Melisa ndi mtsikana wachichepere amene amakhala ku Poland. Ali tsitsi lokongola kwambiri limene limafika cha m’mapewa mwake. Ali ndi maso owoneka mwa brown amene amadwala bwino akamasekerera. Akamapita ku sukulu amakonda Kuvala chipewa cha mtundu wa pink, jinzi ya blue komanso ma sokosi a pink komanso pamodzi ndi zithunzi za agalu a mtundu wakuda ndi woyera. Mu njira monse, Melisa amaoneka mtsikana wabwinobwino. Koma aphunzitsi ake amati siwabwinobwino. Ndiwapadera. Izi ndi chifukwa cha maloto amene adalota ali ndi zaka zisanu ndi zitatu (8). Mu malotomo, Melisa adagona pa kama ku nyumba. Pozungulira iye padali maluwa. Maluwa osauma a mtundu oyera adali ku mutu kwake komanso ena chapamimba pake. Koma kenaka maluwa aja adasitha. Cha m’musi mwa mimba yake kudali maluwa akuda komanso ouma. Maluwa amenewa adali pa miyendo yake. Maluwa ena akuda koma oumanso adali ku mapazi ake. Mngelo wina woipa adaima kumapazi ake kumene kudali maluwa a mtundu wakuda komanso ouma. Iyeyu ankakangana ndi Mngelo wabwino amene adaima kumutu kwake kumene kudali maluwa osauma. “Mtsikanayu ndi wanga.” Mngelo woipa uja adatero. “Iyayi, ameneyu ndi wanga,” Mngelo wabwino uja adayankhira. Mngelo wabwino komanso mngelo woipa uja ankakangana kuti Melisa akhoza kukhala wandani. Kenaka Melisa adadzuka. Maloto amenewa akhoza kuoneka achilendo komanso oopsa kwa ana ena. Koma Melisa adalibe nkhawa. Ku sukulu ankaphunzira za nkangano waukulu pakati pa Yesu ndi Satana. Iye ankadziwa kuti pachiyambi Satana adali wabwinobwino amene ankakhala kumwamba. Koma kenaka Satana adakhala mngelo woipa. Iye ankafuna kuti akhale Mulungu, ndipo adakopa angelo ambiri kukhala mbali yake. Zimenezi zidayambitsa nkhondo kumwamba pakati pa Yesu ndi angelo ake abwino kumbali imodzi komanso Satana pamodzi ndi angelo ake woipa mbali ina. Baibulo limatiuza za nkhondo imene ndiyosaonekayi pa Aefeso 6:12, ndipo limati, “Chifukwa kulimbana kwathu sitilimbana nawo mwazi ndi thupi, komatu nawo maukulu, ndi maulamuliro, ndi kuchita zolimbika a dziko lapansi a mdima uno, ndi a uzimu a choipa m’zakumwamba.” Angelo woipa akumenyana ndi angelo abwino pa miyoyo ya atsikana komanso anyamata wokhala ku Poland komanso dziko lonse. Nkhondo imeneyo idzatha Yesu akabwera ku dziko la pansi ndi kutenga owomboledwa kupita nawo Kwawo kumwamba. Loto lija silidamuchititse mantha Melisa chifukwa amadziwa kuti Yesu pamodzi ndi angelo ake abwino samamumenyera chabe nkhondo komanso amamutetezera iye. Melisa sadaliiwalebe loto lija, ndipo amakhala akuliganizira kawirikawiri. Iye akufuna akhale wabwino komanso kupanga ziganizo zabwino. Iye akufuna kuti Yesu pamodzi ndi Angelo ake abwino nthawi zonse adzikhala naye. Iye akufuna kuti Yesu komanso Angelo ake abwino akhale wopambana kulikonse. Tsiku lina ana ena ankakangana ku sukulu. Aphunzitsi adasokonezedwa maganizo ndipo ankasowa chochita. “Ndingapange bwanji Pamenepa?” Aphunzitsi adafunsa ana amene ankakangana aja. Melisa adakumbukira loto lake lija. Angelo abwino komanso angelo woipa ankamenyana nkhondo yosaoneka ku sukulu kwake. Angelo woipa ndi amene ankapangitsa kuti ana aja adzikangana. Melisa adaimika nkono. “Aphunzitsi, munatiuza kuti tikhale ndi mavuto, Tikhoza kupemphera,” Iye adatero. Aphunzitsi adavomereza ndi mutu wawo. Iwo adaiwala langizo lawo lomwe limene adawapatsa anawa. Lidali ganizo labwino kuti apemphera. Aphunzitsi aja adaitana ana onse pamodzi ndipo adapemphera kwa Yesu komanso angelo ake abwino kuti apambane nkhondoyo. Akupemphera, Satana komanso angelo ake woipa adagonjetsedwa. Yesu pamodzi ndi Angelo ake abwino adapambana ndipo mtendere udabwerera nchimake pa sukulu paja. Zikomo chifukwa cha zopereka za Sabata sukulu zimene zidathandizira ma sukulu apa kachisi ku dziko lonse kufikira ana monga Melisa za chikondi cha Yesu.
WhatsApp: 0984589282/0884867782 Email: demobreyngwira2@gmail.com FACEBOOK PAGE: Tell a Child with Uncle Demo