Professional Documents
Culture Documents
x05_Chichewa Module 4 Final (1)
x05_Chichewa Module 4 Final (1)
x05_Chichewa Module 4 Final (1)
Buku lophunzitsira
m’sukulu za uphunzitsi
Chichewa
Buku 4
Buku lophunzitsira
m’sukulu za uphunzitsi
Chichewa
Buku 4
Email: miedirector@sdnp.org.mw
Website: www.mie.edu.mw
Dr William Susuwele-Banda
Executive Director
Malawi Institute of Education
v
Kuthokoza
Unduna wa za Maphunziro, Sayansi ndi Luso pamodzi ndi Malawi Institute of
Education ukuthokoza anthu onse amene adathandiza mu njira zosiyanasiyana kuti
bukuli lilembedwe.
Okonza
Mkonzi : Max J Iphani
Wotayipa ndi
kuyala bukuli : Catherine Katete
Mkonzi wamkulu : Max J Iphani
vi
Olemba
vii
viii
Zamkatimu
Kuthokoza ……………………………………………………………………..… vi
3 mpaka 8………………..………………...………………………….. 15
ix
MUTU 1 Kuphunzitsa ndi kuyesa ndakatulo ndi nyimbo
2
Zochita 2 Kuphunzitsa kulakatula ndondomeko yoyenera kutsatira
ndakatulo ndi kuimba pophunzitsa kulakatula ndakatulo ndi
nyimbo kuimba nyimbo.
1 Kambiranani momwe
mungaphunzitsire kulakatula Kudziunika ndi kudziyesa
ndakatulo ndi kuimba nyimbo. 1 Perekani zifukwa zophunzitsira
2 Phunzitsani ndakatulo ndi nyimbo ndakatulo ndi nyimbo.
zomwe munapeka. 2 Fotokozani ndondomeko
3 Perekani maganizo anu pa momwe yophunzitsira ndakatulo ndi
maphunziro ayendera. nyimbo m’sukulu za pulayimale.
3 Kodi mlakatuli ayenera kukhala
Malangizo kwa mphunzitsi ndi maluso ati kuti ndakatulo yake
1 Mukonzeretu ndondomeko ipereke tanthauzo loyenera?
yophunzitsira ndakatulo ndi
nyimbo. Matanthauzo a mawu
2 Muonetsetse kuti ophunzira Ndakatulo: Maganizo olembedwa
akupeka ndakatulo/nyimbo mwachidule m’ndime kapena
potsatira ndondomeko yoyenera. Mwampululira
3 Muotsetsenso kuti ophunzira Kulakatula: Kunena za muntima
akulakatula mopatsa chidwi Nyimbo: Maganizo amene
potsatira izi: amanenedwa kudzera m’kuimba.
kukweza ndi kutsitsa kwa
mawu koyenera. Mabuku
kutchula mawu motsindika. Malawi Institute of Education, (2008).
Kulakatula mwanthetemya Maphunziro a m’sukulu zauphunzitsi
kapena kuimba nyimbo mwa Chichewa Buku la mphunzitsi.
mingoli. Domasi: Malawi Institute of
kusonyeza kukondwa kapena Education.
chisoni. Malawi Institute of Education, (2008).
Maphunziro a m’sukulu zauphunzitsi
Kufotokoza mwachidule Chichewa Buku la ophunzira.
M’mutu uno, mwaunika momwe Domasi: Malawi Institute of
munkaphunzitsira ndakatulo ndi Education.
nyimbo. Mwafotokoza zifukwa
zosiyanasiyana zophunzitsira Kuwerenga koonjezera
ndakatulo komanso nyimbo kwa Ministry of Education, Science and
ophunzira a m’sukulu za pulayimale. Technology, (2009). Initial primary
Mwaphunziranso kupeka ndi teacher education through open and
kulakatulo ndakatulo komanso distance learning. Module 2.
kuimba nyimbo mwaluso kuti Lilongwe: Department of Teacher
zipereke matanthauzo oyenera kwa Education and Development
omvera. Pomaliza, mwapereka (DTED).
3
MUTU 2 Kuphunzitsa malonje
4
Zochita 1 Kuunika mitu
yophunzitsira maluso a
kumva ndi kuyankhula
1 Fotokozani mitu yophunzitsira
maluso a kumva ndi kuyankhula
yomwe ikupezeka m’silabasi ndi
mabuku ophunzitsira m’sukulu za
pulayimale.
2 Kambiranani njira zomwe
mungagwiritse ntchito Zochita 1 Kufotokoza za malo
pophunzitsa mitu yosiyanasiyana amene anthu
ya kumva ndi kuyankhula yomwe amalonjerana ndi nthawi
mwatchula. yake
3 Unikani momwe ntchito 1 Pezani malo osiyanasiyana kumene
yophunzitsa kumva ndi anthu amalonjerana ndi nthawi
kuyankhula idayendera m’sukulu yake pogwiritsa ntchito mabuku
zomwe munkaphunzitsa ophunzitsira ndi ophunzirira
4 Fotokozerani anzanu zomwe Chichewa m’sukulu zapulayimale.
mwakambirana. 2 Fotokozerani anzanu zomwe
mwapeza.
Zochita 2 Kukambirana mavuto
omwe mudakumana Zochita 2 Kukambirana kufunika
nawo kopereka malonje
1 Kambiranani mavuto omwe molingana ndi malo
mudakumana nawo pophunzitsa komanso nthawi
maluso a kumva ndi kuyankhula. Kambiranani nkhani yotsatirayi:
2 Fufuzani njira zomwe Bambo Salambula adali mkulu wa
mungagwiritse ntchito kuti mpingo. Tsiku lina kudachitika maliro.
muthetse mavuto omwe Bambo Salambula adapatsidwa
mwatchula. udindo wotsogolera mwambo wa
3 Fotokozerani anzanu zomwe malirowo. Iwo adati, “Moni mabwana
mwakambirana. ndi madoma. Ife tonse tabwera pano
chifukwa chauta watigwera. Choncho
Ntchito 2 Kukambirana za malo tili ndi chisoni chambiri. Tsopano
osiyanasiyana kumene tifuna tiyambe mwambo wa maliro.”
anthu amalonjerana Tsopano yankhani mafunso
Anthu amalonjerana pa malo otsatirawa:
osiyanasiyana molingana ndi zochitika 1 Kodi ndi mtundu wanji wa
za pamalopo. M’gawo lino, malonje womwe waperekedwa mu
mukambirana za malo osiyanasiyana nkhaniyi?
kumene anthu amalonjerana ndi 2 Kambiranani zomwe zalakwika
nthawi yake. m’malonjewa.
5
3 Fotokozani momwe bambo Malangizo kwa mphunzitsi
Salambula akadaperekera Muonetsetse kuti ophunzira ali ndi
malonjewa moyenera. zipangizo zoyenera kukonzekera
4 N’chifukwa chiyani ophunzira phunziro la malonje.
ayenera kuphunzira kupereka Mukonzeretu ndondomeko
malonje moyenera? yophunzitsira malonje
osiyanasiyana.
Ntchito 3 Kuphunzitsa malonje Muombe mkota pa mitundu ya
Mwaunika mavuto osiyanasiyana malonje ndi kaphunzitsidwe kake.
omwe mudakumana nawo
pophunzitsa malonje. Mwafufuzanso Kufotokoza mwachidule
njira zothandizira kuthetsa mavuto M’mutu uno, mwaunika momwe
omwe mudakumana nawo. M’gawo mungaphunzitsire ntchito zomwe
lino, muphunzitsa malonje zingakulitse maluso a kumva ndi
osiyanasiyana. kuyankhula. Mwafotokoza mitu
yosiyanasiyana ya kumva ndi
Zochita 1 Kukambirana kuyankhula komanso malo omwe
ndondomeko anthu amalonjerana. Mwafotokozanso
yophunzitsira malonje momwe munkaphunzitsira malonje
1 Kambiranani ndondomeko yomwe osiyanasiyana ndipo mwaphunzitsa
mudagwiritsa ntchito pophunzitsa ndi kuona maphunziro a malonje.
malonje osiyanasiyana. Pomaliza, mwakambirana njira
2 Konzani phunziro losonyeza zothetsera mavuto amene
momwe mungaphunzitsire mudakumana nawo pophunzitsa
malonje osiyanasiyana. malonje m’sukulu zomwe
3 Uzani anzanu zomwe munkaphunzitsa. Zina mwa njira
mwakambirana. zomwe mwapeza ndi kugwiritsa
ntchito njira zophunzitsira,
Zochita 2 Kusonyeza kuphunzitsa zophunzirira ndi zoyesera zoyenera
malonje komanso kukonzeratu zipangizo
1 Kambiranani momwe zoyenera.
mungaphunzitsire malonje
osiyanasiyana. Kudziunika ndi kudziyesa
2 Sonyezani momwe 1 Tchulani njira zitatu zomwe
mungaphunzitsire malonjewo. mungagwiritse ntchito
3 Zukutani maphunzirowo. pophunzitsa malonje mu Sitandade
1.
2 Fotokozani momwe
mungaphunzitsire malonje
apamalonda mu Sitandade 4.
6
3 Kodi kufunika kwa gawo Malawi Institute of Education, (2008).
losonyeza ophunzira zoyenera Maphunziro a m’sukulu zauphunzitsi
kuchita m’ndondomeko ya m’Malawi: Chichewa buku la
phunziro la malonje n’kotani? mphunzitsi. Domasi: Malawi
Institute of Education.
Mabuku
Malawi Institute of Education, (2008). Ministry of Education, Science and
IPTE Chichewa buku la ophunzira. Technology, (2010). Initial primary
Domasi: Malawi Institute of education through open and distance
Education. learning Chichewa: Module 1.
Lilongwe: Department of Teacher
Education and Development.
7
MUTU 3 Kuphunzitsa ndi kuyesa kuwerenga
Luso Kuwerenga
Nthawi Maola 4 kawerengedwe ka ophunzira
Chigawo Chachitatu pogwiritsa ntchito njira izi:
1 Kugwiritsa ntchito chipangizo
Chiyambi chotchedwa ‘running record’.
M’mbuyomu, mudaphunzira momwe Kuyesa ophunzira pogwiritsa
mungaphunzitsire kuwerenga ndipo ntchito chipangizochi, mphunzitsi
mudaphunzitsa kuwerenga m’sukulu amayesa momwe wophunzira
zapulayimale. aliyense akutchulira mawu, njira
zomwe akugwiritsa ntchito
M’mutu uno, mufotokoza zomwe powerenga, nthawi yomwe
mudakumana nazo pophunzitsa wawerenga komanso ngati
kuwerenga. Mufotokozanso njira akumvetsa zomwe akuwerengazo.
zomwe mudagwiritsa ntchito Kenaka, mphunzitsi amawerengera
pophunzitsa kuwerengako. Kenaka, momwe wophunzirayo wakhozera
musonyeza kagwiritsidwe ntchito ka pa kawerengedwe kake pa ndime
njirazo. yomwe anapatsidwa. Pomaliza,
mphunzitsi amadziwa mabuku
Zizindikiro za kakhozedwe oyenera kumupatsa wophunzirayo
Pakutha pa mutu uno, ophunzira: kuti apititse patsogolo luso lake la
afotokoza njira zomwe adagwiritsa kuwerenga.
ntchito pophunzitsa kuwerenga.
aphunzitsa ndi kuyesa kuwerenga. 2 Kugwiritsa ntchito chipangizo
choonerera komanso kulemba
Mawu otsogolera momwe ophunzira akuwerengera
Ophunzira a m’sukulu zapulayimale (Observation checklist). Pogwiritsa
amawerenga mokweza ndi ntchito chipangizochi mphunzitsi
mwachinunu. Pali njira amakonza mafunso omwe
zosiyanasiyana zophunzitsira agwiritse ntchito poyesa
kuwerenga mokweza monga kawerengedwe ka wophunzira
kuwerenga kwa mavume, kwa aliyense. Onani chitsanzo
m’magulu komanso kwa chotsatirachi:
mmodzimmodzi. Pamene ophunzira
akuwerenga pogwiritsa ntchito njira
zosiyanasiyana, mphunzitsi ayenera
kuwayesa. Mphunzitsi angayese
8
Kodi Akukhoza Akukhoza Akukhoza Ndi
wophunzira kwambiri bwino pang’ono wofunika
chithandizo
1 akutchula
mawu
moyenera?
2 akuwerenga
mosadodoma?
3 akuwerenga
mofulumira?
4 akumvetsa
zomwe
akuwerenga?
9
Ntchito 1 Kufotokoza njira zomwe muthetse mavuto omwe
munkagwiritsa ntchito munkakumana nawo.
pophunzitsa kuwerenga
3 Uzani anzanu zomwe
Kumbukirani zomwe munkachita
mwakambirana.
pophunzitsa kuwerenga. Maphunziro
ena adakusangalatsani pomwe ena Ntchito 2 Kuphunzitsa kuwerenga
adali ndi zovuta zina. Tsopano Kuphunzitsa ndi kuyesa ophunzira
muunika zomwe mudakumana nazo moyenera pamene akuphunzira
pophunzitsa komanso mavuto omwe kuwerenga n’kofunika. Tsopano
mudawapeza. muphunzitsa kuwerenga komanso
muunika njira zoyesera zomwe
Zochita 1 Kufokotokoza zomwe mungagwiritse ntchito pophunzitsa
mudakumana nazo kuwerenga.
pophunzitsa kuwerenga
Zochita 1 Kuphunzitsa luso la
kuwerenga
1 Kambiranani momwe
mungaphunzitsire kuwerenga
pogwiritsa ntchito njira zomwe
mwakambirana.
2 Phunzitsani kuwerenga pogwiritsa
ntchito njira zomwe
mwakambirana.
1 Tengani mafayilo anu ndipo 3 Zukutani maphunzirowo.
muwerenge zotsatira za ntchito
yomwe ndaphunzitsa. Zochita 2 Kuyesa ophunzira luso la
2 Kambiranani zomwe mudakumana kuwerenga
nazo kuchokera pa zomwe 1 Unikani njira zomwe
mwawerenga m’mafayilo anu munkagwiritsa ntchito poyesa
zokhudza kuphunzitsa kuwerenga. ophunzira pa luso la kuwerenga.
3 Perekani maganizo anu pa zomwe 2 Kambiranani mavuto omwe
mwawerenga. munkakumana nawo pogwiritsa
ntchito njira zomwe mwatchula.
Zochita 2 Kuunika mavuto omwe 3 Fotokozani njira zomwe
mudakumana nawo mungagwiritse ntchito kuti
pophunzitsa kuwerenga muthetse mavutowo.
1 Kambiranani mavuto omwe 4 Sonyezani anzanu momwe
mudakumana nawo pophunzitsa mungagwiritsire ntchito njirazo.
kuwerenga. 5 Perekani maganizo anu pa ntchito
2 Fotokozani njira zomwe yomwe anzanu achita.
mungagwiritse ntchito kuti
10
Malangizo kwa mphunzitsi mavuto omwe aphunzitsi
Muombe mkota pa ntchito yomwe amakumana nawo pophunzitsa
ophunzira achita. kuwerenga.
Mukhaliretu ndi njira zoyesera 2 Fotokozani njira zomwe
ophunzira pa luso la kuwerenga. mungagwiritse ntchito
Mulimbikitse ophunzira kusonyeza pophunzitsa ndi kuyesa luso la
kagwiritsidwe ntchito ka njira kuwerenga.
zophunzitsira ndi kuyesera 3 Mphunzitsi wina pasukulu yanu
kuwerenga. amakonda kugwiritsa ntchito njira
ya mavume nthawi zonse
Kufotokoza mwachidule pophunzitsa kuwerenga. Ndi
M’mutu uno, mwafotokoza njira malangizo otani omwe
zomwe munkagwiritsa ntchito mungapereke kwa mphunzitsiyu.
pophunzitsa komanso kuyesa
ophunzira pa luso la kuwerenga. Mabuku
Mwafotokozanso njira zomwe Cunningham, PM & Allington, RL,
mungagwiritse ntchito pothetsa (2011). Classrooms that work: they can
mavuto omwe mungakumane nawo all read and write. Fifth Edition.
pophunzitsa luso la kuwerenga. Boston: Pearson.
Pomaliza, mwaphunzitsa kuwerenga Malawi Institute of Education, (2008).
pogwiritsa ntchito njira zophunzitsira Chichewa buku la mphunzitsi.
komanso zoyesera lusoli. Domasi: MIE.
Malawi Institute of Education, (2008).
Kudziunika ndi kudziyesa English tutor’s handbook. Domasi:
1 Tchulani njira zosiyanasiyana MIE.
zomwe zimathandiza kuthetsa
11
MUTU 4 Kuphunzitsa kulemba chimangirizo ndi kalata
mu Sitandade 4 mpaka 8
Luso Kulemba
Nthawi Maola 4 mawu olaula kapena achipongwe
Chigawo Chachitatu komanso kulemba malembo ooneka
bwino. Kuonjezera apo, polemba
Chiyambi chimangirizo ndi kalata pamafunika
M’chigawo choyamba mudaphunzira kulemba chikonzero chomwe
kalembedwe ka chimangirizo ndi chimathandiza mlembi kusanja
kalata zomwe zimathandiza mfundo mu ndondomeko yoyenera
ophunzira kukulitsa luso la kulemba. kuchokera pa mutu womwe
Chimangirizo komanso kalata wasankha.
zimayenera zilembedwe mu
dongosolo loyenera kuti owerenga Mphunzitsi akadziwa kulemba
athe kumvetsa uthenga womwe chimangirizo ndi kalata moyenera
walembedwa. angathe kuthandiza ophunzira
kulemba ntchito zimenezi mosavuta.
M’mutu uno, mufotokoza momwe Pa chifukwa ichi, mutu uno
munkaphunzitsira chimangirizo ndi ukuthandizani kudziwa zofunika
kalata m’sukulu zomwe kutsatira pophunzitsa kulemba
munkaphunzitsa. Musonyezanso chimangirizo ndi kalata.
kaphunzitsidwe koyenera ka
chimangirizo ndi kalata. Ntchito 1 Kufotokoza momwe
munkaphunzitsira
kulemba chimangirizo
Zizindikiro za kakhozedwe
ndi kalata m’sitandade 4
Pakutha pa mutu uno, ophunzira: mpaka 8
afotokoza momwe ankaphunzitsira Tsopano mukambirana zomwe
chimangirizo ndi kalata m’sukulu mudakumana nazo nthawi yomwe
zomwe ankaphunzitsa. munkaphunzitsa m’sukulu
aphunzitsa anzawo kalembedwe zapulayimale. Mufotokozanso mavuto
koyenera ka chimangirizo ndi omwe mudakumana nawo ndi njira
kalata. zomwe zingathandize kuthetsa
mavutowo.
Mawu otsogolera
Kulemba chimangirizo ndi kalata Zochita 1 Kuunika zomwe
kumafuna kuganizira zinthu zambiri. mudakumana nazo
Zina mwa zinthuzi ndi kusankha pophunzitsa kulemba
mutu womwe wophunzira chimangirizo ndi kalata
sangavutike kupeza mfundo 1 Kambiranani momwe
zikuluzikulu, kusagwiritsa ntchito munkaphunzitsira kalembedwe ka
12
chimangirizo ndi kalata mu sukulu
za pulayimale zomwe Zochita 1 Kufufuza ntchito
munkaphunzitsa. zokhudza chimangirizo
2 Fotokozerani anzanu zomwe ndi kalata m’mabuku a
mwakambirana. ophunzira
1 Pezani ntchito zokhudza
Zochita 2 Kupeza njira zothetsera chimangirizo ndi kalata m’mabuku
mavuto omwe a ophunzira.
mudakumana nawo 2 Kambiranani zomwe mwapeza
pophunzitsa chimangirizo m’makalasi a 1 mpaka 4 ndi 5
ndi kalata mpaka 8.
3 Perekani maganizo anu pa zomwe
mwapeza.
14
MUTU 5 Kuphunzitsa kulemba lembetso ndi zidziwitso
mu Sitandade 3 mpaka 8
Luso Kulemba
Nthawi Maola 3 kukhazikitsa maziko antchito
Chigawo Chachitatu yodzagwira m’tsogolo monga ulembi
ndi ukonzi. Mwapadera, kulemba
Chiyambi lembetso kumathandizanso ophunzira
M’mbuyomu, mudaphunzira kumvetsera mwatcheru zomwe wina
kuphunzitsa ndi kuyesa kulemba akukamba kapena kuwerenga ndi
lembetso ndi zidziwitso. kuwerenga zomwe iwo kapena wina
Mudaphunziranso momwe zinthu walemba.
ziwirizi zimathandizira ophunzira
kukulitsa luso lawo la kulemba. Pali mavuto osiyanasiyana omwe
aphunzitsi amakumana nawo
M’mutu uno, muunikanso pophunzitsa kulemba lembetso ndi
ndondomeko yomwe ingatsatidwe zidziwitso. Ena mwa mavutowa ndi
pophunzitsa kulemba lembetso ndi kusatsatira ndondomeko yoyenera ndi
zidziwitso ndi cholinga choti kusagwiritsa ntchito zipangizo
mukaphunzitse ophunzira moyenera. pophunzitsa. Monga aphunzitsi
muyenera kuphunzira
Zizindikiro zakakhozedwe kaphunzitsidwe koyenera ka lembetso
Pakutha pa mutu uno ophunzira: ndi zidziwitso. Izi zikuthandizani
afotokoza momwe adaphunzitsira kupeza njira zoyenera kugwiritsa
kalembedwe ka lembetso m’sukulu ntchito pophunzitsa kuti ophunzira
zomwe ankaphunzitsa. apindule.
aphunzitsa lembetso potsatira
ndondmeko yoyenera. Ntchito 1 Kufotokoza momwe
munkaphunzitsira
kalembedwe ka lembetso
Mawu otsogolera
ndi zidziwitso
Kuphunzitsa kulemba lembetso ndi
Tsopano muunika momwe
zidziwitso ndi zina mwa ntchito
munkaphunzitsira kulemba lembetso
zofunika kwambiri pophunzitsa luso
ndi zidziwitso. Kuunikaku n’kofunika
la kulemba. Kulemba lembetso ndi
kwambiri chifukwa kukuthandizani
zidziwitso kumathandiza ophunzira
kukonza zomwe simumazidziwa
kulemba mawu ndi ziganizo pa
bwino.
mtima, kulemba zizindikiro
zam’kalembedwe, kukulitsa luso la Zochita 1 Kuunika momwe
kumva ndi kuyankhula, kulemba munkaphunzitsira
mwachangu komanso molondola, ndi lembetso ndi zidziwitso
15
1 Kambiranani momwe chifukwa kumathandiza kuphunzira
munkaphunzitsira kalembedwe ka maluso omwe ena alinawo.
lembetso ndi zidziwitso m’sukulu
zosiyanasiyana zomwe Zochita 1 Kuonerera phunziro la
munkaphunzitsa. lembetso ndi zidziwitso
2 Fotokozani mavuto omwe 1 Kambiranani momwe
munkakumana nawo pophunzitsa mungaphunzitsire lembetso ndi
lembetso ndi zidziwitso. zidziwitso potsatira njira zomwe
3 Kambiranani njira zomwe mwakambirana.
mungagwiritse ntchito pofuna 2 Konzani ndondomeko
kuthetsa mavutowo. yophunzitsira kalembedwe ka
4 Uzani anzanu zomwe lembetso ndi zidziwitso mu
mwakambirana. Sitandade 3 mpaka 8.
3 Onererani phunziro la lembetso
Zochita 2 Kuunika ndondomeko pamene aphunzitsi anu
yomwe munkagwiritsa akuphunzitsa.
ntchito pophunzitsa 4 Perekani ndemanga pa momwe
kalembedwe ka lembetso phunzirolo layendera.
ndi zidziwitso
1 Unikani ndondomeko yomwe Zochita 2 Kuphunzitsa
munkatsatira pophunzitsa kalembedwe ka lembetso
lembetso ndi zidziwitso. ndi zidziwitso
2 Fotokozani mavuto omwe 1 Konzekerani kuphunzitsa
mudakumana nawo pogwiritsa phunziro la lembetso ndi
ntchito ndondomeko yomwe zidziwitso.
mwatchula. 2 Sonyezani anzanu kaphunzitsidwe
3 Perekani njira zomwe koyenera ka lembetso ndi
mungagwiritse ntchito pofuna zidziwitso.
kuthetsa mavuto omwe 3 Zukutani phunziro lomwe
munkakumana nawo. mwaphunzitsa.
17
MUTU 6 Kuphunzitsa akapandamneni
Kufotokoza mwachidule
M’mutu uno, mwaphunzira za
akapandamneni. Mwaphunzira
tanthauzo la kapandamneni ndi
mitundu yake. Pomaliza,
mwaphunzitsa mitundu
yosiyanasiyana ya akapandamneni
ndipo mwazukuta maphunzirowo.
Zochita 1 Kuphunzitsa mitundu ya
akapandamneni Kudziunika ndi kudziyesa
1 Konzekerani kuphunzitsa mtundu 1 Perekani mitundu ya
wa kapandamneni womwe akapandamneni omwe ali ndi
mwapatsidwa. mzere kunsi kwawo m’ziganizo
2 Sonyezani momwe zotsatirazi:
mungaphunzitsire mtundu wa a. Usamayende m’mbali mwa
kapandamneniyo. msewu.
3 Zukutani maphunzirowo. b. Iye wagula malaya okongola
kwabasi.
Zochita 2 Kufotokoza njira ya K-W- c. Ndamanga nyumba yaikulu
L pophunzitsa mitundu ndithu.
ya akapandamneni d. Kuledzera ndi kuphwanya
1 Mphunzitsi mnzanu pasukulu malamulo asukulu.
yanu wakuuzani kuti akufuna e. Anthuwo ankayenda
kuphunzitsa akapandamneni mofulumira kwambiri.
pogwiritsa ntchito njira ya K-W-L 2 Kodi mungaphunzitse bwanji
m’gawo loyamba la phunziro lake ophunzira kuti amvetse mosavuta
koma njirayi sakuidziwa mitundu ya akapandamneni?
kwenikweni. Kambiranani mfundo
zomwe angatsate.
2 Fotokozerani anzanu zomwe
mwakambirana.
3 Perekani maganizo anu pa ubwino
wotsatira njirayi.
19
Mabuku Chichewa. Bookland International,
Ngoma, SJL ndi Chauma, AM, (2014). Blantyre.
Tizame m’Chichewa: malamulo Nkhoma, WA, (1999). Kuphunzitsa
ophunzitsira ndi kuphunzirira Chinyanja. Zomba: Chancellor
College.
20
MUTU 7 Kuphunzitsa mitundu ya ziganizo
Kufotokoza mwachidule
M’mutu uno, mwaphunzira mitundu
inayi ya ziganizo ndi zitsanzo zake.
Mitunduyi ndi chiganizo chopanda
nthambi, chiganizo cha ziganizo
Zochita 1 Kuphunzitsa mitundu ya
zingapo, chiganizo chanthambi ndi
ziganizo
chiganizo cha ziganizo zanthambi.
1 Konzekerani kuphunzitsa mtundu
Pomaliza, mwaphunzitsa ndi
wa chiganizo womwe
kuzukuta phunziro la mitundu ya
mwapatsidwa.
ziganizo.
2 Phunzitsani phunziroli.
3 Kumbukirani kuyesa ophunzira
Kudziunika ndi kudziyesa
pamene mukuphunzitsa.
1 Kodi mwaphunzira zinthu ziti
4 Unikani momwe phunziro lililonse
pamene mumaphunzira mitundu
layendera.
ya ziganizo?
2 Fotokozani kusiyana pakati pa
Zochita 2 Kukonza ntchito
‘chiganizo chanthambi’ ndi
yokachitira kunyumba
‘chiganizo cha ziganizo za
1 Sankhani mtundu umodzi wa
nthambi’.
ziganizo.
3 Pa njira zosiyanasiyana
2 Konzani ntchito yoti ophunzira
zophunzitsira malamulo
anu akachitire kunyumba.
achiyankhulo, ndi njira iti yomwe
Mulemberetu mayankho a
yakusangalatsani pa phunziro la
ntchitoyo.
mitundu ya ziganizo? Fotokozani
zifukwa zake.
22
Matanthauzo a mawu Nkhoma, W, (2016). Kuphunzira
Chiganizo: Gulu la mawu lokhala ndi Chichewa: malamulo a chiyankhulo.
mneni ndipo limapereka ganizo Zomba: Chanco Publications.
lomveka bwino.
Kuwerenga koonjezera
Mabuku Chauma, AM and Ngoma, SJL, (2014).
Banda, FK, (2003). Methods of teaching Tizame m'Chichewa (3rd ed.).
Chichewa. Domasi: Domasi College Blantyre: Bookland International.
of Education. Nkhoma, WA, (1999). Kuphunzira
Nankwenya, IAJ, (1992). Zofunika mu Chinyanja. Zomba: Chanco
galamala ya Chichewa. Blantyre: Publications.
Dzuka.
23
MUTU 8 Kuphunzitsa nthambi za chiganizo
24
payokha ndi nthambi yosaima 2 Kambiranani momwe
payokha. mungazindikirire nthambi yosaima
3 Uzani anzanu zomwe payokha yadzina.
mwakambirana. 3 Pangani ziganizo zokhala ndi
nthambi yadzina.
Zochita 2 Kupanga ziganizo za 4 Fotokozerani anzanu zomwe
nthambi mwakambirana.
1 Pangani ziganizo zokhala ndi
nthambi. Zochita 3 Kuzindikira nthambi ya
2 Siyanitsani nthambizo posankha chiganizo yamfotokozi
zosaima pazokha. 1 Kambiranani momwe
3 Zukutani ziganizo zomwe anzanu mungadziwire nthambi ya
apanga. chiganizo yosaima payokha
yamfotokozi.
Ntchito 2 Kufotokoza ntchito za 2 Pangani ziganizo zokhala ndi
nthambi za ziganizo nthambizi.
zosaima pazokha
3 Sonyezani anzanu zomwe
Nthambi za chiganizo zosaima
mwalemba.
pazokha zimagwira ntchito
zosiyanasiyana molingana ndi
Zochita 4 Kuzindikira nthambi ya
mtundu wake. Tsopano mufotokoza
chiganizo yamuonjezi
ntchito za nthambi yosaima payokha
1 Kambiranani ntchito
yadzina, yamfotokozi ndi yamuonjezi.
zosiyanasiyana za muonjezi.
2 Pangani ziganizo zokhala ndi
Zochita 1 Kukambirana ntchito za
nthambi zosaima pazokha za
nthambi za ziganizo
muonjezi.
zosaima pazokha
3 Fotokozerani anzanu zomwe
1 Pezani nthambi zosaima pazokha
mwakambirana.
za mitundu yosiyanasiyana
kuchokera m’mabuku a ophunzira Ntchito 3 Kuphunzitsa nthambi za
m’sukulu a Sitandade 7 ndi 8. chiganizo
2 Kambiranani ntchito za nthambi za Tsopano muonerera aphunzitsi anu
ziganizo zomwe mwapeza. pamene akuphunzitsa. Kenaka,
3 Uzani anzanu zomwe muphunzitsa mtundu wa nthambi za
mwakambirana. chiganizo womwe mwapatsidwa.
25
2 Onererani pamene aphunzitsi anu Kudziunika ndi kudziyesa
akuphunzitsa nthambi za 1 Kodi pali kusiyana kotani pakati pa
chiganizo. nthambi yoima payokha ndi
3 Perekani maganizo anu pa momwe nthambi yosaima payokha ya
phunzirolo layendera. chiganizo?
2 Mungamuthandize bwanji
Zochita 2 Kuphunzitsa nthambi za wophunzira kusiyanitsa nthambi
chiganizo ya muonjezi yacholinga ndi
1 Konzekerani kuphunzitsa mtundu nthambi ya muonjezi yachifukwa.
wa nthambi za chiganizo womwe 3 Fotokozani momwe
mwapatsidwa. mungaphunzitsire phunziro la
2 Phunzitsani mtundu wa nthambi ‘nthambi za chiganizo’ ndipo
ya chiganizoyo potsatira njira mutchule njira yophunzitsira
yomwe mwasankha. yomwe mwasankha.
3 Unikani momwe maphunziro
ayendera. Matanthauzo a mawu
Nthambi ya chiganizo: gulu la mawu
Malangizo kwa mphunzitsi m’chiganizo lomwe limakhala ndi
Mukhale ndi mabuku okwanira a mneni wakewake.
ophunzira a Sitandade 7 ndi 8.
Mupezeretu zitsanzo za nthambi za Nthambi yoima payokha: gulu la
chiganizo zoima pazokha ndi mawu lokhala ndi mwininkhani
zosaima pazokha za dzina, komanso mneni ndipo limapereka
mfotokozi ndi muonjezi. ganizo lomveka bwino.
Muonetsetse kuti ophunzira
akufotokoza bwino ntchito za Nthambi yosaima payokha: gulu la
nthambi zosiyanasiyana za mawu lokhala ndi mneni wakewake
ziganizo pophunzitsa. koma silimapereka ganizo lomveka
Mukonzekere kuphunzitsa bwino palokha.
nthambi za ziganizo.
Muombe mkota pa zomwe Mabuku
ophunzira achita. Banda, FK, (2003). Methods of teaching
Chichewa. Domasi: Domasi College
of Education.
Kufotokoza mwachidule Nankwenya, IAJ, (1992). Zofunika mu
M’mutu uno, mwaphunzira tanthauzo galamala ya Chichewa. Blantyre:
ndi mitundu ya nthambi za chiganizo. Dzuka Publishing Company
Mwafotokoza ntchito za nthambi za Limited.
chiganizo mogwirizana ndi mitundu Nkhoma, W, (2016). Kuphunzira
yawo. Pomaliza, mwasonyeza momwe Chichewa: malamulo a chiyankhulo.
mungaphunzitsire nthambi za Zomba: Chanco Publications.
chiganizo.
26
Kuwerenga koonjezera
Chauma, AM & Ngoma, SJL, (2014).
Tizame m'Chichewa (3rded.).
Nkhoma, WA, (1999). Kuphunzira
Chinyanja. Zomba: Chanco
Publications
27
MUTU 9 Kuphunzitsa ndi kuyesa kuzukuta
ndakatulo/nyimbo, zilapi/ndagi, nkhani/nthano,
macheza ndi sewero
28
Kodi ndi mfundo yaikulu iti Zochita 2 Kuzukuta
yomwe ili mu ndakatulo/nyimbo, ndakatulo/nyimbo,
zilapi/ndagi, nkhani/nthano, nkhani/nthano, macheza
macheza ndi sewero? ndi sewero
Kodi zipangizo za nsetso (mawu
apadera monga mpeputso,
msemphano, voko ndi
chiyerekezo) zagwiritsidwa ntchito
bwanji?
29
macheza ndi sewero m’sukulu nkhani/nthano, macheza ndi
zomwe munkaphunzitsa. sewero m’sukulu zapulayimale.
2 Kambiranani momwe 2 Kodi ndi mfundo ziti zomwe
mungaphunzitsire kuzukuta zingakuthandizeni kuphunzitsa
ndakatulo/nyimbo, nkhani/nthano, kuzukuta ndakatulo/nyimbo,
macheza ndi sewero pogwiritsa nkhani/nthano, macheza ndi
ntchito njira zomwe sewero moyenera?
mwakambirana mu ntchito 1. 3 Perekani ndondomeko yomwe
3 Sonyezani kuphunzitsa kuzukuta mungatsatire pophunzitsa
ndakatulo/nyimbo, nkhani/nthano, kuzukuta ndakatulo/nyimbo,
macheza ndi sewero pogwiritsa nkhani/nthano, macheza ndi
ntchito njirazo. sewero.
4 Zukutani phunziro lomwe
mwaonera. Matanthauzo a mawu
Mpeputso: mawu osaumitsa thupi
Malangizo kwa mphunzitsi omwe amalowa m’malo mwa oipa.
Limbikitsani ophunzira kupereka
njira zothetsera mavuto omwe Msemphano: mawu onena zina koma
ankakumana nawo. akutathauza zina.
Mukhale ndi mabuku okwanira.
Mukonzeretu mfundo zoyenera Voko: kukuza zinthu
kutsatira pozukuta zazing’ono/mawu omwe amanena
ndakatulo/nyimbo, nkhani/nthano moonjezera kapena kusinjirira chabe.
ndi sewero.
Muombe mkota pa ntchito yomwe Chiyerekezo: kufananitsa mopanda
ophunzira achita. chindunji zinthu ziwiri zosiyana.
31
MUTU 10 Kuphunzitsa nsinjiro zachiyankhulo
32
mikuluwiko yofanana komanso Zochita 2 Kukambirana
yotsutsana m’matanthauzo. mikuluwiko yofanana
m’matanthauzo
1 Kambiranani kusiyana kwa
mkuluwiko ndi mwambi.
2 Fufuzani mikuluwiko
yosiyanasiyana m’mabuku a
ophunzira.
3 Kambiranani matanthauzo a
mikuluwiko yomwe mwapeza.
4 Pezani mikuluwiko yofanana
m’matanthauzo.
5 Fotokozerani anzanu zomwe
mwapeza.
Zochita 3 Kukambirana
mikuluwiko yotsutsana
m’matanthauzo
1 Fufuzani mikuluwiko
yosiyanasiyana m’mabuku a
ophunzira.
2 Kambiranani matanthauzo a
Zochita 1 Kukambirana mitundu ya
mikuluwiko yomwe mwapeza.
nsinjiro za chiyankhulo
3 Pezani mikuluwiko yotsutsana
1 Kambiranani matanthauzo ndi
m’matanthauzo.
zitsanzo za nsinjiro za chiyankhulo
4 Fotokozerani anzanu zomwe
izi:
mwapeza.
a. zining’a
b. ntchedzero/zifanifani
Ntchito 2 Kusintha nsinjiro
c. mipeputso
zachiyankhulo kukhala
d. nseketso
m’mitundu ina
e. mikuluwiko
Mu ntchito 1, munakambirana
f. miyambi
mitundu yosiyanasiyana ya nsinjiro za
2 Fufuzani nsinjiro za chiyankhulozi
chiyankhulo. Tsopano mukambirana
m’mabuku a ophunzira.
momwe mungasinthire
3 Kambiranani matanthauzo a
ntchedzero/zifanifani kukhala
nsinjiro zomwe mwapeza.
zining’a, zining’a kukhala
4 Uzani anzanu zomwe
ntchedzero/zifanifani komanso
mwakambirana.
mikuluwiko kukhala
ntchedzero/zifanifani.
33
Zochita 1 Kusintha Ntchito 3 Kuphunzitsa nsinjiro za
ntchedzero/zifanifani chiyankhulo
kukhala zining’a M’gawo lino, mukambirana za
1 Kambiranani matanthauzo a mipeputso ndi nseketso. Kenaka,
ntchedzero/zifanifani. musonyeza momwe
2 Pezani ntchedzero/zifanifani mungaphunzitsire nsinjiro
m’mabuku a ophunzira. zachiyankhulo.
3 Kambiranani kusiyana kwa
ntchedzero ndi zining’a. Zochita 1 Kupereka matanthauzo a
4 Kambiranani momwe mipeputso
mungasinthire 1 Kambiranani tanthauzo la
ntchedzero/zifanifani kukhala mpeputso.
zining’a. 2 Fufuzani zitsanzo za mpeputso.
5 Fotokozerani anzanu zomwe 3 Fotokozani kufunika kogwiritsira
mwakambirana. ntchito mipeputso.
4 Fotokozani matanthauzo a
Zochita 2 Kusintha zining’a mipeputso yomwe mwapeza.
kukhala 5 Fotokozerani anzanu zomwe
ntchedzero/zifanifani mwapeza.
1 Kambiranani momwe
ntchedzero/zifanifani Zochita 2 Kupereka matanthauzo
zimapangidwira. osiyana a nseketso
2 Pezani zining’a m’mabuku a 1 Kambiranani tanthauzo la
ophunzira. nseketso.
3 Sinthani zining’azo kukhala 2 Fufuzani zitsanzo za nseketso
ntchedzero/zifanifani. m’mabuku a ophunzira.
4 Fotokozerani anzanu zomwe 3 Kambiranani matanthauzo awiri
mwakambirana. osiyana a nseketso iliyonse.
4 Fotokozerani anzanu zomwe
Zochita 3 Kusintha mikuluwiko mwakambirana.
kukhala
ntchedzero/zifanifani Zochita 3 Kuphunzitsa nsinjiro za
1 Pezani mikuluwiko m’mabuku a chiyankhulo
ophunzira. 1 Konzekerani phunziro la nsinjiro
2 Sinthani mikuluwikoyo kukhala za chiyankhulo lomwe
ntchedzero/zifanifani. mwapatsidwa.
3 Fotokozerani anzanu zomwe 2 Kambiranani momwe
mwakambirana. mungaphunzitsire phunzirolo.
3 Sonyezani momwe
mungaphunzitsire phunziroli.
4 Zukutani maphunzirowo.
34
zining’a, ntchedzero/zifanifani,
Malangizo kwa mphunzitsi mipeputso, nseketso, mikuluwiko ndi
Mupezeretu zitsanzo zoyenera za miyambi. Mwakambirana kasinthidwe
nsinjiro za chiyankhulo izi: ka nsinjiro za chiyankhulo kupita ku
zining’a, ntchedzero/zifanifani, mitundu ina. Mwaphunziranso
mipeputso, nseketso ndi momwe mungaphunzitsire nsinjirozi
mikuluwiko. pokulitsa luso la kuganiza mozama
Mupezeretu mabuku a ophunzira mwa ophunzira. Pomaliza,
omwe muli nsinjiro za chiyankhulo mwasonyeza kuphunzitsa nsinjiro za
zosiyanasiyana. chiyankhulo.
Muonetsetse kuti ophunzira
akuphunzitsa potsatira Matanthauzo a mawu
ndondomeko yoyenera. Chining’a: Mawu amodzi kapena
Muombe mkota pa zomwe gulu lochepa la mawu lomwe
ophunzira achita. limakhala ndi tanthauzo lobisika.
35
MUTU 11 Kuphunzitsa mtantho wa mawu
36
1C
2M
3F
4N
5K
6E 7M
8D
9L
Mopingasa Mayankho
1 nthenda yotsokomoletsa Mopingasa
3 fika kumalo ambiri 1 Chifuwa
5 mtundu wa nthenda yotulutsa 3 Fala
timatuza pathupi 5 Katsabola
6 nthenda yosachizika 6 Edzi
8 samalira munthu wodwala 8 Dwazika
9 tulutsa mawu ndi misozi chifukwa 9 Lira
cha ululu
Motsitsa
Motsitsa 1 Chikuku
1 nthenda yotenthetsa thupi ndi 2 Maso
yofiiritsa maso yomwe ana 4 Nthenda
amadwala kawirikawiri 7 Mphere
2 nthenda yomwe imatulutsa 8 Dwala
manthongo m’maso
4 gwero la kudwala kapena kusamva Pomaliza, muyenera kumvetsetsa
bwino m’thupi ndondomeko yomwe mungatsatire
7 nthenda yotulutsa matuza pathupi pophunzitsa mtantho wa mawu kuti
omwe amatuluka mafinya ntchitoyi ikhale yopindulira
8 khala osapeza bwino m’thupi ophunzira. Mutu uno wapereka
chifukwa cha matenda tsatanetsatane wa momwe
mungaphunzitsire mtantho wa mawu.
37
Ntchito 1 Kufotokoza kufunika yoyenera kutsatira pophunzitsa
kophunzitsa mtantho wa mtantho wa mawu. Pomaliza,
mawu
musonyeza momwe
Monga sewero, mtantho wa mawu ndi
mungaphunzitsire mtantho wa mawu
njira yophunzirira yosangalatsa.
kwa ophunzira akupulayimale.
M’gawo lino, mufotokoza kufunika
kophunzitsa mtantho wa mawu.
Zochita 1 Kukambirana
ndondomeko
Zochita 1 Kufotokoza momwe
yophunzitsira mtantho wa
munkaphunzitsira
mawu
mtantho wa mawu
1 Unikani ndondomeko yomwe
1 Fufuzani zitsanzo za mtantho wa
munkatsatira pophunzitsa mtantho
mawu m’mabuku a ophunzira.
wa mawu.
2 Kambiranani tanthauzo la mtantho
2 Fotokozani mavuto omwe
wa mawu.
mudakumana nawo pogwiritsa
3 Fotokozani momwe
ntchito ndondomeko yomwe
munkaphunzitsira mtantho wa
mwatchula.
mawu m’sukulu zomwe
3 Kambiranani ndondomeko
munkaphunzitsa.
yoyenera yophunzitsira mtantho
4 Kambiranani mavuto omwe
wa mawu.
mudakumana nawo pophunzitsa
4 Uzani anzanu zomwe
mtantho wa mawu.
mwakambirana.
5 Perekani njira zomwe
mungagwiritse ntchito kuti
Zochita 2 Kuonerera phunziro la
muthetse mavuto omwe
mtantho wa mawu
munkakumana nawo.
1 Kambiranani momwe
mungaphunzitsire mtantho wa
Zochita 2 Kufotokoza kufunika
mawu.
kwa mtantho wa mawu
2 Onererani pamene aphunzitsi anu
1 Kambiranani kufunika
akuphunzitsa mtantho wa mawu.
kophunzitsa mtantho wa mawu.
3 Perekani maganizo anu pa momwe
2 Fotokozani mfundo zoyenera
phunzirolo layendera.
kutsatira pophunzitsa mtantho wa
mawu.
Zochita 3 Kuphunzitsa mtantho wa
3 Uzani anzanu zomwe
mawu
mwakambirana.
1 Konzani ndondomeko
yophunzitsira mthantho wa mawu
Ntchito 2 Kuphunzitsa mtantho wa
mawu mu kalasi lomwe mwasankha.
Mwakambirana kuti mtantho wa 2 Phunzitsani mtantho wa mawu
mawu ndi wofunika kwambiri pogwiritsa ntchito ndondomeko
pophunzitsa chiyankhulo. M’gawo yomwe mwakonza.
lino, mufotokoza ndondomeko 3 Zukutani maphunzirowo.
38
3 Ndi mfundo ziti zomwe
Malangizo kwa mphunzitsi mungatsate kuti phunziro la
Mukonzeretu ndondomeko mtantho wa mawu m’kalasi lanu
yophunzitsira mtantho wa mawu. likhale losangalatsa ndi lopatsa
Mupezeretu mtantho wa mawu chidwi kwa ophunzira?
woti muphunzitsire. 4 Lembani chitsanzo cha mtantho
Muombe mkota pa ntchito zomwe wa mawu wophunzitsira
ophunzira achita. malamulo a chiyankhulo kapena
zilapi kwa ophunzira a Sitandade
Kufotokoza mwachidule 5.
M’mutu uno, mwaunika momwe
munkaphunzitsira mtantho wa mawu Matanthauzo a mawu
komanso mwafotokoza tanthauzo ndi Mtantho wa mawu: Sewero lolemba
kufunika kwake. Mwaunikanso mawu mopingasa ndi motsitsa
ndondomeko yoyenera kugwiritsa
ntchito pophunzitsa mtantho wa Mabuku
mawu, mfundo zoyenera kuganizira Chilora, H G & Kathewera, REM,
pophunzitsa ndi momwe (2014). Chichewa buku la ophunzira a
mungaphunzitsire. Pomaliza, Fomu 2. Blantyre: Dzuka publishing
mwasonyeza kaphunzitsidwe company limited.
koyenera ka mtantho wa mawu. Malawi institute of Education, (2008).
Maphunziro a m’sukulu zapulayimale
Kudziunika ndi kudziyesa m’Malawi: Chichewa buku la
1 Mwapeza kuti aphunzitsi ena pa mphunzitsi la Sitandade 7. Domasi:
sukulu yanu saphunzitsa Malawi Institute of Education.
mtantho wa mawu m’makalasi
awo. Kodi mungapereke Kuwerenga koonjezera
malangizo otani kwa aphunzitsi Chauma, AM & Ngoma, SJL, (2014).
otere? Tizame m'Chichewa (3rded.).
2 Fotokozani ndondomeko Blantyre: Bookland International.
yoyenera yophunzitsira mtantho
wa mawu.
39