Download as pdf or txt
Download as pdf or txt
You are on page 1of 9

DZINA LA OPHUNZIRA: ______________________________________

2022 CHIFUNGA CLUSTER JCE MOCK EXAMINATIONS

CHICHEWA
PEPALA LACHIWIRI
Monday, 30 May, 2022 (Malikisi 50) Subject Number: J 032/II

Time Allowed: 1 Hr 45 Min

(11:00am – 12:45 pm)

1. Onetsetsani kuti
Nambala Chongani Osalemba umu
pepalali lili ndi
ya funso mafunso
masamba asanu ndi
okhawo
anayi ndipo lili
omwe
mmagawo atatu, A, B,
mwayankha
ndi C.
1
2. Yankhani mafunso
onse mu gawo A, B 2
ndi C.
3
3. Lembani dzina lanu
pamwamba pa tsamba 4
lililonse. 5
4. Perekani pepala lanu Total
kwa woyang’anira
mayeso nthawi yolembera mayeso ikatha.

© 2022 CHIFUNGA CLUSTER TURN OVER

Page 1 of 9
Gawo A (Malikisi 20)

KUMVETSA NKHANI

1. Werengani nkhani ili m’munsiyi mosamala ndipo muyankhe mafunso otsatirawo.

M’dziko mumo komanso mayiko ena a mu Africa anthu amakhala ndi zikhulupiliro
zosiyanasiyana. Nthawi zina anthu ochita kafukufuku amangoti anthu a ku Africa ndi anthu
odalira miyambo ndi zikhulupiliro. Izi zingathe kukhala zoona koma sizitanthauza kuti
anthu amitundu ina alibe miyambo ndi zikhulupiliro zawo ayi.

Tikaonetsetsa tiona kuti “mafirika” akalewo ataunikira adapeza nzeru zozama


zozitetezera komanso kuteteza katundu wawo ku zinthu zina zowononga. Mwachitsanzo,
chikhulupiliro choti ana asamasewere panja usiku asanavale malaya chifukwa mfiti
zingawawerenge mitsempha ndi nzeru yofuna kutetezera anawo ku zibayo’ Makolo athu
amatinso kunkhalango kumapezeka mizimu mwina pofuna kuteteza nkhalango kuti
zisadulidwe mwachisawawa.

Ngakhale pali zikhulupiliro zothandiza ngati zomwe zatchulidwa pamwambapa,


zikhulupiliro zina ndizoononga chitetezo cha miyoyo ya anthu. Kodi ndizoona kuti ana
akamadya mazira azidwaladwala? Zoti mnyamata ndi msungwana akatuluka ku
chinamwali agonane ndi munthu kuti “achotse fumbi” ndikuika moyo pa chiswe ndi mlili
wa Edzi wakulawu.

Miyambo ngati yoletsa amayi kukachilira kuchipatala nthawi yawo yikakwana ndiyo
yatsitsira ntchembere zambiri kulichete. Ndi chifukwa chake Boma ndi mabungwe
osiyanasiyana komanso mipingo zili pakalikiliki kudziwitsa anthu za kuopsa kwa miyambo
ina ngati imeneyi.

Chinthu chofunika kudziwa ndichakuti zinthu zimasintha. Ngakhale miyambo yakhala ili
chomwecho, zinthu zambiri zasinthasintha. Anthu achulukana koposa momwe adalili kale
ndipo zitukuko zosiyanasiyana zachitika. Mitengo yambiri yomwe anthu ankadalira ngati
mankwala idasowa. Choncho kukakamira ina mwa miyamboyi ndi zikhulupiliro zakalezo
ndikulimbira mtunda opanda madzi.

Page 2 of 9
Tsopano yankhani mafunso otsatirawa.

(a) N’chifukwa chiyani anthu aku Africa sayenera kudziwika monga anthu odalira
miyambo ndi zikhulupiliro?

______________________________________________________________________

_______________________________________________________________________
(malikisi 2)

(b) Kodi kufunika kwa miyambo ndi zikhulupiliro ndi kotani? Perekani kufunika kuwiri.

i.
_____________________________________________________________________

_____________________________________________________________________
(malikisi 2)

ii.
_____________________________________________________________________

_____________________________________________________________________
(malikisi 2)

(c) Fotokozani zikhulupiliro ziwiri zomwe zafotokozedwa mnkhaniyi zoononga miyoyo

ya anthu.

i.
_____________________________________________________________________

______________________________________________________________________
(malikisi 2)

ii.
_____________________________________________________________________

_____________________________________________________________________
(Malikisi 2)

Page 3 of 9
(d) Mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani padali zikhulupiliro zoletsa ana kudya mazira?
________________________________________________________________________
________________________________________________________________________
(malikisi 1)

(e) Kodi Boma ndi mabungwe athandiza bwanji kulimbana ndi zikhulupiliro zokhudza
kuchira kwa amayi?

________________________________________________________________________
________________________________________________________________________
________________________________________________________________________
(malikisi 2)

(f) Perekani matanthauzo a mawu otsatirawa monga momwe agwiritsidwira ntchito


munkhani mwawerengayi.

i. mafirika __________________________________________________________
(malikisi 2)

ii. kuika moyopachiswe


_______________________________________________________________________

______________________________________________________________________
(malikisi 2)

iii. yatsitsira miyoyo ya ntchembere zambiri kuli chete

______________________________________________________________________

_____________________________________________________________________
(malikisi 2)

(g) Perekani mutu woyenera wa nkhaniyi.

____________________________________________________________________
(malikisi 1)

Page 4 of 9
Gawo B (Malikisi 20)

NKHANI ZA MCHEZO NDI ZOLEMBEDWA

2. Werengani nkhani ili m’munsiyi ndipo muyankhe mafunso otsatirawo.

SOGA NDI CHIBINGWE

Chibingwe adangoti pakamwa gwii ndipo kenako misozi idalengeza m’maso. Iye
sadayembekezere kuti mlamu wake angamutsukuluze chotero. Mkazi wake Naphiri
ankangokondwera ndi mfundo iliyonse yomwe mchimwene wake adali kuyankhula.
Kawiri kapena katatu konse adayankhira movomereza mchimwene wake. “Ndizoona,
ndiwo mawu a mwamuna awa achimwene.” “ Uyu ndi mlongo wanga, mzime wa m’banja
mwathu. Iyeyu adaponda pamutu pangapa. Ukamandiona ine uzidziwa kuti waona Soga,
mwini mbumba. Usandione kutuwaku, ndimadya zanga ine. Kwanuko kudalibe mbeta zoti
ukadakwatira n’kumazilamulira? Ukachita masewera ndikuyatsira mwatso masana;
usandilowe ngati thekenya.

“Ndamva kuti umamunamiza mlongo wanga kudya galu. Umati akangotula mtolo ali
nawowu basi akatseketse. Akuti umati ana asanu basi akwana. Kodi ana a munthu amachita
kuwerenga ngati mandanda a nkhuku? Akutinso umati popeza iyeyu wakukanira
kukatseketsa umati ndiwe ukatseketse. Kodi ndiwe imbwa kapena ng’ombe yapajoko kuti
ukatseketse? Ndadziwa, ufuna kuti mlongo wanga anthu azimuyoyorera mnyozo kuti
adakwatiwa ndi mtheno. Ndi umunthu ukuchita iwewu?”

Chibingwe adakwatira pamudzi wa a Kombo zaka zisanu zapitazo ndipo banja lake lidali
kale ndi ana anayi. Chaka chilichonse ankabereka. Izi zinkamusangalatsa kwambiri mlamu
wake, Soga, yemwe ankati mbumba yake izikula.

“Achikhala kuti ufumu amalowera kukula kwa mbumba, chaka chino nkadaunyantha.
Ufumu tizilowa ndife oswana ngati mbewa. Ena angoyenda tumbwatumbwa m’muno
chikhalirecho alibe ndi mdzukulu yemwe.” Ankalalata chotere Soga akadakwa.

Soga adali ng’oma ya m’mudzi mwa a Kombo kaamba koti adali mbiyang’ambe. Umphawi
ndi njala zidali abwenzi a banja lake chifukwa adalibe nthawi yogwira ntchito. Kukacha

Page 5 of 9
amangoganiza za mowa. Mkazi wake adamuthawira asadachembeze n’komwe kaamba ka
uchidakwa ndi unyopo. Nthawi zambiri Soga ankadya nsima kwa mlamu wake.

Atadya mutu, Chibingwe adayankhula, “Ndamva mawu anu onse. Zonse akuuzani alongo
anu ndi zoona. Ine ndimavutika kwambiri kupeza zofunika pa banja pano. Mayiwa akamwa
madzi ndiye kuti mnyumba muno tikhalamo anthu asanu ndi awiri. Pa nkhani yachakudya
ndiye kuti tikhalamo asanu ndi atatu. Zikundivuta kwambiri…”

“Thula! Khala chete, mlesi!” Soga adamudula m’kamwa mlamu wake. “Iwe ulibe
ulamuliro pabanja pano. Pamudzi pano usamayese kuti mpazitsiru kuti uzikulirapo
mwendo. Umavutika chiyani pano? Amavutika ndi mlongo wanga. Kodi umamuthandiza
kusenza ndi kutula mitolo?”

Chibingwe ataona kuti mlamu wake wamkitsa nacho chipongwe adamanga katundu wake.
Iye sadatsanzike munthu wina aliyense ndipo sakudziwika komwe adalowera.

Tsopano yankhani mafunso otsatirawa.

(a) Kodi nkhaniyi ikuchitikira kuti?

________________________________________________________________________
(malikisi 1)

(b) N’chifukwa chiyani Soga adakalipira mlamu wake?

______________________________________________________________________

______________________________________________________________________
(malikisi 2)

(c) Perekani makhalidwe awiri a Soga

________________________________________________________________________
________________________________________________________________________
________________________________________________________________________
(malikisi 2)

(d) Perekani zipangizo ziwiri zomwe mlembi wagwiritsa ntchito m’nkhaniyi.


Page 6 of 9
________________________________________________________________________
________________________________________________________________________
(malikisi 2)

(e). Kodi mawu awa akutanthauzanji mnkhaniyi?

i. “kodi umamuthandiza kuseza ndi kutula mitolo?”

________________________________________________________________________
(malikisi 1)

ii. “Soga adali ng’oma ya m’mudzi”

________________________________________________________________________

(malikisi 1)

(f). Mukuganiza kuti a Chibingwe adathawa chiyani?

________________________________________________________________________

(malikisi 1)

3. Werengani ndakatulo ili m’munsimu ndipo muayankhe mafunso

Otsatirawo.

KUSIMBA TSOKA

Anandiuza kuti uku kuli mame


Ndi matope ndisapitireko,
Ine ndibvomera

Koma lero m’mawa sindiye ndili uku


kwatalika ndingopitira komweku:
tsopano si uno?

Tsono matope awa sindiye ndikayang’ana


Sopo, kapena masamba kuti anthu aja
Asakazindikire?
Nanga, zikalephereke zitayang’anana
Page 7 of 9
Watifikitsa pati anthuni:
Ukhutukumve?

Tsopano yankhani mafunso otsatirawa

(a) . Kodi akuyankhula mndakatuloyi ndani?


________________________________________________________
(malikisi 1)

(b) . Nanga kodi woyankhulayu akuti chiyani?


________________________________________________________
(malikisi 2)

(c) Perekani zipangizo zitatu zomwe mlembi wagwiritsa ntchito


m’ndakatuloyi
________________________________________________________
________________________________________________________
________________________________________________________
(malikisi 3)

(d) . Kodi mawu oti “ukhutukumve” mndakatuloyi akutanthauzanji?


________________________________________________________
________________________________________________________
(malikisi 2)

(e) Perekani phunziro limodzi lopezeka m’ndakatuloyi


________________________________________________________
(malikisi 2)
Gawo C (malikisi 10)

4. Masulirani kandime kali m’musika m’Chichewa chomveka bwino.

One day, Hyena visited Antelope. Hyena told him that he wanted them to become friends.
But in reality, Hyena never wanted them to be friends. He wanted to eat Antelope because
Antelope was big and plumb.
Page 8 of 9
________________________________________________________________________
________________________________________________________________________
________________________________________________________________________
________________________________________________________________________
________________________________________________________________________
________________________________________________________________________
________________________________________________________________________
(malikisi 5)

5. Fupikitsani kankhani kali m’munsika kuti kakhale ndi mawu osachepera 11 koma

asapitilire 15.

Nyamata wamtali kwambiri uja, uja nthawi zonse amayenera kuwerama kuti adutse
pakhomo la nyumba yakwathu ija, akuti abwera masiku awiri akubwera kutsogoloku ndi
Joni, Masiye ndi Mavuto kuti azatenge tanaposi, mpiru, mkhwani ndi kabichi.

________________________________________________________________________
________________________________________________________________________
________________________________________________________________________
________________________________________________________________________
________________________________________________________________________
(malikisi 5)

MAFUNSO ATHERA PANO

Page 9 of 9

You might also like