Professional Documents
Culture Documents
Pastoral Letter ECM A5 Chichewa Edit
Pastoral Letter ECM A5 Chichewa Edit
YA DZIKO LA MALAWI
2. Katangale
Pakali pano, katangale wafika poyipa m’dziko lino. Kuyambira
akuluakulu mpaka kutsika m’munsi, anthu odziwika
akusanduka olemera kosasimbika pakanthawi kochepa
podyera anthu osauka ambirimbiri masuku pa mutu.
Chokhumudwitsa ndi chakuti katangale walowerera m’magawo
osiyanasiyana a moyo m’Malawi muno. Umu ndi m’mene zinthu
ziliri masiku ano. Anthu ochita katangale akhala akuyesetsa
kuchita zinthu zofooketsa ndi kulepheretsa mabungwe
olimbana ndi katangale kuti asagwire ntchito yawo mokomera
Amalawi komanso chilungamo. Zimene zikuchitika tsopano ndi
kungobwatikidwa kapena titi kupusitsidwa kuti tiziti ntchito
yolimbana ndi katangale ikuchitika. Ngati anthu okhulupirira
Yesu Khristu, tikuyenera kukhalabe ndi chiyembekezo, osataya
mtima. Potsamira pa Chiyembekezo Chachikhristu, ife
tikuyamikira amene amadzipereka modzikhuthula, ndipo
chitsanzo ndi Bungwe la Zamalamulo (Malawi Law Society) ndi
ena otero, amene amakhulupirira kuti katangale ndi tchimo
ndipo akuchita ntchito yotamandika kulimbana ndi mchitidwe
woyipawu. Iwowa sanatayebe chiyembekezo chakuti,
chilungamo ndi chotheka kuchikwaniritsa pansi pa utsogoleri
wabwino.
3
3. Pansi pa Ulamuliro wa Boma la Tonse Alliance
Kodi chikuchitika nchiyani ndi atsogoleri athu? Ife tazindikira
kuti zina zokhumudwitsa zimene zikuchikita atsogoleri athu
akuona ndiponso nthawi zina akukhudzidwa ndi zotsatirazi:
a. Nkhani ya kuchepetsa ndalama zogwiritsa ntchito
atsogoleri, ndi nkhambakamwa chabe. Nkhani ndi yakuti,
palibe chimene chasintha. Amangopereka zifukwa zopanda
pake kuti akhale paulendo womwe umasowa ndalama
zambiri zapathumba (allowances) komanso anthu
ochuluka okhala nawo pa maulendowa. Mchitidwe
woterewu wasanduka ngati chizolowezi chomwe
chimawonongetsa ndalama zambirimbiri zomwe ndi
misonkho ya anthu osauka.
b. Anthu akudabwa kuti zikutheka bwanji kuti anthu amene
akufufuzidwa pa nkhani ya katangale, akupatsidwa mwai
wochita malonda osowa ndalama mamiliyoni a madola
pamene dziko lathu likusowa ndalama zakunja.
c. Madilu okayikitsa pakati pa Boma ndi ogulitsa katundu
angosanduka chizolowezi pakati pathu. Palibe kuganizira
anthu osauka amene amazunzika tsiku ndi tsiku kuti apeze
zosowa zawo za tsiku ndi tsiku. Kulira kwa anthu osauka
sikumveka chifukwa cha ndondomeko zolakwika zogulira
katundu m’maunduna ndi m’mabungwe ena aboma. Izi
zimachitika chifukwa cha anthu amene amadzitcha
amkhalapakati omwe ena mwa iwo ali ndi ubale ndi alangizi
a President ku Nyumba ya Boma.
d. Tawona akuluakulu ena okayikitsa akutetezedwa popanda
china chilichonse chomwe akuthandizapo pa ubwino wa
4
dziko lino. Izi zimachititsa kuti dziko lathu likhale pa
chiwopsezo chokhala ndi ngongole yambiri kuwonjezera
pa imene tili nayo kale.
e. Tawonapo mtolankhani wina amene akukhala mobisala
chifukwa chonena zoona zokhudza katundu wopita ku
gulu la Asilikari Ankhondo amene munthu wina
woganiziridwa kuti akukhudzidwa nkhani ya katangale
akuyenera kuperekera. Kodi iyi ndi njira yofuna
kutibwezeretsa ku ulamuliro wa chipani chimodzi?
f. Ndife okhumudwa kumva kuti pali mphekesera yakuti
anthu ena akufuna kusintha lamulo la chisankho lakuti
wopambana azipeza mavoti opesera theka la anthu ovota
(50% + 1). Kulimbikitsa maganizo otere, nkulakwa kwambiri
chifukwa kudzakhala ngati kufuna kusintha malamulo
oyendetsera dziko ngati momwe ena m’mbuyomu
ankafuna kuti mtsogoleri wadziko azitha kusankhidwanso
kachitatu. Ngati ndi zoona kuti anthu ena ali ndi maganizo
oterewa, ife tikuwalangiza kuti chinthu chanzeru
nkulekeratu kukhala ndi maganizo oterewa chifukwa
zidzakhumudwitsa anthu ambiri.
g. Mchitidwe wokonderana ndi vuto linanso pakati pathu.
Kalembedwe ntchito ka anthu m’boma kamawoneka kuti
ndi kokondera mtundu kapena chigawo chimodzi. Amalawi
onse ngofanana. Panthawi ya kampeni, tinkamva kuti
mchitidwe wokonderana udzakhala mbiri yakale. Koma
zimene tikuwona tsopano, zikusiyana ndi zimene
zinkalonjezedwa.
5
h. Pali mpungwepungwe wokhudza lipoti lonena za ‘Kusintha
ndi Kukonza Kagwiridwe ka Ntchito M’boma’ (Public
Service Reform Report). Anthu ambiri akuganiza kuti
mulipoti limeneli, muli Mfundo zabwino zambiri zothandiza
kukonzanso kagwiridwe ka ntchito m’boma koma
ndizodabwitsa kuti lipotili likusungidwa mwachinsinsi!
i. Kukuwoneka kuti a Tonse Alliance sakulabadira za
malonjezo amene adachita kwa anthu.
j. Pologalamu yopereka zipangizo zaulimi zotsika mtengo
yangosanduka ngati nthano chifukwa opindula ndi anthu
ochepa. Kodi feteleza uja Amalawi adawuzidwa kuti
adzagula pa mtengo wa K4,995 pa thumba limodzi ali kuti?
Zotsatira za izi, ndizakuti, dziko la Malawi likulephera
kukhala ndi chakudya chokwanira.
k. Mphamvu ya ndalama ya Kwacha yatsika kwambiri
pamene ndalama zimene anthu amapeza ndi zochepa.
l. Mazunzo a anthu okhala kumidzi afika podetsa nkhawa.
Mabanja ena akungogona osadya kanthu chifukwa
sangathe kugula feteleza pa msika. Vutoli lakulanso
kwambiri chifukwa chosowa mvula yokwanira.
m. Makolo ndi alezi akulephera kulipirira ana awo sukulu fizi
ndipo pachifukwa ichi, ophunzira ambiri sakupitiriza
maphunziro. Izi zidzalepheretsa dziko lathu kupita
patsogolo.
n. Miseu yathu ikunka iwonongekerawonongekera. Mwachi-
tsanzo, miseu yaikulu ya M1 ndi M5 ndi yochititsa manyazi
kuyendamo.
6
4. Mabwalo Amilandu
Ngakhale kumabwalo a Milandu, oweruza milandu adaleka
kugwira ntchito mwachilungamo ndipo m’malo mwake,
adalowerera mchitidwe wa katangale ndi wokondera. Kugula
oweruza milandu sichinthunso chotengedwa ngati
choletsedwa. Sichisinsinso ayi kuti anthu ena oyimila anzao pa
milandu (lawyers) akulemera popereka ziphuphu kwa oweruza
milandu pofuna kuti pasakhale chilungamo. Oweruza milandu
ena sawopa munthu wina aliyense chifukwa amadziwa kuti
palibe amene angawadzudzule. Amatenga zaka zambiri kuti
mlandu uthe, koma ngakhale amachita izi poyerayera, palibe
uyo amawadzudzula ndi kuwapatsa Chilango. M’malo mwake,
ndi anthu oterewa amene amakwezedwa pa udindo.
Tikukhulupirira kuti Unduna Wachilungamo ukubwezera
m’mbuyo chidwi cha a Bungwe la Malamulo (Malawi Law
Society) pa ntchito yawo yofuna kukhazikitsa lamulo lothandiza
kuti oweruza milandu azigwira ntchito yawo mwachilungamo.
Lamulo limeneli, ife tikugwirazana nalo chifukwa kukhala ndi
malamulo abwino, ndiye maziko a dziko lirilonse lofuna
kuthetsa katangale.
8
a. kusamalira ndi kusunga bwino nkhalango zathu;
b. kupitiriza ntchito yobzala mitengo;
c. kupeza njira zina zophikira m’malo mwa Makala;
d. kulimbikitsa kugwiritsa ntchito mphamvu ya dzuwa ndi
njira zina zophikira;
e. kulimbikitsa njira zina zokhazikika pogwiritsa ntchito
zachilengedwe;
f. kupititsa patsogolo njira zamakono zaulimi, mwachitsanzo,
njira za mtayakhasu, ndi zina Zotero.
12
d. Ndi chinthu choyenera kuti achinyamata agwiritse
ntchito ufulu wao wovota Chifukwa zotsatira za
chisankho ndi zimene zidzawongolere tsogolo lawo.
e. Nzika iliyonse ili ndi udindo wolankhula za ufulu ndi
chilungamo.
f. Pamene tikuyandikira chisankho, m’Malawi aliyense
akuyembekezeka kukhala nzika yabwino popewa
nkhanza ndi makhalidwe owononga zinthu.
g. Mabungwe ofalitsa mau, ndalama, mphamvu ndi boma
kapena zipani, zingathe kugwiritsidwa ntchito molakwika
ndi anthu andale ndi Cholinga chofuna kupeza mavoti
ochuluka.
h. Ndikofunikira kufunsa oyima nawo pa chisankho
chikubwerachi kuti mbiri yao pankhani yotumikira anthu
ndi yotani. Tisasankhe munthu pa chifukwa chimene iye
ali kapena komwe akuchokera kapenanso potengera
maubale ake ndi anthu ena.
11. Kuwombamkota
Sitikuyenera kupitirira monga m’mene zinthu ziliri m’dziko lathu
lino. Atsogoleri athu asiye mkhalidwe wophangira ndi wotumikira
okhawo amene adawasankha. Tikusowa kupatsa mphamvu
mabungwe amene amayenera kuyang’anira zochita za Boma
mopanda andale kulowererapo. Aphungu aku Nyumba ya
Malamulo, akuyenera kusiya mchitidwe womangokamba
zandale. Zomwe tawona posachedwapa ku Nyumba ya
Malamulo, ndi zochititsa manyazi. Tikuwona ulamuliro wopanda
masomphenya m’dziko muno. Ili ndi gwero la mavuto amene
tikukumana nawo. Pokhapokhapo atsogoleri atasiya mkhalidwe
13
wadyera ndi wophangira, nakhala ndi chidwi choyendetsa bwino
dziko lino ndi kuyesetsa kuthetsa katangale, zinthu zitha
kusintha. Koma tikapanda kutero, tidzapitilira kukhala m’mavuto
amene tili nawo tsopano. Tikupempha kuti pakhazikitsidwe
lamulo lomveka bwino limene lidzathandize kuwongolera bwino
ntchito za ku Mabwalo Amilandu. M’dzina la Ambuye Mulungu,
tikupempha atsogoleri athu kuti amve kulira kwa anthu osauka
ndi kuchitapo kanthu.
Tipempherenso kuti nyengo ya Lent ino ikhale yotithandiza
kutembenuka mtima ndipo chikondwerero chathu cha Kuuka kwa
Yesu Khristu pa chaka cha Paska chikhale chiyambi cha moyo
watsopano wa Amalawi onse. Tipemphe kuti Yosefe Woyera,
bambo womulera wa Ambuye Yesu Khristu, ayang’anire dziko lathu
kuti Mulungu aike mwa ife mtima wodzilemekeza, wachilungamo,
wokonda dziko lathu, wachikondi ndi wamtendere.
Tikupereka zosinkhasinkha zathuzi mowunikiridwa ndi Mzimu
Woyera ndiponso mu uneneri wa Maria, Mfumukazi ya Malawi
ndi Africa.
14
Malawi ndziko lokongola,
La chonde ndi ufulu,
Nyanja ndi mphepo ya m'mapiri,
Ndithudi tadala.
Zigwa, mapiri, nthaka, dzinthu,
N'mphatso zaulere.
Nkhalango, madambo abwino.
Ngwokoma Malaawi.
O Ufulu tigwirizane,
Kukweza Malawi.
Ndi chikondi, khama, kumvera,
Timutumikire.
Pa nkhondo nkana pa mtendere,
Cholinga n'chimodzi.
Mayi, bambo, tidzipereke,
Pokweza Malawi.
15
National Anthem in Chichewa
Signed:
Most Reverend George Tambala President, Archbishop of Lilongwe
Right Reverend Montfort Stima Vice President and Bishop of
Mangochi
Most Reverend Thomas Msusa Archbishop of Blantyre
Right Reverend Peter Musikuwa Bishop of Chikwawa
Right Reverend Martin Mtumbuka Bishop of Karonga
Right Reverend John Ryan Bishop of Mzuzu
Right Reverend Peter Chifukwa Bishop of Dedza
Right Reverend Alfred Chaima Bishop of Zomba
Right Reverend Yohane Nyirenda Auxiliary Bishop of Mzuzu
Right Reverend Vincent Mwakhwawa Auxiliary Bishop of Lilongwe
16