Professional Documents
Culture Documents
02_Chichewa_Module_1_301117
02_Chichewa_Module_1_301117
02_Chichewa_Module_1_301117
Buku lophunzitsira
m’Sukulu za Uphunzitsi
Chichewa
Buku loyamba
Chaka choyamba
Chichewa
Buku loyamba
Chaka choyamba
Omwe adalemba ndi kusindikiza bukuli
Email: miedirector@sdnp.org.mw
Website: www.mie.edu.mw
Okonza
Executive Director
vi
Zam’katimu
vii
MUTU1 Kufunika kwa phunziro la Chichewa
1
Kufotokoza mwachidule 3. N’chifukwa chiyani ophunzira ena
M’mutu uno mwaphunzira tanthauzo sakonda phunziro la Chichewa?
la maluso a chiyankhulo ndi kufunika 4. Mungachite bwanji kuti ophunzira
kwake. Mwaona mgwirizano womwe anu azikonda phunziro la
umakhalapo pa maluso a kumva ndi Chichewa?
kuyankhula, kuwerenga, kulemba,
kuganiza mozama ndi kugwiritsa Mabuku
ntchito malamulo a chiyankhulo. Malawi Institute of Education (2009).
Pomaliza, mwafotokoza kufunika Initial Primary Teacher Education
kophunzitsa phunziro la Chichewa through Open and Distance
kusukulu zapulayimale ndi kusukulu Learning (ODL) Chichewa Module
zophunzitsa ntchito yauphunzitsi. 1. Domasi: MIE.
Malawi Institute of Education (2008).
Kudziunika ndi kudziyesa Maphunziro M’sukulu
1. Pa maluso asanu ndi limodzi a Zauphunztsi m ‘Malawi Buku la
chiyankhulo, mukuganiza kuti ndi Mphunzitsi. Domasi: MIE.
maluso anayi ati omwe ndi
akuluakulu?
2. Kodi maluso ena awiriwa
amathandiza bwanji maluso
akuluakulu anayi a chiyankhulo?
2
MUTU 2 Silabasi, buku la mphunzitsi ndi la ophunzira
3
dongosolo la ntchito ndi chikonzekero 1 Unikaninso mwachidwi silabasi,
cha phunziro. Akuyeneranso kudziwa buku la mphunzitsi ndi la
kulumikizana kwa mitu ya ntchito ophunzira.
kuyambira m’Sitandade 1 mpaka 8. 2 Pitani ku sukulu yapulayimale
yomwe mwayandikana nayo ndi
Ntchito 1 Kufananitsa ntchito kukafufuza momwe mphunzitsi
yopezeka mu silabasi ndi ndi ophunzira amagwiritsira
yomwe ili m’buku la ntchito silabasi, buku la
mphunzitsi ndi la mphunzitsi ndi buku la
ophunzira ophunzira.
3 Perekani maganizo anu pa zomwe
1 Kambiranani tanthauzo la mwapeza.
silabasi.
2 Unikani mwachidwi silabasi, Malangizokwa mphunzitsi
buku la mphunzitsi ndi la
Muombe mkota pa ntchito yomwe
ophunzira.
ophunzira achita.
3 Kambiranani ntchito yopezeka
m’silabasi, m’buku la mphunzitsi
ndi la ophunzira. Ntchito 3 Kugwiritsa ntchito
4 Fananitsani ntchito yopezeka silabasi, buku la
m’mabukuwa. mphunzitsi ndi la
5 Siyanitsani ntchito yopezeka ophunzira
m’mabukuwa. 1 Unikaninso kagwiritsidwe ntchito
ka silabasi, buku la mphunzitsi
Malangizo kwa mphunzitsi ndi la ophunzira.
Mufufuziretu tanthauzo la 2 Zukutani zomwe zikupezeka
silabasi powerenga mabuku ena. m’magawo a silabasi, buku la
Mupezeretu masilabasi, mabuku mphunzitsi ndi la ophunzira.
a aphunzitsi ndi mabuku a 3 Sonyezani momwe
ophunzira a Sitandade 1 mpaka mungagwiritsire ntchito
4. mabukuwa.
Mupempheretu chilolezo kwa 4 Perekani maganizo anu pa ntchito
mphunzitsi wamkulu wa sukulu yomwe anzanu achita.
yomwe ophunzira anu achiteko
kafukufuku.
Malangizo kwa mphunzitsi
Ntchito 2 Kufufuza momwe Muombe mkota pa ntchito yomwe
mphunzitsi ophunzira achita.
amagwiritsira ntchito
silabasi, mabuku
Kufotokoza mwachidule
M’mutu uno mwaphunzira tanthauzo
ophunzitsira ndi
la silabasi, mwaunika ntchito
ophunzirira
zopezeka m’magawo a silabasi, buku
la mphunzitsi ndi la ophunzira.
4
Mwafananitsa ndi kusiyanitsa ntchito
yopezeka m’magawo a silabasi, buku Buku la
la mphunzitsi ndi la ophunzira. mphunzitsi: buku lotsatira silabasi
Kenaka, mwafufuza momwe lomwe limatsogolera
mphunzitsi ndi ophunzira mphunzitsi polemba
akupulayimale amagwiritsira ntchito chikonzekero cha
mabukuwa. Potsiriza, mwasonyeza phunziro ndi
momwe mungagwiritsire ntchito pophunzitsa
silabasi, buku la mphunzitsi ndi la
ophunzira.
Buku la
Kudziunika ndi kudziyesa ophunzira: buku lotsatira silabasi
1 Tchulani magawo a silabasi omwe lomwe ophunzira
mungapezemo izi:
amagwiritsa ntchito
bokosi la kanema
ayankha moni molondola Mabuku
malonje Malawi Institute of Education
amva malonje (2009).Initial Primary Teacher
mafunso ndi mayankho Education (IPTE) through Open
kupatsana moni molondola and Distance Learning (ODL)
2 Fotokozani kusiyana kwa buku la
Chichewa module 1.Domasi:
mphunzitsi ndi buku la
MIE.
ophunzira.
3 Mungachite chiyani ngati Malawi Institute of Education (2008).
pasukulu pomwe mukuphunzitsa Maphunziro M’sukulu
palibe silabasi? Zauphunztsi m ‘Malawi buku la
4 Fotokozani kagwiritsidwe ntchito mphunzitsi. Domasi: MIE.
ka zipangizo zotsatirazi
pophunzitsa:
kalilole (galasi)
bokosi la kanema
nthenga
zithunzi zotukuza
Matanthauzo a mawu
5
MUTU 3 Kaphunzitsidwe ka kumva ndi kuyankhula
Zizindikiro zakakhozedwe
Luso : Kumva ndi kuyankhula Pakutha pa mutu uno, ophunzira:
Nthawi : Maola 5 apeza mitu ya kumva ndi
kuyankhula m’mabuku a
Chigawo: Choyamba Sitandade 1 mpaka 4.
Chiyambi afotokoza mitundu ya maliwu,
Mphunzitsi akuyenera kuphunzitsa malonje ndi zouzidwa.
maluso a kumva ndi kuyankhula asonyeza kaphunzitsidwe ka
moyenera. Ophunzira akaphunzira mitundu ya maliwu, malonje
luso la kumva ndiye kuti adzakhala ndi zouzidwa.
atcheru ndi kumvetsetsa nkhani
zosiyanasiyana zomwe ena Mawu otsogolera
akuyankhula. Akaphunzira luso la M’silabasi ya kupulayimale muli mitu
kuyankhula adzatha kupereka ya ntchito ya kumva ndi kuyankhula
maganizo awoawo kwa ena yosiyanasiyana. Ntchito za m’mituyi
poyankhula mosakayika m’zochitika zimakulitsa maluso akumva ndi
zosiyanasiyana. kuyankhula kwa ophunzira ndi
mphunzitsi. Pali njira zosiyanasiyana
Ngakhale kuti kumva ndi kuyankhula zomwe mphunzitsi angagwiritse
ndi maluso awiri osiyana, ntchito pophunzitsa ntchito za kumva
pophunzitsa amaphunzitsidwira ndi kuyankhula. Mphunzitsi
nthawi imodzi. N’kovuta kuti akuyenera kuzindikira mitundu,
mphunzitsi asiyanitse chifukwa kufunika ndi ndondomeko
kumva ndi kuyankhula kumachitika yophunzitsira mitu ya ntchito ya
nthawi imodzi. Pamene wina kumva ndi kuyankhula kuti athandize
akuyankhula wina amamvetsera. Izi ophunzira moyenera.
zili chimodzimodzi m’kalasi;
ophunzira amayenera amagwiritsa Ntchito 1 Kufotokoza kufunika kwa
ntchito maluso akumva ndi maluso a kumva ndi
kuyankhula. Mphunzitsi amadziwa kuyankhula
kuti ophunzira amva ngati akuchita 1 Kambiranani kufunika kwa
zomwe amva monga poyankha maluso a kumva ndi kuyankhula.
mafunso molondola. 2 Fotokozerani anzanu zomwe
mwalemba.
M’mutu uno, muphunzira momwe 3 Perekani maganizo anu pa ntchito
mungaphunzitsire maluso a kumva yomwe anzanu achita.
ndi kuyankhula mu Sitandade 1
mpaka 4.
6
Malangizo kwa mphunzitsi Ntchito 4 Kufotokoza mitundu ya
Mufufuziretu mfundo zosonyeza maliwu, malonje ndi
kufunika kwa maluso a kumva ndi zouzidwa
kuyankhula.
1 Kambiranani tanthauzo la
Ntchito 2 Kufufuza mitu ya kumva maliwu, malonje ndi zouzidwa.
ndi kuyankhula mu 2 Kambiranani mitundu ya maliwu,
Sitandade 1 mpaka 4 malonje ndi zouzidwa.
3 Lembani zomwe mwakambirana.
1 Unikani mitu ya ntchito ya 4 Fotokozerani anzanu zomwe
maluso a kumva ndi kuyankhula mwalemba.
m’mabuku a Sitandade 1 mpaka 5 Perekani maganizo anu pa ntchito
4. yomwe anzanu achita.
2 Lembani zomwe mwapeza. Malangizo kwa mphunzitsi
3 Fotokozerani anzanu zomwe Mufufuziretu mitundu ya
mwapeza. maliwu, malonje ndi zouzidwa.
4 Perekani maganizo anu pa ntchito Muombe mkota pa ntchito
yomwe anzanu achita. yomwe ophunzira achita.
7
Ntchito 6 Kusonyeza 4 Yerekezani kuti mukuphunzitsa
kaphunzitsidwe ka liwu latsopano /dw/ m’Sitandade
mitundu ya maliwu, 1 ndipo mwawauza ophunzira
malonje ndi zouzidwa kuti aziloza chala m’mwamba
mukatchula mawu oyamba ndi
1 Unikani ndondomeko /dw/. Koma Zondiwe waloza
yophunzitsira maliwu, malonje chala m’mwamba mutatchula
ndi zouzidwa. mawu oti “dala”. Fotokozani
2 Sonyezani momwe zomwe mungachite ndi Zondiwe.
mungphunzitsire mitu yotsatirayi:
a mitundu ya maliwu mu Matanthauzo a mawu
Sitande 1 ndi 2. Kuyankhula kutulutsa mawu
b mitundu ya malonje mu atanthauzo kudzera
Sitandade 1 mpaka 4. pakamwa
c zouzidwa.
Kumva kulandira mawu kudzera
3 Perekani maganizo anu pa ntchito
m’makutu
yomwe anzanu achita.
8
http://www.scsk12.org/scs/subjectarea https://cehdvision2020.umn.edu/blog/
s/kweb/images/nationalreadingpanel_ helping-kids-with-reading/
faq.pdf
9
MUTU 4 Kaphunzitsidwe ka kuwerenga
Luso : Kuwernga
Nthawi: Maola 6 Mawu otsogolera
Chigawo: Choyamba Kuphunzitsa kuwerenga pogwiritsa
ntchito nsanamira zisanu za
Chiyambi kuwerenga kumathandiza ophunzira
Luso la kuwerenga ndi limodzi mwa kuzamitsa luso la kuwerenga.
maluso ofunika m’phunziro la Mphunzitsi ayenera kudziwa ndi
Chichewa. Mphunzitsi ayenera kumvetsa bwino nsanamira zisanu za
kudziwa zolinga zophunzitsira kuwerenga zomwe ndi zotsatirazi:
kuwerenga m’sukulu zapulayimale.
Kumva ndi kutchula maliwu
Kuwerenga kumathandiza ophunzira
Ophunzira ayenera kumvetsetsa kuti
kudziwa chiyankhulo. Ophunzira
mawu amapangidwa ndi maliwu.
amapeza nzeru zambiri kuchokera pa
Mwachitsanzo, mawu oti
zomwe akuwerenga zomwe ndi
“ana”apangidwa ndi maliwu awa: /a/,
zothandiza pa moyo wawo.
/n/ ndi /a/.
M’mutu uno ndi wotsatira,
Kuzindikira malembo ndi maliwu
muphunzira momwe
Ophunzira ayenera kumvetsetsa kuti
mungaphunzitsire kuwerenga
malembo amaimira maliwu, ndipo
m’sukulu za pulayimale potsatira
mawu amapangidwa kuchokera ku
nsanamira zisanu za kuwerenga.
malembowa. Mu Sitandade 1 muli
Zizindikiro zakakhozedwe malembo awa: a, n, i, m, u, k, o, l, e, w
Pakutha pa mutu uno, ophunzira: t, d, s, p, nd, ch, y, b, z, g, r, f, h, j, v,
afotokoza za nsanamira ya dz, mw, nz, kw, ts, th, mb, kh, ng, ns,
kumva ndi kutchula maliwu, mp, nj, ny, bw, mt, ph, ng’, dw, ps, bz,
kuzindikira malembo ndi fw, gw, ml, mv, dy, ms, sw, mk, mz
maliwu ake ndi nsanamira ya ndipo mu Sitandade 2 muli malembo
kuwerenga molondola, awa: mf, m’b, mph, nth, tch, mgw,
ng’w, mch, khw, phw, mg, mm, pw,
mofulumira ndi mosadodoma.
sh, zw, zy, nkh, ngw, mts, mbw, ndw,
asonyeza kaphunzitsidwe ka
thw, thy, tsw, msw, nsw, mpw, ntch,
nsanamira ya kumva ndi
nkhw, mphw, mtch, nthw, mtsw ndi
kutchula maliwu, kuzindikira
mnkhw.
malembo ndi maliwu ake ndi
nsanamira ya kuwerenga Kuwerenga molondola, mofulumira
ndi mosadodoma
molondola, mofulumira ndi
Uku ndi kuzindikira maliwu ndi
mosadodoma mu Sitandade 1
mawu mosataya nthawi.
mpaka 4.
10
Kudziwa mawu ndi matanthauzo Ntchito 2 Kusonyeza
ake kaphunzitsidwe ka kumva
Uku ndi kudziwa matanthauzo a ndi kutchula maliwu mu
mawu osiyanasiyana m’chiyankhulo. Sitandade 1 ndi 2
11
Ntchito 5 Kusonyeza
kaphunzitsidwe ka
Malangizo kwa mphunzitsi
kuzindikira malembo ndi
Mulemberetu malembo onse pa
maliwu ake mu Sitandade
tchati.
1 ndi 2
Musonyeze ophunzira
katchulidwe ka liwu lililonse. 1 Unikani ntchito zophunzitsira
Muthandize ophunzira kutchula nsanamira ya kuzindikira
maliwu a malembowa moyenera. malembo ndi maliwu ake.
Muchite ntchitoyi 2 Sonyezani momwe
mobwerezabwereza mpaka mungaphunzitsire ntchitozo.
ophunzira atadziwa bwino 3 Zukutani phunziro lililonse.
katchulidwe ka maliwu a
Malangizo kwa mphunzitsi
malembowa.
Muonetsetse kuti ophunzira
Ntchito 4 Kukambirana zitsanzo za akutsatira njira yoyamba ndi
ntchito zophunzitsira mphunzitsi, mphunzitsi ndi
nsanamira ya kuzindikira ophunzira, kenaka ophunzira
malembo ndi maliwu paokha moyenera.
Muombe mkota pa ntchito
1 Pezani zitsanzo za ntchito
yomwe ophunzira achita.
zophunzitsira nsanamira ya
kuzindikira malembo ndi maliwu Ntchito 6 Kufotokoza nsanamira ya
ake kuchokera m’buku la kuwerenga molondola,
mphunzitsi ndi la ophunzira la mofulumira ndi
Sitandade 1 ndi 2. mosadodoma
2 Kambiranani zitsanzo zomwe
1 Pezani ntchito zosiyanasiyana
mwapeza.
zomwe zingathandize ophunzira
3 Fotokozerani anzanu zomwe kuwerenga molondola,
mwakambirana. mofulumira ndi mosadodoma
Malangizo kwa mphunzitsi kuchokera m’mabuku a
aphunzitsi a Sitandade 1 mpaka 4.
Mutsogolere ophunzira kupeza 2 Kambiranani njira zomwe
zitsanzo za ntchito zophunzitsira zingathandize ophunzira
nsanamira ya kuzindikira kuwerenga molondola,
mofulumira ndi mosadodoma pa
malembo ndi maliwu ake.
ntchito zomwe mwapeza.
Musonyeze ophunzira kachitidwe
3 Fotokozerani anzanu zomwe
ka ntchito (routine) iliyonse.
mwakambirana.
Muombe mkota pa ntchitoyi.
12
Malangizo kwa mphunzitsi potsatira nsanamira zitatu izi: kumva
Mufufuziretu njira zomwe ndi kutchula maliwu, kuzindikira
zingathandize ophunzira malembo ndi maliwu ake, kuwerenga
kuwerenga molondola, molondola, mofulumira ndi
mofulumira ndi mosadodoma. mosadodoma. Pomaliza, mwazukuta
Musonyeze ophunzira kachitidwe maphunziro omwe mwasonyeza.
ka njira iliyonse.
Kudziunika ndi kudziyesa
Muombe mkota pa ntchito
1 Fotokozani nsanamira zisanu za
yomwe ophunzira achita.
kuwerenga.
Ntchito 7 Kusonyeza 2 Fotokozani njira zosiyanasiyana
kaphunzitsidwe ka zothandiza ophunzira kuwerenga
kuwerenga molondola, molondola, mofulumira ndi
mofulumira ndi mosadodoma.
mosadodoma m’Sitandade
Matanthauzo a mawu
1 mpaka 4
Liwu chimene chimamveka
1 Unikani njira zophunzitsira m’khutu poimba nyimbo,
nsanamira ya kuwerenga ng’oma, beru ndi zina
molondola, mofulumira ndi
Mabuku
mosadodoma.
Adams, MJ (1994). Beginning to read:
2 Sonyezani momwe
thinking and learning about print.
mungaphunzitsire kuwerenga
First Edition. England: The MIT
molondola, mofulumira ndi Press.
mosadodoma. Caldwell, JS (2014). Reading assessment:
3 Zukutani phunziro lililonse. a primer for teachers in the core
era.Third Edition. New York:
Malangizo kwa mphunzitsi
The Guilford Press.
Muonetsetse kuti ophunzira
Centre for Language Studies (2000).
akutsatira njira yoyamba ndi
Mtanthauzira mawu wa
mphunzitsi, mphunzitsi ndi Chinyanja. Blantyre: Dzuka.
ophunzira, kenaka ophunzira
paokha moyenera. Cunningham, PM and Allington, RL
(2011). Classrooms that work:
Muombe mkota pa ntchito
they can all read and write. Fifth
yomwe ophunzira achita.
Edition. Boston: Pearson.
Malawi Institute of Education (2008).
Kufotokoza mwachidule
Maphunziro a m’sukulu za
M’mutu uno, mwaphunzira
uphunzitsi m’Malawi:
nsanamira zisanu za kuwerenga.
Chichewa buku la mphunzitsi,
Mwasonyeza momwe
Domasi: MIE.
mungaphunzitsire kuwerenga
13
Malawi Institute of Education (2008). Student teacher’s handbook 2
Initial primary teacher education
(IPTE): English tutor’s Kuwerenga koonjezera
handbook. Domasi: MIE. https://www.readnaturally.com/resear
ch/5-components-of-reading
Malawi Institute of Education, (2009).
http://www.scsk12.org/scs/subjectarea
Initial Primary Teacher
s/kweb/images/nationalreadingpanel_
Education (IPTE) through
faq.pdf
Open and Distance Learning
https://cehdvision2020.umn.edu/blog/
(ODL): Chichewa Module 1.
helping-kids-with-reading/
First Edition. Lilongwe: MIE
Domasi
14
MUTU 5 Kaphunzitsidwe ka kuwerenga (kupitiriza)
Luso: Kuwerenga
Nthawi: Maola 7 Mawu otsogolera
Chigawo: Choyamba Kuphunzitsa kuwerenga pogwiritsa
ntchito nsanamira zisanu za
kuwerenga kumathandiza ophunzira
Chiyambi kuzamitsa luso la kuwerenga.
Kuwerenga ndi limodzi mwa maluso Mphunzitsi ayenera kudziwa ndi
ofunika kwambiri m’phunziro la kumvetsa bwino nsanamirazi.
Chichewa. Mphunzitsi ayenera
kudziwa momwe ayenera Ntchito 1 Kufotokoza nsanamira ya
kuphunzitsira lusoli kuti athe kudziwa mawu ndi
kuphunzitsa moyenera. M’mutu 4 matanthauzo ake
munaphunzira za luso la kuwerenga. 1 Kambiranani njira zothandiza
M’mutuwo munaphunzira momwe ophunzira kupeza matanthauzo a
mungaphunzitsire kuwerenga mawu atsopano.
m’sukulu zapulayimale potsatira zina 2 Fotokozerani anzanu zomwe
mwa nsanamira zisanu zophunzitsira mwakambirana
kuwerenga. 3 Pezani njira zosiyanasiyana
zomwe zingathandize ophunzira
M’mutu uno, mupitiriza kuphunzira kudziwa mawu ndi matanthauzo
nsanamira ya kudziwa mawu ndi ake kuchokera m’mabuku a
matanthauzo ake ndi ya kumvetsa aphunzitsi a Sitandade 1 mpaka 4.
nkhani. 4 Fotokozerani anzanu zomwe
mwapeza.
Zizindikiro za kakhozedwe
Pakutha pa mutu uno, ophunzira: Malangizo kwa mphunzitsi
afotokoza nsanamira ya Mufufuziretu njira zomwe
kudziwa mawu ndi zingathandize ophunzira kupeza
matanthauzo ake. mawu atsopano ndi matanthauzo
asonyeza kaphunzitsidwe ka ake.
nsanamira ya kudziwa mawu Musonyeze ophunzira kachitidwe
ndi matanthauzo ake. ka njirazi.
afotokoza nsanamira ya Muombe mkota pa ntchito
kumvetsa nkhani. yomwe ophunzira achita.
asonyeza kaphunzitsidwe ka
nsanamira ya kumvetsa
nkhani.
15
Ntchito 2 Kusonyeza
kaphunzitsidwe ka
kupeza matanthauzo a Malangizo kwa mphunzitsi
mawu m’Sitandade 1 Mutsogolere ophunzira
mpaka 4 kusiyanitsa ntchito za
1 Unikani njira zophunzitsira kumvetsera nkhani ndi
nsanamira ya kupeza kumvetsa nkhani zomwe
matanthauzo a mawu. ophunzira awerenga.
2 Sonyezani momwe Muombe mkota pa ntchito
mungaphunzitsire ophunzira yomwe ophunzira achita.
kupeza matanthauzo a mawu
Ntchito 4 Kusonyeza
pogwiritsa ntchito njirazi.
kaphunzitsidwe ka
3 Zukutani phunziro lililonse.
kumvetsa nkhani
Malangizo kwa mphunzitsi m’Sitandade 1 mpaka 4
16
ophunzira, kenaka ophunzira
yomwe
Ntchito 6: Kusonyeza
Ntchito 5: Kuonerera phunziro la kaphunzitsidwe ka
kuwerenga pogwiritsa phunziro la kuwerenga
ntchito nsanamira za potsatira nsanamira za
kuwerenga mu Sitandade kuwerenga
1 mpaka 4
1. Kambiranani m’magulu
1. Kambiranani mfundo zoyenera momwe mungaphunzitsire
kutsatira poonerera phunziro phunziro la kuwerenga mu
la kuwerenga m’makalasi a Sitandade 1 mpaka 4.
Sitandade 1 mpaka 4. 2. Sonyezani momwe
Kodi mphunzitsi akutsatira mungaphunzitsire phunziro
dongosolo loyenera loyamba lomwe mwakonza.
ndi mphunzitsi, mphunzitsi 3. Kambiranani momwe phunziro
ndi ophunzira kenako layendera.
ophunzira paokha?
Malangizo kwa mphunzitsi
Kodi mphunzitsi akutsatira
Mufufuziretu njira zophunzitsira
dongosolo loonetsetsa kuti
kumvetsa nkhani m’Sitandade 1
ophunzira akumvetsa zomwe
mpaka 4.
akuphunzira?
Musonyeze ophunzira kachitidwe
Ndi nsanamira ziti zimene
ka njirazi.
zaphunzitsidwa?
Muombe mkota pa ntchito
Phunziro latenga nthawi
yomwe ophunzira achita.
yochuluka bwanji?
Muonetsetse kuti ophunzira
Lembani zina zomwe mwaona.
akutsatira njira yoyamba ndi
2. Onererani phunziro la
mphunzitsi, mphunzitsi ndi
kuwerenga pogwiritsa ntchito
ophunzira, kenaka ophunzira
mfundo zomwe
paokha moyenera.
mwakambirana.
3. Kambiranani zomwe mwaona.
Kufotokoza mwachidule
Malangizo kwa mphunzitsi
M’mutu uno mwaphunzira nsanamira
Onetsetsani kuti ophunzira ziwiri za kuwerenga. Mwafotokoza za
akudziwa zoyenera kuchita kudziwa mawu ndi matanthauzo ake
poonerera phunziro. ndi kumvetsa nkhani. Kenaka,
Limbikitsani ophunzira kulemba mwasonyeza momwe
zomwe akuona. mungaphunzitsire kuwerenga
pogwiritsa ntchito nsanamirazi.
17
Potsiriza, mwaonerera ndi kuzukuta Malawi Institute of Education
maphunziro a kuwerenga. (2008).Initial primary teacher
education (IPTE): English tutor’s
Kudziunika ndi kudziyesa handbook, Domasi: MIE.
1. Fotokozani njira
zosiyanasiyana zothandiza Ministry of Education, Science and
ophunzira kupeza Technology (2009). Initial
matanthauzo a mawu Primary Teacher Education
atsopano. through Open and Distance
2. Pa maphunziro omwe Learning (ODL): Chichewa
munaonerera, ndi zinthu ziti Module 1. First Edition.
zomwe sizinayende bwino? Lilongwe: DTED.
18
MUTU 6 Kaphunzitsidwe ka kukonzekera kulemba
Luso : Kulemba
phunziro la kukonzekera kulemba
Nthawi: Maola 4
Chigawo: Choyamba akuyenera kutsatira ndondomeko
zomwe zimathandiza ophunzira
kukhala ndi chidwi ndi phunziro.
Chiyambi Imodzi mwa ntchito zomwe
Mphunzitsi ayenera kuchita ntchito mphunzitsi angachite ndi ophunzira
zosiyanasiyana m’phunziro la ndi kulemba zitchetche. Zitchetchezi
konzekera kulemba. Izi zimathandiza zimalembedwa mosiyanasiyana
ophunzira kuti aphunzire kulemba motere:
mosavuta. Choncho mphunzitsi
ayenera kutsatira ndondomeko ya Kwera tsika kwera tsika
phunziro la kulemba moyenera. Chitchetche chothandiza polemba
malembo awa: A, M, N, W, X, V ndi Y
M’mutu uno, muphunzira ntchito monga:
zomwe mphunzitsi angachite ndi
ophunzira pa phunziro la
kukonzekera kulemba. Mufotokoza
kufunika kwa zitchetche. Kenaka, Tsika zungulira kwera
mulemba ndondomeko yophunzitsira
Chitchetche chothandiza polemba
phunziro la kukonzekera kulemba.
malembo awa: o, u, a, b, c, e, g, l ndi t
Pomaliza musonyeza momwe
monga:
mungaphunzitsire kukonzekera
kulemba.
Zizindikiro za kakhozedwe
Pakutha pa mutu uno, ophunzira: Kwera zungulira tsika
19
Chitchetche chothandiza polemba 3 Sonyezani anzanu zomwe
malembo awa: E, F, G, I, K, L ndi T mwalemba.
monga: 4 Kambiranani kufunika kwa
zitchetche.
5 Lembani zomwe mwakambirana.
6 Fotokozerani anzanu zomwe
Pendeka pingasa mwalemba.
20
Ntchito 4 Kuonerera phunziro la Ntchito 5 Kusonyeza
kukonzekera kulemba kaphunzitsidwe ka kukonzekera
kulemba
1. Kambiranani mfundo zoyenera
kutsatira poonerera phunziro 1 Unikani ndondomeko
la kukonzekera kulemba mu yophunzitsira phunziro la
Sitandade 1 ndi 2 motere: kukonzekera kulemba yomwe
Kodi mphunzitsi akutsatira munalemba.
dongosolo loyenera loyamba 2 Sonyezani momwe
ndi mphunzitsi, mphunzitsi mungaphunzitsire kukonzekera
ndi ophunzira, kenaka kulemba mu Sitandade 1.
ophunzira paokha? 3 Perekani maganizo anu pa ntchito
Kodi mphunzitsi akutsatira yomwe anzanu achita.
dongosolo loonetsetsa kuti
Malangizo kwa mphunzitsi
ophunzira akumvetsa zomwe
Muombe mkota pa ntchito yomwe
akuphunzira?
ophunzira achita.
Kodi ophunzira akupatsidwa
mpata wokwanira woyesera Kufotokoza mwachidule
kulemba? M’mutu uno mwaphunzira zomwe
Phunziro latenga nthawi mphunzitsi angachite ndi ophunzira
yochuluka bwanji? pa phunziro la kukonzekera kulemba.
Lembani zina zomwe Mwafotokoza kufunika kwa
mwaona. zitchetche. Pomaliza, mwaphunzitsa,
2. Onererani phunziro la mwaonera ndi kuzukuta phunziro la
kukonzekera kulemba. kukonzekera kulemba.
3. Kambiranani zomwe mwaona.
Kudziunika ndi kudziyesa
Malangizo kwa mphunzitsi 1 Fotokozani ntchito zitatu zomwe
Onetsetsani kuti ophunzira mungachite ndi ophunzira pa
akudziwa zoyenera kuchita. phunziro la kukonzekera
Limbikitsani ophunzira kulemba kulemba.
zomwe akuona. 2 Fotokozani zitsanzo ziwiri za
Onetsetsani kuti mwabweretsa zitchetche.
mabuku ophunzitsira Chichewa 3 Yerekezani kuti mphunzitsi wa
mu Sitandade 1 mpaka 4. Sitandade 1 amanyozera
Perekani nthawi yokwanira kuti kuphunzitsa phunziro la
ophunzira akonzekere phunziro kukonzekera kulemba pogwiritsa
lophunzitsa kuwerenga. ntchito zitchetche. Kodi
mungamulangize zotani?
21
Matanthauzo a mawu zauphunzitsi m’Malawi buku la
Zitchetche: mapatani osiyanasiyana mphunzitsi. Domasi: MIE.
omwe amathandiza
Kuwerenga koonjezera
ophunzira kulemba
Unduna wa za maphunziro (1998).
malembo
Student teachers handbook 2
Mabuku (Revised draft version).
Malawi Institute of Education (2008). Domasi: MIE.
Maphunziro a m’sukulu
22
MUTU 7 Kaphunzitsidwe ka mitundu ya kulemba
Luso: Kulemba
Kulemba
Nthawi: Maola 1
kolumikiza/kwachikhukhudza/
Chigawo: Choyamba
moguza
Chiyambi
Kulemba ndi luso limene munthu Kulemba kwachikhukhudza kulipo
aliyense ayenera kulidziwa. Luso la kwa mitundu iwiri.
kulemba limathandiza ophunzira
Kulemba kwachipama
kudziwa kulemba nkhani zochitika
Kulemba kotereku adayambitsa ndi
ndi zopeka m’njira zosiyanasiyana.
Austin Palmer wa ku America.
M’mutu uno, muphunzira mitudu Kulemba kwachipama kumakhala ndi
iwiri ya kulemba. Kenaka musonyeza timichira ndi makaka ambiri monga:
momwe mungaphunzitsire mitundu
iwiriyi.
23
Ntchito 2 Kulemba ziganizo M’muto uno, mwaphunzira kufunika
potsatira mitundu ya kwa kulemba. Mwaphunzira mitundu
kulemba yakulemba. Kenaka, mwasonyeza
momwe mungaphunzitsire phunziro
1 Unikani mitundu iwiri ya
la mitundu ya kulemba.
kulemba.
2 Lembani ziganizo potsatira Kudziunika ndi kudziyesa
mitundu iwiri ya kulemba. 1 Fotokozani kufunika kwa
3 Sonyezani anzanu zomwe kulemba.
mwalemba. 2 Fotokozani mitundu iwiri ya
4 Perekani maganizo anu pa kulemba.
ntchito yomwe anzanu achita. 3 Perekani maganizo anu pa
mitundu iwiri ya kulemba.
Malangizo kwa mphunzitsi
Muonetsetse kuti muli ndi zitsanzo Matanthauzo a mawu
za mitundu ya kulemba. Kulemba: Kusindikiza malembo
moyenera kuti aoneke
Ntchito 3 Kusonyeza
bwino ndicholinga
kaphunzitsidwe ka
chopereka tanthauzo
mitundu ya kulemba
lomveka bwino.
1 Konzekerani phunziro la mitundu
Mabuku
ya kulemba.
Malawi Institute of Education (2008).
2 Sonyezani momwe
Maphunziro a msukulu
mungaphunzitsire mitundu ya
zauphunzitsi m’Malawi buku
kulemba mu Sitandade 3.
lamphunzitsi. Domasi: MIE
3 Zukutani maphunziro a anzanu.
Unduna wa za maphunziro (1998).
Malangizo kwa mphunzitsi
Student teachers handbook 2
Muombe mkota pa ntchito yomwe
(Revised draft version).
ophunzira achita.
Domasi: MIE.
Kufotokoza mwachidule
24
MUTU 8 Kulemba dongosolo la ntchito
Luso: Kulemba zomwe angalembe m’gawo lililonse.
Nthawi: Maola 3 Magawo a dongosolo la ntchito alipo
Chigawo: Choyamba asanu ndi limodzi. Magawowa ndi
awa:
Chiyambi
Sabata ndi masiku
Ophunzira uphunzitsi ayenera
Mu gawo ili mphunzitsi amalemba
kuphunzira kalembedwe ka sabata ndi masiku omwe aphunzitse
dongosolo la ntchito chifukwa luso la ntchito yomwe wakonza.
kuphunzitsa lagona pa kukonzekera
ntchito yokaphunzitsa. Dongosolo la Zizindikiro za kakhozedwe
ntchito limaonetsa mwatsatanetsatane Izi ndi zomwe ophunzira achite
ntchito zoyenera kukaphunzitsa posonyeza kuti amvetsa zomwe
aphunzira.
ophunzira.
25
Chitsanzo cha dongosolo la ntchito
26
nkhani (2017).
awerenga kuwerenga Chichewa
nkhani nkhani buku la
mofulumira Ophunzira la
mofulumira
Sitandade 2.
Phunziro 5 ndi 6: Domasi : M.I.E
Tsamba…
atsiriza Kutsiriza
mpaka…
mawu mawu
amvetsera Kumvetsera Ntchito ya
nthano m’magulu
nthano
Kutchula
atchula /ch/
liwu la /ch/ Ntchito ya
alemba
Kulemba mmodzimmod
mawu okhala zi
mawu okhala
ndi ch
ndi ch
apanga Kusonyeza
Kupanga
mawu okhala
mawu okhala
ndi ch
ndi ch
27
a mawu Kupereka
matanthauzo
a mawu
Kulemba
mawu
(Ntchito B)
awerega
mabuku Phunziro 9 ndi 10:
oonjezera Kuwerenga
asonyeza mabuku
ntchito oonjezera ndi
yomwe kuyesa
achita ophunzira
m’sabatayi
Kubwereza
abwereza
ntchito ya
ntchito
m’sabatayi
yomwe
sanachite
bwino
m’sabatayi
28
Ntchito 1 Kufotokoza zifukwa 3 Lembani dongosolo la ntchito.
zolembera dongosolo la 4 Sonyezani anzanu zomwe
ntchito mwalemba.
5 Perekani maganizo anu pa ntchito
1 Kambiranani zifukwa zolembera
yomwe anzanu achita.
dongosolo la ntchito.
2 Kambiranani zofunika kuganizira Malangizo kwa mphunzitsi
polemba dongosolo la ntchito. Mulemberetu chitsanzo cha
3 Lembani zomwe mwakambirana. dongosolo la ntchito.
4 Fotokozerani anzanu zomwe
Kufotokoza mwachidule
mwalemba.
M’mutu uno, mwaphunzira zifukwa
Malangizo kwa mphunzitsi zolembera dongosolo la ntchito.
Mufufuziretu mfundo zosonyeza Mwaphunzira zofunika kuganizira
kufunika kolemba dongosolo la polemba dongosolo la ntchito. Kenaka
ntchito. mwafotokoza kalembedwe ka
Mufufuziretu zofunika kuganizira dongosolo la ntchito. Potsiriza
polemba dongosolo la ntchito. mwalemba ndi kuzukuta dongosolo
la ntchito.
29
Unduna wa za maphunziro (1998). Mtunda, FG et al (1997). An
Student teachers handbook 1 intoduction to the theory and
(Revised draft version). practice of teaching. Blantyre:
Domasi: MIE. Dzuka Publishing Company
Limited.
30
MUTU 9 Kulemba chikonzekero cha phunziro
31
Magawowo ndi ntchito ndi njira Ntchito 2 Kulemba chikonzekero
yophunzitsira ntchitoyo. Polemba cha phunziro cha mu
ndondomeko, n’kofunika kuonetsetsa Sitandade 5 mpaka 8
kuti mphunzitsi watsata zizindikiro 1 Kambiranani kalembedwe ka
za kakhozedwe, wayala bwino lomwe chikonzekero cha phunziro.
mfundo mu gawo lililonse komanso 2 Lembani chikonzekero cha
kuti mfundozo zagwirizana bwino phunziro chomwe
n’cholinga chothandiza ophunzira mwakambirana pogwiritsa
kuti amvetse phunzirolo. ntchito mabuku a aphunzitsi ndi a
ophunzira a Sitandade 5 mpaka 8.
Mathero 3 Sonyezani anzanu zomwe
Ili ndi gawo lomwe limathandiza mwalemba.
mphunzitsi kudziwa ngati ophunzira
ake amvetsa bwino phunziro lomwe Malangizo kwa mphunzitsi
amaphunzitsa. Zomwe zimachitika Mulemberetu chitsanzo cha
m’gawoli ndi monga kubwereza chikonzekero cha phunziro cha
ntchito mwachidule, kufunsa mu Sitandade 5 mpaka 8.
ophunzira kuti afotokoze zomwe Mutsogolere ophunzira kulemba
aphunzira kapena kuyankha mafunso, chikonzekero cha phunzirochi.
kuchita sewero, kulemba mawu
kapena ziganizo, kulakatula
Chitsanzo cha chikonzekero cha
ndakatulo ndi kuimba nyimbo.
phunziro cha Sitandade 5 mpaka 8
Kalasi: Sitandade 5
Ntchito 1 Kufotokoza zifukwa
Tsiku: 10 September, 2017
zolembera chikonzekero Phunziro: Chichewa
cha phunziro Nthawi: 8:00 mpaka 8:30 m’mawa
1 Kambiranani zifukwa zolembera Mutu1: Phunziro 4
chikonzekero cha phunziro.
2 Lembani zomwe mwakambirana. Zizindikiro za kakhozedwe
3 Fotokozerani anzanu zomwe Ophunzira:
mwalemba. apatsana moni.
ayankha moni molondola.
Malangizo kwa mphunzitsi …………………………………
Mufufuziretu zifukwa zolembera …………………………………
chikonzekero cha phunziro. …………………………………
Zipangizo zophunzitsira,
zophunzirira ndi zoyesera
Chithunzi cha anthu akupatsana
moni
32
Chithunzi cha anthu Ntchito 3 Kufotokoza kagwiritsidwe
akutsanzikana ntchito ka chikonzekero
…………………………………… cha phunziro
cholemberatu mu
Sitandade 1 mpaka 4
Zochita Zochita
mphunzitsi ophunzira 1 Unikani chikonzekero cha
Chiyambi phunziro cholemberatu cha mu
Uzani ophunzira Kufotokoza Sitandade 1 mpaka 4 (Scripted
kuti afotokoze zomwe anthu Lesson Plan) kuchokera mu buku
zomwe anthu amachita la mphunzitsi.
amachita popatsana moni. 2 Lembani mfundo zoyenera
popatsana moni. kutsatira pophunzitsa (Lesson
notes).
3 Fotokozerani anzanu zomwe
Ndondomeko mwalemba.
Gawo 1 ……………………
4 Kambiranani kufunika kolemba
………………… ……………………
mfundo zoyenera kutsatira
………………… …….
pophunzitsa.
………..
Gawo 2
………………… ……………………
………………… …………………… Malangizo kwa mphunzitsi
………. ……..
Mutsogolere ophunzira kulemba
Gawo 3
mfundo zoyenera kutsatira
………………… ……………………
pophunzitsa.
………………… ……………………
Mutsogolere ophunzira
………. ……..
kuzindikira kufunika kolemba
Mathero
………………… …………………… mfundo zoyenera kutsatira
………………… …………………… pophunzitsa.
……….. ……..
Ndamanga:
Chitsanzo cha mfundo zoyenera
Zomwe Zomwe Zoyenera kutsatira pophunzitsa (Lesson notes).
zayenda sizinayende kuchita Kalasi: Sitandade 2
Tsiku: 10 September, 2017
bwino bwino
Phunziro: Chichewa
Nthawi: 8:00 mpaka 8:30
m’mawa
Mutu: Mutu 1 phunziro 4
33
Zizindikiro za kakhozedwe achite paokha ndi momwe
Ophunzira: achitire.
apatsana moni. Ntchito 3:
ayankha moni molondola. ……………………………………
…………………………………… Lembani zomwe muphunzitse
………………………………… ndi momwe musonyezere.
Zipangizo zophunzitsira, ……………………………………
zophunzirira ndi zoyesera Lembani zomwe inu ndi
Chithunzi cha anthu akupatsana ophunzira muchite
moni ndi momwe muchitire.
Chithunzi cha anthu ……………………………………
akutsanzikana Lembani zomwe ophunzira
…………………………………… achite paokha ndi momwe
……………………… achitire.
Mathero:
Chiyambi Lembani mathero ogwirizana ndi
Imbani nyimbo iliyonse yogwirizana phunziro.
ndi phunziro.
Ndondomeko Ndamanga:
Ntchito 1: Zomwe Zomwe Zoyenera
…………………………………… zayenda sizinayende kuchita
Lembani zomwe muphunzitse bwino bwino
ndi momwe musonyezere
……………………………………
Lembani zomwe inu ndi
ophunzira muchite Ntchito 4 Kufananitsa ndi
ndi momwe muchitire. kusiyanitsa chikonzekero cha
…………………………………… phunziro cha mu Sitandade 5 mpaka
Lembani zomwe ophunzira 8 ndi chikonzekero cha phunziro
achite paokha cholemberatu cha mu Sitandade 1
ndi momwe achitire. mpaka 4.
Ntchito 2: 1 Fananitsani chikonzekero cha
…………………………………… phunziro cha mu Sitandade 5
Lembani zomwe muphunzitse mpaka 8 ndi chikonzekero cha
ndi momwe musonyezere phunziro cholemberatu cha mu
…………………………………… Sitandade 1 mpaka 4.
Lembani zomwe inu ndi 2 Siyanitsani chikonzekero cha
ophunzira muchite phunziro cha m’Sitandade 5
ndi momwe muchitire. mpaka 8 ndi chikonzekero cha
…………………………………… phunziro cholemberatu cha mu
Lembani zomwe ophunzira Sitandade 1 mpaka 4.
34
3 Fananitsani zikonzekero ziwirizi Kufotokoza mwachidule
ndi mfundo zoyenera kutsata M’mutu uno mwaphunzira zifukwa
pophunzitsa (Lesson notes) zolembera chikonzekero cha phunziro
zomwe munalemba mu ntchito 3. ndipo mwalemba chikonzekero cha
4 Fotokozerani anzanu zomwe phunziro. Mwasonyeza momwe
mwapeza. mungagwiritsire ntchito chikonzekero
cha phunziro cholemberatu mu
Sitandade 1 mpaka 4. Mwafananitsa
Malangizo kwa mphunzitsi
ndi kusiyanitsa chikonzekero cha
Mutsogolere ophunzira
phunziro cholemberatu cha Sitandade
kufananitsa chikonzekero cha
1 mpaka 4 ndi cha Sitandade 5 mpaka
phunziro cha m’Sitandade 5
8. Pomaliza, mwasonyeza momwe
mpaka 8 ndi chikonzekero cha
mungagwiritsire ntchito chikonzekero
phunziro cholemberatu cha mu
cha phunziro cholemberatu
Sitandade 1 mpaka 4 komanso
pophunzitsa mu Sitandade 1 mpaka 4.
mfundo zoyenera kutsatira
pophunzitsa zomwe ophunzira Kudziunika ndi kudziyesa
analemba mu ntchito 3. 1 Fotokozani zomwe mungalembe
Muombe mkota pa ntchito m’magawo a chikonzekero cha
yomwe ophunzira achita. phunziro.
2 Fotokozani ubwino ndi kuipa kwa
Ntchito 5 Kusonyeza kagwiritsidwe chikonzekero cha phunziro
ntchito ka chikonzekero cholemberatu.
cha phunziro
Matanthauzo a mawu
cholemberatu
Chikonzekero cha phunziro:
1 Unikaninso chikonzekero cha
Dongosolo la ntchito imene
phunziro cholemberatu.
mphunzitsi amalemba pokonzekera
2 Unikaninso mfundo zoyenera
kukaphunzitsa mosadodoma pa tsiku
kutsatira pophunzitsa.
lotsatira kuchokera mu dongosolo la
3 Sonyezani momwe
ntchito lomwe adalemba kale.
mungagwiritsire ntchito
chikonzekero cholemberatu Mabuku
pophunzitsa mu Sitandade 1 Malawi Institute of Education (2008).
mpaka 4. Maphunziro a msukulu
4 Perekani maganizo anu pa ntchito zauphunzitsi mMalawi buku la
yomwe anzanu achita. mphunzitsi. Domasi: MIE
35
Mtunda, FG et al (1997). An
Intoduction to the theory and
practice of teaching. Blantyre:
Dzuka.
36
MUTU10 Kulemba zotsatira za ntchito yomwe
ndaphunzitsa
37
la ntchito ndi chikonzekero cha gawo la zotsatira za ntchito
phunziro. yomwe ndaphunzitsa?
3 Fotokozerani anzanu zomwe
Matanthauzo a mawu
mwalemba.
Zotsatira za ntchito yomwe
4 Zukutani ntchito yomwe anzanu ndaphunzitsa: Dongosolo lomwe
alemba. limasonyeza ntchito yomwe ophunzira
achita ndi momwe ntchitoyo yayendera
Malangizo kwa mphunzitsi mu sabata.
Muonenetse kuti muli ndi
Mabuku
chitsanzo cha zotsatira za ntchito
Malawi Institute of Education (2008).
yomwe ndaphunzitsa.
Maphunziro a m’sukulu
Muombe mkota pa ntchito
zauphunzitsi m’Malawi Buku la
yomwe ophunzira achita.
mphunzitsi. Domasi: MIE
Kufotokoza mwachidule
Unduna wa za maphunziro (1998).
M’mutu uno, mwaphunzira kulemba
Student teachers handbook 1
zotsatira za ntchito yomwe
(Revised draft version).
ndaphunzitsa. Kenaka, mwalemba
Domasi: MIE.
ndi kuzukuta gawo la zotsatira za
ntchito yomwe ndaphunzitsa. Mtunda, FG et al (1997). An
Intoduction to the theory and
Kudziunika ndi kudziyesa
practice of teaching. Blantyre:
1 Fotokozani zomwe mungalembe
Dzuka Publishing Company
m’magawo a zotsatira za ntchito
Limited.
yomwe ndaphunzitsa.
2 Pophunzitsa, mwazindikira kuti Obanya, P (1980). General methods of
ophunzira ambiri sanamvetse teaching. London: Macmillan
phunziro, mungalembe zotani mu Education LTD.
38
MUTU 11 Kaphunzitsidwe ka malamulo a chiyankhulo
asonyeza kaphunzitsidwe ka
Luso: Kugwiritsa ntchito
malamulo a chiyankhulo phunziro la kugwiritsa ntchito
malamulo a chiyankhulo
Nthawi: Maola 6
Mawu otsogolera
Chigawo: Choyamba:
Chiyankhulo chilichonse chimakhala
Chiyambi ndi malamulo ake amene
Luso la kugwiritsa ntchito malamulo amagwiritsidwa ntchito poyankhula
a chiyankhulo ndi lofunika kwambiri kapena polemba. Malamulowo ndi
kwa ophunzira. Mphunzitsi ofunika kwambiri chifukwa
akuyenera kuzindikira lusoli ndi amathandizira kuti zoyankhula
cholinga choti athandize ophunzira kapena zolemba zipereke tanthauzo
moyenera. lomveka bwino. Choncho ndi
koyenera kuti mphunzitsi azindikire
M’mutu uno, muphunzira kusiyana
kuphunzitsa moyenera phunziro la
kwa chiyankhulo cha Chichewa
kugwiritsa ntchito malamulo a
cham’madera. Muphunzira kufunika
chiyankhulo.
kwa kugwiritsa ntchito malamulo a
chiyankhulo. Muphunziranso Ntchito 1 Kufotokoza kusiyana kwa
kugwiritsa ntchito mawu oyenera chiyankhulo cha
m’chiganizo. Muchita kafukufuku wa Chichewa cha m’madera
mitundu ya mawu. Kenaka,
1 Kambiranani kusiyana kwa
mufotokoza njira ndi ndondomeko
chiyankhulo cha Chichewa
zophunzitsira, zophunzirira ndi
cham’madera.
zoyesera kugwiritsa ntchito malamulo
2 Lembani zomwe
a chiyankhulo. Pomaliza, musonyeza
mwakambirana.
momwe mungaphunzitsire phunziro
3 Fotokozerani anzanu zomwe
la kugwiritsa ntchito malamulo a
mwalemba.
chiyankhulo.
Malangizo kwa mphunzitsi
Zizindikiro zakakhozedwe
Mufufuziretu zitsanzo zosonyeza
Pakutha pa mutu uno, ophunzira:
kusiyana kwa Chichewa
afotokoza zomwe zimalepheretsa choyankhulidwa m’madera
ophunzira kugwirita ntchito osiyanasiyana.
malamulo a chiyankhulo.
agwiritsa ntchito mawu oyenera
m’chiganizo.
39
Ntchito 2 Kufotokoza zomwe 2 Konzani ntchito yomwe
zimalepheretsa mungaphunzitse mu Sitandade
ophunzira kugwiritsa 4 ndi mayankho oyenera.
ntchito malamulo a 3 Fotokozerani anzanu zomwe
chiyankhulo mwakonza.
4 Zukutani ntchito yomwe
1 Kambiranani kufunika kwa
anzanu akonza.
malamulo a chiyankhulo.
2 Kambiranani zomwe Malangizo kwa mphunzitsi
zimalepheretsa ophunzira
Mukonzeretu mayankho a
kugwiritsa ntchito malamulo a
Ntchito 3.
chiyankhulo.
Muonetsetse kuti ntchito ndi
3 Lembani zomwe mwakambirana.
mayankho omwe ophunzira
4 Fotokozerani anzanu zomwe
akonza akugwirizana ndi ntchito
mwalemba.
yomwe apatsidwa.
5 Perekani maganizo anu pa zomwe
anzanu afotokoza. Ntchito 4 Kuchita kafukufuku wa
mitundu ya mawu
Malangizo kwa mphunzitsi
Mufufuziretu mfundo zosonyeza 1 Kambiranani matanthauzo a
kufunika kwa malamulo a mitundu ya mawu iyi:
chiyankhulo. a. dzina
Mufufuziretu zomwe b. mlowam’malo
zimalepheretsa ophunzira c. mneni
kugwiritsa ntchito malamulo a d. mfotokozi
chiyankhulo. 2 Chitani kafukufuku wa mitundu
ya mawu omwe mwapatsidwa.
Ntchito 3 Kugwiritsa ntchito mawu
3 Fotokozerani anzanu zomwe
oyenera m’chiganizo
mwapeza.
1 Konzani ziganizo zotsatirazi
Malangizo kwa mphunzitsi
kuti zikhale m’Chichewa
Muwapatsiretu ophunzira mitu
chomveka bwino.
ya ntchito yomwe afufuze.
a. Misozi amapanga mantha
Limbikitsani ophunzira kuti apeze
kuyenda usika.
nthawi yapadera yochitira
b. A Beni ntchito yawo ndi
kafukufuku.
yofotokoza njinga.
c. Maliya akuchapa mbale.
d. Amayi avaya kumsika
kukagula ndiwo.
e. Mavuto akuchapa zovala
padeni.
40
Ntchito 5 Kufotokoza kugwiritsa ntchito malamulo a
kaphunzitsidwe ndi chiyankhulo.
kayesedwe ka kugwiritsa 4 Perekani maganizo anu pa ntchito
ntchito malamulo a yomwe ophunzira anzanu achita.
chiyankhulo
Malangizo kwa mphunzitsi
1 Kambiranani njira zophunzitsira, Muombe mkota pa ntchito
zophunzirira ndi zoyesera yomwe ophunzira achita.
kugwiritsa ntchito malamulo a
Kufotokoza mwachidule
chiyankhulo.
M’mutu uno, mwaphunzira kusiyana
2 Kambiranani ndondomeko
kwa chiyankhulo cha Chichewa cha
yophunzitsira kugwiritsa ntchito
m’madera osiyanasiyana komanso
malamulo a chiyankhulo.
kufunika kwa kugwiritsa ntchito
3 Lembani zomwe mwakambirana.
malamulo a chiyankhulo. Mwachita
4 Fotokozerani anzanu zomwe
kafukufuku wa mitundu ya mawu.
mwalemba.
Kenaka, mwafotokoza njira ndi
Malangizo kwa mphunzitsi ndondomeko zophunzitsira,
Mufufuziretu njira zophunzitsira, zophunzirira ndi zoyesera kugwiritsa
zophunzirira ndi zoyesera ntchito malamulo a chiyankhulo.
kugwiritsa ntchito malamulo a Pomaliza, mwasonyeza
chiyankhulo. kaphunzitsidewe ka phunziro la
Mufufuziretu ndondomeko kugwiritsa ntchito malamulo a
yophunzitsira kugwiritsa ntchito chiyankhulo.
malamulo a chiyankhulo.
Kudziunika ndi kudziyesa
1 Fotokozani kufunika kwa
Ntchito 6 Kusonyeza
kugwiritsa ntchito malamulo a
kaphunzitsidwe ka
chiyankhulo.
phunziro la kugwiritsa
2 Perekani mitundu ya nthawi za
ntchito malamulo a
aneni.
chiyankhulo
3 Fotokozani njira ziwiri
1 Unikani njira zophunzitsira, zophunzitsira, zophunzirira ndi
zophunzirira ndi zoyesera zoyesera phunziro la kugwiritsa
kugwiritsa ntchito malamulo a ntchito malamulo a chiyankhulo.
chiyankhulo.
Matanthauzo a mawu
2 Unikaninso ndondomeko
Kugwiritsa ntchito malamulo a
yophunzitsira kugwiritsa ntchito
chiyankhulo Luso la kutchula,
malamulo a chiyankhulo.
kuyankhula, kuwerenga, kulemba
3 Sonyezani momwe
mungaphunzitsire phunziro la
41
mawu ndi ziganizo moyenera ndi Chilora HG & Kathewera REM (2000).
molondola. Chinyanja Buku la mphunzitsi la
Fomu 1. Blantyre: Dzuka
Mabuku
Publishing Company Limited.
Malawi Institute of Education (2008).
Maphunziro a m’sukulu Ngoma SJL& Chauma AM (2011).
zauphunzitsi m’Malawi buku la Tizame m’Chichewa Malamulo
mphunzitsi. Domasi: MIE. Ophunzitsira ndi ophunzirira
Chichewa. Blantyre: Bookland.
Nankwenya, IAJ(2008). Zofunika mu
galamala ya Chichewa. Blantyre:
Dzuka Publishing Company
Limited.
42
Mutu 12 Kaphunzitsidwe ka ndagi, nthano ndi sewero
asonyeza kaphunzitsidwe ka
Luso: Kuganiza mozama
ntchito zomwe zingakulitse luso la
Nthawi: Maola 6 kuganiza mozama.
Chigawo: Choyamba
Mawu otsogolera
Kuganiza mozama ndi luso lofunikira
Chiyambi kwambiri pa moyo wa munthu
Munthu aliyense amaganiza. aliyense. Anthu ena amaganiza kuti
Ngakhale kuti aliyense amaganiza, ophunzira saganiza mokwanira. Izi si
kuganiza kwathu kumakhala zoona. Mphunzitsi aliyense ayenera
kosiyana ngakhale pa chinthu kuzindikira kuti ophunzirawo ali ndi
chimodzi. Mwachitsanzo, pamalo zizindikiro zambiri zomwe
pakagwa vuto, pali anthu ena omwe zimasonyeza kuti iwo amaganiza
amasowa chochita pamene ena mozama. Zizindikirozo ndi izi:
amatha kuganiza mozama n’kupeza kukhala achidwi, kufunsafunsa
yankho logwira mtima lothetsera mafunso, kufuna kuphunzira,
vutolo. Kawirikawiri anthu omwe kusankha njira zochitira kanthu,
amaganiza mozama amachita zinthu kuika zinthu m’magulu kapena
zabwino ndipo amalemekezedwa m’ndondomeko, kukonda kusewera
komanso amadalirika. m’magulu komanso kuchita zisudzo.
43
Ntchito 2 Kufotokoza ntchito Ntchito 4 Kuonerera
zomwe zingakulitse luso kaphunzitsidwe ka
la kuganiza mozama ndagi, nthano ndi sewero
44
Malangizo kwa mphunzitsi Malawi Institute of Education (2015).
Muombe mkota pa ntchito yomwe Critical thinking training manual
ophunzira achita. for Malawi. Domasi: MIE.
Matanthauzo a mawu
Kuganiza mozama kuunika zinthu
mwachidwi ndi kusinkhasinkha
mwakuya ndi cholinga chofuna
kudziwa kapena kupeza choonadi
Mabuku
Malawi Institute of Education (2006).
Maphunziro a m’sukulu za
uphunzitsi m’Malawi Chichewa
buku la mphunzitsi. Domasi:
MIE.
45