Professional Documents
Culture Documents
1 - Chichewa Guide - Nthondo
1 - Chichewa Guide - Nthondo
KUZUKUTA
BUKHU
LA
NTHONDO
MAWU KWA APHUNZITSI NDI OPHUNZIRA
Bukhu la Nthondo ndi limodzi mwa mabukhu anayi omwe ali mu ndondomeko yatsopano
.Tebulo ili m’munsiyi ikusonyeza mabukuwa ndipo ayenera kuwerengedwa motere:
Bukhu la Nthondo ndi la tinkhani (novel) ndipo choyamba ophunzira ayenera kudziwa zoyenera
kumaunika powerenga nkhaniyi (elements of novel) monga malo ndi nthawi komwe nkhaniyi
ichitikira (setting), atengambali (characters), mfundo zikuluzikulu (themes) ndi zina
M’bukhuli muli zina zofunika kwambiri monga zikhulupiliro za maloto, mankhwala azitsamba.
M’bukhu laNthondo mtengambali wamkulu ndi Nthondo amene mlembi wafuna kuonetsa kuipa
kwa makhalidwe oipa komanso ubwino wa makhalidwe abwino.
1. Umodzi – akazi onse am’mudzi anapita kunyumba ya mayi ake a Nthondo kukaona
mwana
2. Chikondi –amayi awo a abambo ake a Nthondo ndi mwana wawo wamkazi anapita
kukaona matenda komanso mwana atauzidwa ndi mnyamata.
3. Kulimba mtima – mnyamata wokanena uthenga wa matenda anabwerera tsiku lomwe
ngakhale dzuwa linali litalowa.
4. Umphawi – kunalibe madzi oti aphikire phala loti amwetse mwana Nthondo
5. Kumvera – mnyamata atatumidwa kukanena uthenga kwa abale bambo ake a Nthondo
sanakane.
6. Nkanza – asilikari anawamanga abambo ake a Nthondo popanda chifukwa chenicheni.
ZIPANGIZO
1. Zining’a
(i) Kumbuyo kulibe maso
(ii) Chakudzas ichiyimba ng’oma
2. Mvekero
(i) Mphale vuuu! Tsuketsuke, phuu! Munsi tengu,
ZOLANKHULA ENA
(iii) “Ha! Mwana wakomadi. Mchombowu adatenga yani? Ife kwathuku makolo athu kulibe
wamchombo waukulu”
a. Adanena mawuwa ndani?
Mayi abambo ake a Nthondo
ATENGAMBALI
3. Kapitawo
4. Mwalapa
Adakokoloka ndimadzi pa mtsinjewina
5. A Dziko
Adapha samba nthawi ya chirimwe bambo a Nthondo adapita kwa iwo
13. Nthondo
1. Kapitawo
Wankhanza
Waukali
Adakalipira bambo a Nthondo ndi ena omwe anagwidwa pamene amafunsa malo
ogona
2. Bambo a Nthondo
Adalota atalembelera chulu ndipo atatsiriza kupanga litala, zinatuluka zochuluka. Anauza
mwana wawo wamkazi kuti auze amake kuti abwere ndimtsuko wodzatengeramo inswazo,
Wina anati malotowa atanthauza mwayi. Ngakhale akuvutika tsiku lina adzamasulidwa.
ZIKHULUPILIRO PA MUTU 2
1. Zikhulupiliro za maloto
2. Zikhulupiliro za mankhwala
3. Mwana osayenda akamutengera paphewa amayamba kumera mano a mmwamba
chizindikiro choti ndi mfiti.
4. Zikhulupilro za maula – atadwala litsipa bambo ake a Nthondo ankhoswe akuchikazi ndi
akuchimuna adapita ku ula kuti akadziwe gwero la matenda ndipo ula udagwera mlongo
6. Pochoka kumanda koika bambo a Nthondo adzukulu adagulula makasu ndipo adafika
kunyumba anatenga zinyatsi nawaula kuti azimu achoke.
7. Nthondo adamupatsa mkalo (dothi la kumanda) naponya mdzinje la manda kuti aiwale
msanga.
MFUNDO ZIKULUZIKULU PA MUTU 2
a. NKHANZA
Kapitawo adakalipira omangidwa ndi asirikali
Atsibweni ake a Nthondo amammenya kapena kumupha munthu akapanga
zosayenera kapena kuoneka ngati wawanyoza.
b. UMPHAWI
Bambo a Nthondo adatuma mwana wawo kukapempha nkhuku zolipira
anamwino. Nkhuku zake zinafa ndi chideru.
MAFUNSO PA MUTU 2
1. Bambo aNthondo ankagwira ntchito yanji atatengedwa ndi asirikali?
2. Chidadzutsa mapiri pachigwa n’chiyani kuti bambo ake a Nthondo apatsidwe ntchito
mwatchulayo.
3. Tsimikizani popereka mfundo imodzi kuti kapitawo adali wankhanza.
4. Kodi maloto a chulu ndi inswa zambiri omwe bambo ake a Nthondo adalota
amatanthauzanji? Tsimikizani popereka mfundo imodzi.
5. Ndi makobidi angati omwe kapitawo adapereka kwa bambo ake a Nthondo atamaliza
kugwira ntchito?
6. Fotokozani mmene ndalamayo adayigwiritsira ntchito.
7. Kodi pamene asirikali amawatenga bambo a Nthondo adawapeza akuchita chiyani?
8. Tchulani zinthu ziwiri zomwe zikutsimikiza kuti makolo a Nthondo amakhala m’moyo
waumphawi.
9. Bambo a Nthondo nthawi ina anali ndi nkhuku zambiri pakhomo pawo.
10. Kodi m’manja mwa mwana ngati mukuzuna ndiye kuti akudwala nthenda yanji?
11. Tsimikizani popereka mfundo ziwiri kuti bambo a Nthondo sakadafa akadathamangira
nawo kuchipatala.
12. Tsimikizani kuti umbuli ndi zikhulupiliro ndi gwero la mikangano ndi imfa zina zopezeka
m’bukhuli. Lembani mfundo zinayi.
b. Chipindatchika
c. Mbuzi yakumitu
d. Mkalo
e. “kudulu”
15. “Ine ndine nkhalamba sindingakwatiwenso”
a. N’chifukwa chiyani mayi ake a Nthondo adanena mawuwa?
b. Mawuwa adanena kwa yani?
i. Amasowa nkhuku
ii. Amasowa chimanga choti akonole
i. Makhalidwe awo
ii. Mayankhulidwe awo
iii. Kusasowa kwawo
iv. Luso lawo
Mowa utatha anthu anabalalika asanamange nyumbayo. Munthu wina ataona izi anamva
chisoni natsirizitsa.
a. WABODZA
i. Pamene nyumba inapsa mayi ake anamuuza Nthondo kuti awamangire tsindwi
koma iye anangovomera koma sanamange. (p27)
ii. Pamene wina anamudzudzula Nthondo posamangira mayi ake nyumba iye
kufuula kuti iye wawaber. Koma tsiku la mlandu iye sanatsutse zoti iye anaba.
iv. Nthondo ananena bodza powuza mayi ake kuti amasewera pamene
mwake Nthondo adanena bodza pouza atsibweni ake kuti ena ake
anamupempha kuti akawasosolere nkhuku (pg33). Apa atsibweni akewo
anatenga mtengo namuthamangitsa kuti ammenye.
vi. Nthondo adanena bodza pouza atsibweni ake kuti iye anasiy mayi ake
akudwalabe pamene iye amapita kwa mnzake wadzina. Ilitu linali bodza popeza
iwo anayamba kudwala Nthondo atathawira kwa mbzake wadzinayo atapalamula
kwawo.
vii. Nthondo adanena bodza atapalamula kwaa Mdima pamene adalephera
kuthandiza kumanga tsindwi la nkhokwe ponena kuti iye akudwala ntchofu.
i. Nthondo adayamba kuba ndiwo, mazira ndi zina za mnyumba mwa amake
pokhumbira zimene anzake amadya kumphala. Ali kumphala Nthondo
adaperekeza anzakewo kokaba misinde koma iye samadya nawo. Amaona
nkhuku zobedwa zikuotchedwa koma iye samadya nawo poopa kuti angalumale.
ii. Nthondo adaba zipwete kumunda kumene amasaka mbewa. Mwini zipwete
anamuona koma iyeanathawira pa tchire osamugwiranso.
iii. Mmawa mwake Nthhondo anaba nkhunda ndipo eni ake anamuthamangitsa
namugwira. Anthu adamumenya Nthondo namuikira nthenga za nkhunda mtsitsi
lake nayamba kuyimba nyimbo uku akupita naye kwawo. Atsibweni ake analipira
vi. Nthondo adaba thumba lachikopa chambuzi kuti akaikemo ufa (pg39)
vii. Nthondo adaba ufa omwe udayanikidwa pa dzuwa nakaubisa ku phanga kuti
azikadya popita ku Harare. (pg39). Ufawo anakawusiya kwa mnyamata
i. Ngakhale adadziwa kuti nkhuku yomwe anzake adaba idali yamayi ake, Nthondo
sadaulule. Amake adadandaula kusowa kwa nkhuku yawo komaiye sadamve
chisoni.adaumitsa mtima pofuna kukondweretsa anzakewo.
ii. Nthondo adagenda ndi mwala alendo omwe amafunsa njira. Atanena kwa a
mfumu alendowo adalephera kuloza yemwe adawagenda poti sanamudziwe.
Amfumu adati amafuna amulipiritse ogendayo.
iii. Amake a Nthondo adadandaulira Nthondo kuti amange nyumba yomwe idapsa
ndimoto komaiye anangovomera koma sanamange.
iv. Nthondo atawuzidwa zakudwala kwamayi ake ndi munthu yemwe anatenga
Iye adaumitsa mtima ngakhale amfumu anati ana awo afa ndinjala chifukwa
chakubedwa kwa ufawo (pg39)
d. WOSAMVERA
i. Nthondo sadamvere mayi ake atamupempha kuti awamangire nyumba. (pg27)
ii. Nthondo anakalipira munthu yemwe adamulangiza kuti awamangire amake
a. NTHONDO
i. WACHISONI
Nthawi zina Nthondoo amakana nsima amake akampatsa poona kuti amake
sakusangalala pamene abambo a Nthondo anamwalira. Amake akamufunsa
amangoti kukhosi kwake kwada.
ii. WAMANTHA
Pamene Nthondo adatsatira anzake kukaba misinde, iye amatsalira m’mbuyo kuti
eni ake akawagwira adzakane kuti iyesamaba nawo.
Iye samadya nawo nkhuku zakuba kuopa kulumala poti panthhawiyo kunali chambu
b. MAYI AKE A NTHONDO
i. Achikondi
Adachenjeza mwana wawo Nthondo kuti asayerekeze kukaba misinde malinga kuti
kutero akalasidwa.
Amake a Nthondo akaona chakudya amatemera Nthondo naye Nthondo akapeza
amatemera mayi ake (p21)
Amake a Nthondo sanamuzenge mlandu pamene mwana wina anatentha nyumba
yawo chifukwa analimwana wapamodzimodzi pomwepo. Iwo adatero polinga
mawa.
a. KU MPHALA
i. Kuba – anzake a Nthondo amamjutenga pamene amapita kukaba zinthu
zosiyanasiyana monga misinde
ii. Kupilira – ngakhale ku mphala kunali mphutsi, Nthondo anapilira nazo.
iii. Kusunga chinsinsi –iye sananene kwa mayi ake ataona nkhuku yawo itabedwa
ndi kuphedwa ndi anzake ku mphala.
b. KU UBUSA
i. Kupilira – ngakhale amauzidwa kuchita ndeu ndi wina, iye sanaleke kupita ku
ubusa.
ii. Kutumika – mtsogoleri akawauza kuchita chinthu iwo samawilingula, amachita
chinthucho. Mtsogoleri amawauza kuchita zinthu monga kuchita ndewu popanda
kuyambana kapena amawuza kubusa mbuzi.
iii. Ndewu – mtsogoleri akawauza kuchita ndewu ndi wina popanda kuyambana
ndipo amamenyanadi
iv. Kulimba mtima – chifukwa cha ndewu yomwe anyamatawa ankachita kuubusa,
iwo adaphunzira kulimba mtima.
MFUNDO ZIKULUZIKULU PA MUTU 3
1. KUBA
Nthondo adalowerera nayamba kuba zinthu za mayi ake komanso za eni. Iye adaphetsa
3. KUPIRIRA
Kupilira kwaonetsedwa ndi anyamata a kumphala omwe mnyumba ngakhale
mulimphutsi zimawaluma.
4. UMPHAWI
Anyamata ku mphala amagona mwaumphawi poti mphutsi zimawaluma.
“Iyayi, sindifuna ine chifukwa anzanga angamandiseke kuti ndine munthu wogona
m’kuka”.
a. Tchhulani anthu awiri omwe akuyankhulana mkankhanika.
Nthondo ndi mayi ake
b. Tchulani makhalidwe abwino awiri omwe Nthondo adaphunzira ku mphala
Kutumika ndi kupilira
c. Ndi chiyani chomweNthondo amakhumbira kumphala kuja?
Kuweta mbuzi
d. Kodi mtsogleri amamusankha bwanji ku ubusa?
Abusa amenyana ndipo yemwe amaposa ena amakhala mtsogoleri.
2. “Masulani mbuzi, lero ndikaziweta ndine.”
a. Nthondo amayankhula kwa yani?
A Msinda
7. “Dzulo lija ndinachedwa chifukwa auje adandituma kuti ndikawasosolere nkhuku.”
a. Kodi Nthondo ankayankhula ndi yani?
A Mdima
11. “Ine sindikakonza nawo chifukwa ntchofu yandivuta kwambiri.”
a. Anzake a Nthondo ankagwira ntchito yanji?
Yokonza tsindwi la nkhokwe
b. Ndi khalidwe lanji Nthondo waonetsa pamenepa?
Waulesi, wachinyengo. Adanena bodza kuti akudwala ntchofu pozemba ntchito.
MUTU 4 : MAULENDO AKE
a. MATENDA
Mnyamata wina adamva litsipa pa Dzalanyama (p42). Anzake adafuna kangaluche
Anzake a Nthondo anamuuikira namumenya chifukwa cha ulesi wake. Iye adakakana
kukagwira ntchito pamudzi wina kuti apeze chimanga. Iye adanama nati dzanja lake
likuwawa.
c. KUSOWA CHAKUDYA
Chifukwa chakutalika kwa ulendo, matumba awiri omwe adapatsidwa atagwira ntchito
pamudzi uja chidawathera ndipo ankadya maswu (p43). Onse anayamba kuwonda ndi
njala moti pamene amaoloka Zambezi nkuti ali mafupa okhaokha.
d. KUTALIKA KWA ULENDO
Ulendo wawo udali wautali kotero kuti adayenda masiku ambiri ndipo pamene amafika
akudwala.
Chifukwa cha mantha iye adakana kufunsa ntchito kwa mzungu yemwe anzake
anamuuza kotero kuti wina anachoka naye napita naye napeza ntchito yoweta nkhuku.
a. WANZERU
Nthondo adaonetsa khalidweli pogwiritsa ntchito bwino malipiro ake. Iye adagula
bulangeti ndipo zina anasunga.
b. WAKUBA
Nthondo adaonetsa khalidweli popita kukaba maungu atatu m’munda mwa mzungu.
Mwatsoka mlonda adamugwira nampereka kwa mzungu wake. Mzungu analemba
palibe kanthu.
Atatulitsidwa kugadi Nthondo adapita kwa bwana wake ndi cholinga choti akapitirizenso ntchito.
Kodi Nthondo adakumana ndi zotani?
mnzakeyo sadafe. Iye adati akadafa mnzakeyo ndiye kuti nayenso akanaphedwa.
MALOTO ENA A NTHONDO KUNDENDE
a. Iye adalota atapita ku uzimba ndi anzake ndipo mikango iwiri imamuthamangitsa,
nimugwira nikumudya. Atadzuka Nthondo adayamba kulingilira kuti mwina panali wina
amene adamuchitira mankhwala kuti azichimwa popeza anzake amakhala
mwamtendere.
b. Tsiku lina adalota munthu wina amene adavala nsalu zoyera adali ndi ndodo yowala
ndipo adamuloza ndi ndodo yakeyo ndi kuti: “Ndizakulanga ukapanda kusiya zoipa
zakozi”. Pamene adadzidzimuka adayamba kusisima chifukwa camaloto amenewa.
ZIKHULUPILIRO
i. Nthondo adakhulupilira kuti maloto omwe adalota amatanthauza kuti amfiti
akumutambira
ii. Nthondo amakhulupilira za umfiti. Iye adanamiza anzake tsiku lina kuti akudwala
napita kwa sing’anga kuti akampatse mankhwala a thupi kuti mfiti zisamafike
pakhomo pake.
Ndoda ija idamuwuzanso nthondo za mankhwala a liphopho, mankwala a mdima
ndi mchira wafisi kuti azikabera. Iye adampatsa sing’angayo ndalama khumi ndi
zisanu.
NTHONDO ABWERERA KWAWO
Nthondo adanamiza mzungu wake pomuuza kuti m’bale wake wamwalira pofuna kuti
amulole kuti apite. Iye anamuuza Nthondo kuti adzabwerere kukapitiriza ntchito.
Atauza anzake aja anamukanira nati iwo apitabe mtsogolo.
Ananyamuka ndi anthu oyandikira kwawo koma anasiyana pamudzi wina pamene iwo
anamuukira Nthondo kuti amasekachomwe samachidziwa. Nthondo adawauza kuti
Mnjira wina anati amulandire katundu poti amaoneka otopa. Atampatsa katunduyo
munthuyo anamubera pamene iye amachotsa thekenya ndikumwa madzi kumtsinje.
Atafika kunyumba atsibweni ake anamulandira. Anapereka nkhuku kwa anyamatawo
Nthondo udaganiza zaupandu chifukwa chotopa ndi kusekedwa ndi anthu. Adapita kwa
munthu yemwe anabwera ku Harare nakaotcha nyumba. Popita akaone motowo, iye
anakaba chuma chake.
1. Mtsogoleri paulendowu anali Nthondo popeza anali wokula msinkhu uposa anyamata
onse.
2. Iwo ankafuna kukatenga katundu ku Kapata kukatola ku Kabula.
3. Iwo anamva kuti ntchito yamtengatenga munthu amapatsidwa ndalama khumi ndi
zisanu.
mtsogoleri.
d. Nthondo adakola pamsampha wanjira pamene amathawa kugwiridwa pamene amati
akabe nkhuni pakhomo pa munthu wina. Nthondo adamenyedwa kwambiri
nammangirira ku mzati wa nkhosa. Nthondo adamulipitsa napitilira mpaka kukafika ku
Kapata.
Unali mudzi wabwino. Munali mitengo yambiri yamitawa, anyamata ndi asungwana
ambiri.
3. Adakaonerera gule wa ngoma pamudzi wina omwe adagona. Nthondo adavina
guleyo.
4. Adaona udzu omera pamwamba pamadzi. Udzu umenewu umatchedwa Gumbwa
omwe adachita nawo chidwi.
Atafika ku Kapata mzungu wina adawapatsa thonje ndi kalata yokaperekera katunduyo.
Adalota ataona atate ake amene adafa kale akupha nsomba ndipo Nthondo adapemphako,
koma atate ake adamukanira namuuza kuti si iyenso mwana wawo popeza akuwachititsa
manyazi ndi kuba kwakeko. Pamenepo Nthondo mosadziwika anabako nsomba imodzi. Atatero
atate ake adayamba kumpitikitsa. Nthondo adayesetsa kuthawa ndi kuuluka koma osatheka
Chithandizo
Anamuwuza kuti azisamba mankhwala aziwanda kuti asadzapenge mtsogolo mwake. Ena
anamuuza kuti akakumbe mtengo wamathulitsa ena amati chivumulo.
ULENDO WA KU KABULA
kuti Nthondo achier. Nthondo adachira koma winayo sadachirebe. Adakhalabe mpaka
tsiku la Sabata.
Chisanu chitawavuta anapita kukaothera dzuwa komwe adamva beru kuti nge! Nge!
Nge! nge! Atafunsa anauzidwa kuti linali tsiku lopita kukapemphera ku tchalitchi
kukapembedza Mulungu.
Nthondo ndi anzake adapita nawo ku tchalitchi komwe iye adasilira nyimbo zomwe
zinkaimbidwa. Iye adati akadakhala kwawo bwenzi akuimbira nsasi.
Kutchalitchiko Nthondo adamva ulaliki omwe udamukhudza kwambiri. Mphunzitsiyo
adati onse ochita zoipa monga kuba, dama, kupha, ndi zina sadzalowa mu ufumu wa
Mulungu. Iye adamva chisoni chifukwa mwini kba, dama ndi kupha adali iyeyo.
Nthondo adakhumbira sukulu.
“……………..koma ngakhale ndipite kwathu kuba ndi zina ndaleka lero. “adatero Nthondo
pamaso pa anzake aja polengeza za kulapa kwake. Izi anachita potsatira ulaliki omwe adamva
ku tchalitchi kuja.
MALOTO A NTHONDO
Nthondo adalota akupita kudziko lachilendo. Kumeneko adapeza anthu akunzunzika ndi moto
wophulitsa maso ndipo anthu ena anali kuyimba nyimbo zonga zomwe zakutchalitchi kuja.
Kugulu lakumotolo kunali munthu woopsa wanyanga ziwiri ndi mchira. Kugulu linali kunali
munthu wamtali wovala zoyera. Anthu awiri amene anali atsogoleri anayamba kumulimbirana
Nthondo ndi anzake aja adafika ku Kapata nasiya katunduyo kwa mzungu uja. Adafotokozera
mzungu chifukwa chomwe adachedwera mu msewu ndipo adawapatsa ndalama zawo napita
1. “Komai ne ndidziwa kuti mnyamata wina anandinenera kwa mzungu wanga kuti
asandilandirenso chifukwa masiku onse ngakhale nimagwira ntchito samandiona ndi
maso abwino. Chilipochilipo paja galu wa mkota sakandira padzenje lopanda kanthu.”
a. Ndi ntchito yanji yomwe Nthondo amagwira kwa mzungu amaneyu?
Nthondo adaleka kuvomera mumtima mwake kuti khalidwe lake lakuba ndi lomwe
lamuchotsetsa ntchito koma adayamba kudzudzula anzake ogwira nawo ntchito pa
kuchotsedwa kwake.
c. Chifukwa chiyani mzungu wa Nthondo sadamulandirenso Nthondo atabwera kugadi?
Iye samafuna munthu wakuba pakhomo pake
d. Nthondo adakhala kugadiko nthhawi yotalika bwanji?
Masabata atatu
e. Ndi nkhanza zanji zomwe adamuchitira kundende?
Anammenya zikoti zinayi
f. Fotokozani zomwe zidamuchitikira Nthondo atafika kwa bwana wake kuti
ayambenso ntchito.
Mzungu adaitana agalu ake nayamba kumupitikitsa Nthondo. Akuthawa adapunthwa
ndipo galu wina adamuluma pa msolo. Mzungu uja anamulanditsa kwa agalu aja
koma sanasiyire pomwepo koma anayambanso kummenya makofi. Iye adanyamuka
kupita komwe amakhala nayamba kulira.
g. Perekani matanthauzo a ziganizo izi:
i. Samandiona ndi maso abwino
Samasangalala nane
ii. Galu wamkota sakandira padzenje lopanda kanthu
Zinthu zina zikamachitika zimalosera zovuta zochitika mtsogolo
2. “Mukaona zii ndiye kuti ndagwiridwanso chifukwa ndine munthu watsoka.”
Litsipa laching’alang’ala
b. Kodi Nthondo amatanthauzanji ponena kuti “ine ndisagonetse m’dziko lino”?
mmaloto
b. Nthondo anali kuti panthawiyi?
Ku Kapata
10. “Kuyendakwina………..Ha! kuyenda uku nako. Tiona nako malodza lero.”
a. Nthondo ndi anzake anali kuti panthawiyi?
adaphunzira izi:
i. Kusoka mphasa
Sankakana akamtuma.
Atsibweni ake adampatsa mkazi koma iye adamkana chifukwa anali wamng’ono.
Wina adamulangiza kuti sibwino ukwatira msuweni wako popeza amanyada. Msuweni
wa Nthondo ndi Mdzitula.
Atakhala kwa kanthawi Nthondo adapempha kuti amtenge chitengwa mkazi wakeyo
poti anali yekhayo mphwake wa mfumu. Makolo nawo adati adalibe mwamuna kotero
Mzungu adakondwera atamva kuti mafumu onse avomera zoti sukulu akuifuna. Iye
adapereka mabulangeti kwa mafumuwo ndi thumba lamchere.
Adawapatsa kalata yoti akapereke kwa mzungu waku boma kuti adziwe.
1. UMPHAWI
Nthondo ndi anzake adapita kumtengatenga ku Kapata chifukwa adalibe zovala
2. KUMVERA
4. KUKHUMBIRA
5. KHAMA
Nthondo sadajombe pamene anayamba sukulu ndipo iye adakondetsa kuwerenga
b. Kodi chifukwa chiyani ena adalangiza Nthondo kuti sayenera kukwatira msuweni
wake?
amanyada
3. “Sindigathe kuchita choipa ngakhale wina atandituma sindingathe, koma ndi kulingilira
za mkazi kumene ndingampeze.”
Adamva anzake
c. Tchulani zoipa zomwe Nthondo ankachita poyamba.
Kuba
Ndewu
Kugenda alendo odutsa
4. “Lekeni! Ndiye mkazia meneyu. Ichitha mbeta, ha! Siotukwanitsa. Ndikapita kumudzi
ndikauza atsibweni anga kuti akatume munthu wina akandifunsire mbeta.”
Kale mnyamata amatuma wina kukafunsa mbeta mmalo mwake pamene masiku
ano munthu umafunsira wekha.
b. Kodi mawu oti “mbeta yotukwanitsa” atanthauzanji?
Mkanda
9. “Ha! Kodi! Wanena pafupi ndimtuma wina akanene kwa nkhoswe zakuchikazi”.
a. Kodi Nthondo akuyankhula ndi yani?
Nthondo
MUTU 6 : UFUMU WAKE
Anthu akulu pamudzipo adaitana akazi akukuluakulu nawafunsa uyo angathe kukhala
mfumu ndipo iwo adatchula Nthondo.
“Iyati nkoyipa.”`
Mbuzi
2. “A Mzingwa, tiyeni tichoke. Tamvani zachibwana akukamba mfumuzi”
a. Kodi adayankhula mawuwa ndani?
A mfumu Dzeya
b. Kodi a Mzingwa ndi yani?
Imodzi mwa mfumu zazing’ono
c. Kodi a Mzingwandi anzawo adali kuti panthawiyi?
Kunyumba kwa Nthondo
d. Kodi zachibwanazanji inkayankhula mfumuyi?
ziganizo zothandizira.
Kulemba mfundo ziwiri mnime imodzi kumasokoneza ochonga ndipo mapeto ake
malikisi aaperekedwa a mfundo imodzi basi
1. Fotokozani kufunika kwa maloto anayi amene Nthondo analota pa unyamata wake.
Nthondo nanalota maloto osiyanasiyana omwe anali ofunika kwambiri pa moyo wake.
Mfundo yoyamba pamene adamangidwa chifukwa chakuba maungu atatu m’munda
mwa bwana wake nkuponyedwa mu gadi ku Harare Nthondo analota atalowa mdziko
mikango iwiri. Ali mndende ku Harare kuja pamene adamenya ndi kukomola mnzake,
iye adalota atapita ku uzimba ndi mnzake ndipo mikango iwiri imamuthamangitsa
nimugwira ndikumudya.
Atadzidzimuka Nthondo adayamba kulingalira kuti mwina panali wina amene
adavala nsalu zoyera. Munthuyo adali ndi ndodo yowala ndipo adamuloza ndi ndodo
yakeyo ndi kuti: “Ndidzakulanga ukapanda kusiya zoipa zakozi”. Pamene adadzidzimuka
Nthondo adayamba kusisima chifukwa cha maloto amenewa.
Malotowa adali ofunika chifukwa adamuchititsa kutsutsika mumtima mwake ndipo
patsogolo pake ndi pamene adapanga chisankho chotembenuka mtima.
Mfundo yomaliza ikudza pamene Nthondo adalota ataona atate ake amene adafa kale.
Iye adalota atate akewo akupha nsomba ndipo Nthondo adapemphako koma iwo
adamukanira namuuza kuti si iyenso mwana wawo popeza akuwachititsa manyazi ndi
kuba kwakeko. Pamenepo Nthondo mosadziwika adabako nsomba imodzi. Atateto atate
2. Tsimikizani popereka mfundo zinayi zosonyeza kuti Nthondo anali wamakhalidwe oipa
aadatembenuke mtima.
NHPL