuka 'bale ako
Ati: "Mwana, tapemphera,
Ndi onse uwakonda;
Ine sindidzakukana."
Pemphera 'dani ako
Amene akutonza.
2 Mbuye, ndinu Mfumu yanga
Dzipempherere wekha
Yolemera ndi yamphamvu;
Mulungu akusunge;
Ndikapemphatu zambiri,
Tchulanso popemphera
Simundimanira kanthu.
Dzinalo la Ambuye.
3 Ndikabwera ndi katundu
3 Akakusowa malo
Wa zoipa zanga zonse;
Opempheramo m'tseri,
Mwazi wake wa Ambuye,
Komatu m'mtima mwako
Udzandiyeretsa konse.
Mwalowatu zoyera;
Anazilonga m'mwemo
4 Mbuye, ndinalema ine,
Ndi Mzimu Wakuyera;
Mlowe Inu m'mtima mwanga;
Zolingirira zija
Mkhale m'mwemo mwini wake
Kwa Mulungu zidzakwera.
Mantha mwandichotsera 'ne.

5 Ndine mlendo pansi pano, 4 Tilibe madalitso


Akulingana n'lino
Mndilimbitse ndi chikondi;
Atate atipatsa,
Bwenzi, mundilondolere
Kupempherabe bwino.
Njira pa ulendo wonse.
Ukamvatu chisoni,
Kwa Ambuye kapemphera.
6 Mndidziwitse ntchito yanga,
Adzakusangalatsa,
Mphamvu yake mundipatse;
Pemphero adzamvera.
Mundilimbikitse m'mtima
Ndikakhale kwa Atate.
198
197 1 Pokupempherani
Mundiphunzitse 'ne
1 Pemphera m'mbanda kucha,
Ndi Mzimu wanu Woyera,
Pempheranso usana;
Ndikayanjane nanu, Atate,
Pemphera m'dzulo momwe,
Ndi kukulemekezani 'Nu.
Pemphera ndi usiku.
Ndi mtima wonse idza,
78 NJIRA YACHIKRISTU PEMPHERO
2 Mndikumbutse zomwe 2 Tili nazo zotiyesa,
Munandichitira Zitidetsa nkhawamu;
Ndikakuyamikireni, Tisadandaule chabe,
Ndikweze Dzina lomwe angelo Timpemphere Mbuyathu.
Aliimbira Kumwambako. Kodi tikaona wina
Timkhulupiriremo?
3 Mndimvetse chisoni Yesu atidziwa bwino,
Pakuululira Timpemphere yekhayo.
Zochimwa zanga zambiri;
Mumtima ndi kupatsa mtendere 3 Kodi tikulema nazo
Mutachotsera zoipazo. Zotiwawa m'mtimamo?
Atipulumutsa Yesu,
4 Chikondi, chimwemwe, Timpemphere Iyeyu.
Chifatso, chiletso, Kodi adathawa 'bale?
Zipatso zonse za Mzimu Pempheratu Bwenzilo;
Mundibalitse, ndikafanane Akusunga m'mkono mwake,
Ndi Mbuyathu popempherapo. Udzapumuliramo.

5 Pakupempherera
Anzanga ndi onse
200
Akusokera mumdima, 1 Zokoma ndithu nthawizi
M'wapulumutse ndi k'wachitira Kwa Mlungu zondifitsadi;
Zomwe mufuna k'wapatsawo. Kumpando wachifumuwo
Ndiuza zanga zonsezo
6 Polowa ndi Inu Pobvuta ine mtimamo
M'chipinda cham'tseri, Nditulapo pa Yesuyo;
Posonkhananso pamodzi, Pakuyesedwa ndinkatu
Muyandikire nafe, Atate, Kwa Mbuye, sindikhala duu,
Mtibvomere, mtidalitsepo. Pakuyesedwa ndinkatu
Kwa Mbuye, sindikhala duu.
199 2 Zokoma inde nthawizi
1 Bwenzi lathu ndiye Yesu Zotama Dzina lomweli
Atikonda ifetu; La Yesu, ndi woonayo
Zifunsiro zathu zonse Ndilakalaka Iyeyu
Tipemphere Mbuyathu. Wofera ine pansitu;
Mtima phee tisowa tonse, Pakuda nkhawa ine bii
Zitibvuta chabeko, Nditchula Dzina lomweli
Kaamba sitimanka konse Pakuda nkhawa ine bii
Kumpemphera Mlunguyo. Nditchula Dzina lomweli.
NJIRA YACHIKRISTU PEMPHERO 79
3 Zokoma etu nthawizi" 202
Ndicheza naye Mlungudi; 1 Akristu ndi abale, tiziyenderana tonse,
Komatu kwathu m'Mwambamo Mulungu mmodzi tili naye, ndi
Kumwona ndi koposako. ...Ambuye yemwe,
Pobvula ine thupili, Chitsime chomwe, njira yomwe
Ndilowa Dziko lakedi; ...yokhulupirira;
Ndidzati nthawi yomweyo; Tiyeni tonse, m'Mpingo 'modzi
"Tsalani bwino pansipo." ...tiziyenderana.
Ndidzati nthawi yomweyo;
"Tsalani bwino pansipo." 2 Atate yemwe anatuma Mpulumutsi
......mmodzi
MPINGO WA MULUNGU Kudzatifera kuti atiyanjanitse tonse,
Ndi Mzimu yemwe ayeretsa akumvera
201 .........onse;
1 Mtidzutse, Mbuyetu, Tiyeni tonse, m'Mpingo 'modzi
Mtionekeremu; ........tiziyenderana.
Munene zakumvekazi,
Timvere ifetu. 3 Anatipatsa Mawu onse olimbitsa
......mtima;
... ... Mtidzutse, Mbuyetu, Kumwamba komwe tinka ndi kulonda
... ... Mtipatse moyonso; .......njira yomwe.
... ... Mudzetu, Mbuye, mudzetu, Tibalalikiranji ife akutsata Yesu?
... ... Tidalitseni 'fe. Tiyeni tonse, m'Mpingo 'modzi
......tiziyenderana.
2 Mtidzutse, Mbuyetu,
Tikweze Dzinali; 4 Satana apambana tikayamba kusiyana;
Tiuzireni Mpweyawo Tikayanjana, yemwe adzagonja ndi
M'mitima yathuyi. .......kuthawa;
Mbuyathu adzamthyola konse ndi
3 Mtidzutse, Mbuyetu, .......kumlamulira.
Timvere Mawudi; Tiyeni tonse, m'Mpingo 'modzi
Zoona zanu tonsefe .......tiziyenderana.
Tikhulupire 'zi.
5 Tiphatikane tonsefe okonda Yesu
4 Mtidzutse, Mbuyetu, ...Kristu;
Mthirenso moyowo; Tisalekane pakugwira ntchito za
Ulemu ngwanu nokha 'Nu, ........Mbuyathu;
Dalitso nlathulo. Tilimbitsane pakuyenda m'njira yonka
........kwathu.
80 MPINGO WA MULUNGU
Tiyeni tonse, m'Mpingo 'modzi 6 Pa la Mulungu tibwera kulandira
.......tiziyenderana. ...zidazo;
Mphamvu yanu ndi chikondi
203 ...zititsogolere ife;
1 Mbuye, Mpingo wanu usauka kwa Machitidwe ndi mkhalidwe zikokere
......kukuludi; ...ena kwanu.
Kale lija munatsitsa Mzimu wanu
.......Wakuyera;
Lero linonso muchite, ulimbike 204
...Mpingo wanu. 1 Aulendo amayenda
Muusiku wo'psyawo,
2 Tidza kwa Mulungu Inu, ndinu wa Namaimba nyimbo zawo
...chifundo; Kunka kwawo m'Mwambamo.
Mutipatse Mzimu wanu tsopanoli,
tere ...lino; 2 Kuunika kuoneka
Tikakhale ndi chimwemw kuti Koingitsa mdimawu;
...tilimbike ndithu. Mbale amakondwerera,
Osaopa konse 'yi.
3 A! maliro m'Mpingo mwanu kulirira
.. ..'balewo 3 Mlungu amaunikira
... Adasokerera kale ndi zoipa zapa . ... Anthu ake onsewo,
....dziko. Namachotsa mantha omwe,
.. Muwabwezerenso kwanu kuti . Nayeretsa m'njira mbee!
...akakhale mommo.
4 Anthu osawerengeka
4 Ndi chikondi mtithandize kuigwira Amtamira onsewa,
...nkhondoyi; Nagonjetsa zosautsa
Mwa kulema ndi kulimba Pomtamira Mbuyeyo.
...mutipempherere ife,
Kuti tilimbane naye Satanayo, 5 Pakufika tsidya lija,
...osam'wopa. Zotibvuta zonse phee!
Mfumu yathu yopambana
5 Pakubweradi Woyesa tidzamlaka Idzatikondweretsadi.
ifetu;
Angelonso adzabwera kutithandizira 6 Nthawi yina adzadzuka
... ...ife Ogonera m'mandamo,
Kuti tilimbike ife ndi kumchotsa Kuthawatu mphamvu zonse
...m'mtima mwathu. Zotivuta pansipa.
MPINGO WA MULUNGU 81
MPINGO WA MULUNGU- Dzuwa lathu m'Mwambamo,
KUPEMPHERA KWAMAMAWA M'wale m'kati m'mtimamo.
205 2 Konse kuli mdima bii
1 Tadzuka mzimu wanga'we Kosakhala Inutu;
Ugwire ntchito zakozi; Nlosakondwa tsikuli
Kukondwa uketengedi, Mosawala Inu 'mu.
Pemphero ulikwezedi. Ndionetu m'katimo
Mwakuwala kwanuko.
Pemphero, pemphero,
Pemphero ulikwezedi;
3 Mudze, mlowe m'mtimamu,
Pemphero, pemphero,
Mchotse monse mdima bii;
Pemphero ulikwezedi.
Mdzaze ndi kuyeraku,
Mchotse zosamverazi;
2 E, nthawi ya mamawayi
Ndi kuyera kwanuku
Umtamandire Mbuyeyo,
Ndikaone bwinotu.
Nuyese lero ngatitu
Tsiku lakumalizalo.
MPINGO WA MULUNGU-
KUPEMPHERA KWAMADZULO
3 Munkhani zako zonsetu
Unene molungamadi, 207
Nudziwe kuti Mbuyako 1 Ambuye munapatsa tsiku
Adziwa zachinsinsizi. Limene langopitali,
M'mamawa nyimbo zathu zomwe;
4 Pa tsikuli, Mbuyanga 'Nu, Mukhale nafe nthawiyi.
Munditsogoze m'njiramo;
Ulemerero wanuwo Mukhale, mukhale,
Undilimbitse monsetu. Mukhale nafe nthawiyi;
Mukhale, mukhale,
5 Timlemekeze Mlunguyu Mukhale nafe nthawiyi.
Wa madalitso onsewo;
Timlemekeze tonsefe, 2 Tipempha kuti Mpingo wanu
Atate, Mwana, Mzimunso. Ukhale ponse m'dzikoli;
Mumdima monse muwaletu,
206 Kuwala kwanu kudzedi.
1 Kristu wakuyeratu,
Kristu wakuwalayo, 3 M'maiko monse, zisi zomwe,
Wolungama mdzuketu, Kuwala kumafikamo;
Muingitse mdimawo. Kupempha sikuleka konse
Kuyamikira Yesuyo.
82 MPINGO WA MULUNGU KUPEMPHERA KWAMAMAWA
4 Pogona ife, amadzuka 209
Abale akutaliwo; 1 Atate ndiyamika, mwandisamalira
Panthawi yonse anthu ena ........leroli;
Alemekeza Mbuyeyo. Mulungu wondikonda, mndisungenso
....... m'mdima muno bii.
5 Ufumu wanu, Mbuye Yesu,
Ukhala nthawi zonsedi; 2 Mundikumbutse, ndikapanda tulo,
Magulu onse adzagonje, za Kumwambako;
Nalowe m'njira mwanumu. Zoganizira zoipitsa m'mtima
.........muchotseremo.

208 3 Zochimwa za usana uno


1 Mukhale ndine, dzuwalo lalowa, ........mndikhululukire 'ne;
Wagwa usiku, bwenzi lindisowa; Mtendere wanu mulowetse m'mtima
Ndilibe wina wakundithandiza, ndikagone phee.
Wamphamvu ndinu, mkhale ndinetu.
4 Mundilimbitse ndikayese manda ngati
2 Kamoyo kanga katha lero lino, .......mphasayi,
Zidzachokanso zinthuzo za dziko; Nditagonamo ndikadzuke tsiku
Zimasinthika zonse zooneka, .....lomalizalo.
Simusinthika, mkhale ndinetu.
5 Tiyamike Mlungu wotipatsa
3 Koma kalelo mnakhalitsa pano, ....... zachifundozi,
Mukhale ndine, msandichokerenso, Amyamike onse a Kumwamba ndi
Sin'pempha kuti Mbuye mungotsotse, ...... apansipa.
Komatu mukhalitse ndinetu.
210
4 E, tsiku lonse Inu ndifunitsa; 1 Dzuwa lapitira,
Ndi mphamvu yanu yokha ndisungika; Wadza mdimawo,
Mukatsogola ndidzadikha mtima; Mthunzi wamadzulo
Usiku, msana, mkhale ndinetu. Wagwa m'mwambamo.
5 Adani sindiopa mukalipo; 2 M'mwambamo nyenyezi
Muletse tsoka ndi chisoni chino; Zithwanima mbee;
Ikadza imfa n'dzalimbika m'mtima; Zonse zili m'tulo,
M'moyo ndi m'imfa mkhale ndinetu. Pansi pali duu.

3 Yesu mutipatse
Tulo toti phee;
MPINGO WA MULUNGU KUPEMPHERA KWAMADZULO 83
Ndi mdalitso wanu 4 Mkhululukire,
Mndifonetse 'ne. Mkhululukire
Zoipazi zathu zonse.
4 Mpatse ana 'ng'ono
Alotemo mbee; 5 Lero tigone,
Anthu aulendo ...Lero tigone,
Msungesungebe. Tigonemo mumtendere.
5 Mutonthoze mtima 6 Ndife ananu,
Wopwetekawo; Ndife ananu,
Akutsata tchimo 'Tate Mlungu wotikonda.
Mletse onsewo.
7 Aleluya!
6 Wonsewu usiku
...Aleluya!
Andisunge 'ne
Aleluya! Aleluya!
Amithenga anu
Akuyera mbee.
212
7 Ndidzukanso m'mawa, 1 Madzulo aja kalelo
Kucha koti mbuu, Odwala anagona duu;
Ndiyeretu mtima Opwetekedwa nthendazo
M'maso mwanumo. Munachiritsa Inutu.
8 Titamadi 'Tate,
2 Tsopano lino kwada bii,
Mwana wakeyo
Nafenso timva m'mtimamo;
....Mzimu Woyeranso,
Simuoneka, komatu
Nthawinthawizo.
Tidziwa muli nafedi.

211 3 Wopulumutsa mudzetu;


Adwala ena m'mtima bii,
1 Dzuwa lapita, Ena sakukondani 'Nu,
Dzuwa lapita, Ena sasamalira 'yi.
Mlungu, mutigonetse phee.
4 Ndi ena sanamvera 'yi,
2 Mdima wafika, Enanso alemedwatu,
Mdima wafika, Zoopsya nazo tifadi;
Mutisunge tonse bwino. Mukadza tidzaposatu.
3 Tibvomereze, 5 Wopulumutsa, Inunso
Tibvomereze Munasauka kalelo;
Zakuchimwa zathu zonse.
84 MPINGO WA MULUNGU KUPEMPHERA KWAMADZULO
Muona zoda m'mtimamu 3 Madzulo ano mkhaletu
Tibisa ndi manyaziwo. Pafupi ndine, Yesudi;
Ndisanagone tuloto,
6 Mutichiritse ifenso Ndilingalira Inudi.
Mutiphunzitse zanuzi;
Timve tsopano mawuwo 4 Kapena wina leroli
Ochiza nthenda yathuyi. Wasokerera m'njirayi
Ya Inu Mbuye, mbwezetu,
Mumpulumutse iyedi.
213
1 Mpulumutsi tikagona
Mtidalitse m'mtimamo; 215
Tingolapa zakuipa, 1 Lero mwatipatsa moyo,
Muzichotse zonsezo. Wadza mdima, kwada bii;
Kukadetsa bii usiku Mtigonetsetu usiku,
Inu mutipenya 'fe; Mchotse zakuipazi.
Simulema, simugona; Yesu mutisunga ife;
Anthu anu msungabe. Tidzakhulupirabe.
Yesu mutisunga ife;
2 Atipsinjadi masoka, Tidzakhulupirabe.
Mibvi iponyekatu;
Atisungadi angelo, 2 Ndife anthu aulendo,
Moyo mutipatsa 'Nu. Tili ndi adaniwo;
Ngatitu usiku uno M'manja mwani mtigonetse,
Ikabwera imfayo, Mtichotsere manthawo.
Mtiukitse m'mawa kwanu, Ndipo pakumuka ife,
Mpatsenso zoyerazo. Kwanu tidzapumabe.
Ndipo pakumuka ife,
214 Kwanu tidzapumabe.
1 Mulungu wanga, Dzuwatu
La mtima wanga ndinudi; MPINGO WA MULUNGU-
Palibe mdima ngatitu TSIKU LA MULUNGU
Mukawalira inedi. 216
1 Kwacha lero kwati mbee,
2 Muchotse zonse zoti bii
Tsikku la Mulunguli;
Zobisa nkhope yanuyo;
Dzuwa liwaliradi
Mudzazetu mtimangawo
Thambo ndi zapansipa;
Ndi kuunika kwanuko.
Upumira mpweyawu
Wa Mulungu konseku.
MPINGO WA MULUNGU KUPEMPHERA KWAMADZULO 85
2 M'nyumba yanu, Mlungu, 'yi 3 Timvere Mawu anu
Tisonkhana teretu, Tsiku lopatula;
Ndi mitundu yonseyi Muwadalitse ndithu
Tikulambireni 'Nu; Tsiku lopatula.
Yesu Mbuye wathuyo Mtiperekeze kwathu,
Ndiye Mfumu ponsepo. Msunge mitima yathu;
Mpatse chisomo chanu
3 Inu Mlungu kalelo Tsiku lino lopatula.
Mutalenga zonsezi
Munapuma tsikulo; 218
Tipumadi ifenso. 1 Dzuwa la Mulungu
Mommo tilansiratu Ladzatu labwino;
Zopumitsa mtimawu. Ndi chimwemwe ife
Tiliona lero.
4 Yesu munadzukanso Lithawitsa nkhawa,
M'manda lero lomwetu; Lichotsanso mantha,
Ntchito munayambayo Ndimo m'mtima mwathu
Yakudzutsa anthu 'fe, Likhalitsa bata.
Kuti ndi mitimayi
Tigwirebe ntchitozi. 2 Tikondwera kuti
Tipumula lero;
Tazileka ntchito
217 Kuti tipemphere.
1 Ambuye, tasonkhana Koma ntchito zathu
Tsiku lino lopatula; Zapa lero lino
Tidzapembedza Inu Nzakumvera Yesu,
Tsiku lino lopatula. Kumlandira bwino.
Bwenzilo lakufatsa,
Mbweretu kutipatsa MPINGO WA MULUNGU-
Mtima wakumvetsetsa NYUMBA YA MULUNGU
Tsiku lino lopatula.
219
2 Sitinanyalanyalaza 1 Ndi lokoma m'Mwambamo,
Tsiku lino lopatula, Mbuye, Bwalo lanulo;
Tigwadirira m'mantha Ndi mwabwino muli 'Nu
Tsiku lopatula. Dziko losachimwali;
Mbwezetu maganizo, Mtima wanga wonsewu
Mtimvetse malangizo; Umakhumba m'Mwambamo
Tchimo mufafanize Nkhope ya Mbuyathuyu,
Tsiku lino lopatula. Mlungu wa chisomoyo.
86 MPINGO WA MULUNGU TSIKU LA MULUNGU
2 Zimbalame zonsezi Olinda m'nyumba mwakemo.
Zimayamikira 'Nu; Myamike, muimbiretu
Anthu amakondwanso Mulungu Mbuye wathuyo.
Okhumbira m'Mwambamo;
Njiwa yosapumayo 2 Mugwade pansi m'nyumbayo,
Inafika m'chombocho; Mpembedze nonse Mlungutu;
Okhulupirira 'Nu Mugadamire m'Mwambamo,
Amapuma kwanuko. Mtamande Mbuye wanutu.

3 Anthu opembedzawo 3 Yehova adalitse 'nu,


Amakondwa m'mtimamo; Ndiyeyo wachifundocho,
Munapatsa madzitu, Asunge moyo wanuwu;
Munagwetsa manawo; Amtame anthu onsewo.
Mumakoma mtimatu
Tidzayamikiratu, 222
Pa chimpandocho chanucho 1 Kwezani mitu yanuyo,
Mkhale Mfumu yathudi. Zipata zamuyaya,
Ikalowemo Mfumu ya
Ulemereroyo!
220 Amfumu awa ndaniko?
1 Yesu mkhale nafe Ambuye ndiyeyo,
Nthawi yomweyi, ...Mulungu wogonjetsa onse,
Kuti mphamvu zanu Wolimba mphamvu njo!
Tilandirezi. Mulungu wogonjetsa onse,
Wolimba mphamvu njo!
2 Mzimu Wakuyera
Mutipatsetu, 2 Tatsegukani inutu,
Mtima wathu wonse Zitseko zosathera,
Usakhale duu. Amfumu a Kumwambako
Alowe mwanumo.
3 Moyo watsopano Amfumu awa ndaniko
Ulimbitse 'fe; Wolemereroyo?
Mlungu wathu yemwe Mulungu wa makamu ndiye,
Timdikirabe. Wolemereroyo.
Mulungu wa makamu ndiye,
MPINGO WA MULUNGU- Wolemereroyo.
KUYAMIKIRA
Aleluya, aleluya,
221 Aleluya, aleluya,
1 Antchito a Mulungu 'nu Aleluya!
Amen, amen, amen.
MPINGO WA MULUNGU NYUMBA YA MULUNGU 87
223 Tibatizidweko,
1 Mulungu ali muno, Tiyeretsedwedi
Tonse timgwadire, Ndi Ambuye leroli.
Mantha omwe timchitire;
Ali mukachisi, 2 Mwa anthu onsewo
Tonse tili chete, Umayenda mtsinjewu,
Ndi ulemu timpembedze; Nuwachiritsadi
Ndiye yekha Mlungu wathu Okhulupirirawo.
Atipulumutsa, 3 Tikondwereratu
Tizimlemekeza. Pakumvera Yesuyo,
Abwere onsewo
2 Mwini madalitso, Ndi kulowa m'mtsinjewu.
Mndikonzere m'mtima,
Mbuye, ndingokhulupira.
M'Mwambamo angelo 225
Agwadira Inu, 1 Atate, muwapenye
Ife tigonjanso kuno; Anzathu ali pano,
Mpingo wonse uchititse Abvomereza Inu
Chifuniro chanu Ambuye Mfumu yawo;
Ponse pansi pano. Alonjezetsa lero
Kutsata Mbuye onse,
3 Yesu Mbuye wanga, M'wathangatire iwo
Mkhale m'mtima mwanga, Asabwerere konse.
Ndiwotu kachisi wanu.
Ikafika imfa, 2 Tsopano alandira
Mundisunge kwanu Chizindikiro chanu
Kuli Inu ndi angelo. Munachiika ndinu
Moyo wanga ulimbike Cha Ubatizo wanu.
Kufikira ine Mulembe Dzina lanu
Ndidzakupenyani. M'mitima mwa onsewa;
M'wabatizenso Mbuye,
MPINGO WA MULUNGU- Ndi Mzimu Wakuyera.
UBATIZO
3 Muwalimbikitse onse
224 Akhazikike m'mtima,
1 Mtsinje woyerawo Akhale chikhalire
Wotuluka m'nyumbayo Oyera ndi olimba;
Ya Mlungu wathuyo Mutithandize tonse
Uyeretse tonsefe. A Mpingo wa Mulungu
Ife tifikeko
88 MPINGO WA MULUNGU NYUMBA YA MULUNGU
Tikhale oyera Muchite ichi nonsenu,
Ndi okondana ndithu. Ndi chikumbutso changatu."

4 Ndiponso m'manja chikhocho


226 'Nakweza, natamandamo
1 Monga zomera zonsezo Mulungu, mtima wake mya,
Zikulua ponsepo, Nanena mawu omwewa:
Mulungu mumeretsazo,
Momwemo anawo. 5 "Chikho cha mwazi wangachi
Chitsuka mtima woda bii,
2 Munali mwana, Yesu 'Nu Cha mapangano omwewo
Wamng'ono kalelo, Chisomo cha Kumwambako.
Ndi munakula m'msinkhu ndi
Kutama 'Tatewo. 6 Chikondi chili m'chikhomu
Chodzala; 'mwani nonsenu,
3 Ndi ife tinga mbewuzo Chipitirire konseko,
Zomera m'mundawo; Ndi chikumbutso changacho."
Mumtima mutidyetsedi,
Tikule bwinomo;
4 Ndi kutsukidwa m'mwazimo 228
1 Sindili woyenera 'ne,
Mumtima mwathu mbee, Ambuye, kudzamo;
Tionetsedwe konseko Munene mawu, ndimvebe
A Mlungu ana 'ke. Okondweretsawo.

MPINGO WA MULUNGU- 2 Sindili woyenera 'ne;


MGONERO WA AMBUYE Mumtima mwanga zi;
227 Munene, ndikachiradi,
Ndilibe moyo 'yi.
1 Usiku uja kalelo
Anampereka Yesuyo, 3 Sindili woyenera 'ne;
Usiku womwe m'manja mbuu Pamtanda panupo
'Natenga mkate Iyeyo. Munamaliza mlandu phe
2 Natamndira Mlunguyo Ndi mwazi wanuwo.
Wolamulira pansipa,
Natema mkate, natitu 4 Ndilawako tsopanoli
Kwa omwe anatsatawo: Zakudya zanuzo;
Mudzaze mtima wanga ndi
3 "Ndi thupi lopatsidwali Kukonda kwanuko.
La Ine, mtenge, mudye, ndi
MPINGO WA MULUNGU UBATIZO 89
229 5 Tadzanitu, okhulupiradi,
1 Mongatu mawu anuwo, Talandira zachinsinsizi.
Ndi mtima chete phee,
Mbuyanga kufa kwanuko 6 Ndiye wa moyo wonse Mwiniyo,
Ndikumbukire 'ne. Moyo wosatha atipatsa 'fe.

2 Chakudya chakumwambachi 7 Ndiye wodyetsa anthu omwewo,


Ndi thupi lanudi; natipatsa mwazi, moyo wakewo.
Chikho cha chipanganochi
Ncha mwazi wanuwo. 8 Yesu Mbuyathu, Inu nomwe 'Nu,
Tsopano mkhalebe ndi ifetu.
3 Getsemane ndionako
Ndi nkhope yanu dwii, 231
Thukuta la pamphumilo 1 Mommuno, Mbuye, tionanetu,
La myazi yanuyi. Mommuno ndizikhudza zanu phee,
Mommuno zachinsinsi zanu mbuu,
4 Ndi mtanda uli m'maso mbuu, Mwa Inu mtima ndipumirabe.
Ndiona m'menemo,
A Yesu kufa kwanuko, 2 Mommuno, Mbuye, mkate wanuwu,
Kuthetsa imfazo. Mommuno vinyo yakumwambako,
Mommuno zolemera zanga du,
5 Pamene padzakhalapo Chisomo chanu ndidzalawanso.
Milomo yanga phee,
Mukadza ndi Ufumunso, 3 Ndilibe wondithangata 'ne 'yi,
Mukumbukire 'ne. Ndilibe wina wondisunga 'ne;
Zikwaniratu mphamvu zanuzi,
Inde, Ambuye, mphamvu nzanudi.
230
1 Mudze, anthuni, talawani 'nu 4 Tsopano nthawi yake phwandili,
Mkate ndi chikhocho cha Mbuyathu. Loyala ili m'gome mwanumu;
Ndidye ndimwere zakukomazi,
2 Kristu ndi mwini moyo wathuwu, Ndiyanjanebe nanu, Mbuyathu.
Pamtanda anafera ifetu. 5 Chakudya ichi chidzapita du,
Chizindikitsa za Kumwambazo;
3 Anatifera nsembe Iyeyo, Zosapitazo tidzalawatu,
Ndiye Wamsembe wake Iyenso. Za Yesu mwini wakukondako.
4 Imfa ndi mdima zinathawa zii! 6 Tikadya phando zaka zonsezi,
Ndipo chisomo chikuwala mbuu. Ndipo zakudya zimalozatu
90 MPINGO WA MULUNGU MGONERO WA AMBUYE
Kuphwando lija la Kumwambako, 2 Ndifuna kumva Inu,
Komwe tidzadya kwa Mulungutu. E, Mawu anuwo,
Ndisamve za Satana
Zonyenga zakezo;
232 Adani anga onse
1 Ndinamva njala, Yesu, Andizingiratu;
Ya mtima wakusowa; Mukhaletu pafupi,
Mndidyetse ngati mana Mundithangate 'Nu.
Anagwa m'chipululu.
3 A! Yesu mwapangana
2 Ndimamva ludzu Yesu, Ndi anthu anuwo
Mulowe mwanga lero; Adzakhala ndinu
Mndimwetse ngati madzi Ku Dziko lanulo;
Anatuluka m'mwala. Inenso ndapangana
Ndisabwerere 'yi;
3 Ndi mkate wanu, Yesu Mndipatse mphamvu yanu
Ndi thupi lobvulala, Ambuye ndinudi.
Mndilimbitse, Mbuye,
Mundikhutitse mtima. 4 Mundionetse, Yesu,
Mapazi anuwo,
4 Mwa chikho chokumbutsa Ndidzapondera awa
Chikondi chopambana, Munjira monsemo;
Mndipatse moyo wanu, Ndithangateni ine
Ndikayanjane nanu. Ndisalefuke 'yi;
Mundilandire m'Mwamba
5 Mndidyetse m'chipululu Ndikamwaliradi.
M'ulundo wanga wonse;
Mndimwetse, ndipirire
Osalefuka konse. 234
1 Mundimvere, Mbuye wanga
Nkana ine ndimalakwa,
233 Koma ndinu moyo wanga;
Mbuye, mkhale ndine.
1 A! Yesu, ndapangana
Kutumikira 'Nu 2 Ndine mlendo pansi pano,
Ndi moyo wanga wonse,
Msanditaye m'dzanja lanu,
Mbuyanga ndinutu;
Mundisunge mwana wanu;
Mukhaletu pafupi
Masikku onsewo,
Mbuye, mkhale ndine.
Sindidzaopa konse, 3 Munafera ine kale
Mutsogolereko. Kuti mukandimasule,
MPINGO WA MULUNGU MGONERO WA AMBUYE 91
Lero lino mndinyamule; MPINGO WA MULUNGU-
Mbuye, mkhale ndine. ZOPEREKA

4 Mundidzze ndi chikondi,


236
1 Ambuye, Mwini zonsezi,
Mndiyeretse m'mtima monse,
Ulemu tiperekadi;
Chifuniro change mthyole;
Chikondi tionetsanji?
Mbuye, mkhale ndine.
Mwatipatsatu.
5 Imfa ikandifikira,
2 Dzuwa ndi mvula yonseyo
Inu ndidzakangamira;
Ndi mame mwatipatsanso,
Ndikalowa ine m'mdima,
Masika 'dzera kwanuko;
Mbuye, mkhale ndine.
Mwapatsatu.'

3 Mwapatsa Mwana wanu, ndi


235 Mapulumutsa dzikoli;
1 Anu Mbuye ndifetu! E, zaulere zonsezi
Mutimvere kwanuko; Mwapatsatu.
Anu tikhalirebe
Kuno ndi Kumwambako. 4 Tibwezeretu bwanjiko?
Ziperewera zathuzi;
2 Anu Mbuye ndifetu! Ndi moyo tili nawowo
Mwanu tipumiredi; Mwapatsatu.
Ndinu Mbuye wanthu 'fe,
Mutisunge nthawizi. 5 Ambuye zathu zonsezi
Kwa Inu tibwezeredi;
3 Anu Mbuye ndifetu! Tingopereka zanuzi;
'Dikireni tonsefe; Mwapatsatu.
Moyo ndinu, n'choona,
M'njiramo tiyendebe.
237
4 Anu Mbuye ndifetu! 1 Peturo 'nafusa Hananiya:
Ndife nkhosa zanuzi; "Zopereka zili kuti?"
Mwanu tibisalemu, Hananiya ananena:
Mwanu mosungikadi. "Zopereka ndinapereka.”
Munthu aganize
5 Anu Mbuye ndifetu!
Zimene anachita Hananiya;
Tsogolani nthawizo;
Mtiyendetse m'moyomu Munthu aganize
Kunkabe Kumwambako. Njira yakuunika.
92 MPINGO WA MULUNGU MGONERO WA AMBUYE
2 Nthano ya Hananiyayo Ndi wofatsa ndi wabwino
Inali yodabwitsatu; Ndi woyerayeradi,
Ananyengatu Peturo: Kuti tiyenere Dzina
"Zopereka ndinapereka." La Mbuyathu Yesuyo.

3 Ife tonse tichenjere 5 Tisaiwalire 'bale


Tingadzachite zomwezo; Athu osadziwa 'Nu,
Tisaname ndi kunena: Akulira ndi odwala
"Zopereka ndinapereka." Tiwapemphereratu;
Titsanzenso Mbuye Yesu
4 Mulungu akondadi leroli Ndi k'wathangatira 'wo.
Wopereka mokondwera;
Tikapereka motero 6 Dalitseni, Mbuye, zonse
Tidzalandira dalitso. Zomwe taperekazi,
Mzilandire, nsambe yathu yonse
238 Tikuyamikirani.
1 Mbuye wathu mutipatsa
Zonse tili nazozo, MPINGO WA MULUNGU-
Mutikomeratu mtima ZOLALIKIRA
Osaleka konseko, 239
Mutikonda, mutisunga, 1 Polenga dzikoli,
Mutisamalira 'fe.
Pakumva Inudi,
Kwayeratu;
2 Dzuwa, madzi, kudya, mpweya, Mumve pempheroli,
Moyo, zonse nzanuzi, Ndipo pamenepo
Si za ife, nzaulere, Palibe mawuwo,
Tingozilandiradi; Muwaletu.
Zifumira kwa Atate
Wotikondakondatu. 2 Inu wakudzatu
Kuwachiritsadi
3 Monga tilandira, Mbuye, Anthendawo,
Mtiphunzitse tonsefe Kupatsa moyowo,
Tipereke chuma chathu Kuona m'masomo,
Ndi kusangalalatu; Pa anthu onsewo
Zakukhalala m'manja mwathu; Muwaletu.
Tiziyese nzanudi.
3 Mzimu woonadi
4 Tikhaletu nawo, Mbuye, Ndi wachikondicho,
Mtima wosauma 'yi Idzanitu;
MPINGO WA MULUNGU ZOPEREKA 93
Muunikepo 241
Pali zamdimazo,
1 Anthu akum'mawa
Pa dziko ponsepo Nanka msangako,
Muwaletu. Nzure 'nali nazo,
Nafatsansowo;
4 Inu Atatuwo, Nanka kuli Mwana
Wodala Mlunguyo, Anabadwayo;
Timveretu; Anatsogozedwa
Pa dziko ponsepo Ndi nyenyeziyo.
Muchotse mdimawo,
Mutume Mawuwo, 2 Anapeza Mwana
Muwaletu. Ali m'kholamo,
Namgwadira Iwo
Mbuye wawoyo;
240 Anthu onse omwe
1 Adzapambana Yesu ponse Ali pansipa,
Pakuyenda dzuwalo; Azitsata Mbuye
Adzamverabe namgwadira Ndi nyenyeziyo.
Pa dziko lonse pansipa.
3 Mu ulemerero,
2 Sadalekeza kuyamika Yesu m'Mwambamo
Ndi kuimbaimbabe; Muli eni ake;
Adzapemphera nsiku zonse Anthu onsewo
Natchula Dzina lakelo. Osadziwa konse,
Akutalinso,
3 Pomveka konsekonse mbiri Akokedwe iwo
Yake ya Wokondayo, Ndi nyenyeziyo.
Ang'ono akwezanso mawu
Poimba nyimbo zawozo. 4 Akukhala kunja,
Osokeranso,
4 Ufumu wake udalitsa M'wawalire Mbuye,
Osauka onsewo; Asagone 'wo;
Otopa amapuma chete, Amumdima omwe,
Magoli amathyoka thyo! Olemedwanso,
Mtsogoleri wawo
5 Zolengedwa zonse zidze Ndi nyenyeziyo.
Kugwadira Mfumu yathu,
Amlemekeze akumwamba, 5 Paulendo wathu
Tiimbe pansipa: Amen. Tili pansipa,
Muwalire tonse
94 MPINGO WA MULUNGU ZOLALIKIRA
Tili m'njiramo; .......momwemo
Mutitsogolere
Anthu tonsefe, 2 Mbendera yake ikupiza
Mutifitse tonse ......m'mlengalengamo,
Ndi nyenyeziyo. Kufanana ndi nyenyezi younika
.......m'mdimamo.
242
3 Ankhondo a Mulungu 'nu, yendani
1 Tamva mawu amwewo
.......m'njiramo,
Atitu: Yesuyo
Mitima yanu yonseyo iyeretsedwe
Mpulumutsi ndiyedi,
.......mbuu!
Yesuyo, Yesuyo.
Pita m'midzi monsemo.
4 Tsatani Mbuye Yesuyo ndi mtanda
Dziko lonse limvetu,
.........wakewo;
...Pita iwe konseko,
Mlaliketu Uthengawo kwa anthu
Mveratu Mbuyeyo.
........onsewo.
5 Musamaopa kanthu 'yi, tamani
2 Imbadi za Iyeyo,
........Yesuyo;
Amvetu anthuwo
Kaimbireni nyimboyi ndi mphamvu
Kuti Yesu 'nafadi
........zonsezo.
Kalelo, kalelo.
Atikonda ifetu,
6 Zipata zatsegudwa mbee! Za
Natifera indedi
........m'dziko monsemo;
Kuchotsera tchimoli,
Ambuye wapambanatu ndi mtanda
Yesuyo, Yesuyo.
........wakewo.
3 Bukitsani mawunso
Konseko, konseko;
Kaitane anthuwo 244
Ponsepo, ponsepo. 1 Pamaiko pali mdima,
Kodi wina samvatu? Penya mtima chetetu;
Pitako, pitako 'we; Leroli malonjezano
Angofuna onsewo Angokwaniridwatu.
Yesuyo, Yesuyo. Kondwerani, kondwerani,
Yesu muwalitsetu.
243 2 Adze amitundu yonse,
1 Zipata zachitsulo zitseguke zonse Adze akutaliwo;
.......mbee! Ayang'ane mtanda uja
Ambuye wa Kumwamba alowe Woti nji paphiripo.
MPINGO WA MULUNGU ZOLALIKIRA 95
Mbiri yanu, mbiri yanu
Ibukike ponsepo.
246
1 Anyamata a Mulungu,
3 Ponse padakhala mdima Muzigwira nkhondoyo,
Pakawale dzuwali; Mumenyane ndi Satana
Kumalire konsekonse Mzimu wakunyengayo.
Muthawitse mdima bii!
Mpulumutsi, Mpulumutsi, 2 Komwe asauka anthu
Muyeretse zonsezi. Akukhala m'mdimamo
Osamdziwa Mpulumutsi,
4 Ibukike mbiri yanu, Phunzitsani konseko.
Ifikire konseko,
Iwagwire anthu mtima, 3 Pomangidwa anthu nayo
Iwathyole m'katimo. M'yambo yoipitsayo,
Mphamvu yanu, mphamvu yanu, Pomwe amaopa chabe,
Idziwike konseko. Masulani golilo.

4 Walitsani nyali yanu


245 Ikachotse mdima bii!
1 Mbwere Mlungu Mbuye wathu, Mpaka ikainga zonse
Msunge zakuonazo, Zasautsa m'dzikoli.
Mudalitse anthu onse
Ndi chifumu chanucho. 5 Akutopa ndi ofoka
M'watonthoze mtima phee!
2 Mbwere Yesu Mwini moyo, Osokera, onyozeka
Ukuletu 'lemuwo; Muwafunefunebe.
Gonjetsani anthu onse,
Mpatsenso mtenderewo. 6 Achisoni, obvutidwa,
M'wathandize msangatu;
3 Mbwere Mzimu Wakuyera, Zosautsa zawo zonse
Mutitsitsimutseko; Yesu azichotsadi.
Muthawitse mdima wonse, 7 Anyamata limikani,
Muwalitse m'mtimamo. Gwirani nkhondoyi;
Yesu salephera mwini,
4 Anthu onse taukani, Satiiwalira 'yi.
Imbarani Mlunguyo;
Zichuluke zomtamanda 8 Isaleke ntchito yake
Pansi ndi Kumwambako. Mpaka anthu onsewo
Alambira Mfumu yathu,
Namgonjera konseko.
96 MPINGO WA MULUNGU ZOLALIKIRA
Onse alibe mphamvu 'yi
247 Omwewo ndithangate 'ne.
1 Anthu ali m'mdima akuitanitsa
Unikani! Unikani! 4 Ndiphunzitseni, Mbuyetu,
Alikumwazika mungawalanditse, Ndidziwe nzeru zanuzo;
Unikani! Unikani! Munole mibvi yangayi,
Ipyole yonse m'mtimamo.
........Tumizani kuunikako,
........Kuoneketu kwa onsewo; 5 Ndipumulire panupo,
........Tumizani kuunikako, Ndinene motonthoza phe!
........Nthawi zonsedi kuwaletu. Ndi mawu opumitsawo
Olema ndikanenebe.
2 Tamva aku Makedonyako atero,
Unikani! Unikani! 6 Ambuye, ndi chikondi tho!
Tititu, Ambuye tizinka komweko, Mudzaze mtima wangawu;
Unikani! Unikani! Ndinene zachikondicho,
Ndiyamikire monsemu.
3 Tisaleme pakuchita zabwinozi,
Unikani! Unikani! 7 Ndichitireni, Mbuye 'ne,
Tidziunjikire ngale zakumwamba, Monse mufuna mwanumo;
Unikani! Unikani! Kumwamba tionane mbee,
Maso ndi maso Kwanuko.
MPINGO WA MULUNGU- POMANGA NYUMBA YA
ATUMIKI MULUNGU
248 249
1 Munene Mbuye 'nenetu, 1 Mulungu wa Kumwamba,
Nditsanze mawu anuwo; Tabwera kunoku
Munandifuna inetu, Ndi mtima wokondwera
Ine ndifune zanuzo. Kulowa m'nyumbayi;
Chifukwa cha zabwino
2 Nditsogolere m'njirayi Mwatichitirazi
Nkhosazo zisokerazo; Tikukuyamikirani.
Ndidyetse, Mbuye, zanuzi Leroli.
Zimene zifa njalayo.
........Inde, tikuyamikani, Atate, leroli,
3 Ndilimbikitse, Mbuye, nji! ........Mwatimangira 'fe kuno
Pamwalapo ndiimebe; ........Kachisi wanuyu!
MPINGO WA MULUNGU ZOLALIKIRA 97
........Ndi ulemerero wanu Waulemerero wonse
........Mudzaze m'nyumbayi; Ndi wamphamvu ponsepo.
........Muyeretse, mudalitse munomu.
UKWATI
2 Tikondwa tonse ndi kukuthokazani Nu
Poyamba kupemphera
251
Ndi kuimbiramu; 1 Anakwatira kale
Mommuno nsiku zonse Pa Edeni pajapo;
Mukhale nafetu, Ulipo lero lino
Monga angelo anu Mdalitso womwewo.
M'Mwambamo.
2 Awiri aimamu,
3 Ikhale ngati nyali Mwamuna ndi mkaziyu;
Yowala nyumbayi, O! Mzimu Wakuyera,
Yakutsogoza onse Madalitso mpatsetu.
Ophunthwa m'mdima bii;
Akunja ndi Akristu 3 Mulunzanitse awa,
M'wapulumutse ndi Atate, leroli;
Kuunika kotuluka Munakwatits' Adamu
Munomu. Ndi Hava kalelo.

4 Mukhale nawo, yesu,


250 Mongatu kalelo
1 Kristu ndiye mwala wathu, Ukwati mnadalitsa
Kristu timangirapo; Pa Kana pajapo.
Wosankhidwa ndi Mulungu,
Atimange tonsefe; 5 M'wasunge, m'wayendetse
Iye ndi Mthandizi wathu, Munjira yanuyo,
Timkhulupirira 'Ye. Akhale ndi kudala
Pabanja pawopo.
2 Mudalitse nyumba yathu;
Mbuye, nthawi zonsetu
Muthandize anthu onse 252
Odza kuphunzira 'mu, 1 Yehova Mlungu wathu,
Ndi antchito anu omwe Amene mumapatsa
Odza k'waphunzitsa 'mu. Zipatso za chikondi
Polenga anthu anu,
3 Tiyamike Mlungu 'Tate, Mupatse awa 'wiri
Tiyamike Mwanayo, Mitima yokondweretsa,
Tiyamike Mzimu wake, Yofana m'munda muja
Onse omwe Mmodzitu,
98 POMANGA NYUMBA YA MULUNGU
........
Munayendamo kale. Mulungu wawo mukhalenso
........Mulungu wa anawo.
2 Mbuyathu wokondedwa,
Pokhala m'dziko muno 3 Tikasokera m'njira mutilondolere
Munadza ku ukwati, ........ ndithu,
Ukwatiwu mukonze, Chakudya ndi chobvala mutipatse
Mukhale nafe pano; ........ tsiku n'tsiku.
Iwowa m'wadalitse
M'chifundo chanu chonse. 4 Mtifungatire ndi mapiko paulendo
........pathu,
3 Ndi Mzimutu Woyera E, tikafike okondwera kwa Atate
Mufike nayo mphamvu, ........wathu.
Mukatsagane nawo
Akupangana omwe; 5 Tipempha madalitso ano mpatse ife
Mupatse 'wo chisomo ........tonse;
Chokometsa mtima; Tisankha Inu ndithu Mlungu wathu
Chikuletu chikondi ........nthawi zonse.
Chitsanzo nchanu chomwe.
254
4 Mulungu mwa Atatu,
1 Mlungu wathu mwatifitsa
Atate, Mwana, Mzimu,
Kufikira leroli;
Tikhaletu wokondwa
Moyo wathu munasunga
Ndi Inu m'chiyanjano;
M'njira yonse yathuyi;
Titama Inu Mlungu,
Mtsogoleri wathu ndinu
Wokonda ife ndinu;
Paulendo pomwepo;
M'ulendo wathu wonse
Tingakutameni bwanji
Tiyende m'chikondano.
Kaamba zonse zanuzo?

CHAKA CHATSOPANO 2 E! chisomo chosaleka


253 Tichiona kalelo;
Masungidwe ndi chikondi
1 Mulungu wa Yakobo Inu, mdyetsa Zikalimo momwemo;
........anthu anu, Pausana, pausiku,
Kalelo munatsofolera makolo Muli nafe ponsepo;
........athuwo. Madalitso anu omwe
Tili ndi ambiriwo.
2 Tsopano tipereka mapemphero athu
ano,
POMANGA NYUMBA YA MULUNGU 99
3 Tinayenda muli mdima Mphamvu zosachimwa konse;
Wotidetsa nkhawawo, Zoipitsa mtichotsere zonse.
Pena tinangosauka Mtithandize tizimvera
Ndi zobvuta zathuzo; Kuyambira leroli,
Koma Inu munalimo Ndi kugwira ntchito zanu
Mumitambo yomweyo, Chaka chatsopanochi.
Nafe tinathandizana
Ndi mdalitso wanuwo. 4 Inde, 'Tate, mtiyendetse
M'njira yolungamo yanu,
4 Ena atsagana nafe M'mtima mwathu mtiyeretse
Natsiriza njirayo, Kuti tikondane nanu.
Nafikira kuli Inu, Zaka zonse muli nafe,
Natilindirirako; Sitiopa konse 'yi.
Tithadi ulendo wathu 'Tate tikkuthokozani
Ndi kupita komweko, Chaka chatsopanochi.
Mutitsogolere 'Tate
Kukuwala kosatha. DZINJA NDI MASIKA
256
255 1 Tilimalima m'minda,
1 Mbuye, tikuthokozani, Tibzala mbewu zathu,
Ndinu mwatitsogolera; Komatu zibvumbidwa
Zaka zonse mwatisunga; Ndi Mlunguyo wamphamvu.
Tiyamika mokondwera, Dzuwalo awalitsa
Zotibveka, zotidyetsa, namatumiza mphepo,
Mphamvu, moyo zonsezi; Mbewuzo nameretsa
'Tate tikuthokozani Mulunguyo wabwino.
Chaka chatsopanochi.
........Mphatso zonse zathu
2 Ndinu mwatithangatira ........Zifunika wa Mulungu,
Pakuona zosautsa; ........Tilemekeze Mbuye wathu,
Polefuka ndi podwala Atikondadi
Ndinu mwatitsitsimutsa. 2 Wolenga ndi Yemweyo
Munatiteteza bwino Wa zinthu zonse zathu;
Tili ana kalelo, Maudzu ameretsa,
Ndipo zomwe mwazichita Nayatsanso nyenyezi.
Chaka chotitheracho. Mphepozo zonse zimva,
3 Chaka chino mutipatse Nyamazo aziweta;
Sadzaiwala konse
Anake kuwadyetsa.
100 CHAKA CHATSOPANO
3 Tiyamikira 'Tate, Muwapulumutse 'wo;
Zabwino zonse zino, Zopweteka zawozo
Kubzala ndi kukunkha Ziwathere zonse phe;
Ndi moyo tili nawo. 'Dzani mu Ufumu ndi
Kuninkha Inu Mbuye Kwasonkhetsa onsewo.
tilibe mtulo wina,
Komatu tipereka 258
Mitima yoyamika. 1 Oyamika Mlungu mbwere,
Za masika mudzaimbe;
Dzinthu zathu takolola,
257 Siziwonongeka m'minda.
1 Yamikani nonse 'nu, Mlungu Mlengi asamala,
Pomwimbira nyimbozi Zotisowa, akonzera;
Za masika athuwa; Mlowe m'nyumba ya Chauta,
Potumiza mvulayi, Mkweze nyimbo zamasika.
Mlengi wathu yemwedi
Atipatsa zonsezi; 2 Dziko lonse nla Mulungu
Timwimbire m'nyumbayi Kuti limbalire dzinthu;
Za masika athuwa. M'munda zonse zimamera...
Zakukoma ndi zoipa;
2 Dziko lathu lonseli Mmera udza, bwino ngala,
Nla Mulungu yemweyu; Maso omwe amakwima;
Atumiza mphatsozi Mutilole, Mwini dzinthu,
Zakutilimbitsadi, Tikakhale dzinthu zanu.
Mmera wathu wonsewu,
Mbewu zathu zonsezi; 3 Adzabwera Mbuye wathu
Timtamande Mbuyeyu Kukulola dzinthu zawo;
Wotipatsa zonsezi. M'munda mwawo akachotse
Minga ndi zoipa zonse.
3 Nthawi yina Mbuyeyu Adzatumanso angelo
Adzafika pansipa, Minga akaponye m'moto,
Nadzakonza zonsetu; Koma tirigu amsunge
Zosakondweretsazi M'nkhokwe yake nthawi
Naziponya m'motowo, ....zonse.
Koma m'nkhokwe mwakemo
Mudzadzala mbewu tho!
Zomkomera bwinotu. 259
1 Chifukwa cha zokoma mtima zonse za
4 'Dzani Mbuye msangatu, .......ulerezo,
Msonkhanitse zonse phe; Timlambire Mbuye;
Anthu anu onsewa Tikweze nyimbo yathu yakukondwa
.......
DZINJA NDI MASIKA 101
kuli 'Ye, Timlambire Mbuye;
Timgwadiretu. Kumene moyo wa anthu
...okhulululukidwa
2 Dzinja lokondweretsa lafikanso, uli wokomatu,
......litapumatu, Timgwadiretu.
Timlambire Mbuye; Alaluya, Amen!
Mvula igundanso, Mulungu wotikonda
.......'fe, ULENDO
Timgwadiretu.
260
3 Dziko lonse lilikukondwa, 1 Mlengi wathu Wakuyera,
...mlengalenga mpheponso, Mutimvere 'fe,
... Timlambire Mbuye; M'wasungire akutali,
... Zapansi pano zonse zimtamandire Bwinodi.
Mulungu wathuyo,
Timgwadiretu. 2 Mbuye Yesu, myandikire,
M'wakondweretsebe;
4 Maluwa abwino aphuka m'mapiri Mulimbitse mphamvu zawo
ndi m'madambomo, Zonsezo.
Timlambire Mbuye;
Masamba awisi ang'ono 3 Akaona masautso
...agwedezekanso, Mkhale nawodi;
timgwadiretu. Akondwere mwa chikondi
Chanucho.
5 Zanu zapansi nzokoma Mbuye;
...tikondwera 'fe, 4 Mpulumutsi wakukoma,
Timlambire Mbuye; Muwagwirize;
Koma kwanu Kumwamba komwe Nsiku zonse akulemekezeni
...kwapambanatu, ........(Akule-mekezeni)
Timgwadiretu.
5 Mzimu wanu Wakuyera,
6 Nafenso tidzadzuka kwa 'ke ngati Awayeretse;
...maluwawo, Agonjetse ndi chisomo,
Timlambire Mbuye; M'nkondoyi.
Oyera mtima adzabvala mbuu!
...Pakudza Kristuyo, 6 'Tate, Mwana, Mzimu, ndinu
Timgwadiretu. Mlungu mmodzitu,
Muwasunge m'fupi mwanu
7 Tidzakhala naye nthawi zonse ndi Ponsepo.
...kuimbako,
102 DZINJA NDI MASIKA

261 263
1 Yesu, munditsogoza 1 Mlungu, Inutu,
M'njira yanga yonseyo; Mwalenga dzuwali,
Wakunditsogozatu Nyenyezi, mwezi mbee,
Ndinu, mundisungetu; Ndi dzikoli.
Inde, paulendowo
Mundisunge kolimba. 2 Koma ineyu
Simuiwala 'yi;
2 Monga may' asusuza Mundisamala 'ne
Mwana wake polira, Ndisagwe 'yi.
Wakunditonthozatu
Ndinu, munditonthoze, 3 Mbuye, Msungi 'Nu,
Inde, m'njira yanuyi Mutuma indedi
Munditsogoleretu. Za moyo wangawu
Zokomazi.
3 Mbuye, ndinu wamphamvu,
Mumatola ananu, 4 yesu Mwanatu
Anthu onse pansipa Anafa imfayo
Ali otaikatu; Achotsa zoti bii;
Muchitire chifundo, Nadzukanso;
Muwatole onsewo.
5 Kuti m'Mwambamo
NYIMBO ZA ANA- Ndikatamandetu
MULUNGU MTETEZI Wondisamalabe,
262 Mbuyangayu.
1 Mlungu ali nane;
Amadziwazi NYIMBO ZA ANA-
Ndizinena, penanso KUBADWA KWA KRISTU
Za mumtimamo.
264
2 Mlungu ali nane 1 A! Mulungu,
Ndi usikuwo, ...A! Mulungu
Nandiona momwemo Anatuma Mwana wake
Mu usanamo. Uja, ndiye Yesu.

3 Mlungu ali nane; 2 Anabadwa,


Zachinsinsizo Zachinsinsizo
Zosaonekerako Anabadwa,
Azidziwatu. Ndi Mariya mbeta ija
ULENDO 103
M'Betlehemu muja. 3 Falitsani mbiriyi,
Inudi abusa 'nu;
3 Ndi angelo, Nkhosa zanu zonsezo
...Ndi angelo Mwasiy'ranji m'phirimo?
Anaimba: "Ndiye Yesu
Mpulumutsi wanu." 4 Pochezera m'dambomo,
Tinaona 'ngelotu
4 Alanditsa, Oimbira mawuwo
Alanditsa A mtendere pansipa.
Ife anthu muzoipa
Zonse tazichita. 5 Mwana wakuyera 'Nu,
Munakonda ifedi;
5 Yesu Mfumu, Munasiya kwanuko
Yesu Mfumu, Ndi kufika pansipa.
Timagonja, mutisunge
Moyo wathu wonse. 6 Mtiphunzitse bwinotu,
Mwana wakuyera 'Nu,
6 Mutitsuke,
Tifanane nanudi
...Mutitsuke,
...M'mwazi wanu, tikakhale
M'makhalidwe anuwo.
Ana anu tonse.
266
265 1 Tiimbe ndi kulalikira
1 Taonani m'kholamo Mthenga wa chikondicho
Mwabadwira Mfumuyo Anamva Mlungu m'Mwambamo
Yakulonjezedwadi, Kulira kwathu pansipa.
Nsembe yathu ndiyeyu.
(Ndikhulupirira Yesu
Kondwerani nonsenu Wobadwira m'kholamo;
Pomvetsedwa mbiriyi Iye ndiye Mfumu yathu,
Yakumveka m'mzindamo: Timtame nthawi zonse.)
"Wabadwira m'Betlehemu."
2 Kwa ife lero anabadwa
2 Adagona m'ndyeromo Mwana wa Mariyayo,
Wochokera m'Mwambayo, Pamsinkhu, inde mn'gono koma
Adasiya mpandowo Mwini dziko lonseli.
Yesu Kristu Mfumuyo.
3 Anadza nazo mphatso zake
Anatikonzeratu;
Anatseguliradi
104 NYIMBO ZA ANA KUBADWA KWA KRISTU
Pakhomo pa Ufumuwo. Inu nonse ana 'nu.

4 Ambuye, tikutamandani 3 Taukani, taonani


Tsiku lakubadwali, M'mwamba monse mwakuyera;
Mwa Inu tonse tikondwera, Amithenga a Mulungu
Tisekera tonsefe. Aimbabe nyimboyo.
Yesu Kristu anatsika,
5 A! Yesu Mbuye wakuyera, Anachoka kwawoko;
Munagona m'kholamo; Lero lonse tiimbenso
Mudzikonzere leronso Nyimbo yathu yomweyo.
Mugona m'mtima mwangamu.

6 Ulemerero m'Mwambamwamba 268


Ndi mtendere pansipa; 1 Kale m'mzinda wachifumu
Tiimbe nafe nyimboyi, Munalimo m'kholamo,
Timyamike Mbuyathu. Momwe mkazi anaika
Mwana wake m'ndyeromo,
(Yesu ndiye Mfumu, Ndiye mkaziyo Mariya,
Yesu ndiye Mfumu! Yesu Kristu Mwanayo.
Ndikhulupirira Yesu
Wobadwira m'kholamo.) 2 Uyu 'natsikira kuno,
Mlungu Mbuye wathuyo
Anabadwa uyu m'khola
267 Anagona m'dyeromo.
1 Ana inu, ana inu, Mwa osowa ndi oipa
Taukani, ndi kumvera Yesu anakhalamo.
Amithenga akumwamba;
Anafika kalelo, 3 Mwa ubwana wake wonse
Natiuza Mpulumutsi Anakula m'mtima phee!
Anabadwa pansipa. Anakonda, anafatsa,
Zaka zonse, tsiku lomwe Amay' wake namvabe;
Umamveka mthengawu. Ndipo ana nonsenu,
Mukamtsate bwinotu.
2 M'nyumba zonse ponseponse
Zimamveka nyimbo izi, 4 Ndipo Mwana uyu Yesu
Kuti Yesu anabadwa, Anakulakulabe;
Anagona m'kholamo. Ndi wamng'ono ndi wofoka,
Anafika Mpulumutsi Anangonga enawo.
Wotikondweretsadi, Nsoni zathu anazimva
Kondwerani, kondwerani, Ndi chimwemwe chathunso.
NYIMBO ZA ANA KUBADWA KWA KRISTU 105
NYIMBO ZA ANA-
5 Ndi chifukwa atikonda, KUFERA KWA KRISTU
Tidzampenya masowa, 270
Kuti Mwanayo wofatsa
1 Kale anthu m'kholamo
...Ndiye mwini m'Mwambamo;
'Napembedza Mwanayo.
Atengera ana ake
Komwe adapitako. Ndiye Mbuye, Mfumu yanga,
Ndiye Mbuye wa Kumwamba.
6 Koma sitimpenya m'khola Agwadire anthuwo,
Muli ng'ombe momwemo; Timtamande Mfumuyo.
Ayi, tidzamwona m'Mwamba
Muli Mlungu 'Tatewo. 2 Wosauka Iyedi
Ana akuyera mbuu Anagwira ntchitozi.
Adzamzunguliratu.
3 Ndani kodi Munthuyo
Woyesedwa m'bwinjamo?
269
1 Usikuwo woyerawo! 4 Analira ndaniyo
Mwana adamlerayo Pomwalira Bwenzilo?
Akakhale Mfumuyo.
...Anabadwa m'kholamo, 5 M'munda muja ndaniyo
...Mfumu ya mafumu Mwazi wake dontho do?
Ndi ya anthuwo.
6 Iye ndani pamtanda
2 Mwanayo wa Mulunguyo Anafera 'daniwo?
Andikonda inetu,
Nan'tayira chumacho 7 Mkucha wake ndaniyo
Nadzagona m'udzumumo. 'Natuluka m'mandamo?
Ndiyamika Mbuye 8 Ndani pachimpandocho
Wanga Yesuyo. Alamula ponsepo?

3 Usikuwo woyerawo! 271


Wadzatu mtenderewo
1 Kuli kaphiri m'talimo
Ife tonse anthuwo
Kunja kwa mzindamo
Atitenga Mlunguyo.
Kwapachikidwa Yesuyo
Mlemekeze 'Tate, Nafera ifetu.
Mwana, Mzimunso.
(Kuli kaphiri m'talimo
Kunja kwa mzindawo,
106 NYIMBO ZA ANA KUBADWA KWA KRISTU
Kwapachikidwa Yesuyo Namukondweretsadi.
Nafera ifetu.)
3 Anafika 'kazi omwe
2 Zoopsya sitidziwapo Ndi tiana tawoto;
Anazitengazo, Yesu anatiyangata,
Komatu tidziwitsa 'fe Anatidalitsatu.
Anatiferapo.
4 Amithenga akumwamba
3 Anatifera tonsefe Amamyamikiratu;
Towomboledweko, Zikwi zosawerengeka
Tifike momwe m'Mwambamo Zimtamanda Mfumuyo.
Ndi mwazi wakewo.
5 Ana inu, yamikani
4 Kulibe wokwanira 'yi Bwenzi lanu lomweli;
Kulipa mlanduwo, M'Mwamba momwe mudzampenya
Wina wakutsegula 'yi Ndi kumtamandirabe.
Pakhomo pakepo.

5 Anatikondakonda 'Ye.
273
Timkonde ifenso; 1 Ananu, ziimbani,
Tizimtsatira, tithetu Aleluya, Amen.
Zintchito zakezo. Ambuye tamandani,
Aleluya, Amen.
NYIMBO ZA ANA- Kwezani mawu anu,
KUYAMIKIRA KRISTU Patsani mtima wanu,
Afuna kumva inu,
272 Aleluya, Amen.
1 Ana inu, myamikeni
Mpulumutsi Yesuyo, 2 Bwerani, kondwerani,
Kaamba ka chikondi chake Aleluya, Amen.
Ndi chipulumutsocho. Ambuye akumvani,
Aleluya, Amen.
Aleluya! Aleluya! Amatitsogolera,
Timwimbire Yesuyo. Kalelo natifera,
Aleluya! Aleluya! Kukonda salekera,
Timwimbire Yesuyo. Aleluya, Amen.
2 Iye anachoka kwawo, 3 Mbuye timlemekeze,
Anakhala pansipa, Aleluya, Amen.
Kale ana 'namwimbira Kwawo tikabwereze,
NYIMBO ZA ANA KUFERA KWA KRISTU 107
Aleluya, Amen.
Kumwamba timtamire,
Tikamgwadire ife, 275
Tikhale chikhalire, 1 Akazi anadza
Aleluya, Amen. kwa Yesu ndi anawo,
Anawaletsa anyamata
274 nawakana ndithu;
1 Mnandidzera, Ambuye, Ambuye nawapezadi,
Kumwambako, Anati: "Musatero 'yi,
Munasiya ukuluwo; Lolani ana abwere kwa Ine,
Koma m'mudziwotu munabadwamo Lolani ana abwere kwa Ine.
Munasowa pogonapo.
2 "Ndidzawalandira,
Idzani mumtima mwanga, k'wasunga m'manja mwanga;
Muli malo a Inu'mo. Ndi Mbusa wao Inetu,
msachotse ana anga;
2 Amithenga 'naimba pamlengapo, Akandipatsa mtimawo,
Nalalika ulemuwo; Adzanka ndine Kwathuko;
Koma Inu munadza mofatsatu, Lolani ana abwere kwa Ine,
Munabadwa mukholamo. Lolani ana abwere kwa Ine."

3 Zili nazotu nkhwimba zirombozo, 3 Wokoma Mbuyathu


Ndi mbalamenso zisatu; kwitana ana onse;
Koma Inu Ambuye mwapandadi Atsalanso ambiri ena
Potsamirapo mutu duu! sanamvera zake;
Sanamva mawu akewo,
4 Munaneneratu mawu a moyonso Sadziwa kuti 'natinso;
Omasula ochimwawo; "Lolani ana abwere kwa Ine,
Koma omwe ochimwa 'nanyozatu, Lolani ana abwere kwa Ine."
Nakuphani pamtandapo.
4 Afike masiku
5 Pakubweranso Inu m'Ufumuwo .......akuti anthu onse
Ndi zamphamvuzo zanunso, ...Adzamva mawu anu
Mundimvetse za kwanu . .. .....ndi kutsata inu nokha;
...Kumwambako ...Muwale mtima mwawomo,
Kuli malo a ine 'ko. ...Adziwe muwakondanso;
...Kopani anthu abwere kwa Inu,
Ukondwere mtima wanga ...Kopani anthu abwere kwa Inu.
Pakumvera zokomazo.
108 NYIMBO ZA ANA KUYAMIKIRA KRISTU
276 3 Zitsamba zakuyera
'Naponya pansipo;
1 Ana a Yerusalemu
Kukondwa kunamveka
Anatama Mbuye wawo;
Paphiri ponsepo.
Lero lomwe ife ana ambuye yemwe Mfumutu
Timwimbira nyimbo yawo. Nakwera cheteko;
Tiana toyamika
Mverani, aimba anawo, Sanatinyozato.
Mverani, aimba anawo
Zakutama, zakutama, 4 "Osana m'Mwambamwamba!"
Zakutama Mbuyeyo. Nyimboyi t'iimbenso,
Pokhala Kristu Mfumu
2 Tamva tikondane naye, Ndi Mpulumutsiyo.
Tiwerenge Mawu ake, Timtamandire Iyeyu
M'njira mwake tiyendemo, Ndi mtima wonsewo;
Tiziimba nyimbo zake. Tipite kwawo komwe
Tikaimbirenso.
3 Apunzitsi, ana omwe,
Ndi akulu, t'iimbe tonse;
Nyimbo zathu zidzakwera 278
Zikamveke m'Mwamba monse. 1 Ngolizo zilira
Za 'mithengawo,
Ndi zipata zonse
277 Zatsegudwa mbee!
1 Osanatu, osana, Kristu, Mfumu yathu,
'Naimba anawo; Mbuye wathudi,
M'kachisi wa Mulungu Wapambana monse,
Mwamveka nyimboyo. Alamulabe.
'Nalemekeza Yesuyo
Wak'wadalitsayo; Ntchito zake zatha,
Anamuyamikira Timwimbiretu;
M'ubwana wawowo. Yesu wakwera,
Timtamandetu.
2 Kuphiri la 'Zitona, 2 'Natipulumutsa
Mumpingo wa 'nthuwo, Natiferako,
'Namkupizira mnjedza Ali Mfumu ndithu
...Naimba nyimboyo. Kwa Atatewo;
Angelo akumwambako Osasautsidwa,
Napokerezanso; Osafanso 'yi,
“Osana m'Mwambamwamba Yesu, Mfumu yathu
Kwa Mlungu wathuyo.”
NYIMBO ZA ANA KUYAMIKIRA KRISTU 109
Adakweradi. 280
1 Ndikonda mbiri yomwe
3 Atipempherera Ya amithengawo
M'malo 'dalawo, Ya Mbuye, Mfumu yathu
Tinke kwathu komwe Pofika pansipa;
Ndi chisomocho; Zochimwa zindizinga,
Akonzera malo Koma ndidziwatu
Ana akewo; Anawombola ine
Yesu alipobe, Pakundikondadi.
Atikondanso.
2 Ndikondwa kuti Yesu
279 'Nakhala mwanatu,
1 Ndikondwa kuti Atate Chitsanzo atipatsa
wam'Mwamba Cha moyo wakewo;
Atidziwitsa chikondicho chake; Ndikati ndimtsatire
Ndimawerenga m'Uthenga Wabwino Zochita zakezo,
Kuti Ambuye akonda anake. Sadzandiyoza konse
Pakundikondadi.
Ndikondwa kuti Yesu akonda,
Yesu akonda, andikondabe, 3 Pakumyamika Iye
Ndikondwa kuti Yesu akonda, Ndidzamwimbiratu;
Amandikondabe. Ngakhale sindimwona
Amandimveradi;
2 Yesu ndimkonda, akondanso ine, Pakuti walonjeza
Anandifera pamtanda woopsa. Adzalandira 'ne
Wosayenera, woipa ndi ine; Ndiimbe ndi angelo,
Tsoka langalo Ambuye 'nachotsa. Pakundikondadi.

3 Mzimu Woyera akhala mwa ine,


Atsimikiza chikondi cha Yesu;
281
Ine n'tachimwa amandikumbutsa; 1 Yesu andikonda ine,
"Lapa mwana 'we, akukonda Yesu," Amatero m'Buku Iye;
Akafoka mwana wake
4 Ndikadzaona Ambuye Kumwamba, Adzamlimbikitsa Mbuye.
Sindidzaopa pokhala akonda;
Anandikonzera kalelo nyumba, Yesu akonda,
Ndidzakhalamo wokondwa, Yesu akonda,
...wokoma. Yesu akonda,
Atero m'Bukumo.
110 NYIMBO ZA ANA KUYAMIKIRA KRISTU
2 'Nafera Mbuye wanga 5 Yesu Mbuye 'Nu wabwino,
Anditsegulire m'Mwamba, M'manja mwanu ndikhalemo;
Ndi machismo anga onse Mzimu wanu mundipatse,
Adzandichotsera konse. M'mtima mwangatu mukhale.

3 Mbuye Yesu andisunga 283


M'njira ya Kumwamba kuja; 1 Yesu, ndikabwera
Andigwira m'dzanja langa Mundikondweretsa,
Ndingagweremo m'makwawa. Nsoni zanga mun'chotsera
Zonsezo.
4 Yesu andikonda ine;
Ndikadzafa tsiku lina Ndikabwera, Mbuye
Atengera ine kuno, Ndidzakondwa ine;
Ndikakhale naye kwawo. Muitana ana onse
Onga 'ne.

NYIMBO ZA ANA- 2 Yesu, ndikabwera,


KUKHULUPIRIRA KRISTU Mumva mapemphero.
Mundikonda, mnandifera
282 Inetu.
1 Yesu Mbuye 'Nu wafatsa
Muyang'anedi kamwana, 3 Yesu, ndikabwera
Mndichitiretu chifundo; Dzanja mdzandigwira;
Mundilole kwa Inutu. Nokha mdzandilondolera
Njirayo.
2 Ndimalira kwa Inutu,
Mpatse mtimawo wabwino; 4 N'takafika kwanu
M'Dziko lanu lowalalo Ndidzakhala bwino,
Mulandire mwana wanu. N'dzaonana ndi ananu,
Ndi Yesu.
3 Yesu, E, ndikufunani,
Ndinu chuma change chonse
Mtima wanu ngwofatsadi; 284
Kale munali kamwana. 1 Yesu wa Kumwamba,
Mutimvere ife;
4 Wonga Inu ndikhaledi, Tikugwadirani,
Mtima wanu mundipatse; Mwana wa Mulungu.
Yesu ndinu wokomatu, 2 Ndinu wakuyera,
Mndiphunzitse kukonda 'Nu. Mfumu yakumveka;
Ife sit'yenera,
NYIMBO ZA ANA KUYAMIKIRA KRISTU 111
Koma mutimvere.
3 Ndife akuchoka, Ndi wamphamvu yolanditsa;
Mwina tisokera; Yesu wathu, Yesu wathu,
M'njira ya Kumwamba Tidzatu tiana tanu.
Mutitsogolere. 4 Tifunitsa Inu tere,
Chifuniro chanu ndicho;
4 Mutiletse, Mbuye, Mbuye wathu, Mpulumutsi,
Lero tisachimwe; Mutikonzetu m'katimo;
Tikondane ndinu Yesu wathu, Yesu wathu,
Mutitsuke m'mtima. Mtikondebe ana anu.
5 Mukatiitana
Tikakhale kwanu, 286
Tidzayankha, "Mbuye, 1 Mzinda woyerawo!
Tsono tili pano.” Konse nkotsekako;
Kanthu koipa,
(Yesu, Yesu, Kanthu koipa,
Tikugwadirani Sikangalowemo.
Mwana wa Mulungu!)
2 Yesu ndafikatu,
Mbuyanga kwanuku;
285 Mundiyeretse,
1 Mpulumutsi, Mbusa wathu, Mundiyeretse,
Mutitsogolere ife; Mnditsuke m'mtimamu.
Mutiwete, mutisunge,
M'khola mwanu mtilandire; 3 Mbuye ndikhaletu
Yesu wathu, Yesu wathu, Mwana wokonda 'Nu,
Mnatigula ana anu. Ndi wosungidwa,
Ndi wosungidwa,
2 Ndife ana, mutikonda, Ndi mphamvu zanuzo.
M'njira mutiperekeze;
Mchotse nsoni ndi zoipa, 4 Mpaka ndabvala mbuu!
Osokera muwabweze; Wowomboledwatu,
Yesu wathu, Yesu wathu, ...Woyera mtima,
Mumve mapemphero athu. Woyera mtima,
Kwanu Kumwambako.
3 Munanena mulandira
Osauka ndi oipa;
Inu ndinu wachifundo
112 NYIMBO ZA ANA KUKHULUPIRIRA KRISTU
NYIMBO ZA ANA- Popemphera ndi poimba;
KUTSATA KRISTU Mutimvere, Yesu.
287 5 Mutiletse tisaname
1 Mbuye, tili ana anu, Ndi kunena zotukwana,
Tiyamike Inutu; Mtiphunzitse kukondana;
Zinthu zonse zili zanu, Mutimvere, Yesu.
Tingadike m'mtimamo.
Tiganize zake Yesu,
Za Kumwamba kuli 'Ye; 289
Tisachite zomsautsa, 1 Yesu atiuza tiwale 'fe,
Aziona zonsezo. Monga nyali m'mdima tiunike
mbee!
2 Amakumbukira zonse Pansi pali mdima walanitu,
Tizichitia zomwezo. Inu m'malo mwanu ndi ine 'mu.
Tidzamukomana tonse,
Sitinyazitsidwako. 2 Yesu atiuza tiyambemo,
Mukhululukire ife Ationa bwino ndi kuwalako;
Tchimo lathu lonselo; Ayang'ana pansi powala 'fe,
Mutitsogolere ife Inu m'malo mwanu ndi ine 'mu.
M'njira ya Kumwambako.
3 Yesu atiuza tiwale pa
288 Anthu ali m'mdima osaukawa;
Tiwalire onse, tonsefetu,
1 Yesu, muli pa chimpando
Inu m'malo mwanu ndi ine 'mu.
Chakuwala mbee! Kumwamba;
Mutipenya ife ana;
Mutimvere, Yesu. 290
1 Anyamata inutu,
2 Ife ana sitiopa, Anamwali inunso,
Mukabwera mutiona, Muti: "Tingachitenji,
Tamva kale mutikonda; Ang'ono ndifetu,
Mutimvere, Yesu. Kuthandiza Ufumu
Wa Yesu?"
3 Ife tikondana nanu,
2 Aphunzitse anthuwo,
tiimba nyimbo zanu,
Awalalikiredi,
tiyamika mphamvu yanu;
akukhala moipa
Mutimvere, Yesu.
Mumdima wakunja,
Alowetu m'Ufumu
4 Lero mkhale nafe ndithu,
Wa Yesu.
Posewera ndi pantchito,
NYIMBO ZA ANA KUKHULUPIRIRA KRISTU 113
3 E! ang'ono ndifetu,
Nzeru sizimafika Ndinena zakufatsa,
Kuti tingaphunzitse; Zakukondweretsa Yesuyo.
Titani tonsefe
Kuthandiza Ufumu 5 Tizikondana, tisekere
Wa Yesu? Tsiku lonse kwathuko,
Muyere m'mtimamo popeza
4 Inu nonse anzanga, Yesu ndi Woyerayo.
Tiziganiza bwino,
tinganene mofatsa, 6 Palibe mwana wakuchepa
Timverenso Mbuye Kunyamula mtandawu;
Kuthandiza Ufumu Ambuye Yesu mutipatse
Wa Yesu. Mtima wokondanatu.

5 Pothandiza amathu,
Pak'wakonda anzathu, 292
Pakusiya zoipa, 1 Usachimwe konse,
Pokhaladi bwino, Lekati kukwiya;
tithandize Ufumu Uli mwana wake,
Wa Yesu. Mwana wa Mbuyathu.

2 Yesu ndi wofatsa,


291 Yesu ndi woyera;
1 Tiana ife tingofoka, Ana ake omwe
Sitikhala 'mphamvu 'yi; Aziyera m'mtima.
Tikhoza kukachitiranji
Yesu kumkondweretsadi? 3 Mzimu wakuipa
Ukusuzumira,
2 Tiana ta Ambuye tili Umakuyesera
N'ntchito yaikuludi, Kuti ukachimwe.
Kudzichepetsa, ndi kusiya
Tchimo lili lonseli. 4 Koma usalole
Mawu a Satana;
3 Kapena m'mtima ndimakwiya, Bweza tchimo lake,
Nditukwana mnzangayo, Chita zolungama.
Kapena ndidzitama - izi
Ndilekere Mbuyeyo. 5 Yesu ndi Mbuyako,
mbuyeyo ngwabwino;
4 Mdileke kulimbna ndi Ana ake omwe
Kuwanamiza enawo; Aziyera m'mtima.
114 NYIMBO ZA ANA KUTSATA KRISTU
2 Yesu wakufatsa mtima
293 Mlendo pansi pano 'Ye,
1 Tchimo musalole, 'Natifera, natisunga,
Musadziipitse, Atitsogolere 'fe.
Myese kudzikana,
Muzilimbikadi; 3 Tamverani, aitana:
Mwamphamvu mpirire, "Ana, munditsatetu."
Mgonjetse zabiizi; Yesu, tisapite kwina,
Mpenye kuli Yesu, Tizikutsani 'Nu.
Adzakusungani.
4 Posachedwa tilekana
...... Mpemphe Mbuye asunge Osalankhalananso,
..... .Atonthoze m'mtimau, Koma tidzaona tonse
..... .Alikukufunani, Wina mnzake m'Mwambamo.
...... Akasunge inutu.

2 Mlewe oipawo,
295
Ayi msatukwane, 1 Yesu ndiye Mbusa,
Dzina la Mbuyathu Mbusa wakukoma,
Muzilikwezadi; Anyamula ana
Khalani achangau, Ake akuopa;
Oona, abwino; Tizitsata Yesu,
Mpenye kuli Yesu, Atitsogolera,
Adzakusungani. Kwina kuli mdima,
3 Yesu alandira Kwinanso koyera.
Akupirirawo;
Chikhulupiriro 2 Yesu ndiye Mbusa,
Chiwathandizadi. Atipenyetsetsa,
Mbuye athangata Mawu ake onse
Onse akumvera; Atikondweretsa.
Mpenye kuli Yesu, Mwina alangiza
Adzakusungani. Mwana wakulakwa;
Atsogola bwino,
Ife tizimtsata.
294
1 Nthawi yaubwana yatha, 3 Yesu ndiye Mbusa,
Sukulu yathu yathanso; Anafera kale
Nkhawa ndi zowawa zomwe Kuyeretsa ana
Zitibisaliranso. Nawo mwazi wake,
NYIMBO ZA ANA KUTSATA KRISTU 115
Tsono awalemba Ndikangomtsata Yesu m'njira
Ndi chizindikiro: Yonseyi.
"Ana anga onse
Andikhulupira." 4 Zondipingitsa zonse
Zolowa m'mtimamo
4 Yesu ndiye Mbusa Achotsa, nandisunga
Wakusunga ife, M'ulendo wonsewu.
Ali wachifundo Sindidzaopa kanthu,
Chachikulu ndithu; Ngakhale imfayo,
Sitiopa imfa Pomtsata Yesu yekha kunka
Akhala nafe, Kwathuko.
Yesu Mbuye wathu
Alandira ife.

297
296 1 Mpulumutsi Yesu,
1 Pompano pandikonda Mumve nyimbo yathu;
Poyendayenda 'ne; Tikuyamikani
Pawala mosekera Mumitima mwathu.
Ndi dzuwa loti mbee! Zonse tili nazo;
Ndikondwa nsiku zonse Thupi, mzimu womwe,
Ndikale m'dzikoli, Inde, moyo wonse,
Potsata Yesu m'njira yake Tipereka zonse.
Yonseyi.
... Komwe ndi chimwemwe
2 Ulendo ungoyamba ... Tidzaimba tonse,
Wakunka kwathuko; Tidzatama Mbuye
Amati: ''Udzapeza Osalema konse.
Zakusautsa 'mo."
Zobvuta ndi chisoni 2 Tiyandika, Mbuye,
Sindiziopa 'yi; M'fupifupi ndinu,
Ndidzangomtsata Yesu m'njira Tikugwadirani,
Yonseyi. Mtilandire bwino.
Inu munatsika
3 Zoipa ndi zabwino Kutifera ife;
Zakundigwerazo, Inu munakwera
Ndingonka nazo zonse Kuti titsatire.
Ndimuze Yesuyo;
Zowawa adzachotsa 3 Haya! Tipitenso
Zondiliritsazi; M'njira yomwe ija
116 NYIMBO ZA ANA KUTSATA KRISTU
Ana a Mulungu
Onse adaponda. 5 Ine ndine mlendo
Tizisiya zonse, Wa Kumwambako;
tiziyenda msanga, Kundiyandikira
Tisamachewuka Kwathu komweko.
Mpaka tapambana.

4 Tero tidzakwera 299


Kwawo kwa Mulungu, 1 M'manja a Yesu wanga
Tidzaziiwala Ndilikugonamo,
Zotibvuta ife. Mommo aphimba ine
Komwe ndi chimwemwe Nacho chikondicho.
Tidzaimba tonse, Mvera! Mudzera m'Mwamba
Tidzatama Mbuye Mawu a Yesu wanga;
Osalema konse. "Mwana, ndidzakusunga
Pano pamtima panga."
NYIMBO ZA ANA- M'manja Yesu wanga
ZA KUMWAMBA Ndilikugonamo,
298 Mommo aphimba ine
1 Ine ndine mlendo Nacho chikondicho.
Wa Kumwambako;
2 M'manja a Yesu wanga
Pansi pandikonda,
Nkhawa zonsezo zi!
Koma mpoipa.
Momwe zoipa zanga
Sizindibvuta 'yi.
2 Kwathu nkopambana,
Mommo mulibe nsoni,
Nkosachimwako;
Mommo mokoma monse;
Zosautsa zonse
Sindiliranso msozi,
Sizikhalamo.
Ndikondwa m'mtima monse.
3 Koma azibvala
3 Mtima umabisala
Mwana zoti mbuu!
M'manja mwa Yesumu;
Woachmwa konse
Mbuye, musunge ine,
M'mtima mwakemu.
Munandifera 'ne.
4 Yesu, mndiyeretse, Ndilinda mopirira
Mndimveretsedi; Mpaka wachoka mdima.
Mzimu, mndiyendetse Ndikaonana naye
M'njira yanuyi. Yesu Ambuye wanga.
NYIMBO ZA ANA KUTSATA KRISTU 117
301
300 1 Yesu adza kuwerenga
1 Yesu ndiye Bwenzi lathu, Ana ake abwino,
Kumwamba kuli kwawo; Ndi kubvala zachifumu
Amakonda tonse, Zakuwalazo zake.
Akulu ndi tiana;
Anzathu sapirira; .........Ana ake angonga
Amalekana nafe, ..........Nyenyezi zam'mwamba,
Komabe kutiyanja ...... Adzawala m'Ufumu
Saleka Yesuyo. .........Wa Mbuye Yesu.

2 Ana ake adzapuma 2 Yesu adza kukundika


Kumwamba mokondwera, Ana ake ankhosa,
Amene anamkonda Ndiye Mbusa wakufatsa
Natsaka Yeu yekha; Namalezatu lere.
Sauko ndi zobvuta
Zotitopetsa kuno, 3 Kudzachera tsiku lijalo
Sitiziona konse Msangatu msanga,
Kumwamba kwathuko. Kudzawala m'mawa wake
Pompano ponse.
3 Tidzalandirabe komwe
Zobvala za mitima
Yoyera, ndi kubvula 302
Zakale za kuchimwa; 1 Kwa Yesu ndi kwabwinoko,
Chimwemwe ndi chikondi Nkoti mbee! Nkoti mbee!
Tidzangokhala nazo, ...Kulibe zoipitsako,
Za ndewu ndi chisoni ...Nkoti mbee! Nkoti mbee!
Sitizipeza 'yi. Kuimba amaimbako,
Ndi amithenga omweo
4 Woyenera ndani kunka Akondwerera kokhako.
Kukhala ndi Atate, Nkoti mbee! Nkoti mbee!
Kuimba nyimbo zake,
Za Mpulumutsi wathu? 2 Zochimwa sizilowako,
Tidzanka ife tonse Mwayitu! Mwayitu!
Tamtsata pansi pano; Misozi m'maso mwawo 'yi,
Tiyeni ana onse, Mwayitu! Mwayitu!
Yambani leroli. Chisomo chili m'mtimamo,
Aona nkhkope yakeyo
Ya Yesu adalitsawo.
118 NYIMBO ZA ANA ZA KUMWAMBA
Mwayitu! Mwayitu! NYIMBO ZA ANA-
MAMAWA
3 Oipa tili tonsefe;
Mwaziwo, mwaziwo,
304
Wa Yesu watigulatu; 1 Dzuwa liwala, m'tulotu
Mwaziwo! Mwaziwo! Landidzukitsamo;
Tiyeretsedwa nawowo, 'Tate chikondi chanucho
Mtendere wa Mbuyathuyo Chindidalitsapo.
Ukhala nafe komweko.
Mwaziwo! Mwaziwo! 2 Dzuwa la lero lonseli
Mundisungire 'ne;
Mchotse zoipa zangazi,
303 Nanu ndikhalebe.
1 Dziko lilipolo 3 M'mtima mwangamu mlowemo,
Lokondwatu, Mwini chifundocho,
...Oyera 'khalamo, Kuti ndikafananetu
Abvala mbuu! Ndinu Mbuyangayo.
Tamvani nyimboyo;
"Mfumu tiyamikeyo, NYIMBO ZA ANA-
Mkwezeni Dzinalo, MADZULO
Mwimbenibe."
305
2 Tiye kudzikolo, 1 Yesu Mbusa, mutimvere,
Tiyeni 'nu; Dalitsani ifetu,
Musakayikebe, Ndi usiku mutisunge,
Tidzukenso bwinotu.
Muchedwatu.
Tikondwendwedi,
2 Lero lino mwatipatsa
Tchimo ndi zoipa zii! Zonse tili nazotu,
Mbuye timwona ndi Moyo womwe; miyamiko
Kukondwabe. Landireni Mbuye 'Nu.
3 Maso a m'dzikomo 3 Tchimo lathu lonse, Yesu,
Onse nga mbuu! Mukhululukire 'lo;
Mkono wa 'Tatewo Mtitengere kwanu komwe
Ngwosungatu. Kumpumulo wanuwo.
Tiye ku dzikolo,
Mgwira 'nu ufumuwo. NYIMBO ZOMALIZIRA
M'mwamba mwa dzuwamo 306
Tikhalebe. 1 Tilikuimba nyimbo yomweyi,
Yakuyamika Mbuye wathuyo;
NYIMBO ZA ANA ZA KUMWAMBA 119
Mtendere wake tiufunadi, Ndi Yesu Bwenzi lathuli.
Titapemphera tinke kwathuko.

2 Titanka kwathu mkhale nafeko, 308


Tikufunani Yesu Mbuyathu; 1 Tikutha kupemphera,
Musunge ife nthawi zonsezo, Tipita kwathu tonse;
Mutiyeretse m'mtima mwathu mbuu! Mtiperekeze, Mbuye,
Panjira zathu zonse;
3 Usiku uno mutisungedi, Titamva Mawu anu,
Khalani m'fupi m'nyumba Mawuwo ndi amoyo,
...mwathumo; Alowe m'mtima mwathu,
Mamawanso mudzatidzutse nji! Akhazikikemo.
Kuti tigwire ntchito zathuzo.
2 Ambuye, Mzimu wanu
4 Mtitsogolere nthawi zonsezo; Atikumbutse tonse,
Kuyenda tokha sitikhoza 'yi.
Atithandize lero
Ngati mukhala Mbuye m'fupimo,
Sitidzaopa kanthu kena 'yi.
Kumvera Mawu onse.
Kumudzi mkhale nafe,
Musatisiye konse;
307 Machimo onse mletse,
1 Ambuye, mtidalitsetu, Tiyere m'mtimamo.
Musunge Mawu m'mtimamu;
Muyatse moto wanuwo, ZOYAMIKIRA MULUNGU
Chikuletu chikondicho.
Pokhala moyo imfanso, 309
Ambuye mtiwalirepo. 1 Tiyamike Mlunguyo,
Anthu ndi zinthu zonsezi
2 Lalowa dzuwa, kwada bii! Ndi onse a Kumwambako
Mwapenya ntchito zathuzi; Mlungu amyamikiredi.
Taletsa mwina tchimolo,
Mwinanso tangolakwapo. 310
1 Mulungu akhale nawo
3 Mufafanize m'bukumo ulemerero ndi dalitso,
Zolakwa zathu zonsezo, Ndiye Atate, Mwana,
Ndi kutipatsa ifetu Mzimu Woyera, Mlungu mmodzi:
Mtendere wanu m'katimu.
2 Tsopano, poyamba paja,
4 Chimwemwe chomwe mpatseko
masiku onse alinkudza,
Ndi kukondana ndinunso
Mphamvu, ulemerero,
Tifuna kufananadi
dalitso, chipambano.
120 NYIMBO ZA ANA MAMAWA
312
NYIMBO ZINA 1 Mulungu, anthu 'fe
Mutidalitsetu;
311 Chisomo chiwalire 'fe
1 Yehova, Mbusa wangadi, Cha nkhope yanuyo.
Ndilibe kusowa;
Andigonetsa bwinoli 2 Potero onsewo
Mumsipu wokoma. Okhala pansipa
2 Ku madzi ake odikha Adzamva bwino msangatu
Anditsogolera; Za njira yanuyi.
Ndi moyo wanga wofoka
Aulimbikitsa. 3 Ayamikire 'Nu
Padziko ponsepa,
3 Anditsogolera m'njira Mitundu yonse ipfu'le,
Zakulungamazo; Mokondwereratu.
Chifukwa changaay', koma
4 Pakuti Mfumuyo
Cha dzina lakelo. Ndi Inu nokha 'Nu;
Mudzalangiza bwinotu
4 Ndipyola kodi chikhwawa Mafuko onsewo.
Cha mthunzi wa imfa?
Ndilibe mantha ngati 'Nu 5 Zipatso zakezi
Mundiperekeza. Labala dzikolo;
Adzadalitsa ifetu
5 Chakudya changa chabwino Mulungu wathuyu.
Mwandikonzera pha!
Pamaso pa adaniwo 6 Adzadalitsa 'fe
Mudyetse mtimanga. Mulungu mwiniyo;
Padziko ponse anthuwo
6 Mwadzoza mutu wanga ndi Adzamuopatu.
Mafuta okoma,
Mwadzaza chikho changadi,
Inde, chisefuka. 313
1 Nonse okhala pansipa,
7 Zokoma ndi zakuyanja Muyamike Mlunguyo;
Zidzanditsatako; Ndi nyimbo mtumikire 'Ye;
Ndikhala m'nyumba ya Mlungu Mubwere mokondweratu.
Ku nthawi zonsezo.
2 Yehova ndiye Mlungudi,
Anatilenga yekhayo;
NYIMBO ZOMALIZIRA 121
Amatidyetsa ake 'fe, 6 Monga m'Mwamba mupambana
Ndi nkhosa zake ifetu. Zonse pansi pano;
Choncho maganizo ake
3 Lowani m'nyumba mwakemu Apitira athu.
Ndi nyimbo zokondweratu;
Mumyamikire Mlunguyo, 7 Anthu onse a padziko
Mulemekeze Dzinali. Adzamvera Mlungu;
Adzakhala ndi chimwemwe,
4 Pakuti Mbuye Mlunguyo Nadzamtama ndithu.
Wokoma mtima ndiyedi
Woona adzakhalabe 315
Kunthawi zonsetu. 1 Tiyamike Mlunguyo,
...Tiyamike Mlunguyo,
Watidzera ndi mtendere
314 (Ndi mtendere.)
1 Muli ndi ludzu, idzani
Kumadzi amoyo; 2 Anatuma Mtetezi,
Imwani nonse kolere ...Anatuma Mtetezi,
Kuchitsime konko. Ndiye Mfumu Yesu Kristu
(Yesu Kristu.)
2 Munka kangati kulawa
Madzi onyengera? 3 Tinafunafunatu,
Musataye mphamvu yanu, ...Tinafunafunatu,
Musataye chuma. Osapeza Mpulumutsi
(Mpulumutsi)
3 Imvani Yesu akuti:
"Chuma ndili nacho, 4 Tinafuna m'phirimo,
Landirani, yemwe amva ...Tinafuna m'phirimo,
Akhale ndi moyo." Koma osampeza mommo
(Osampeza)
4 Funani Mlungu tsopano,
...Akulindirani; 5 Tinafena m'nyanjamo,
...Iye ndiye wachifundo, ...Tinafuna m'nyanjamo,
...Akulandirani. Koma osampeza mommo
(Osampeza)
5 Ali wokhululukira;
6 Yesu ndiye Mtetezi,
Imvani ananu; ...Yesu ndiye Mtetezi,
Mtima wake usiyana Wina saoneka ayi
Ndi mitima yathu. (Saoneka)
122 NYIMBO ZINA
7 Dzina lake Yesuyo, 5 Yesu ati,
...Dzina lake Yesuyo, Yesu ati: " Muzisiye
Lidzakhala nthawi zonse ...Zoipa
(Nthawi zonse) ...Zimene muzichita, muzisiye,
Muzisiye,
8 Tonse timyamiketu, Muzisiye inu nonse."
...Tonse timyamiketu,
Mpulumutsi wamuyaya 6 Titi bwanji?
(Wamuyaya) Titi bwanji ife anthu?
Ndi Yesu
316 Anatifera ife akuchimwa;
Akuchimwa,
1 Aitana,
Akuchimwa tinke kwawo.
Aitana dziko lonse,
Imvani,
Mukhaliranji chete? Aitana, 317
Aitana, 1 'Tate 'Nu,
Aitana dziko lonse. ... 'Tate 'Nu, mtione 'fe
Tadza kupemphera kwa Inu.
2 Mfumu iyi,
Mfumu iyi ya Kumwamba 2 Imvani
Ndi Yesu, ...Imvani Amfumu 'Nu
Ndi Mpulumutsiyo wa anthu onse, Mawu athu tinene lero.
Anthu onse,
Anthu onse, tinke kwawo. 3 Tipempha,
...Tipempha mdalitsetu
3 Aitana, mpingo wanu woyera uno.
Aitana inu mayi,
Ndi Yesu, 4 Imvani,
Amene anakhetsa mwazi wake; ...Imvani akunjawo
Mwazi wake, Akulira opanda Yesu.
Unagwera inu mayi.
5 Ayenda,
4 Aitana, ...Ayenda munjirazo
Aitana inu 'tate, Zakupita kuchitayiko.
Ndi Yesu,
Amene anakhetsa mwazi wake; 6 Ambiri,
Mwazi wake, ...Ambiri akufadi
Unagwera inu 'tate. Osadziwa za Krsitu Yesu.
NYIMBO ZINA 123
7 Auke, 319
...Auke akrsituwo, 1 Yesu, Bwenzi la ochimwa,
Akhale antchito anu. Yesu wondikondabe,
Ena samandikwanira,
8 M'watame, Yesu salephera 'yi.
...M'watame antchitowo Aleluya Mpulumutsi!
Alalike Uthenga wanu. Aleluya Bwenzilo!
Amakonda, amasunga;
9 Ubwere, Ndimufuna Yesuyo.
...Ubwere Ufumuwo,
Uoneke padziko ponse. 2 Yesu ndiye mphamvu yanga,
Andilimbikitsatu;
Poyesewa ndi adani
318 andipambanitsadi.
1 Perekani mtima wanu,
yesu aitana nonsenu; 3 Yesu atonthoza mtima
Osauka, amasiye, Ndikadera nkhawa 'ne
Yesu anakuferani 'nu. Pakukhala ndi chisono
Andisangalatsabe.
Perekani, perekani
Mtima wani nonsenu; 4 Yesu ndiye Mtsogoleri
Yesu akulindirani, Pakuyenda m'njiramo,
Perekani mtimawo. Ndipo ndikafuna kugwa
Andigwira dzanjalo.
2 Tsugulani mtima wanu
Nonse, Yesu akalowemo; 5 Yesu ndimafuna Inu,
Akuchimwa, Iye adzalowa Mwapambana zonsezo;
Nazo zakukomatu. Mlamulire mtima wanga,
Mndikhalitse wanutu.
3 Mtembenuke mtima wanu,
Inu osamvera Mlunguyo; 320
Yesu aitana ife 1 Walira Yesu m'dziko linoli,
tikamtsate m'njira yakeyo. Walira Yesu m'ntchito zakozi,
Walira Yesu pofanana ndi
4 Perekani mtima wanu Ambuyathu Yesu Kristu.
Kwa Mbuyathu Mpulumutsiyo,
Ndiye wakudziwa kuchiritsa ......Tiwaliretu, tiwaliretu
Anthu akuchimwatu. ......Ambuye Yesu wotikonda 'fe,
......Mlemekeze 'Ye tsiku lonseli,
......Inde tiwalire Yesu.
......
124 NYIMBO ZINA
2 Walira Yesu pazobvutazo, 5 Ndi ponse paphiri ndi padambopo
Walira Yesu pakukondwanso, Ndi makwawa, indetu,
Walira Yesu, imbani 'nu Kunakwera kupfuula .
Ambuyathu Yesu Kristu. ...Kumwambako,
"Kondwani, ndaipeza yanga!"
3 Walira Yesu wolimbitsayo, Nd' angelo a Mlungu nabwezanso,
Walira Yesu m'moyo monsemo, "Kondwani Ambuye 'napeza yawo.”
Walira Yesu; tidzaonatu
Ambuyathu Yesu Kristu. 322
1 Muthire, Yesu, m'mtimanga
321 Kukonda kwanuko;
1 Zambiri zagona m'kholamo, Mwa Mlungu ndidzalimbika,
Zosungika bwino 'mo; Ndisasokerenso,
Koma imodzi inasokeradi, Ndisasokerenso.
Nitayika m'thengomo 2 E, moto wanu woyera
Kutali kuphiri loopsalo,
Uyake mwa ine;
Kutali ndi mbusa wakeyo.
Utenthe zonse zoti bii,
Undiyeretsedi,
2 Ambuye, muli nazo zambirizi,
Undiyeretsedi.
Kodi sizifikirazi?
Koma Mbusa nanena, 'Yangayo
3 Munagwa pa Atumwiwo;
Yatayika naneyo;
Dzazani mwa ine;
...Ngakhale njira njoopsadi,
Mzimu wamoto Woyera,
Ndilinga kuphiri kuipezanso."
Ndipempha mudzetu,
Ndipempha mudzetu.
3 Koma zina sizinadziwa ayi,
Makwawa 'napyola 'ye,
4 Ndikhazikike inetu,
ndi mdima woopsa wa usikuwo
Mumtima muli mwai;
Ambuye nailonda yake.
Ndi Yesu ndikondanetu,
Anamva kulira kutaliko,
Si kanthu kena 'yi,
Naipeza yofoka, yakufayo.
Si kanthu kena 'yi.
4 Ambuye, wakuti ndi mwaziwo
Panjira ponsepo? 323
"Ndaukhetsa potsata iwetu, 1 Atate Wamkulu ndi wamphamvu
Kukubweza ku kholalo," .......zonse,
Ndi m'manja mwalaswa bwanjimo? Atate Wamkulu ndi wamphamvu
"Ndalaswa ndi minga pofuna iwe." .......zonse,
Khalani ndi chifundo ndi ife lero.
.......
NYIMBO ZINA 125
2 Ifetu kuchimwa, Mbuye, 5 M'mwazi wake tisambamo;
Ifetu kuchimwa, Mbuye, Zichotsedwa zakuipa zathu zonse.
Mutume Mzimu wanu atiphunzitse.
(Ona Mwanawanakhosayo
3 Mwa Mzimu mulowe mumitima Wakusenza zakuipa
...yathu, Zathu zonse.)
Mwa Mzimu mulowe mumitima
...yathu,
Zoipa zathu zonse mtiululire. 325
1 Yesu anali khanda
4 Tafika kwa inu mutiunikire, M'Betlehemumo;
Tafika wa inu mutiunikire, Mngelo anasimba za
Chifuno chathu chonse taleka lero. Kubadwa kwake.
......Kubadwa kwa Yesu
5 Tifuna kuchita chifuniro chanu, ......M'Betlehemumo;
Tifuna kuchita chifuniro chanu, ......Khandalo linagona
Chifuno cha Mulungu nchabwino ......M'khola la ng'ombe.
chokha.
.........
2 Mngelo anatumidwa
6 Atate, mupatse zomwe tapemphazi, Kuwasimbira
Atate, mupatse zomwe tapemphazi, Abusa a nkhosa za
Tapempha m'Dzina lake la Mpulumutsi. Kubadwa kwake.

324 3 Anapita nasiya


1 Ona Mwanawankhosayo Nkhosa zawozo;
Wakusenza zakuipa zathu zonse. Anapita kumudzi
Kukamlambira.
......Mwanawankhosa
Watisenzera 4 "Tadodoma, abusa,
.... ..Zakuipa zathu zonse. Kwachitikanji?
Mwazisiyira yani
2 Anasenza m'thupi mwake; Nkhosa zanuzo?"
Pakukhomedwa pamtanda anali duu.
5 "Posunga nkhosa ife
3 Ona pamtanda Yesuyo Kubusa kwathu
Anabvutika chifukwa cha anthu 'fe. Mngelo anasimba za
Kubadwa kwake."
4 Imva kulira kwa Yesu
Pamene anasiyidwa muimfayo.
126 NYIMBO ZINA
326 "Pemphera, ndipo udzalandira."
1 Atate, tifika pamaso panu;
Mukomane ndi ife, Mbuye wathu. 5 Ndipempha, Ambuye,
Mundidzaze n'chikondi,
2 Mitima yathu iyi nayo njanu, Mtima wangawu ukukondeni.
Muiyeretse zinthu zanu zokha.

3 Ndi maso athu awa nawo nganu,


328
Muwapenyetse zinthu zanu zokha. 1 Dziko lonse mlambire
Yesu Mbuye wathuyi,
4 Ndi manja athu awa nawo nganu, Muimbire ndi chimwemwe
Agwiretu ntchito yanu yokhayo. Dzinalo.

5 Ndi miyendo yathu iyinso njanu, 2 Mbwere nonse muone


Ithamange m'ntchito yanu yokhayo. Zomwe achita Yesu;
Nzozizwitsa, nzodabwitsa
6 Ndi milomo yathu iyinso njanu, Ntchitozo.
Ilalike Mawu anu kwa onse.
3 Aweruza ndi mphamvu
7 Ndi makutu athu awanso nganu, Ku nthawi yamuyaya;
Muwamvetse Mawu anu okhawo. Diso lake lisamala
Am'dziko.
8 Tidziperekadi konse kwa Inu
Tikakhale anthu anu okhawo. 4 Mbwere mudzamve nonse
Zamphamvu za Yehova;
Mumwimbire, mumyamike
327 Yehova.
1 Atate, ndipempha
Tsopano mundimvere, 5 Tisonkhane tonsefe,
Ndipempha kuti mundithandize. Timgwadire Ambuye;
Timlambire, timlambire
2 Ine ndili munthu Yehova.
...Wochimwa pansi pano,
...Munditsuke Mbuye, ndiyeretu 329
3 Ndalema ndathodwa 1 Mlungu akuyang'aniredi
Ndi zinthu zapadziko, Kufikira tionana;
Adzasunga nkhosa zake;
Zakhalatu goli londimanga.
Mlungu akuyang'nairedi.
4 Yesu Mfumu Inu
Mumandiuza kuti:
NYIMBO ZINA 127
E! tidzakomanansotu Mwandisiy'ranjitu Ine,
Pamapazi a Yesu; Mundikweze m'Mwambamo,
E! tidzakomanansotu; Landirani mzimu wanga."
Mlungu akuyang'aniredi.
4 Ankhondowo poona
2 Mlungu akuyang'aniredi, Zinachitika pamtanda,
M'dzanja mwake akulere, Anabaya m'nthitimo,
Ndi mapiko akubise; Munatuluka magazi.
Mlungu akuyang'aniredi. Paphirilo la Golgota
...Anaferapo Mbuyeyo
330 Nasauka koopsya
1 Potuluka m'mudzimo Ndi zoipa zathu izi.
Yesu anasenza mtanda,
Pokwera ku Gologota 331
Kukampachikatu Mbuye. 1 Tumphatumpha moyo wanga,
Pilatoyo, mfumu yawo, Sangalala ndi Mtetezi;
Inampereka kwa 'Yuda, Kuwombola kwa Yehova
Kuti amapachiketu Kwatuluka m'dziko lako.
Kufera zoipa zathu.
Mulungu wakwezekatu,
... ... (Atate 'nu, amayi 'nu, nonsenu, Mpulumutsi m'dziko lako,
... ...Onani Yesu wasenza mtanda; Wakwezekatu Chitetezo
... ...Atate 'nu, amayi 'nu, nonsenu, Wabvundikira iwedi,
... ...Onani Yesu wasenza mtanda.) Mzimu wanga 'we wafunda,
Lulutiratu moyo wanga.
2 Zoopsya zopambana
Zinachitika pamtanda 2 Bvinabvina moyo wanga,
Kuti mdima unadza, Lulutira mtima wanga;
Dzuwa linabisikanso. Wa mawuwo a Yehova
Chinsalucho cha m'kachisi Watuluka m'dziko lako.
Chinang'ambika pakati,
Myala inaswekanso, 3 Imbirira moyo wanga,
Dziko linagwedezeka. Mtendere wako wafika;
Mbendera ya Chitetezo
3 Pomwalira Mbuyeyo Waikwezetsa ndi Yesu.
Anapfuula kokweza 4 Ukondwere moyo wanga,
Naitana Atate Kuunika kuoneka,
Kupereka mzimu wake; Ndi mdimawo uthawatu;
"Mlungu wanga, Mlungu wanga, Lulutira moyo wanga.
128 NYIMBO ZINA
5 Usekere moyo wanga, 333
Ndi Yehova akufuna; 1 Lidze msanga dzuwa lanu
Wakwezatu mbenderayo Lolonjezedwa, Ambuye.
Ya Chitetezo, sekera. Mnalinena polawira
Kwa anyamata, Ambuye.
332
1 Pakuona imfayo Kuli chimwemwe m'dzuwalo
Chisonicho chikula, Lakufika Ambuye,
Ndilira misozi. Ha! Ambuye bwerani,
Ha! Ha! Ambuye bwerani.
Ndilira, ndilira,
... .... Ndilira Mbuye Yesu wangadi.
... ... 2 M'dziko lino chimwemwecho
... .. .Ndaimba ndi kulira ndi kusisima, Chakudza ndi Yesu Mbuye.
... .. .Ndimba ndi kulira ndi kusisima, Mfumu yathu ya Kumwamba
........Ha! Ha! Aleluya! Ndi dziko lonse lapansi.
........Ha! Ha! Aleluya!
........Mwasiyiranji Ambuye Yesu? 3 Adzakhala pampandopo
Wakuweruza makamu;
2 Ndinasiya amayi, Amitundu adzaima
Ndinasiya atate, Pamoso pa Mbuye Yesu.
Abale komweko.
4 Adzanena kwa anthuwo
3 Kazembe wanga m'matenda, Akudzanjatu lamanja,
Ndili m'manja mwa Mbuye. "Lowani 'nu m'chikondwero
Abale tsalani. Cha Atate nthawi zonse."

4 Zoipa zakanikadi,
Sizikhoza kuchotseka, 334
...Ndilira misozi. Amen, Amen, Amen.

5 Angelo aitana,
Aitana Kumwambako, 335
Tiyeni, tikwere! 1 Ndidze pafupi pa
Mlungu wanga,
6 Munafera pa mtanda Ngakhale pamtanda
Chifukwa cha inedi, Mundikweza;
Si cha wina ayi. Koma ndiimbabe,
Mbuye mndikhalitse,
Mbuye mndikhalitse
M'fupi Ndinu.
NYIMBO ZINA 129
2 Ngakhale kuthengo Ndi ku Betlehemuko
Ndasokera, Pakubadwa Inu,
M'mdima ndigonapa Nyumba zawo 'nakukanani.
E, pamwala;
Koma m'kulotako ... ...Mbuye Yesu, lowani m'mtima,
Ndiyandikizanso ... ...Nyumba yanu ndi mtimanga.
Ndiyandikizanso ... ...Mbuye Yesu lowani m'mtima,
M'fupi Ndinu. ... ... Nyumba yanu ndi mtimanga.

3 Pajapo ndipenya 2 Akumwambawo


Pokwerapo, Naimbitsatu
Angelo atsika Kukulemekezani;
Kumwambako, Koma monga mwana
Ndiwo akodola M'dziko munabadwa,
Kuti ndikabwere, Munadzichepetsadi.
Kuti ndikabwere,
M'fupi Ndinu. 3 Nyama za m'thengo
Ndi mbalamezo
4 Tsono poukanso Zili nazo zogonamo,
Wokondwatu, Koma Mwana wa Mlungu
Ndipeza pomwepo Analibe nyumba,
Pali Mlungu; M'mapululu nagonatu.
Ndipo masautso
Andisendezanso, 4 Munadzera ndi
Andisendezanso, Mawu a moyo
M'fupi Ndinu. Akupulumutsa anthu;
Anakaniza,
5 Pena pakufadi, Anasautsa,
N'kweza m'Mwamba, Anapachika Inu.
Dzuwa ndi nyenyezu
Zitsalira; 5 M'mene mubwera
Pomwe ndiimbanso, Kutiweruza
Ndi angelo aimbira,
Ndidza pafupi pa,
Mundiitane,
Ndidza pafupi pa
Muti , "Idza 'we,
Mlungu wanga.
Khala nane Kumwamba."
336 .. ...Mtima wanga udzakondwera,
1 Munasiyatu .. ...M'mene mundilandiranso.
Dziko lanulo, ... ...Mtima wanga udzakondwera,
E, chifukwa cha ine; ... ...M'mene mundilandiranso.
130 NYIMBO ZINA
337 Omvana ndi Yesu.
1 Kasupe ali wodzaza Omvana ndi Yesu,
Ndi wazi wa Yesu; Omvana ndi Yesu;
Omwe asamba mwa uyu Zopulumutsa onsewa
Ataya zoipa. Omvana ndi Yesu.
... ..... .Ataya zoipa,
... ...... Ataya zoipa; 338
... ...... Omwe asamba mwa uyu 1 Yesu and'itana,
... ...... Ataya zoipa. Adzandiyeretsa
Ndi mwazi wake wokhetsa
2 Woba wakufa 'napenya Pa phiri Gologota.
Kasupe, nakondwa,
Ndilikudzatu,
Ndimo inenso mwa uyu Ndidza kwa Inu;
Ndisamba ndiyera. Munditsuke m'mtimamo
.. .........Ndisamba ndiyera, Ndi mwazi wanuwo.
... ..........Ndisamba ndiuera;
2 Ndafoka, ndaipa,
... .........Ndimo inenso mwa uyu Mundilimbitsetu;
... .........Ndisamba ndiyera. Mundiyeretse konseko,
3 Mwazi wa Yesu wokondwa Ndiyereyere mbuu.
Ukhala wamphamvu
Kwa ana onse a Mlungu, 3 Atero ndaniyo?
Uchita kwombola. Ndi Yesu wabwino;
Apatsa mvani, mtendere,
Uchita kwombola, Ndi mphamvu m'mtimamo.
Uchita kwombola;
Kwa ana onse a Mlungu 4 Yesu akhazika
Uchita kwombola. Zonse za m'katimo,
Nalonga Mzimu Woyera
4 M'mene ndapenya mwazi wa
Munafoipamo.
Mabala anuwo,
Kukonda kwanu nditama
...Kwa kutha kwa moyo.
5 Nditama mwaziwo!
Nditama chifundo!
... ...Kwa kutha kwa moyo, Nditama Yesu Ambuye,
... ...Kwa kutha kwa moyo; Nditenga mphamvu 'ko.
... ...Kukonda kwanu nditama
.. ...Kwa kutha kwa moyo.
339
5 Kumwamba ndikaimbanso
1 Ndi misozi ndi chisoni
Zimphamvu za Mlungu,
Ndiliratu kwa Inu Yesu,
Zopulumutsa onsewa
NYIMBO ZINA 131
Ndi chifundo chandigwira 6 Mawu a Yesu ati: "Msangatu
ndilira kuti ndili wanu. Idza, wochedwa, lowa
m'nyumbamo."
E! kwa Inu, E! kwa Inu!
Ndilira kuti ndili wanu. 7 Msanga adzachitseka chitseko,
Adzakuuza: "Choka, chokatu."
2 Mbuye Yesu ndi Atate, Choka, choka,
Mundiona ndili wosowa. Anena chokatu.
Ndimasowa Mzimu wanu
Kuyinga zonse za mumtima. 341
1 Pamtandapo, pamtanda,
3 Mtenderewo wosanyenga Yesu 'nafera;
Ndilira ine m'mtima wanga, Pamutupo chilemba,
Kundimvetsa chimwemwetu, Chisoni ine.
Ndilira ine m'mtima wanga. Analira, "Eloi, Mlungu wanga!
Lama sabakatani,
4 Kalekale ndinathawa, Mwandisiyiranji?"
Ndinakana kumvera Inu;
Koma lero ndamva kuti 2 Kumandako, kumanda
Muli Mwini wake wa moyo. Yesu nauka;
Anaposa imfayo,
340 Watha zonsezi
1 Malo alimo m'nyumba ya Yesu, Ndikondwera, Mbuyanga 'naukadi
Ndi nyimbo zake zikuitana: Sekerani nonsenu,
Yesu ngwamoyo.
"Lowa, lowa
Tsopano lowatu." 3 Pakukwera Kumwamba
Yesu anati,
2 Mdima ufika, dzuwa lalowa, "Musachoke m'mudzimu,
Nthunzi zilipo, wadza usiku. Pempheranitu;
Mzimu Wakuyeradi adzabwera,
3 Nyumba yodyera ilikudzaza; Kuthangata nonsenu,
Idza nulowe, Mkwati anena: Kuti msafoke."

4 Chakudya ichi ndi cha iwenso, 4 Uzanitu abale,


Madzi amoyo umwe kolere. Onse alongo,
Ndi amitundu yonse
5 Onse am'Mwamba ali mowemo, Adzakondwera,
ndimo angelo akuitana: Musaope ntchitoyo yokomadi,
132 NYIMBO ZINA
Mphotho yake Kumwamba, 2 Tidzimba komweko nyimbo
Moyo wosatha. Za abwino omvera Yesu,
Sitidzamva chisoni ife,
342 Tidzakondwa masiku onse.
1 M'dziko lino tikhalamo
Utibvuta moyo, 3 Tidzatama Atate wathu
Koma dziko la mtendere Kuti Iye 'napatsa Yesu
Lili kwa Mulungu. Kuchotsera zochimwa zonse,
Ndi kutidalitsira ife.
2 Watitsogolera Mbuye,
Komwe kwa Atate,
Ndimo tidzatsata naye
344
Moyo wathu wonse. 1 Apita anzathu dzuwa lino
Kosaoneka,
3 Ndi tsopano tilindira Apita anzathu dzuwa lino,
M'dziko lathu lino; Apita anzathu dzuwa lino
Ntchito atipatsa Mlungu, Kosaoneka.
Tizigwira bwino.
A! Kumwamba
4 Ngati zakuipa zathu A! kuli a Yesu.
Zikatisautsa,
Tithawire kwa Mbuyathu, 345
Atipulumutsa. 1 Ine ndili ndi manyazi
Kuti kale lomwelo
5 Timpemphere kutipatsa Ndinanyoza kudza komwe
Mtima watsopano, Kwa Mtetezi wanga Yesu,
Kutithandizira kunka Ndati sindimfuna 'yi.
Paulendo uno.
2 Koma Iye wandipeza;
343 Ndamuona m'mtandamo,
1 Kuli dziko labwino m'Mwamba Mwa kufera ine momwe;
Lakuwala koposa dzuwa; Ndipo ndati m'mtima wanga:
Yesu atikonzera malo Mbuye, ndikufunani.
Pokhalira ife komweko.
3 Nsiku zonse kwanja kwake
Bwinoli tipita, Kunandithandizatu,
Tikumana mwa Dziko lija, Kunandichiritsatu,
Bwinoli tipita, Ndipo ndati: Mpulumutsi Ndinu
Tikumana mwa Dziko lija. ...Mbuye wangatu.
NYIMBO ZINA 133

4 Sindifuna Mbuye wina,


347
Koma Yesu yekhayo; 1 Tate, ndili mwana wanu,
Ine ndili munthu wake, Nkana ndinachimwa,
Iye anandigonjetsa Ndingolirira kwa Inu;
Ndi kukonda kwakeko. Khululukireni.

Machimo anga ngambiri


346 Osawerengeka,
1 Kondwani nonsenu, Ndingoyang'ana kwa Inu;
Mpulumutsi anadza; Khululukireni.
Onani kukhola,
Ndi mtanda ndi manda. 2 Ndinachimwa poganiza
Ndi polankhulanso,
Mlemekeze, bukitsani, M'ntchito zanga ndachimwanso;
Naferatu kale; Khululukireni.
Kondwerani, mlemekeze
3 Ndinachita mphulupulu,
Akhaladi moyo.
Ndinakunyozani,
M'ntchito zanga ndalephera;
2 Kondwani nonsenu, Khululukireni.
Anakhetsa mwazi,
Natiwombola nawo, 4 Zonse ndinakonda kale
Tikhale ana 'ke. Ndi zopanda pake,
Sindikhuta nazotu;
3 Kondwani nonsenu, Khululukireni.
Atikhululukira,
Wosachimwa nafera
Anthu 'fe oipa. 348
1 Mema nkhondoyo, wadza mdaniyo,
4 Kondwani nonsenu, Kweza mbendera ya Mbuye.
Mfumu yathu yakwera; Bvala zidazo, imba nyimboyo,
Kwa Atate Kumwamba Khazikikatu pa Mulungu.
Atipempherera.
... ...Haya, anzathu, itilinda nkhondo;
5 Kondwani nonsenu, ... ...Limbikanitu, nkhondo nja Yesu.
Adzabweranso Yesu, ... ...Musafoke, m'thyole linga lawo;
Waulemu, wamphamvu, ...... Mbuye ndiye Wopambanayo.
Kuweruza dziko.
2 Mlungu mverani, mphamvu patseni,
Tithandizeni, tipempha.
Nkhondo itatha, titapambana,
134 NYIMBO ZINA
Tidzalandiratu korona. 2 Yendani, Munthu Wachisoni,
M'mudzi wa Yerusalemu;
3 Mleke mdaniyo, mwimbe m'njiramo Angelo amapenya 'Nu
Mpaka nkhondoyo ileka. M'mene mwafera anthuwo.
Zida konzani,mantha tayani,
Pitikitsani adaniwo. 3 Yendanitu, Wansembe wathu,
Mtanda wanu mwanyamula
Watisandukira dalo,
349 Watitengera moyowo.
1 M'manda nagonamo
Yesu Ambuye, 4 Yendani mwaulemerero,
Anadikiratu Akulindirani mphotho,
Tsiku lija. Moyo wanu wosatha
Watilonjezera moyo.
.. ...M'manda naukamo
... ...
Napambana 'dani akewo; 351
.. ...Anauka kupambana imfayho,
... ...
ali moyo ndi oyera mtimawo. 1 Kamwana Yesu 'nabadwa,
... ...
Waukaka, wauka! Ndi Iye Mlungu Wamphamvu;
.. ...Aleluya, wauka! Angelo anapembedza
Mwana wakhanda Iyeyu.
2 M'manda munalibe
Yesu Ambuye, 2 Kamwana kaja 'nayamba
Nadikira chabe Kuonetsera Atate,
Alondawo. Lero anena Kumwamba:
"Tiana tidze kwa Ine."
3 Imfa yalephera
3 Tibwera ndi tianato
Kumutsekera,
Kukabatiza 'menewa;
Anachotsa zonse
Muwachitire chifundo,
Zomzingazo.
M'wapatse Mzimu Woyera.

350 4 Angelo anu asunga


1 Yendani, Mfumu yamtendere Tiana tathu tofoka;
Anthu akuimbirani; Pa njira yanu tiyenda,
Apfuuletu Hosana, Mulembe m'Mwamba maina.
Agonjeranso athuwo.
5 Mukonda nyimbo za ana,
Kokoma amaimbatu;
Yendanitu m'ulemudi,
Ndi ana athu atama
Pulumutsani anthuwo.
Atate, Mwana ndi Mzimu.
NYIMBO ZINA 135
352 4 Pemphero ndiwo mweyawo
1 Yesu Mbuye, onani Apuma akhristu;
Tadza poitana Inu; Ndi mapemphero tilowa
M'dzina lanu tifika Dziko la imfalo.
Osekera kwa Atate;
Mkhale nafe Inu nokha 5 Mutiphunzotse, Mbuyathu,
Tikaimba nkupemphera. Kupempha kotero,
Kuyandikira kwa Mlungu
2 Mbuye, Mzimu Woyera Ndi mtima wabwino.
Munapatsa ana anu
Kukalonga mumtima 354
Mawu ndimo mvanu womwe; 1 Ndisauka, ndinachimwa,
Zinthu zonse pansi pano Koma Inu mnandifera,
Sizikondweretsa ife. Ndimo ndamva mund'itana;
Mwana Mlungu, ndingubwera.
3 Mzimu, mlonge m'mtimamo
Maphunziro achifundo; 2 Ndisauka, ndimasowa
timve lero ndi mawa Mphamvu ya kuyera m'mtima,
Ndi masiku onse Yesu. Mwazi wanu wanditsuka;
Ndimo m'Mwamba tidzaona Mwana Mlungu, ndingubwera.
Tidazimva pansi pano.
3 Ndisauka, sindikhoza
Kuiletsa nkhondo m'mtima,
353 Ndi chisoni, mantha, nkhawa;
1 Pemphero ndiko kufuna, Mwana Mlungu, ndingubwera.
Kulakalakatu;
Ndi monga moto liyaka 4 Ndisauka, sindiona;
Mumtima wa munthu. Ndingudwala, ndilefuka,
Zonse ndizitaya kwa 'Nu,
2 Pemphero ndiko kulira, Mwana Mlungu, ndingubwera.
Ngakhale misozi,
Kupenyetsetsa Kumwamba, 5 Inde, Yesu, mulandira,
Mulungu mpafupi. Muchiritsa, mpulumutsa,
Mawu anu ndibvomera,
3 Pemphero ndiko kufuna Mwana Mlungu, ndingubwera.
Kwa mwana wamng'ono;
Ndiponso mawu amphamvu 6 Inde, Yesu, mundikonda,
A munthu wamvanu. Zonse zina ndazitaya;
Tsono kukakhala wanu,
Mwana, Mlungu, ndingubwera.
136 NYIMBO ZINA
355 2 Kukondwa kwa wodwalayo
1 Yesu, ndipemphera Kunali kopambana;
Mndithangate Iye anatumphatumpha,
Kukonda Inutu, Kuzungulira
E, kwambiri. Sunagoge yense.
Koposa zonsezo
Za pansi panopo, 3 Lero lino Mbuye Yesu
Ndikondane Aitana nonsenu;
Ndinu, Mbuye. Mukamvera ndi kumtsata,
Mudzakondwera
2 Kale ndinafuna Ndi mdalitso wake.
Za pansipa,
Tsopano ndilira
Inu nokha. 357
Ndifuna kukonda 1 Yesu watidzera, watidzera,
Inu kopambana Way'tana anthu onse,
Zinthu zonse Udzimvere wekha.
Za pansipa.
Aleluya, Aleluya!
3 Inu ndidzatama Aleluya, Aleluya!
Nthawi zonse, Udzimvere wekha.
Imfa ikafika
Ndidzanena: 2 Kudziwa ukudziwa,
"Ndifuna kukonda Kulibe zachisoni,
Inu, Mbuye wanga, Udzimvere wekha.
Kopambana
Zonse zanga." 3 Atumwi atummika, atumika,
Akulalika Yesu.
Udzimvere wekha.
356
1 Panalitu wakudwala 4 Yesu Mpulumutsi, Mpulumutsi
Amene anakhala Wa dziko lili lonse.
Udzimvere wekha.
Pakhomo la sunagoge,
Kuti anthu ena 5 Kumva ulikumva, ulikumva,
Amuone iye. Ungonyalanyaza.
Yenda iwe, yenda, Udzimvere wekha.
Yenda iwe, yenda,
Silva ndilibe; 6 Bwerani inu nonse, inu nonse,
Mwa Yesuyo, yenda! Mudzalandire moyo.
NYIMBO ZINA 137
Mudzimvere nokha. 4 Yesu Mfumu, ine ndisekere
(Yesu) Inu Mpulumutsi wanga
358 Pamene mukhala nane;
Yesu, Yesu.
1 Mudze kwa Yesu, musachedwe,
Kalata ilozera njira;
Amaitanatu tonsefe, 360
Bvomerani Iye. 1 Lekani kubvutika ndi zinthu za padziko,
Musekere kuti tidzaimbira Yesu.
......Tidzakondweradi m'Mwambamo
......Posonkana komwe kuli 'Ye; ......Imbira!
......Tidzakhala naye komweko Timwimbire Yesu,
......Ku Dziko losafa. Mpulumutsi wathu!
......Imbira!
2 Lolani ana, mumve Mlungu, Timwimbire Yesu,
Tsegulani mitima yanu, Tonse tidzakondwera.
Sankhani Iye, Bwenzi lanu;
Musachedwe, mudze. 2 Musadziunjikire chuma cha padziko,
Dzimbiri ndi njenjete zimachiwononga.
3 Ganizansoni, ali pano,
Mthenga wake mverani lero; 3 Koma mudzisungire chuma cha
Mawu okoma ati lero, ....Kumwamba
Musachedwe, mudze. Kumene anapita Mtsogoleri wanu.

4 Aliponso adani am'kati ndi akunja;


359 Yesu watisekera, tidzakuimbitani.
1 Mwa ine, moyo wanga ndi Yesu
5 Aliponso mabvuto, ena ndi oipa;
(Yesu) Yemwe anafera ine,
Yesu mutimasule kwa adani athu.
Ndiye anandiwombola;
Yesu, Yesu.
361
2 Mwazi wake ndi chitsime changa, 1 Ndine Mbusayo wabwino,
(Yesu) Pamene ndikasambamo Ndinafera nkhosazo;
Zochimwa zanga zidzatha; Yotayika ndaifuna,
Yesu, Yesu. Mpaka ndataya moyo.

3 Yesu Mfumu, ine ndingadzafe .........Mbulu wanding'amba m'nthiti,


(Yesu) Ngati mundisiya ndekha, .........Wanding'ambanso m'manja,
Kukhala ndekha sinditha; ........ Wanding'ambira zobvala,
Yesu, Yesu. ........ .Ndatsala waumphamwi.
138 NYIMBO ZINA
2 Nkhosa zanga zimandimva 4 Likalira llipengalo,
Ndikaziitanazo; Ndipezeke mwa Yesuyo
Ndimazipatsa moyowo, Wobvekedwa, wolungama,
Atate nazisunga. Wopanda banga konseko.
3 Atate wondipatsazo,
Ali nazo mphamvutu 363
Kuzidyetsa, kuzisunga; 1 Tiyamike Mbuye Yesu
Palibe wolandazo. Yemwe anatifera
Imfa ija yoopsetsa
4 Musaone zobvalazo, Kuwombola tonsefe.
M'kati ali fisiyo;
Musanyengedwa anthuni, IFE, tapulumukadi,
Ine ndine Mbusayo. IFE, tapulumukadi,
IMFA, imfa yoopsa ija ya pamtanda,
5 Tamverani anthu inu, IMFA, imfa yoopsa ija yapamtanda.
Ine ndine Mbusayo;
ndine Njira, ndine Khomo, 2 Panalibe mwa abale
Thawani mimbuluyo. Yemwe akadakhoza
Kupereka moyo wake
362 Kuwombola tonsefe.
1 Chiyembekezo changacho
Chamangidwa pa mwaziwo; 3 Tikondwera ife tonse
Sindikhulupira pena, Pakuona ntchitoyo
Ndingotsamira pa Yesu. Anachita Mbuye Yesu
Kuwombola tonsefe.
......Ndaima nji pa Kristuyo,
......Ndiye Chinthathwe cholimba, 364
............Maziko ena mpa mchenga. 1 Mzimu ndi mtsogoleri
M'njira yachikristuyo,
2 Nkhope yake 'kabisika, Atitsogoleratu
Ndipuma m'chisomo chake; Paulendo wathuwu.
......
M'namondwe ndi mphepo zonse, M'yoyo ikondweratu
......
Nangula wanga ali nji! Pomva mawu akewo,
Pakunena Mzimuyo,
"Osokera, bwerani.”
3 Pangano lake m'mwaziwo
Lindisunga m'chigumula;
2 Bwenzi lathu ndinutu,
Zondizinga zikachoka,
Mkhale m'fupi nafetu;
Yesu ndiye Thathwe langa.
Msatisiye tokha 'fe
NYIMBO ZINA 139
Pakuyenda m'mdimamu; 366
pakuwomba mphepozo 1 Mverani mbiri yozizwitsa
Timaopa m'mtimamo, Ya Yesuyo kalelo;
Tsono timve mawuwo: Iyeyo 'nandza pansi pano
"Amantha 'nu, bwerani." Kutipulumutsa 'fe.

3 M'mene ntchito yathatu, ......Ndani anatiwombola?


M'mene tidikira 'Nu, ......Mwana wa Mulungu pa mtanda,
pakukhumba m'Mwambamo, ......Anatani?
Tsono tipempherabe. Anafera.
Nthawi ya mabvutowo ......Ali kuti?
Tikhulupirira 'Nu, Akhaladi m'Mwamba
Tsono timve mawuwo, ......kutipempherera.
"Okondedwa, bwerani.”
2 Palibe mmodzi akanatha
365 Kulowa m'malo mwake;
Ngakhale anali wamkulu
1 Maso ndi mason di Kristu,
'Nasiyidwa namnyoza.
Kodi mndidzachitanji
M'mene ndidzaona Yesu,
Yemwe anandifera? 3 Kodi mudzampembedza Mbuye
Mpulumutsi wathuyo?
.... .. Ndidzamwona maso ndi maso Kodi inu mudzalowamo
Kuseri kwa mitambo;
......... Mu Ufumu wakewo?
Posachedwa ndidzamwona
.........
M'ulemerero wake!
.........
2 Tsopano ndimwona Iye 367
Mwa chizimezimetu; 1 Ufuna kuwomboledwa kodi?
Tsiku lija ndidzaona Ilipo mphamvu m'mwazi wake;
Ulemerero wake. Ufuna kugonjetsa zoipa?
Muli mphamvu m'mwazi wake.
3 M'mene masautso onse, Muli mphamvu yodabwitsatu
Nthenda, infa zidzatha, M'mwazi wa Yesuyo.
Dziko likadakonzedwa, Muli mphamvu yodabwitsatu
ndidakondwa koposa. M'mwazi wa Mwana wankhosa.
4 Lodala tsiku lomwelo 2 Ufuna kuleka kunyadako?
Ndidzamwona Yesuyo, Ilipo mphamvu m'mwazi wake;
Mpulumutsi wanga yemwe Idzatu pa mtanda nutsukidwe,
Anandikonda ine. Muli mphamvu m'mwazi wake.
140 NYIMBO ZINA
3 Ufuna kuyera kopambana? Mlowetseni (mlowetsenutu);
Ilipo mphamvu m'mwazi wake; ...Mtsegulire msangatu,
Zoipa zonse adzayeretsa, Wakuyerayerayo,
Muli mphamvu m'mwazi wake. Mwana wa Mulunguyo,
Mlowetseni (mlowetsenitu).
4 Ufuna kugwira ntchito yake?
Ilipo mphamvu m'mwazi wake; 2 Utsegule mtimawo,
Ufuna kumuimbira Iye? Mlowetseni (mlowetsenitu),
Muli mphamvu m'mwazi wake. Ukachedwa achoka,
Mlowetseni (mlowetsenitu),
...Ndiye Bwenzi lakolo,
368 'Dzakupulumutsa 'we;
1 Mpulumutsi Wokondedwa, 'Dzakusamaliranso,
Mwandipulumitsa ine; Mlowetseni (mlowetsenitu).
Ndine wanu, wanu nokha,
Wotsukidwa m'mwaziwo. 3 Imva mawu akewo,
...... Aleluya, Aleluya, Mlowetseni (mlowetsenitu),
Mwanawankhosa ndinutu; Sankha Iye leroli,
Mwazi wanu wanditsuka, Mlowetseni (mlowetsenitu),
Aleluya kwa Yesu. Wangoima pa khomo,
'Dzakusangalatsa 'we,
2 Mtima wanga wabvutika, Udzamlemekezatu,
Zaka zonse ndangochimwa; Mlowetseni (mlowetsenitu).
Tsono sindikangalika,
ndingopuma mwa Yesu. 4 Mlendo wa Kumwambayo
3 Mwandipatulira ine, Mlowetseni (mlowetsenitu),
Kwa Inu ndidzipereka, 'Dzakupatsa zonsezo,
M'moyo, m'imfa mboni yanu Mlowetseni (mlowetsenitu),
Ya chipulumutsocho. 'Dzakhululukira 'we,
Ndipo potsirizapo
4 Aleluya, mwandigula, 'Dzakutenga m'Mwambamo,
Ndipo mudzandisungabe; Mlowetseni (mlowetsenitu).
Mwazi wanu ndi wamphamvu
Kuyeretsa konseko. 370
1 Ndipereka zanga zonse
369 Mwaufulu kwa Yesu;
1 Mlendo ali pakhomo, Ndidzamkonda kopambana,
Mlowetseni (mlowetsenitu), Tsiku lili lonsetu.
Wadza kalekalelo,
NYIMBO ZINA 141
Ndiperekatu
Zonse kwa Yesu; Adzandipyoletsa pamene ndafoka;
Ndipereka zonse kwa 'Nu, Ndipo dziko lapansi sindiyesa
Dalitseni. ...kwathu.

2 Ndipereka zanga zonse 3 Mayi watsogola ku Ulemerero,


Pamapazi a Yesu; Ndifuna kugwira dzanja lake konko,
Zapadziko ndazikana, Andidikiranso pakhomo la'Mwamba;
Nditengeni Yesu 'Nu. Ndipo dziko lapansi sindiyesa kwathu.

3 Ndipereka zanga zonse, 4 Mu ulemerero tidzakhala m'yaya,


Ndipo n'khale wanutu; Oyera mtimawo ali kulamira;
Mzimu wanu 'ndidziwitse Ati, "Aleluya kwa Mlungu
Kuti ndine wanudi. ...Wamphamvu."
Ndipo dziko lapansi sindiyesa
4 Ndipereka zanga zonse, ....kwathu.
Ndili wanu ndense 'ne;
Nditamanda Dzina lanu,
Aleluya, Ambuye. 372
1 Chisomo chodabwitsacho
Chapulumutsa 'ne,
371 Woipa wopambanatu;
1 Kwathu sipadziko, ndingopitirira, Ndapeza moyo 'ne.
Ndadzikundikira chuma
...Kumwambako; 2 Chisomocho chachotsadi
Mngelo akodola pakhomo la Mantha a imfayo
...m'mwamba; Pakukhulupirira 'Ye,
Ndipo dziko lapansi sindyesa Ambuye Yesuyo.
...kwathu.
Mbuye ndinu bwenzi langa ndithu, 3 Chisomo chandisungadi
Ndichitenji ngati Kumwamba Panjira yangayo,
sikwathu? Chisomo chidzasunga 'ne
Mngelo akodola pakhomo la Mpakatu kwathuko.
m'Mwamba,
Ndipo dziko lapansi sindiyesa 4 Kwathu ndidzaimba nyimbo
kwathu. Ya chisomo chake,
Yolemekeza Mlunguyo
2 Andiyembekeza, chinthuchi Kunthawi zosatha.
....ndidziwa,
Mpulumutsi wanga wandikhulukira;
142 NYIMBO ZINA
373 Tapeza chipulumutso ndithu;
1 Chitetezo chachikulu Nanga inu? Nanga inu?
Chotuluka m'mwaziwo
Wa Ambuye Yesu Kristu ......Masiku onse timakondwera
Mpulumutsi wathuyo. ......Pakumva Mawu ake a Yesu;
Mpulumutsi, chitetezo ......Wolalikira tidzamumvera;
Chipezeka m'mwaziwo. Nanga inu? Nanga inu?
......
2 Ife tiyembekezera Yesu,
2 Ndi chimwemwe ndimaona
Nanga inu? Nanga inu?
Mtsinjewo wa mphamvutu;
Chimwemwecho chili mumtimamu;
Zonditsutsa zachotsedwa,
Nanga inu?
Yesu wanditsuka mbuu!
Mpulumutsi, chitetezo
3 Titasokera tinabwerera,
Chindisangalatsatu.
Nanga inu? Nanga inu?
Tadziwa kuti ndiwo uchimo;
3 Tchimo lonse ligonjera
Nanga inu?
Chikondicho cha Yesu,
Maganizo 'yeretsedwa;
4 Tinachoka munjira ya imfa,
ndingofuna zakezo.
Nanga inu? Nanga inu?
Mpulumutsi, chitetezo
Takopeka ndi Mawu a Yesu;
Chagonjetsa mtimawu.
Nanga inu?
4 Ndili nawo moyo w'satha
Wochuluka mwa Yesu, DZIKO NDI BOMA
Mzimuyo wadzaza mtima 375
Ndi chimwemwe chakecho. 1 Mbuye dalitsani Afrika,
Mpulumutsi, chitetezo, Itukulidwa nyanga yake;
Chiyanjano chomwenso. Mverani mapemphero athu,
Ndipo mtidalitse ife ana anu.
5 Mantha, nkhawa, ndi chisoni
Zochotsedwa zonsezo; Mbwere Mzimu,
Mbuyeyo ndimkhulupira, Mbwere Mzimu, mbwere!
Anditsogoleratu. Mbwere Mzimu,
Mpulumutsi, chitetezo Mbwere Mzimu, mbwere!
Ndimkonda Yesuyo. .......Mbwere Mzimu
Woyera, Woyera,
374 Mbuye, dalitsani
1 Ambiri tikondwera mwa Yesu, Ife ana anu.
Nanga inu? Nanga inu?
NYIMBO ZINA 143
2 Dalitsani mafumu athu, CHIONJEZERO
Akumbukire Mlengi wawo;
Aope ndi kunjenjemera,
Ndipo m'wadalitse iwo ana anu. 377
1 Anthu m'maiko onse
3 Dalitsani mafuko onse, Akhala mitundu;
Aweruze bwino maiko; Kapena m'dziko lino
Adzichepetse ndi kuopa, Akhala anzathu;
Ndipo mtidalitse tonse ana anu. Agona mwa zoipa,
Apulukiradi,
376 Ati, Mutilangize
1 Mlungu dalitsani Malawi, Abale, bwerani.
Mumsunge m'mtendere;
Gonjetsani adani onse, 2 Ngakhale alemera
Njala, nthenda, nsanje; Ndi chuma cha dziko,
Luzitsani mitima yathu Kodi akakondwera
Kuti tisaope, Opanda Mulungu?
Mdalitse Mtsogoleri, nafe, Kodi akhala mwawi
Ndi Mayi Malawi. Otsata zawozo?
Iyay', awonongeka,
2 Malawi dziko lokongola, Apeza tsokalo.
La chonde ndi ufulu,
Nyanja ndi mphepo ya m'mapiri, 3 Ndi ife akudziwa
Ndithudi tadala; Chikondi cha Mlungu,
Zigwa, mapiri, nthaka, dzinthu, Kodi tidzawamana
Mphatso zaulere; Kuwala kwa Ktistu?
Nkhalango, madambo abwino, Chipulumutso! Inde,
Ngwokoma Malawi. Tichibukitsetu,
Kuti mitundu yonse
3 O! ufulu tigwirizane Ibwere kwa Yesu.
Kukweza Malawi;
Ndi chikondi, khama kumvera, 4 Akhristu nyamulani
Timutumikire; Maneno a Mulungu,
Pa nkhondo nkana pa mtendere Ndi moyo lalikani
Cholinga n'chimodzi, Pa dziko lonselo;
Mayi, Bambo, tidzipereke Ndi Yesu Mpulumutsi
Pokweza Malawi. Anatiferatu;
Adzabvomera onse:
Ndi Mwana wa Mlungu
144 CHIONJEZERO
378 Werengani lina linanso,
1 Padziko pano tikhalira Ndimo mudzazizwa
potsirizapo.
M'moyo wosauka;
Komatu kwa Mulungu kuli 2 Kodi mubvutidwa naye katundu?
Dziko lakudala; Ngwolemera mtanda muusenzatu?
mbuyathu Yesu wapitako, Werengani madalitso anuwo,
Iy 'natsogola; Ndimo mudzimba dzuwa lonselo.
Tidzamtsatira ife tonse,
Tsiku lomaliza. 3 Poyang'ana ena ndi ndalamatu,
Ganizani kuti Mbuye wanudi
Tiyeni, tiyeni,
Ku dziko lakudala; Adzakupatsani zake zonsezo,
Tidzafikara m'dziko ilo Chosagula chuma chanu chonsecho.
Tsiku lomaliza.
2 Masiku tikatsala ife 380
M'dziko mwathu momwe 1 Yesu Mbuyetu, mwafera
Mulungu watipatsa ntchito, Mphulupulu zanga,
Tikazigwiritse. Ndimo ndamva mund'itana
Pamene zakuipa zathu Mutitu, Msachedwa.
Zisautsa ife,
2 Zonse za m'dziko zidzatha,
Tikapemphera Mbuye wathu Koma za moyo m'Mwamba
Atipulumutse. Zomwe zidzakhalitsatu,
Chakatu ndi chaka.
3 Ulendo wathu ukadzatha
Tidzafika kwathu, 3 Nyengo ifika, chenjera!
Adzatifikitsa ife komwe Adzakukana m'Mwamba.
Yesu Mbuye wathu. Lapa zoipa zakozo,
Sitidzapeza masautso Kuti ukalowe.
M'dziko la Mulungu,
Tidzakondwera chindwere 381
Nthawi zonse zathu. 1 Tamandani Mbuye,
Inu atate,
379 Mpatse Yesu mitima yanu.
1 Pozunzidwa inu ponseponsepo 2 Tamandani Mbuye,
Ndi kufoka m'mtima nazo zonsezo, Inu mafumu,
Werengani madalitso anuwo Mpatse Yesu mitima yanu.
Ndimo mudzazizwa potsirizapo.
.........Werengani madalitsotu 3 Tamandani mbuye,
.........Anakupatsani Mlungudi. Inu abale,
.........
..................
CHIONJEZERO
. 145
Mpatse Yesu mitima yanu. Mtima wanga mudziwa,
M'ndiphunzitse kukonda.
4 Tamandani Mbuye,
Inu nonsetu, 383
Mpatse Yesu mitima yanu. 1 Mbuye mtsitsimutse
Ntchito zonse zanu!
5 Tamandani Mbuye, Utsani anthu akufa,
Mipingo yonse, Ndi mawi a mphamvu.
Aleluya, Aleluya!
2 Mbuye mtsitsimutse
Ntchito zonse zanu!
382 Tauzarani pa ife
1 Mvera mtima wanga 'we Ndi mweya wa Mzimu.
Akufunsa Ambuye:
"Wosauka wa'mphawi, 3 Mbuye mtsitsimutse
Kodi undikondadi?" ntchito m'mitimamo!
Mumvetse njala kwa Inu
2 "Ndakupeza womanga, Mutikhutitsenso.
Ndamasula zinsinga,
Ndakulonda kutali, 4 Mbuye mtsitsimutse
Kodi undikondadi?" Nchito m'kati mwa 'nthu!
Chikondi chawo chikule,
3 "Akaleka amake Muchikolezetu.
Kusungira mwanake
Ine sin'kuleka 'yi, 5 Mbuye mtsitsimutse!
Kodi undikondadi?'' Mawu alimbike,
Pamene aphunzitsidwa
4 "Ndakukonda ku imfa Onsewa amvere!
ndi chikondi chosatha,
Kwaulere, kwambiri, 6 Mbuye mtsitsimutse!
Kodi undikondadi?" Mzimu adzazetu!
Kwa ife 'dzakhala mwayi,
5 "Msanga ndidzabweratu, Kwa Inu ulemu.
Udzaona ulemu,
Udzakhala ndi Ine, 384
Kodi undikondadi?" Chikhulupiriro chathu
Tatchulachi pakamwapo,
6 Mbuye ndisaukadi, Mulungu athandize 'fe
Chimachepa chikondi, Chikhale cha mumtimamo.

You might also like